Machitidwe a Atumwi 9 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Machitidwe a Atumwi 9:1-43

Kutembenuka Mtima kwa Saulo

1Pa nthawi imeneyi, Saulo ankaopsezabe okhulupirira Ambuye nafuna kuwapha. Iye anapita kwa mkulu wa ansembe, 2ndi kukapempha makalata a chilolezo kuti apite nawo ku masunagoge a ku Damasiko, kuti ngati atakapezeka ena kumeneko otsata Njirayo, kaya ndi amuna kapena amayi, akawamange ndi kuwatenga kubwera nawo ku Yerusalemu. 3Akuyandikira ku Damasikoku paulendo wake, mwadzidzidzi kuwala kochokera kumwamba kunamuzungulira iye. 4Iye anagwa pansi ndipo anamva mawu akuti, “Saulo, Saulo ukundizunziranji Ine?”

5Saulo anafunsa kuti, “Ndinu yani Ambuye?”

Ambuye anayankha kuti, “Ndine Yesu amene iwe ukumuzunza.” 6“Tsopano dzuka, lowa mu mzindamo, ndipo udzawuzidwa zoyenera kuchita.”

7Anthu amene anali naye paulendo, anasowa chonena; iwo anamva mawu koma sanaone wina aliyense. 8Saulo anayimirira, ndipo pamene anatsekula maso ake sanathe kuona. Kotero anamugwira dzanja ndi kulowa naye mu Damasiko. 9Anakhala wosaona kwa masiku atatu ndiponso sanadye kapena kumwa kanthu kalikonse.

10Ku Damasiko kunali wophunzira wina dzina lake Hananiya. Ambuye anamuyitana mʼmasomphenya kuti, “Hananiya!”

Iye anayankha kuti, “Ine Ambuye.”

11Ambuye anamuwuza iye kuti, “Nyamuka, pita ku nyumba ya Yudasi imene ili pa Njira Yolunjika ndipo ukafunse za munthu wochokera ku Tarisisi dzina lake Saulo, pakuti akupemphera. 12Ndipo waona mʼmasomphenya munthu, dzina lake Hananiya atabwera ndi kumusanjika manja kuti aonenso.”

13Hananiya anayankha kuti, “Ambuye, ndinamva zambiri za munthu uyu ndi zonse zoyipa anachitira oyera mtima a ku Yerusalemu. 14Ndipo wabwera kuno ndi ulamuliro wa akulu ansembe kuti adzamange onse amene amayitana pa dzina lanu.”

15Koma Ambuye anati kwa Hananiya, “Pita! Munthu uyu ndi chida changa chosankhika chonyamulira dzina langa pamaso pa anthu a mitundu ina ndi mafumu awo ndiponso kwa anthu a Israeli. 16Ine ndidzamuonetsa zowawa zonse zimene ayenera kumva chifukwa cha dzina langa.”

17Pamenepo Hananiya ananyamuka ndi kukalowa mʼnyumbayo. Anamusanjika manja Sauloyo ndipo anati, “Mʼbale Saulo, Ambuye Yesu, amene anakuonekera pa msewu pamene umabwera kuno wandituma kuti uwonenso ndi kudzazidwa ndi Mzimu Woyera.” 18Nthawi yomweyo mʼmaso mwa Saulo munachoka zinthu zokhala ngati mamba ansomba, ndipo anayambanso kuona. Iye anayimirira nabatizidwa, 19ndipo atadya chakudya, anapezanso mphamvu.

Saulo Alalikira ku Damasiko

Saulo anakhala masiku angapo ndi ophunzira a ku Damasiko. 20Posakhalitsa anayamba kulalikira mʼsunagoge kuti Yesu ndiye Mwana wa Mulungu. 21Onse amene anamva iye akulalikira anadabwa ndipo anafunsa kuti, “Kodi uyu si munthu amene anayambitsa kuzunza okhulupirira ku mpingo wa ku Yerusalemu? Kodi siwabwera kuno kuti awamange ndi kuwapereka kwa akulu a ansembe?” 22Koma mphamvu za Saulo zinali kukulirakulira ndipo anathetsa nzeru Ayuda okhala ku Damasiko powatsimikizira kuti Yesu ndi Mpulumutsi.

23Patapita masiku ambiri, Ayuda anapangana zoti aphe Saulo, 24koma iye anadziwa za chiwembucho. Anthu ankadikirira usana ndi usiku pa zipata za mzindawo kuti amuphe. 25Koma ophunzira ake anamutenga usiku, namutsitsira kunja kwa mpandawo mʼdengu.

Saulo ku Yerusalemu

26Saulo atafika ku Yerusalemu, anayesetsa kulowa mʼgulu la ophunzira koma onse anamuopa chifukwa sanakhulupirire kuti anali wophunziradi. 27Koma Barnaba anamutenga napita naye kwa atumwi. Iye anawafotokozera iwo za mmene Saulo anaonera Ambuye pa njira paja, ndi kuti Ambuye anamuyankhula, ndi momwe analalikira ku Damasiko mʼdzina la Yesu mosaopa. 28Kotero Saulo anakhala nawo nayendayenda mwaufulu mu Yerusalemu akulalikira molimba mtima mʼdzina la Ambuye. 29Anayankhula ndi kutsutsana ndi Ayuda a Chihelene, koma iwo ankafuna kumupha. 30Abale atadziwa zimenezi, anamutenga Saulo ndi kupita naye ku Kaisareya, ndipo anamutumiza ku Tarisisi.

31Pamenepo mpingo wa ku Yudeya konse, ku Galileya ndi ku Samariya unakhala pamtendere, unalimbikitsidwa; ndi kupatsidwa mphamvu ndi Mzimu Woyera, unakula mʼchiwerengero, ndi kukhala moopa Ambuye.

Eneya ndi Tabita

32Pamene Petro amayendera mpingo, anapita kukachezera oyera mtima a ku Luda. 33Kumeneko anakapeza munthu dzina lake Eneya, wofa ziwalo amene anagona pa mphasa kwa zaka zisanu ndi zitatu. 34Petro anati kwa iye, “Eneya, Yesu Khristu akukuchiritsa iwe, dzuka ndipo yalula mphasa yako.” Nthawi yomweyo Eneya anayimirira. 35Anthu onse amene anakhala ku Luda ndi ku Sharoni anamuona ndipo anatembenukira kwa Ambuye.

36Ku Yopa kunali wophunzira wina dzina lake Tabita (mʼChigriki amati Dorika) amene nthawi zonse ankachita zachifundo ndiponso kuthandiza osauka. 37Nthawi imeneyi anadwala ndipo anamwalira, anasambitsa thupi lake, namugoneka mʼchipinda chammwamba. 38Popeza ku Yopa kunali pafupi ndi Luda; pamene ophunzira anamva kuti Petro anali ku Luda, anatuma anthu awiri kuti akamudandaulire kuti, “Chonde bwerani kuno msanga!”

39Petro ananyamuka, napita nawo, ndipo atafika anamutengera ku chipinda chammwamba. Amasiye onse anayima momuzungulira akulira ndi kumuonetsa mwinjiro ndi zovala zina zimene Dorika ankapanga akanali moyo.

40Petro anatulutsa anthu onse mʼchipindamo; ndipo anagwada pansi ndi kupemphera. Anatembenukira mtembo uja nati, “Tabita, dzuka,” Tabita anatsekula maso ake, ndipo ataona Petro anakhala pansi. 41Petro anamugwira dzanja, namuyimiritsa. Ndipo anayitana okhulupirira ndi amasiye namupereka wamoyo. 42Zimenezi zinadziwika ku Yopa konse, ndipo anthu ambiri anakhulupirira Ambuye. 43Petro anakhala ku Yopa kwa masiku ambiri kwa munthu wina, dzina lake Simoni, mmisiri wa zikopa.

New Russian Translation

Деяния 9:1-43

Обращение Савла

1Савл по-прежнему дышал злобой, желая смерти ученикам Господа. Он пришел к первосвященнику 2и попросил у него письма к синагогам Дамаска, чтобы он мог арестовывать и приводить в Иерусалим всех принадлежащих Пути9:2 Принадлежащие Пути – это определение является ранним самоназванием последователей Иисуса Христа, Который и есть «Путь» (см. Ин. 14:6; Деян. 19:9; 19:23; 22:4; 24:14, 22)., которых сможет там найти, будь то мужчины или женщины.

3Когда он уже приближался к Дамаску, его внезапно озарил свет с неба. 4Он упал на землю и услышал голос:

– Савл, Савл, почему ты Меня гонишь?

5– Кто Ты, Господи? – спросил Савл.

– Я Иисус, Которого ты преследуешь, – ответил Он. 6– Вставай и иди в город, там тебе скажут, что ты должен делать.

7Люди, путешествовавшие вместе с Савлом, стояли онемев: они слышали звук, но никого не видели. 8Савл поднялся с земли, но когда он открыл глаза, оказалось, что он ничего не видит; и его за руку привели в Дамаск. 9Три дня он был слеп и ничего не ел и не пил.

10В Дамаске жил ученик по имени Анания. Господь сказал ему в видении:

– Анания!

– Да, Господи, – ответил тот.

11Господь сказал ему:

– Пойди на улицу Прямую в дом Иуды и спроси там человека из Тарса по имени Савл. Он сейчас молится, 12и в видении он видел человека по имени Анания, который пришел и возложил на него руки, чтобы он прозрел.

13Анания ответил:

– Господи, я от многих людей слышал об этом человеке, о том, как много зла он причинил Твоим святым в Иерусалиме. 14И сюда он пришел, получив от первосвященников полномочия арестовывать всех, кто призывает Твое имя.

15Но Господь сказал ему:

– Иди, потому что человек этот – Мое орудие, которое Я избрал, чтобы возвестить имя Мое перед язычниками, перед царями и перед народом Израиля. 16Я покажу ему и то, сколько ему предстоит пострадать из-за Моего имени.

17Анания пошел, вошел в тот дом, возложил на Савла руки и сказал:

– Брат Савл, Господь Иисус, Который явился тебе на твоем пути сюда, послал меня к тебе, чтобы ты опять мог видеть и был исполнен Святым Духом.

18В тот же момент будто чешуя спала с глаз Савла, и он прозрел. Он встал и принял крещение. 19Затем он поел, и к нему вернулись силы.

Савл проповедует в Дамаске

Савл провел несколько дней с учениками в Дамаске 20и сразу же начал возвещать в синагогах о том, что Иисус – Сын Бога. 21Все, кто его слышал, удивлялись и говорили:

– Разве не он истреблял в Иерусалиме призывающих это имя и разве он не пришел сюда, чтобы арестовывать их и вести к первосвященникам?

22Савл проповедовал все с большей силой и приводил в замешательство живших в Дамаске иудеев, доказывая, что Иисус есть Христос.

23Когда же прошло немало дней, среди иудеев был составлен заговор с целью убить Савла. 24Однако Савлу стало известно об этом. Заговорщики день и ночь сторожили у ворот города, чтобы убить его, 25но его ученики ночью взяли и спустили его в корзине по городской стене.

Савл в Иерусалиме

26Савл пришел в Иерусалим и пытался присоединиться к ученикам, но они боялись его и не верили, что он тоже ученик. 27Варнава же привел его к апостолам и рассказал им о том, как Савл на пути встретил Господа, как Господь говорил с ним и как в Дамаске он смело проповедовал во имя Иисуса. 28Савл пробыл с ними некоторое время и свободно ходил по Иерусалиму, смело проповедуя во имя Господа. 29Он часто беседовал и спорил с грекоязычными иудеями, и те пытались убить его. 30Когда братья узнали об этом, они отвели Савла в Кесарию и оттуда отправили его в Тарс.

31Между тем для церкви по всей Иудее, Галилее и Самарии наступило мирное время. Церковь укреплялась и росла, живя в страхе перед Господом и получая ободрение от Святого Духа.

Исцеление Энея

32Петр, посещая город за городом, решил навестить и святых, живущих в Лидде. 33Там был один человек, которого звали Эней, он был парализован и не вставал с постели восемь лет. 34Петр сказал ему:

– Эней! Иисус Христос исцеляет тебя. Встань и собери постель.

В тот же момент Эней встал. 35Когда все жители Лидды и Шарона увидели его исцеленным, они обратились к Господу.

Воскресение Тавиты

36В Яффе была одна ученица по имени Тавита, что значит «газель». Она всегда делала добро и помогала бедным. 37И вот в это время она заболела и умерла. Ее омыли и положили в верхней комнате. 38Поскольку Лидда находится недалеко от Яффы, ученики, услышав, что Петр находится там, послали к нему двух человек с просьбой:

– Приди срочно к нам!

39Петр пошел с ними, и когда он прибыл, его провели в верхнюю комнату. Вокруг него собрались все вдовы. Они плакали и показывали ему платья и другую одежду, которую сшила им Газель, когда она была жива. 40Петр выслал всех из комнаты, стал на колени и помолился. Затем он повернулся к умершей и сказал:

– Тавита, встань!

Она открыла глаза, увидела Петра и села. 41Он взял ее за руку и помог встать на ноги. Затем он созвал вдов и других верующих и представил им Тавиту живой. 42Об этом стало известно во всей Яффе, и много людей поверило в Господа.

43Петр пробыл в Яффе еще немало дней, он остановился у кожевника Симона.