Luka 24 – CCL & PCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Luka 24:1-53

Yesu Auka kwa Akufa

1Pa tsiku loyamba la Sabata, mmamawa kwambiri, amayi anatenga zonunkhira napita ku manda. 2Anaona mwala wa pa manda utagubuduzika 3ndipo atalowamo sanapeze mtembo wa Ambuye Yesu. 4Pamene iwo ankadabwa za zimenezi, mwadzidzidzi, amuna awiri ovala zovala zonyezimira kwambiri anayimirira pambali pawo. 5Ndi mantha, amayiwo anaweramitsa nkhope zawo pansi, koma amunawo anawawuza kuti, “Nʼchifukwa chiyani mukufuna wamoyo pakati pa akufa? 6Iye sali muno ayi. Wauka! Kumbukirani zimene anakuwuzani pamene anali nanu ku Galileya: 7‘Mwana wa Munthu ayenera kuperekedwa mʼmanja mwa anthu ochimwa, napachikidwa ndipo tsiku lachitatu adzaukitsidwanso.’ ” 8Ndipo anakumbukira mawu ake.

9Atabwerera kuchokera ku mandako, anafotokoza zinthu zonse kwa khumi ndi mmodziwo ndi kwa ena onse. 10Amayi anali Mariya Magadalena, Yohana, Mariya amayi a Yakobo, ndi ena anali nawo amene anawuza atumwi. 11Koma iwo sanawakhulupirire amayiwa, chifukwa mawu awo amaoneka kwa iwo ngati opanda nzeru. 12Komabe Petro anayimirira ndi kuthamangira ku manda. Atasuzumira, anaona nsalu zimene anamukulungira zija zili pa zokha, ndipo iye anachoka, akudabwa ndi zimene zinachitikazo.

Zochitika pa Njira ya ku Emau

13Ndipo tsiku lomwelo, awiri a iwo ankapita ku mudzi wotchedwa Emau, pafupifupi makilomita khumi ndi imodzi kuchokera ku Yerusalemu. 14Iwo ankayankhulana za zonse zimene zinachitikazo. 15Pamenepo Yesu mwini wake anabwera ndi kuyenda nawo pamodzi; 16koma iwo sanamuzindikire.

17Iye anawafunsa kuti, “Kodi mukukambirana zotani mʼnjira muno?”

Iwo anayima ndi nkhope zakugwa. 18Mmodzi wa iwo wotchedwa Kaliyopa anamufunsa kuti, “Kodi ndiwe wekha wokhala mu Yerusalemu amene sukudziwa zinthu zimene zachitika mʼmasiku awa?”

19Iye anafunsa kuti, “Zinthu zotani?”

Iwo anayankha nati, “Za Yesu wa ku Nazareti, Iye anali mneneri, wamphamvu mʼmawu ndi mu zochita pamaso pa Mulungu ndi anthu onse. 20Akulu a ansembe ndi oweruza anamupereka Iye kuti aphedwe, ndipo anamupachika Iye; 21koma ife tinkayembekezera kuti Iye ndiye amene akanawombola Israeli. Ndipo kuwonjeza apo, lero ndi tsiku lachitatu chichitikireni izi. 22Kuwonjezanso apo, ena mwa amayi athu atidabwitsa ife. Iwo anapita ku manda mmamawa 23koma sanakapeze mtembo wake. Iwo anabwera ndi kudzatiwuza ife kuti anaona masomphenya a angelo amene anati Yesu ali moyo. 24Kenaka ena mwa anzathu anapita ku manda ndipo anakapeza monga momwe amayiwo ananenera, koma Iye sanamuone.”

25Iye anawawuza kuti, “Inu ndinu anthu opusa, osafuna kukhulupirira msanga zonse zimene aneneri ananena! 26Kodi Khristu sanayenera kumva zowawa izi ndipo kenaka ndi kulowa mu ulemerero wake?” 27Ndipo kuyambira ndi Mose ndi aneneri onse Iye anawafotokozera zimene zinalembedwa mʼmalemba wonse zokhudzana ndi Iye mwini.

28Atayandikira mudzi omwe amapitako, Yesu anachita ngati akupitirira. 29Koma iwo anamupempha Iye kwambiri kuti, “Mukhale ndi ife, popeza kwatsala pangʼono kuda, ndipo dzuwa lili pafupi kulowa.” Ndipo Iye anapita kukakhala nawo.

30Iye ali pa tebulo pamodzi nawo, anatenga buledi ndipo anayamika, nanyema nayamba kuwagawira. 31Kenaka maso awo anatsekuka ndipo anamuzindikira Iye, ndipo anachoka pakati pawo. 32Iwo anafunsana wina ndi mnzake kuti, “Kodi mitima yathu sinali kutentha mʼkati mwathu pamene Iye ankayankhulana nafe pa njira ndi mmene anatitsekulira malemba?”

33Nthawi yomweyo iwo anayimirira ndi kubwerera ku Yerusalemu. Iwo anapeza khumi ndi mmodziwo ndi ena anali nawo nasonkhana pamodzi 34ndipo anati, “Ndi zoonadi! Ambuye auka ndipo anaonekera kwa Simoni.” 35Kenaka awiriwo anawawuza zimene zinachitika pa njira, ndi mmene iwo anamudziwira Yesu, Iye atanyema buledi.

Yesu Aonekera kwa Ophunzira

36Akufotokoza zimenezi, Yesu mwini wake anayimirira pakati pawo ndipo anati, “Mukhale ndi mtendere.”

37Koma chifukwa choti anathedwa nzeru ndi kuchita mantha, ankaganiza kuti akuona mzukwa. 38Iye anawafunsa kuti, “Nʼchifukwa chiyani mukuvutika? Nʼchifukwa chiyani mukukayika mu mtima mwanu? 39Taonani manja anga ndi mapazi anga. Ine ndine amene! Khudzeni kuti muone. Mzukwa ulibe mnofu ndi mafupa monga mukuonera ndili nazo.”

40Iye atanena izi anawaonetsa manja ake ndi mapazi ake. 41Ndipo pamene iwo samakhulupirirabe, chifukwa cha chimwemwe ndi kudabwa, Iye anawafunsa kuti, “Kodi muli ndi chakudya chilichonse pano?” 42Iwo anamupatsa Iye kachidutswa ka nsomba yophika. 43Iye anakatenga ndi kukadya iwo akuona.

44Iye anawawuza kuti, “Izi ndi zimene ndinakuwuzani pamene ndinali nanu: chilichonse chiyenera kukwaniritsidwa chimene chinalembedwa cha Ine mʼbuku la Malamulo a Mose, Aneneri ndi Masalimo.”

45Kenaka anawatsekula maganizo kuti azindikire Malemba. 46Iye anawawuza kuti, “Izi ndi zimene zinalembedwa: Khristu adzazunzika ndipo adzauka kwa akufa tsiku lachitatu. 47Ndipo kutembenuka mtima ndi kukhululukidwa kwa machimo zidzalalikidwa mu dzina lake kwa anthu amitundu yonse kuyambira mu Yerusalemu. 48Inu ndinu mboni za zimenezi. 49Ine ndidzakutumizirani chimene Atate anga analonjeza. Koma khalani mu mzinda muno mpaka mutavekedwa mphamvu yochokera kumwamba.”

Kupita Kumwamba

50Iye atawatengera kunja kwa mzindawo mpaka ku Betaniya, anakweza manja ake ndi kuwadalitsa. 51Iye akuwadalitsa, anawasiya ndipo anatengedwa kupita kumwamba. 52Pamenepo anamulambira Iye ndipo anabwerera ku Yerusalemu ndi chimwemwe chachikulu. 53Ndipo iwo anakhalabe ku Nyumba ya Mulungu, akulemekeza Mulungu.

Persian Contemporary Bible

لوقا 24:1-53

عيسی زنده می‌شود

1روز يكشنبه، صبح خيلی زود، زنها دارو و عطرياتی را كه تهيه كرده بودند، با خود برداشته، به سر قبر رفتند. 2وقتی به آنجا رسيدند، ديدند سنگ بزرگی كه جلو دهانهٔ قبر بود، به كناری غلطانيده شده است. 3پس وارد قبر شدند. اما جسد عيسای خداوند آنجا نبود!

4ايشان مات و مبهوت ايستاده، در اين فكر بودند كه بر سر جسد چه آمده است. ناگاه دو مرد با لباسهايی درخشان و خيره كننده، در مقابل ايشان ظاهر شدند. 5زنان بسيار ترسيدند و آنان را تعظيم كردند.

آن دو مرد پرسيدند: «چرا در بين مردگان به دنبال شخص زنده می‌گرديد؟ 6‏-7عيسی اينجا نيست! او زنده شده است! به یاد آوريد سخنانی را كه در جليل به شما گفت كه می‌بايست به دست مردم گناهكار تسليم شده، كشته شود و روز سوم برخيزد!»

8آنگاه زنان گفته‌های عيسی را به یاد آوردند. 9پس با عجله به اورشليم بازگشتند تا آن يازده شاگرد و سايرين را از اين وقايع آگاه سازند.

10زنانی كه به سر قبر رفته بودند، عبارت بودند از مريم مجدليه، يونا، مريم مادر يعقوب و چند زن ديگر. 11ولی شاگردان گفته‌های زنان را افسانه پنداشتند و نمی‌توانستند باور كنند.

12اما پطرس به سوی قبر دويد تا ببيند چه اتفاقی افتاده است. وقتی به آنجا رسيد، خم شد و با دقت به داخل قبر نگاه كرد. فقط كفن خالی آنجا بود! او حيران و متعجب به خانه بازگشت.

در راه عموآس

13در همان روز يكشنبه، دو نفر از پيروان عيسی به دهكدهٔ «عموآس» می‌رفتند كه با اورشليم حدود ده كيلومتر فاصله داشت. 14‏-15در راه درباره وقايع چند روز گذشته گفتگو می‌كردند، كه ناگهان خود عيسی از راه رسيد و با آنان همراه شد. 16اما خدا نگذاشت كه در آن لحظه او را بشناسند.

17عيسی پرسيد: «گويا سخت مشغول بحث هستيد! موضوع گفتگويتان چيست؟»

آن دو، ايستادند. آثار غم و اندوه از چهره‌شان نمايان بود. 18يكی از آن دو كه «كلئوپاس» نام داشت، جواب داد: «تو در اين شهر بايد تنها كسی باشی كه از وقايع چند روز اخير بی‌خبر مانده‌ای!»

19عيسی پرسيد: «كدام وقايع؟»

گفتند: «وقايعی كه برای عيسای ناصری اتفاق افتاد! او نبی و معلم توانايی بود؛ اعمال و معجزه‌های خارق العاده‌ای انجام می‌داد و مورد توجه خدا و انسان بود. 20اما كاهنان اعظم و سران مذهبی ما او را گرفتند و تحويل دادند تا او را به مرگ محكوم ساخته، مصلوب كنند. 21ولی ما با اميدی فراوان، تصور می‌كرديم كه او همان مسيح موعود است كه ظهور كرده تا قوم اسرائيل را نجات دهد. علاوه بر اينها، حالا كه دو روز از اين ماجراها می‌گذرد، 22‏-23چند زن از جمع ما، با سخنان خود ما را به حيرت انداختند؛ زيرا آنان امروز صبح زود به سر قبر رفتند و وقتی بازگشتند، گفتند كه جسد او را پيدا نكرده‌اند، اما فرشتگانی را ديده‌اند كه گفته‌اند عيسی زنده شده است! 24پس چند نفر از مردان ما به سر قبر رفتند و ديدند كه هر چه زنان گفته بودند، عين واقعيت بوده است، اما عيسی را نديدند.»

25آنگاه عيسی به ايشان فرمود: «چقدر شما نادان هستيد! چرا اينقدر برايتان دشوار است كه به سخنان انبیا ايمان بياوريد؟ 26آيا ايشان به روشنی پيشگويی نكرده‌اند كه مسيح پيش از آنكه به عزت و جلال خود برسد، می‌بايست تمام اين زحمات را ببيند؟» 27سپس تمام پيشگويی‌هايی را كه درباره خودش در تورات موسی و كتابهای ساير انبیا آمده بود، برای آنان شرح داد.

28در اين هنگام به دهكده عموآس و پايان سفرشان رسيدند و عيسی خواست كه به راه خود ادامه دهد. 29اما چون هوا كم‌كم تاريک می‌شد، آن دو مرد با اصرار خواهش كردند كه شب را نزد ايشان بماند. پس عيسی به خانه ايشان رفت. 30وقتی بر سر سفره نشستند، عيسی نان را برداشت و شكرگزاری نموده، به هر يک تكه‌ای داد. 31ناگهان چشمانشان باز شد و او را شناختند! همان لحظه عيسی ناپديد شد.

32آن دو به يكديگر گفتند: «ديدی وقتی در راه، مطالب كتاب آسمانی را برای ما شرح می‌داد، چگونه دلمان به تپش افتاده بود و به هيجان آمده بوديم؟»

33پس بی‌درنگ به اورشليم بازگشتند و نزد يازده شاگرد عيسی رفتند كه با ساير پيروان او گرد آمده بودند، 34و می‌گفتند: «خداوند حقيقتاً زنده شده است! پطرس نيز او را ديده است!» 35آنگاه آن دو نفر نيز ماجرای خود را تعريف كردند و گفتند كه چگونه عيسی در بين راه به ايشان ظاهر شد و به چه ترتيب سر سفره، هنگام پاره كردن نان، او را شناختند.

عيسی به شاگردان ظاهر می‌شود

36در همان حال كه گرم گفتگو بودند، ناگهان عيسی در ميانشان ايستاد و سلام كرد. 37اما همه وحشت كردند، چون تصور كردند كه روح می‌بينند!

38عيسی فرمود: «چرا وحشت كرده‌ايد؟ چرا شک داريد و نمی‌خواهيد باور كنيد كه خودم هستم! 39به جای ميخها در دستها و پايهايم نگاه كنيد! می‌بينيد كه واقعاً خودم هستم. به من دست بزنيد تا خاطرجمع شويد كه من روح نيستم. چون روح بدن ندارد، اما همينطور كه می‌بينيد، من دارم.» 40در همان حال كه سخن می‌گفت، دستها و پايهای خود را به ايشان نشان داد. 41آنان شاد و حيرت‌زده بودند و نمی‌توانستند آنچه را كه می‌ديدند، باور كنند.

عيسی از ايشان پرسيد: «آيا در اينجا چيزی برای خوردن داريد؟» 42آنها مقداری ماهی پخته به او دادند. 43او نيز در برابر چشمان شگفت‌زده ايشان، آن را خورد.

44آنگاه به ايشان فرمود: «آيا به ياد داريد كه پيش از مرگم، وقتی با شما بودم، می‌گفتم كه هر چه در تورات موسی و كتابهای انبیا و زبور داوود، درباره من نوشته شده است، همه بايد عملی شود؟ حال، با آنچه كه برای من اتفاق افتاد، همه آنها عملی شد!» 45آنگاه ذهنشان را باز كرد تا همهٔ پيشگويی‌های كتاب آسمانی را درک كنند.

46سپس فرمود: «بلی، از زمانهای دور، در كتابهای انبیا نوشته شده بود كه مسيح موعود بايد رنج و زحمت ببيند، جانش را فدا كند و روز سوم زنده شود؛ 47و اين است پيغام نجاتبخشی كه بايد از اورشليم به همهٔ قومها برسد: ”همه كسانی كه از گناهانشان توبه كنند و به سوی من بازگردند، آمرزيده خواهند شد.“ 48شما ديده‌ايد و شاهد هستيد كه همه اين پيشگويی‌ها واقع شده است.

49«اينک من روح‌القُدُس را كه پدرم به شما وعده داده است، بر شما خواهم فرستاد. از این رو پيش از آنكه اين پيغام نجاتبخش را به ديگران اعلام كنيد، در اورشليم بمانيد تا روح‌القدس بيايد و شما را با قدرت الهی از عالم بالا، مجهز كند.»

صعود عيسی به آسمان

50آنگاه عيسی ايشان را با خود تا نزديكی «بيت‌عنيا» برد. در آنجا دستهای خود را به سوی آسمان بلند كرد و ايشان را بركت داد، 51و در همان حال از روی زمين جدا شد و به سوی آسمان بالا رفت. 52شاگردان او را پرستش كردند و با شادی بسيار به اورشليم بازگشتند، 53و به خانه خدا رفتند. آنان همواره در آنجا مانده، خدا را شكر و ستايش می‌كردند.