Machitidwe a Atumwi 12 – CCL & HHH

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Machitidwe a Atumwi 12:1-25

Petro Apulumuka Mʼndende

1Inali nthawi yomweyi imene mfumu Herode anamanga ena a mu mpingo ndi cholinga chakuti awazunze. 2Iye analamula kuti Yakobo mʼbale wa Yohane, aphedwe ndi lupanga. 3Ataona kuti zimenezi zinakondweretsa Ayuda, anawonjeza ndi kugwiranso Petro. Izi zinachitika pa nthawi ya Chikondwerero cha Buledi wopanda Yisiti. 4Atamugwira Petro, namutsekera mʼndende, anamupereka kwa magulu anayi a asilikali kuti amuyangʼanire, gulu lililonse linali ndi asilikali anayi. Herode anafuna kumuzenga mlandu pamaso pa anthu onse chikondwerero cha Paska chitapita.

5Kotero Petro anasungidwa mʼndende, koma mpingo unamupempherera kolimba kwa Mulungu.

6Usiku woti mmawa mwake Herode amuzenga mlandu, Petro amagona pakati pa asilikali awiri, atamangidwa maunyolo awiri, ndiponso alonda atayima pa khomo. 7Mwadzidzidzi mngelo wa Ambuye anaonekera ndipo kuwala kunawunika mʼchipindamo. Mngeloyo anamugwedeza Petro mʼnthiti ndi kumudzutsa. Iye anati, “Fulumira, imirira!” Ndipo maunyolo anagwa kuchoka mʼmanja a Petro.

8Kenaka mngelo anati kwa iye, “Vala zovala ndi nsapato.” Ndipo Petro atachita izi mngeloyo anamuwuzanso kuti, “Funda chovala chako ndipo unditsate.” 9Petro anatsatira natuluka mʼndende, koma sanazindikire kuti zimene mngeloyo amachita zimachitikadi; iye amaganiza kuti amaona masomphenya. 10Iwo anadutsa gulu loyamba ndi lachiwiri la asilikali ndipo anafika pa chitseko chachitsulo cholowera mu mzinda. Chitsekocho chinatsekuka chokha ndipo anadutsa. Pamene anayenda kutalika kwa msewu umodzi, mwadzidzidzi mngelo uja anachoka.

11Pamenepo Petro anazindikira nati, “Tsopano ndikudziwa mosakayika kuti Ambuye anatuma mngelo wake kudzandipulumutsa mʼmanja mwa Herode, ndi ku zoyipa zonse zimene Ayuda amafuna kundichitira.”

12Atazindikira zimenezi anapita ku nyumba ya Mariya amayi ake a Yohane, wotchedwanso Marko, kumene kunasonkhana anthu ambiri ndipo amapemphera. 13Petro anagogoda pa chitseko cha panja, ndipo mtsikana wantchito dzina lake Roda anabwera kuti adzatsekule chitseko. 14Atazindikira mawu a Petro anakondwa kwambiri ndipo anabwerera osatsekula ndipo anafuwula kuti, “Petro ali pa khomopa!”

15Anthuwo anati kwa iye, “Wopenga iwe!” Atalimbikira kunena kuti zinali zoona, iwo anati, “Ameneyo ndi mngelo wake.”

16Koma Petro anapitiriza kugogoda ndipo atatsekula chitseko ndi kumuona, anthuwo anadabwa kwambiri. 17Petro anakweza dzanja ndi kuwawuza kuti akhale chete ndipo anawafotokozera mmene Ambuye anamutulutsira mʼndende. Iye anati, “Uzani Yakobo ndi abale ena za zimenezi.” Kenaka anachoka napita kumalo ena.

18Pamene kunacha kunali phokoso lalikulu pakati pa asilikali, iwo anafunsa kuti, “Kodi chamuchitikira Petro ndi chiyani?” 19Herode atamufunafuna ndipo wosamupeza, anawafunsa asilikali ndipo analamulira kuti asilikaliwo aphedwe.

Imfa ya Herode

Kenaka Herode anachoka ku Yudeya ndi kupita ku Kaisareya ndipo anakhala kumeneko kwa kanthawi 20Herode anakwiyira anthu a ku Turo ndi Sidoni; anthuwo anagwirizana zoti akambirane naye. Atapeza thandizo kuchokera kwa Blasito, wantchito wokhulupirika wa mfumu, anapempha kuti pakhale mtendere, chifukwa dziko lawo limadalira dziko la mfumuyo pa chakudya chawo.

21Pa tsiku limene anasankha Herode, atavala zovala zake zaufumu, anakhala pa mpando wake ndipo anayankhula kwa anthuwo. 22Anthuwo anafuwula nati, “Amenewa ndi mawu a mulungu osati a munthu ayi.” 23Nthawi yomweyo mngelo wa Mulungu anamukantha chifukwa sanapereke ulemu kwa Mulungu ndipo anadyedwa ndi mphutsi nafa.

24Koma Mawu a Mulungu anapitirirabe kufalikirafalikira.

25Barnaba ndi Saulo atamaliza ntchito yawo anachoka ku Yerusalemu, atatenga Yohane wotchedwanso Marko.

Habrit Hakhadasha/Haderekh

מעשי השליחים 12:1-25

1באותם הימים התנכל המלך הורדוס למאמינים אחדים, 2אף הוציא להורג את יעקב השליח, אחיו של יוחנן. 3כשראה הורדוס שהדבר מצא־חן בעיני מנהיגי היהודים, אסר את פטרוס באמצע חג הפסח. 4הורדוס התכוון להעמיד את פטרוס למשפט פומבי בתום החג, ועל כן השליך אותו בינתיים לכלא והפקיד עליו שישה־עשר שומרים. 5אולם הקהילה התפללה בעד פטרוס ללא הרף בעת מעצרו.

6בלילה שקדם למשפט הפומבי ישן פטרוס בין שני חיילים, כבול בשרשרת כפולה, והשומרים שמרו בזהירות על פתח הכלא. 7לפתע זרח אור בתוך התא, ומלאך ה׳ עמד לצידו של פטרוס. המלאך נגע בירכו של פטרוס והעירו משנתו. ”קום, מהר!“ קרא המלאך. באותו רגע נפלו השרשרות מעל־ידיו. 8”התלבש ונעל את נעליך“, הוסיף המלאך, ופטרוס עשה. ”עכשיו לבש את מעילך ובוא אחרי!“ פקד.

9פטרוס יצא מהתא בעקבות המלאך, אולם כל הזמן חשב שזהו רק חלום או חזיון; הוא לא יכול היה להאמין שכל זה קורה לו במציאות! 10הם חלפו על פני גוש התאים הראשון והשני, והגיעו אל שער הברזל הפונה לרחוב. השער נפתח לפניהם מעצמו, והם עברו דרכו. הם המשיכו ללכת עוד מרחק קצר, ולפתע נעלם המלאך.

11פטרוס הבין לבסוף את המתרחש. ”אין זה חלום!“ אמר לעצמו. ”אלוהים באמת שלח את מלאכו להציל אותי מיד הורדוס וממזימותיהם של היהודים!“ 12לאחר שעיכל את הדבר במוחו הלך אל ביתה של מרים, אמו של יוחנן מרקוס. שם התאספו מאמינים רבים לתפילה.

13פטרוס דפק על דלת הבית, ונערה בשם רודה ניגשה לראות מי זה. 14כשהכירה את קולו של פטרוס היא שמחה כל־כך, עד ששכחה לפתוח את הדלת. היא מיהרה להיכנס אל הבית וסיפרה לכולם שפטרוס עומד בחוץ.

15האחים לא האמינו לה. ”יצאת מדעתך!“ קראו. אולם מאחר שרודה עמדה על שלה, חשבו: ”אולי זהו המלאך של פטרוס. הם ודאי הרגו אותו.“

16בינתיים המשיך פטרוס לדפוק על הדלת, וכשיצאו לבסוף האחים לפתוח את השער, הם הופתעו מאוד! 17פטרוס אמר להם לשתוק, וסיפר להם כיצד חילץ אותו האדון מבית־הכלא. ”ספרו זאת ליעקב ולאחים“, ביקש מהם, והלך לו למקום בטוח יותר.

18עם אור הבוקר שררה מבוכה גדולה בכלא: מה קרה לפטרוס? 19הורדוס שלח את אנשיו לחפש את פטרוס, אך הם לא מצאו אותו. משום כך ציווה הורדוס לאסור את שישה־עשר השומרים, להעמידם לדין ולהוציאם להורג. לאחר מכן עזב את העיר ועבר לגור בקיסריה.

20בהיותו בקיסריה הגיעה משלחת מהערים צור וצידון כדי לראותו. הורדוס לא היה ביחסים טובים עם תושבי הערים האלה, אולם חברי המשלחת התיידדו עם בלסטוס המזכיר של המחוז וביקשו שלום, כי מבחינה כלכלית הייתה ארצם תלויה במסחר עם ארצו של הורדוס. 21נקבע להם ראיון עם הורדוס, וביום המיועד הוא לבש את בגדי מלכותו, ישב על כסא מפואר ונאם לפניהם. 22בתום הנאום הריע לו הקהל בתשואות רמות וצעק: ”זהו קולו של אל, ולא של בן־תמותה!“

23באותו רגע הכה מלאך ה׳ את הורדוס במחלה קשה; גופו נמלא תולעים שכרסמו אותו, וכעבור זמן קצר מת, משום שקיבל את סגידת האנשים במקום שיחלוק את הכבוד לאלוהים.

24בשורת הישועה של אלוהים התפשטה במהירות, ומאמינים רבים נוספו לקהילה.

25לאחר שסיימו בר־נבא ושאול את שליחותם בירושלים, לקחו איתם את יוחנן מרקוס ושבו לאנטיוכיה.