Luka 23 – CCL & BDS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Luka 23:1-56

1Kenaka gulu lonse la anthuwo linayimirira ndi kumutengera kwa Pilato. 2Ndipo iwo anayamba kumuneneza nati, “Ife tinapeza munthu uyu akusokoneza anthu a mtundu wathu ndipo amatsutsa zopereka msonkho kwa Kaisara komanso amati ndi Khristu, Mfumu.”

3Pamenepo Pilato anamufunsa Yesu kuti, “Kodi Iwe ndiwe Mfumu ya Ayuda?”

Yesu anayankha kuti, “Mwatero ndinu.”

4Kenaka Pilato anawawuza akulu a ansembe ndi gulu la anthu, “Ine sindikumupeza cholakwa munthuyu.”

5Koma iwo analimbikirabe kuti, “Iyeyu amasokoneza anthu ku Yudeya konse ndi chiphunzitso chake, Iyeyu anayambira ku Galileya ndipo wayenda mtunda wonse mpaka kuno.”

6Pakumva zimenezi, Pilato anafunsa ngati munthuyo ndi Mgalileya. 7Iye atamva kuti Yesu anali pansi pa ulamuliro wa Herode, anamutumiza kwa Herodeyo, amene pa nthawi imeneyo analinso mu Yerusalemu.

8Herode ataona Yesu, anakondwa kwambiri, chifukwa kwa nthawi yayitali, ankafunitsitsa atamuona. Kuchokera pa zimene anamva za Iye, anayembekezera kuti achita zodabwitsa. 9Iye anamufunsa mafunso ambiri, koma Yesu sanayankhe. 10Akulu a ansembe ndi aphunzitsi amalamulo, anayimirira pamenepo ndi kumuneneza kwambiri. 11Pamenepo Herode ndi asilikali ake anamuseka ndi kumunyoza Iye. Atamuveka mkanjo wonyezimira, anamutumizanso kwa Pilato. 12Tsiku limenelo, Herode ndi Pilato anakhala abwenzi. Zisanachitike izi anali adani.

13Pilato anasonkhanitsa akulu a ansembe, oweruza ndi anthu, 14ndipo anawawuza kuti, “Munabweretsa munthuyu kwa ine ngati ndiye amawuza anthu kuti awukire. Ine ndamufunsa pamaso panu ndipo sindinapeze chomuyimbira mlandu. 15Herodenso sanapeze chifukwa pakuti wamutumizanso kwa ife monga mmene mukuoneramu. Iyeyu sanachite chinthu chakuti aphedwe. 16Nʼchifukwa chake, ine ndingomulanga, nʼkumumasula.” 17(Pa nthawi yachikondwerero cha Paska iye ankayenera kumasula munthu mmodzi).

18Onse pamodzi anafuwula kuti, “Muchotseni munthuyu! Timasulireni Baraba!” 19(Baraba anaponyedwa mʼndende chifukwa choyambitsa chipolowe mu mzinda ndi kupha).

20Pofuna kumumasula Yesu, Pilato anawadandaulira iwo. 21Koma iwo anapitirirabe kufuwula kuti, “Mpachikeni! Mpachikeni!”

22Kachitatu anawafunsanso iwo kuti, “Chifukwa chiyani? Kodi munthu uyu wachita choyipa chanji? Ine sindinapeze cholakwa mwa Iye chakuti aphedwe choncho ndingomukwapula ndi kumumasula.”

23Koma ndi mawu ofuwulitsa, analimbikirabe kuti Iye apachikidwe, ndipo kufuwulako kunapitirira. 24Choncho Pilato anatsimikiza kuchita zofuna zawozo. 25Iye anawamasulira munthu amene anaponyedwa mʼndende chifukwa choyambitsa chipolowe ndi kupha, amene ankamufunayo, ndipo anawapatsa Yesu mwakufuna kwawo.

Kupachikidwa kwa Yesu

26Ndipo pamene ankapita naye, anagwira Simoni wa ku Kurene, amene ankachokera ku munda, namusenzetsa mtanda namuyendetsa pambuyo pa Yesu. 27Gulu lalikulu la anthu linamutsata Iye, kuphatikiza amayi amene ankabuma ndi kumulirira. 28Yesu anatembenuka nati kwa iwo, “Ana aakazi a Yerusalemu, musandilirire Ine; dzililireni nokha ndi ana anu. 29Pakuti nthawi idzabwera imene inu mudzati, ‘Ndi odala amayi osabereka, mimba zimene sizinabereke ndi mawere amene sanayamwitse!’ 30Kenaka,

“adzawuza mapiri kuti tigwereni ife;

zitunda kuti tiphimbeni ife.

31Chifukwa ngati anthu akuchita izi pa mtengo wauwisi, chidzachitike nʼchiyani ndi wowuma?”

32Amuna ena awiri, onsewo achifwamba, anatengedwanso pamodzi ndi Yesu kukaphedwa. 33Pamene anafika pamalo otchedwa Bade, anamupachika Iye pamodzi ndi achifwambawo, mmodzi kudzanja lake lamanja ndi winayo la ku lamazere. 34Yesu anati, “Atate, akhululukireni, pakuti sakudziwa chimene akuchita.” Ndipo anagawana malaya ake mochita maere.

35Anthu anayimirira nʼkumaonerera, ngakhalenso akuluakulu ankamulalatira Iye. Iwo anati, “Iye anapulumutsa ena; adzipulumutse yekha ngati ndi Khristu wa Mulungu, Wosankhidwayo.”

36Asilikalinso anabwera ndi kumunyoza Iye. Iwo anamupatsa vinyo wosasa, 37ndipo anati, “Ngati ndiwe Mfumu ya Ayuda, dzipulumutse wekha.”

38Ndipo panalembedwa chikwangwani pamwamba pake chimene chinati: uyu ndi mfumu ya ayuda.

39Mmodzi wa achifwambawo, amene anapachikidwa, anamunenera Iye zamwano nati, “Kodi sindiwe Khristu? Dzipulumutse wekha ndi ifenso!”

40Koma wachifwamba winayo anamudzudzula iye nati, “Suopa Mulungu, iwenso ukulandira chilango chomwechi? 41Ife tikulangidwa mwachilungamo, pakuti ife tikulandira monga mwa ntchito zathu. Koma munthu uyu sanachimwe kanthu.”

42Kenaka anati, “Yesu, mundikumbukire ine pamene mulowa mu ufumu wanu.”

43Yesu anayankha kuti, “Zoonadi, ndikukuwuza kuti lero lino udzakhala ndi Ine mʼparadaiso.”

Imfa ya Yesu

44Linali tsopano pafupi ora lachisanu ndi chimodzi, ndipo mdima unagwa pa dziko lonse mpaka ora lachisanu ndi chinayi, 45pakuti dzuwa linaleka kuwala. Ndipo chinsalu cha mʼNyumba ya Mulungu chinangʼambika pakati. 46Yesu anafuwula ndi mawu okweza kuti, “Atate, ndikupereka mzimu wanga mʼmanja mwanu.” Atanena zimenezi, anamwalira.

47Kenturiyo, ataona zimene zinachitikazi, analemekeza Mulungu ndipo anati, “Zoonadi, uyu anali munthu wolungama.” 48Anthu onse amene anasonkhana kudzaonerera izi, ataona zinachitikazo, anadziguguda pachifuwa ndipo anachoka. 49Koma onse amene anamudziwa Iye, kuphatikiza amayi amene anamutsatira kuchokera ku Galileya, anayimirira akuona zinthu izi.

Yesu Ayikidwa Mʼmanda

50Ndipo taonani panali munthu wina wotchedwa Yosefe, mmodzi wa gulu loweruza, munthu wabwino ndi wolungama. 51Iye sanavomereze zimene anzake abwalo anagwirizana ndi kuchita. Iye ankachokera ku mudzi wa Arimateyu wa ku Yudeya ndipo ankayembekezera ufumu wa Mulungu. 52Atapita kwa Pilato, iye anakapempha mtembo wa Yesu. 53Ndipo anawutsitsa, nawukulunga nsalu yabafuta nawuyika mʼmanda wosemedwa mʼmwala, amene panalibe wina amene anayikidwamo. 54Linali tsiku lokonzekera ndipo Sabata linatsala pangʼono kuyamba.

55Amayi amene anabwera ndi Yesu kuchokera ku Galileya, anatsata Yosefe ndipo anaona manda ndi momwe mtembo wake anawuyikira. 56Kenaka anapita ku mudzi ndi kukakonza mafuta onunkhira. Koma anapuma pa tsiku la Sabata pomvera malamulo.

La Bible du Semeur

Luc 23:1-56

Jésus devant Pilate et Hérode

(Mt 27.2, 11-14 ; Mc 15.1-5 ; Jn 18.28-38)

1Toute l’assemblée se leva et l’emmena devant Pilate. 2Là, ils se mirent à l’accuser : Nous avons trouvé cet homme en train de jeter le trouble parmi notre peuple : il interdit de payer l’impôt à l’empereur et il déclare qu’il est le Messie, le roi !

3Alors Pilate l’interrogea : Es-tu le roi des Juifs ? lui demanda-t-il.

– Tu le dis toi-même, lui répondit Jésus.

4Pilate dit alors aux chefs des prêtres et aux gens rassemblés : Je ne trouve chez cet homme aucune raison de le condamner.

5Mais ils insistaient de plus en plus, disant : Il soulève le peuple avec ses idées ! Il a endoctriné toute la Judée ! Il a commencé en Galilée et il est venu jusqu’ici.

6Quand Pilate entendit parler de la Galilée, il demanda si cet homme était galiléen. 7Apprenant qu’il relevait bien de la juridiction d’Hérode, il l’envoya à ce dernier qui, justement, se trouvait lui aussi à Jérusalem durant ces jours-là.

8Hérode fut ravi de voir Jésus car, depuis longtemps, il désirait faire sa connaissance, parce qu’il avait entendu parler de lui, et il espérait lui voir faire quelque signe miraculeux. 9Il lui posa de nombreuses questions, mais Jésus ne lui répondit pas un mot.

10Pendant ce temps, les chefs des prêtres et les spécialistes de la Loi se tenaient là debout, lançant, avec passion, de graves accusations contre lui. 11Alors Hérode le traita avec mépris, ses soldats en firent autant, et ils se moquèrent de lui, en le revêtant d’un manteau magnifique. Hérode le fit reconduire ainsi chez Pilate. 12Hérode et Pilate, qui jusqu’alors avaient été ennemis, devinrent amis ce jour-là.

Jésus condamné à mort

(Mt 27.15-26 ; Mc 15.6-15 ; Jn 18.39-40 ; 19.4-16)

13Pilate convoqua les chefs des prêtres, les dirigeants et le peuple. Il leur dit : 14Vous m’avez amené cet homme en l’accusant d’égarer le peuple. Or, je l’ai interrogé moi-même devant vous, et je ne l’ai trouvé coupable d’aucun des crimes dont vous l’accusez. 15Hérode non plus, d’ailleurs, puisqu’il nous l’a renvoyé. Cet homme n’a rien fait qui mérite la mort. 16Je vais donc lui faire donner le fouet et le relâcher.

[17A chaque fête, Pilate devait leur accorder la libération d’un prisonnier23.17 Ce verset est absent de plusieurs manuscrits. Voir Mt 27.15 ; Mc 15.6..]

18Mais la foule entière se mit à crier : A mort ! Relâche Barabbas !

19Ce Barabbas avait été mis en prison pour une émeute qui avait eu lieu dans la ville et pour un meurtre.

20Mais Pilate, qui désirait relâcher Jésus, adressa de nouveau la parole à la foule, 21qui se mit à crier : Crucifie-le ! Crucifie-le !

22– Mais enfin, leur demanda-t-il pour la troisième fois, qu’a-t-il fait de mal ? Je n’ai trouvé en lui aucune raison de le condamner à mort. Je vais donc lui faire donner le fouet puis le remettre en liberté.

23Mais ils devinrent de plus en plus pressants et exigèrent à grands cris sa crucifixion. Finalement, leurs cris l’emportèrent.

24Pilate décida alors de satisfaire à leur demande. 25Il relâcha donc celui qu’ils réclamaient, celui qui avait été emprisonné pour une émeute et pour un meurtre, et leur livra Jésus pour qu’ils fassent de lui ce qu’ils voulaient.

La mort de Jésus

(Mt 27.32-44 ; Mc 15.21-32 ; Jn 19.17-22)

26Pendant qu’ils l’emmenaient, ils se saisirent d’un certain Simon de Cyrène23.26 Capitale de la Cyrénaïque située en Afrique du Nord., qui revenait des champs, et l’obligèrent à porter la croix derrière Jésus. 27Une foule de gens du peuple le suivait. Il y avait aussi beaucoup de femmes en larmes, qui se lamentaient à cause de lui. 28Se tournant vers elles, il leur dit : Femmes de Jérusalem, ne pleurez pas à cause de moi ! Pleurez plutôt à cause de vous-mêmes et de vos enfants 29car, sachez-le, des jours viennent où l’on dira : « Heureuses les femmes qui ne peuvent pas avoir d’enfant et celles qui n’en ont jamais eu et qui n’ont jamais allaité. » 30Alors on se mettra à dire aux montagnes : « Tombez sur nous ! » et aux collines : « Recouvrez-nous23.30 Os 10.8.! » 31Car si l’on traite ainsi le bois vert, qu’adviendra-t-il du bois mort ?

32Avec Jésus, on emmena aussi deux autres hommes, des bandits qui devaient être exécutés en même temps que lui.

33Lorsqu’ils furent arrivés au lieu appelé « le Crâne », on cloua Jésus sur la croix, ainsi que les deux bandits, l’un à sa droite, l’autre à sa gauche.

34Jésus pria : Père, pardonne-leur, car ils ne savent pas ce qu’ils font23.34 Ces paroles de Jésus sont absentes de certains manuscrits..

Les soldats se partagèrent ses vêtements en les tirant au sort. 35La foule se tenait tout autour et regardait. Quant aux chefs du peuple, ils ricanaient en disant : Lui qui a sauvé les autres, qu’il se sauve donc lui-même, s’il est le Messie, l’Elu de Dieu !

36Les soldats aussi se moquaient de lui. Ils s’approchaient et lui présentaient du vinaigre 37en lui disant : Si tu es le roi des Juifs, sauve-toi toi-même !

38Au-dessus de sa tête, il y avait un écriteau portant ces mots : « Celui-ci est le roi des Juifs ».

39L’un des deux criminels attaché à une croix l’insultait en disant : N’es-tu pas le Messie ? Alors sauve-toi toi-même, et nous avec !

40Mais l’autre lui fit des reproches en disant : Tu n’as donc aucune crainte de Dieu, toi, et pourtant tu subis la même peine ? 41Pour nous, ce n’est que justice : nous payons pour ce que nous avons fait ; mais celui-là n’a rien fait de mal.

42Puis il ajouta : Jésus, souviens-toi de moi quand tu viendras régner.

43Et Jésus lui répondit : Vraiment, je te l’assure : aujourd’hui même, tu seras avec moi dans le paradis.

(Mt 27.45-56 ; Mc 15.33-41 ; Jn 19.25-30)

44Il était environ midi, quand le pays tout entier fut plongé dans l’obscurité, et cela dura jusqu’à trois heures de l’après-midi. 45Le soleil resta entièrement caché23.45 Certains manuscrits ont : le soleil s’obscurcit.. Le grand rideau du Temple se déchira par le milieu. 46Alors Jésus poussa un grand cri : Père, je remets mon esprit entre tes mains23.46 Ps 31.6..

Après avoir dit ces mots il mourut.

47En voyant ce qui s’était passé, l’officier romain rendit gloire à Dieu en disant : Aucun doute, cet homme était juste.

48Après avoir vu ce qui était arrivé, tout le peuple, venu en foule pour assister à ces exécutions, s’en retourna en se frappant la poitrine. 49Tous les amis de Jésus, ainsi que les femmes qui l’avaient suivi depuis la Galilée, se tenaient à distance pour voir ce qui se passait.

Jésus mis au tombeau

(Mt 27.57-61 ; Mc 15.42-47 ; Jn 19.38-42)

50Il y avait un homme, appelé Joseph, un membre du Grand-Conseil des Juifs. C’était un homme bon et droit 51qui n’avait pas approuvé la décision ni les actes des autres membres du Grand-Conseil. Il venait d’Arimathée23.51 Village situé à environ 35 kilomètres au nord-ouest de Jérusalem., en Judée, et attendait le royaume de Dieu. 52Il alla demander à Pilate le corps de Jésus. 53Après l’avoir descendu de la croix, il l’enroula dans un drap de lin et le déposa dans un tombeau taillé en plein rocher, où personne n’avait encore été enseveli. 54C’était le soir de la préparation, avant le début du sabbat. 55Les femmes qui avaient accompagné Jésus depuis la Galilée suivirent Joseph, elles regardèrent le tombeau et observèrent comment le corps de Jésus y avait été déposé. 56Ensuite, elles retournèrent chez elles et préparèrent des huiles aromatiques et des parfums23.56 En Israël, on embaumait les morts avec de l’huile aromatique et des parfums.. Puis elles observèrent le repos du sabbat, comme la Loi le prescrit.