Maliro 4 – CCL & CCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Maliro 4:1-22

1Haa! Golide wathimbirira,

golide wosalala wasinthikiratu!

Amwazamwaza miyala yokongola ya kumalo opatulika

pamphambano ponse pa mzinda.

2Haa! Ana a Ziyoni amtengowapatali

amene kale anali ngati golide,

tsopano ali ngati miphika ya dothi,

ntchito ya owumba mbiya!

3Ngakhale nkhandwe zimapereka bere

kuyamwitsa ana ake,

koma anthu anga asanduka ankhanza

ngati nthiwatiwa mʼchipululu.

4Lilime la mwana lakangamira kukhosi

chifukwa cha ludzu,

ana akupempha chakudya,

koma palibe amene akuwapatsa.

5Iwo amene kale ankadya zonona

akupemphetsa mʼmisewu ya mu mzinda.

Iwo amene kale ankavala zokongola

tsopano akugona pa phulusa.

6Kuyipa kwa anthu anga kunali kwakukulu

kuposa anthu a ku Sodomu,

amene anawonongedwa mʼkamphindi kochepa

popanda owathandiza.

7Akalonga ake anali owala koposa chisanu chowundana

ndi oyera kuposa mkaka.

Matupi awo anali ofiira kuposa miyala ya rubi,

maonekedwe awo ngati miyala ya safiro.

8Koma tsopano maonekedwe awo ndi akuda kuposa mwaye;

palibe angawazindikire mʼmisewu ya mu mzinda.

Khungu lawo lachita makwinyamakwinya pa mafupa awo;

lawuma gwaa ngati nkhuni.

9Amene anaphedwa ndi lupanga aliko bwino kuposa

amene anafa ndi njala;

chifukwa chosowa chakudya cha mʼmunda

iwowa ankafowoka ndi njala mpaka kufa.

10Amayi achifundo afika

pophika ana awo enieni,

ndiwo anali chakudya chawo pamene anthu

anga anali kuwonongeka.

11Yehova wakwaniritsa ukali wake;

wagwetsa pansi mkwiyo wake woopsa.

Ndipo wayatsa moto mʼZiyoni

kuti uwononge maziko ake.

12Mafumu a pa dziko lapansi sanakhulupirire,

kapena wina aliyense wokhala pa dziko lonse,

kuti adani kapena ankhondo akhoza kulowa

pa zipata za Yerusalemu.

13Koma izi zinachitika chifukwa cha kuchimwa kwa aneneri ake

ndi mphulupulu za ansembe ake,

amene ankapha anthu osalakwa pakati pawo.

14Tsopano akungoyendayenda mʼmisewu ya mu mzinda

ngati anthu osaona.

Iwo ndi odetsedwa kwambiri ndi magazi

palibe yemwe angayerekeze nʼkukhudza komwe chovala chawo.

15Anthu akuwafuwulira kuti, “Chokani! Inu anthu odetsedwa!”

“Chokani! Chokani! Musatikhudze ife!”

Akamathawa ndi kumangoyendayenda,

pakati pa anthu a mitundu yonse amati,

“Asakhalenso ndi ife.”

16Yehova mwini wake wawabalalitsa;

Iye sakuwalabadiranso.

Ansembe sakulandira ulemu,

akuluakulu sakuwachitira chifundo.

17Ndiponso maso athu atopa nʼkuyangʼana,

chithandizo chosabwera nʼkomwe,

kuchokera pa nsanja zathu tinadikirira mtundu

wa anthu umene sukanatipulumutsa.

18Anthu ankalondola mapazi athu,

choncho sitikanayenda mʼmisewu yathu mu mzinda.

Chimaliziro chathu chinali pafupi, masiku athu anali owerengeka,

chifukwa chimaliziro chathu chinali chitafika.

19Otilondola akuthamanga kwambiri

kuposa ziwombankhanga mu mlengalenga;

anatithamangitsa mpaka ku mapiri

ndi kutibisalira mʼchipululu.

20Wodzozedwa wa Yehova, mpweya wathu wotipatsa moyo,

anakodwa mʼmisampha yawo.

Tinaganiza kuti tidzakhala pansi pa mthunzi wake

pakati pa mitundu ya anthu.

21Kondwera ndi kusangalala, mwana wamkazi wa Edomu.

Iwe amene umakhala mʼdziko la Uzi.

Koma iwenso chikho chidzakupeza;

udzaledzera mpaka kukhala maliseche.

22Iwe mwana wamkazi wa Ziyoni, chilango chako chidzatha;

Iye sadzatalikitsa nthawi yako ya ukapolo.

Koma Yehova adzalanga machimo ako, iwe mwana wamkazi wa Edomu,

ndi kuyika poyera mphulupulu zako.

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

耶利米哀歌 4:1-22

沦陷的耶路撒冷

1黄金竟失去光泽,

纯金竟变色,

宝石竟被弃之街头。

2锡安的宝贝子民本来贵如黄金,

现在竟被视为陶匠制作的瓦器!

3豺狼尚且哺养自己的幼儿,

我的子民却像荒野的鸵鸟一样残忍无情。

4婴儿干渴难忍,舌头紧贴上膛;

孩童乞求食物,却无人给予。

5昔日锦衣玉食、生活奢侈的,

如今却流落街头,

躺卧在粪堆中。

6虽然无人攻击,所多玛却在顷刻之间倾覆。

我子民比所多玛受到的惩罚更重。

7锡安的首领曾比雪纯净,

比奶更白,

身体比红宝石更红润,

相貌美如蓝宝石。

8现在,他们的面目比煤炭还黑,

走在街上无人认得。

他们骨瘦如柴,干如枯木。

9死于刀下的胜过死于饥饿的,

后者因田间缺粮而活活饿死。

10我的百姓遭毁灭时,

慈母亲手煮自己的儿女充饥。

11耶和华大发烈怒,

倾倒祂的怒气,

锡安燃起大火,

焚毁城的根基。

12世上的君王和居民都不相信敌人能闯进耶路撒冷的城门。

13这都是因为她的先知和祭司的罪行。

他们在城中杀害义人。

14他们如盲人在街上游荡,

沾满血污,

无人敢碰他们的衣服。

15人们向他们喊道:

“走开!你们是不洁的!

走开!走开!不要靠近我们。”

于是他们逃亡、流荡,

列国的人说:

“他们不可住在我们这里。”

16耶和华亲自驱散他们,

不再眷顾他们;

人们不再尊重祭司,

也不再敬重长老。

17我们望眼欲穿,

盼望援军的到来,

盼来的国家却无力拯救我们。

18敌人步步紧逼,

使我们不敢上自己的街。

我们的结局近了,

我们的日子到头了,

我们的末日来了!

19追赶我们的人比飞鹰更快,

他们在山上追捕我们,

在旷野伏击我们。

20耶和华膏立的王——我们的生命之气落入他们的陷阱。

我们原希望借他的荫庇立足于列国中。

21乌斯地区的以东人啊,

只管欢喜作乐吧!

因为盛满耶和华愤怒的杯也要传到你们那里。

你们必喝醉,以致赤身露体。

22锡安城啊!你已经受到了应得的刑罚,

耶和华必不再使你流亡。

以东啊,耶和华要惩罚你,

揭露你的罪恶!