Luka 22 – CCL & BDS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Luka 22:1-71

Yudasi Avomera Kumupereka Yesu

1Phwando la buledi wopanda yisiti lotchedwa Paska litayandikira, 2akulu a ansembe ndi aphunzitsi amalamulo amafunafuna mpata woti amuphere Yesu, pakuti ankachita mantha ndi anthu. 3Kenaka Satana analowa mwa Yudasi, wotchedwa Isikarioti, mmodzi wa khumi ndi a iwiriwo. 4Ndipo Yudasi anapita kwa akulu a ansembe ndi akulu oyangʼanira Nyumba ya Mulungu ndi kukambirana nawo za mmene iye angaperekere Yesu. 5Iwo anakondwa ndipo anagwirizana zomupatsa ndalama. 6Iye anavomera, ndipo anayamba kufunafuna mpata wabwino wakuti amupereke Yesu kwa iwo pamene panalibe gulu la anthu pafupi.

Paska Womaliza

7Kenaka linafika tsiku la buledi wopanda yisiti pamene mwana wankhosa wa Paska amaperekedwa nsembe. 8Yesu anatuma Petro ndi Yohane nati, “Pitani kukatikonzera Paska kuti tikadye.”

9Iwo anafunsa kuti, “Kodi mukufuna tikakonzere kuti?”

10Iye anayankha kuti, “Taonani, mukamalowa mu mzinda, mudzakumana ndi mwamuna atanyamula mtsuko wamadzi. Mulondoleni ku nyumba imene akalowe, 11ndipo mukamuwuze mwini nyumbayo kuti, ‘Aphunzitsi kufunsa kuti, chili kuti chipinda cha alendo, kumene Ine ndi ophunzira anga tikadyere Paska?’ 12Iyeyo adzakuonetsani chipinda chachikulu chapamwamba, chokhala ndi zonse. Kachiteni zokonzekera mʼmenemo.”

13Iwo anapita nakapeza zinthu monga mmene Yesu anawawuzira. Tsono anakonza Paska.

Za Mgonero wa Ambuye

14Ora litakwana, Yesu ndi ophunzira ake anakhala pa tebulo. 15Ndipo Iye anawawuza kuti, “Ine ndakhala ndikuyembekezera kudya Paska uyu ndi inu ndisanamve zowawa. 16Pakuti Ine ndikukuwuzani kuti sindidzadyanso Paska wina mpaka Paskayi itakwaniritsidwa mu ufumu wa Mulungu.”

17Atanyamula chikho, Iye anayamika ndipo anati, “Tengani ndipo patsiranani pakati panu. 18Pakuti ndikukuwuzani kuti, Ine sindidzamwanso zochokera ku chipatso cha mphesa mpaka ufumu wa Mulungu utabwera.”

19Ndipo Iye anatenga buledi, nayamika ndipo anamunyema, nagawira iwo nati, “Ili ndi thupi langa lomwe laperekedwa kwa inu; muzichita zimenezi pokumbukira Ine.”

20Chimodzimodzinso, utatha mgonero, anatenga chikho nati, “Chikho ichi ndi pangano latsopano la magazi anga, amene akhetsedwa chifukwa cha inu. 21Koma dzanja la amene akundipereka Ine lili pamodzi ndi langa pa chakudya pano. 22Mwana wa Munthu apita monga mmene zinalembedwera, koma tsoka kwa munthu amene amupereka Iye.” 23Iwo anayamba kufunsana pakati pawo kuti ndi ndani wa iwo amene akanachita ichi.

Mkangano Pakati pa Ophunzira

24Komanso mkangano unabuka pakati pawo kuti ndani mwa iwo amene amaganiziridwa kukhala wamkulu. 25Yesu anawawuza kuti, “Mafumu a anthu a mitundu ina amaonetsa mphamvu za ufumu wawo pa anthuwo; ndipo amene ali ndi ulamuliro, amapatsidwa dzina la kuti ‘Opindula.’ 26Koma inu simuyenera kukhala choncho. Mʼmalo mwake, wamkulu pakati panu akhale ngati wamngʼono pa onse, ndipo iye amene alamulira akhale ngati wotumikira. 27Pakuti wamkulu ndani, iye amene ali pa tebulo kapena iye amene akutumikira? Kodi si iye amene ali pa tebulo? Koma ndili pakati panu ngati mmodzi wokutumikirani. 28Inu ndinu amene mwayima nane mʼmayesero. 29Ndipo Ine ndikupatsani inu ufumu, monga momwe Atate anga anandipatsiranso Ine, 30kuti inu muthe kudya ndi kumwa pa tebulo langa mu ufumu wanga ndi kukhala pa mipando yaufumu kuweruza mafuko khumi ndi awiri a Israeli.”

Yesu Aneneratu kuti Petro Adzamukana

31“Simoni, Simoni, Satana wapempha kuti akupete ngati tirigu. 32Koma Ine ndakupempherera Simoni, kuti chikhulupiriro chako chisafowoke ndipo pamene udzabwerera kwa Ine, udzalimbikitse abale ako.”

33Koma iye anayankha kuti, “Ambuye, ndine wokonzeka kupita nanu ku ndende ndi kufa komwe.”

34Yesu anayankha kuti, “Ine ndikukuwuza Petro, tambala asanalire lero lino, udzandikana katatu kuti sukundidziwa Ine.”

35Kenaka Yesu anawafunsa iwo kuti, “Ine nditakutumizani wopanda chikwama cha ndalama, thumba kapena nsapato, kodi inu munasowa kanthu?”

Iwo anayankha kuti, “Palibe chimene tinasowa.”

36Iye anawawuza kuti, “Koma tsopano ngati muli ndi chikwama cha ndalama, chitengeni, ndiponso thumba. Ndipo ngati mulibe lupanga, gulitsani mkanjo wanu ndi kugula. 37Zalembedwa kuti, ‘Ndipo Iye anawerengedwa pamodzi ndi anthu ochimwa,’ ndipo Ine ndikuwuzani kuti izi ziyenera kukwaniritsidwa mwa Ine. Inde, zimene zinalembedwa za Ine, zikukwaniritsidwa.”

38Ophunzira anati, “Taonani Ambuye, awa malupanga awiri.”

Iye anayankha kuti, “Amenewa akwanira.”

Yesu Apemphera ku Phiri la Olivi

39Yesu anapitanso monga mwa masiku onse ku Phiri la Olivi, ndipo ophunzira ake anamutsatira Iye. 40Atafika pamalopo, Iye anawawuza kuti, “Pempherani kuti musagwe mʼmayesero.” 41Iye anapita patsogolo pangʼono patali ngati kuponya mwala, anagwada napephera kuti, 42“Atate ngati mukufuna chotsereni chikho ichi. Komatu muchite zimene mukufuna osati zimene ndikufuna ine.” 43Mngelo wochokera kumwamba anafika namulimbikitsa. 44Ndipo mopsinjika mtima, anapemphera moona mtima, ndipo thukuta lake linali ngati madontho a magazi akugwera pansi.

45Iye atamaliza kupemphera, ndi kubwerera kwa ophunzira ake, anawapeza atagona atafowoka ndi chisoni. 46Iye anafunsa kuti, Nʼchifukwa chiyani mukugona? “Dzukani ndipo pempherani kuti inu musagwe mʼmayesero.”

Amugwira Yesu

47Pamene Iye ankayankhulabe, gulu la anthu linabwera, ndipo munthu wotchedwa Yudasi, mmodzi wa khumi ndi awiriwo analitsogolera. Iye anamuyandikira Yesu kuti amupsompsone. 48Koma Yesu anamufunsa kuti, “Yudasi, kodi ukupereka Mwana wa Munthu ndi mpsopsono?”

49Otsatira Yesu ataona zimene zimati zichitike, anati, “Ambuye, kodi timenyane ndi malupanga athu?” 50Ndipo mmodzi wa iwo anatema wantchito wamkulu wa ansembe, nadula khutu lake lamanja.

51Koma Yesu anayankha kuti, “Zisachitikenso zimenezi!” Ndipo Iye anakhudza khutu la munthuyo ndi kumuchiritsa.

52Kenaka Yesu anafunsa akulu a ansembe, akuluakulu oyangʼanira Nyumba ya Mulungu ndi akuluakulu ena amene anabwerawo kuti, “Kodi Ine ndikutsogolera gulu lowukira kuti mubwere ndi malupanga ndi zibonga? 53Tsiku lililonse ndinali nanu mʼmabwalo a mʼNyumba ya Mulungu ndipo inu simunandigwire. Koma iyi ndi nthawi yanu pamene mdima ukulamulira.”

Petro Akana Yesu

54Pamenepo anamugwira Iye, napita naye ndipo anamutengera ku nyumba ya mkulu wa ansembe. Petro anamutsatira patali. 55Koma pamene anasonkha moto pakati pa bwalo la milandu, anakhala onse pansi ndipo Petro anakhalanso pansi. 56Mtsikana wantchito anamuona atakhala nawo pafupi ndi moto. Iye anamuyangʼanitsitsa ndipo anati, “Munthu uyu anali ndi Yesu.”

57Koma Petro anakana nati, “Mtsikana, ine sindimudziwa ameneyu.”

58Patatha kanthawi pangʼono, wina wake anamuona ndipo anati, “Iwenso ndiwe mmodzi mwa iwo.”

Petro anayankha kuti, “Munthu iwe, ayi sindine.”

59Patatha pafupifupi ora limodzi, munthu winanso anati, “Zoonadi, munthu uyu anali ndi Iye, pakuti ndi mu Galileya.”

60Petro anayankha kuti, “Munthu iwe, sindikudziwa zimene ukunena apa.” Pamene iye ankayankhula, tambala analira. 61Ambuye anachewuka namuyangʼanitsitsa Petro. Pamenepo Petro anakumbukira mawu amene Ambuye anayankhula kwa iye kuti, “Asanalire tambala lero lino, udzandikana Ine katatu.” 62Ndipo iye anapita panja nakalira kwambiri.

Asilikali Amuchita Chipongwe Yesu

63Anthu amene ankalonda Yesu anayamba kumuchita chipongwe ndi kumumenya. 64Anamumanga mʼmaso ndi kumufunsa kuti, “Tanenera! Wakumenya iwe ndi ndani?” 65Ndipo iwo anamunena zachipongwe zambiri.

Yesu Pamaso pa Pilato ndi Herode

66Kutacha, bungwe la akuluakulu, pamodzi ndi akulu a ansembe ndi aphunzitsi amalamulo, anakumana pamodzi, ndipo anamuyika Yesu patsogolo pawo. 67Iwo anati, “Tiwuze, ngati ndiwe Khristu.”

Yesu anayankha kuti, “Ine nditakuwuzani simungandikhulupirire. 68Ine nditakufunsani inu, simungandiyankhe. 69Koma kuyambira tsopano, Mwana wa Munthu adzakhala ku dzanja lamanja la Mulungu wamphamvu.”

70Onse anafunsa kuti, “Ndiye kuti ndiwe Mwana wa Mulungu?”

Iye anayankha kuti, “Mwanena ndinu kuti Ndine.”

71Pamenepo iwo anati, “Nanga tikufuniranjinso umboni wina? Ife tamva kuchokera pa milomo yake.”

La Bible du Semeur

Luc 22:1-71

À Jérusalem : mort et résurrection de Jésus

La trahison

(Mt 26.1-5, 14-16 ; Mc 14.1-2, 10-11 ; Jn 11.47-53)

1On était à quelques jours de la fête « des Pains sans levain », appelée la Pâque. 2Les chefs des prêtres et les spécialistes de la Loi cherchaient un moyen de supprimer Jésus, mais ils avaient peur de la réaction du peuple.

3C’est alors que Satan entra dans le cœur de Judas surnommé l’Iscariot, l’un des Douze. 4Judas alla trouver les chefs des prêtres et les officiers de la garde du Temple22.4 Il s’agit des gardes chargés de la police du Temple (voir v. 52). pour s’entendre avec eux sur la manière dont il leur livrerait Jésus. 5Ils en furent tout réjouis et convinrent de lui donner de l’argent. 6Il accepta et, dès lors, il chercha une occasion favorable pour leur livrer Jésus à l’insu de la foule.

Jésus célèbre la Pâque avec ses disciples

(Mt 26.17-19 ; Mc 14.12-16)

7Le jour de la fête des Pains sans levain, où l’on devait tuer l’agneau de la Pâque, arriva. 8Jésus envoya Pierre et Jean en leur disant : Allez nous préparer le repas de la Pâque.

9– Où veux-tu que nous le préparions ? lui demandèrent-ils.

10– Eh bien, quand vous entrerez dans la ville, vous rencontrerez un homme portant une cruche d’eau. Suivez-le jusqu’à la maison où il entrera. 11Et voici comment vous parlerez au maître de maison : « Le Maître te fait dire : Où est la pièce où je prendrai le repas de la Pâque avec mes disciples ? » 12Alors il vous montrera, à l’étage supérieur, une grande pièce aménagée ; c’est là que vous ferez les préparatifs.

13Ils partirent donc, trouvèrent tout comme Jésus le leur avait dit et préparèrent le repas de la Pâque.

(Mt 26.26-29 ; Mc 14.22-25 ; voir 1 Co 11.23-25)

14Quand ce fut l’heure, Jésus se mit à table, avec les apôtres. 15Il leur dit : J’ai vivement désiré célébrer cette Pâque avec vous avant de souffrir. 16En effet, je vous le déclare, je ne la mangerai plus jusqu’au jour où tout ce qu’elle signifie sera accompli dans le royaume de Dieu.

17Puis il prit une coupe, prononça la prière de reconnaissance et dit : Prenez cette coupe et partagez-la entre vous, 18car, je vous le déclare : dorénavant, je ne boirai plus du fruit de la vigne jusqu’à ce que le royaume de Dieu vienne.

19Ensuite il prit du pain, remercia Dieu, le partagea en morceaux qu’il leur donna en disant : Ceci est mon corps [qui est donné pour vous. Faites cela en souvenir de moi.

20Après le repas, il fit de même pour la coupe, en disant : Ceci est la coupe de la nouvelle alliance conclue par mon sang qui va être versé pour vous…22.20 Les mots entre crochets sont absents de certains manuscrits. . ]

(Mt 26.20-25 ; Mc 14.17-21)

21D’ailleurs, voici, celui qui va me trahir est ici, à table avec moi. 22Certes, le Fils de l’homme s’en va selon ce que Dieu a décidé, mais malheur à l’homme par qui il est trahi !

23Alors les disciples se demandèrent les uns aux autres lequel d’entre eux allait faire cela.

Grandeur et service

(Mt 20.25-28 ; Mc 10.42-45)

24Les disciples eurent une vive discussion : il s’agissait de savoir lequel d’entre eux devait être considéré comme le plus grand.

25Jésus intervint : Les rois des nations, dit-il, dominent leurs peuples, et ceux qui exercent l’autorité sur elles se font appeler leurs « bienfaiteurs22.25 Le titre de bienfaiteur (grec : Evergète) était porté par divers rois de l’Antiquité.». 26Il ne faut pas que vous agissiez ainsi. Au contraire, que le plus grand parmi vous soit comme le plus jeune, et que celui qui gouverne soit comme le serviteur. 27A votre avis, qui est le plus grand ? Celui qui est assis à table, ou celui qui sert ? N’est-ce pas celui qui est assis à table ? Eh bien, moi, au milieu de vous, je suis comme le serviteur…

(Mt 19.28)

28Vous êtes restés fidèlement avec moi au cours de mes épreuves. 29C’est pourquoi, comme mon Père m’a donné le royaume, je vous le donne, à mon tour : 30vous mangerez et vous boirez à ma table, dans mon royaume, et vous siégerez sur des trônes pour gouverner les douze tribus d’Israël.

Jésus annonce le reniement de Pierre

(Mt 26.31-35 ; Mc 14.27-31 ; Jn 13.36-38)

31Simon, Simon ! fais attention : Satan vous a réclamés pour vous passer tous au crible, comme on secoue le blé pour le séparer de la bale. 32Mais moi, j’ai prié pour toi, pour que la foi ne vienne pas à te manquer. Et toi, le jour où tu seras revenu à moi, fortifie tes frères.

33– Seigneur, lui dit Simon, je suis prêt, s’il le faut, à aller en prison avec toi, ou même à mourir !

34– Pierre, reprit Jésus, je te l’assure : aujourd’hui même, avant que le coq chante, tu auras, par trois fois, nié de me connaître.

Sur le mont des Oliviers

35Puis, s’adressant à l’ensemble des disciples, il continua : Quand je vous ai envoyés sans bourse, ni sac de voyage, ni sandales, avez-vous manqué de quoi que ce soit ?

– De rien, dirent-ils.

36– Eh bien maintenant, poursuivit-il, si vous avez une bourse, prenez-la ; de même, si vous avez un sac, prenez-le, et si vous n’avez pas d’épée, vendez votre manteau pour en acheter une. 37Car il est écrit : Il a été mis au nombre des criminels22.37 Es 53.12., et cette parole doit s’accomplir pour moi. Car tout ce qui a été écrit de moi va s’accomplir.

38– Seigneur, lui dirent-ils, voilà justement deux épées.

– Cela suffit ! leur répondit-il.

(Mt 26.36-45 ; Mc 14.32-41)

39Alors il sortit et se dirigea, comme d’habitude, vers le mont des Oliviers. Ses disciples s’y rendirent aussi avec lui. 40Quand il fut arrivé, il leur dit : Priez pour ne pas céder à la tentation22.40 Autre traduction : pour ne pas entrer en tentation..

41Puis il se retira à la distance d’un jet de pierre, se mit à genoux et pria ainsi : 42O Père, si tu le veux, écarte de moi cette coupe22.42 Voir note Mt 26.39.! Toutefois, que ta volonté soit faite, et non la mienne.

[43Un ange venu du ciel lui apparut et le fortifia. 44L’angoisse le saisit, sa prière se fit de plus en plus pressante, sa sueur devint comme des gouttes de sang qui tombaient à terre22.44 Les mots entre crochets sont absents de certains manuscrits..]

45Après avoir ainsi prié, il se releva et s’approcha de ses disciples. Il les trouva endormis, tant ils étaient accablés de tristesse.

46– Pourquoi dormez-vous ? leur dit-il. Debout ! Et priez pour ne pas céder à la tentation22.46 Voir 22.40 et note..

L’arrestation de Jésus

(Mt 26.47-55 ; Mc 14.43-49 ; Jn 18.2-11)

47Il n’avait pas fini de parler, quand toute une troupe surgit. A sa tête marchait le nommé Judas, l’un des Douze. Il s’approcha de Jésus pour l’embrasser. 48Mais Jésus lui dit : Judas, c’est par un baiser que tu trahis le Fils de l’homme !

49En voyant ce qui allait se passer, les compagnons de Jésus lui demandèrent : Maître, devons-nous frapper avec nos épées ?

50Et, immédiatement, l’un d’eux frappa le serviteur du grand-prêtre et lui emporta l’oreille droite. 51Mais Jésus les retint en disant : Laissez faire, même ceci22.51 Autre traduction : laissez, tenez-vous-en là.!

Puis il toucha l’oreille du blessé et le guérit. 52Il se tourna ensuite vers les chefs des prêtres, les chefs des gardes du Temple et les responsables du peuple qui avaient accompagné cette troupe pour le prendre.

– Me prenez-vous pour un bandit pour que vous soyez venus avec épées et gourdins ? 53J’étais chaque jour avec vous dans la cour du Temple, et personne n’a mis la main sur moi ; mais maintenant c’est votre heure et les ténèbres vont exercer leur pouvoir.

Pierre renie son Maître

(Mt 26.57-58 ; Mc 14.53-54 ; Jn 18.15-16)

54Alors ils se saisirent de lui et le conduisirent dans le palais du grand-prêtre. Pierre suivait à distance. 55Au milieu de la cour, on avait allumé un feu et les gens étaient assis autour. Pierre s’assit au milieu du groupe.

(Mt 26.69-75 ; Mc 14.66-72 ; Jn 18.17-18, 25-27)

56Une servante, en le voyant là près du feu, l’observa à la clarté de la flamme et dit : En voilà un qui était aussi avec lui.

57Mais Pierre le nia en disant : Mais non, je ne connais pas cet homme.

58Peu après, quelqu’un d’autre, en apercevant Pierre, l’interpella : Toi aussi, tu fais partie de ces gens !

– Mais non, déclara Pierre, je n’en suis pas !

59Environ une heure plus tard, un autre encore soutint avec insistance : C’est sûr, cet homme-là était aussi avec lui ! D’ailleurs, c’est un Galiléen !

60– Mais non, je ne sais pas ce que tu veux dire, s’écria Pierre.

Au même instant, alors qu’il était encore en train de parler, le coq se mit à chanter. 61Le Seigneur se retourna et posa son regard sur Pierre. Alors Pierre se souvint de ce que le Seigneur lui avait dit : « Avant que le coq chante aujourd’hui, tu m’auras renié trois fois ! » 62Il se glissa dehors et se mit à pleurer amèrement.

(Mt 26.67-68 ; Mc 14.65)

63Les hommes qui gardaient Jésus se moquaient de lui et le frappaient. 64Ils lui couvraient le visage et criaient : Hé ! Fais le prophète ! Dis-nous qui te frappe !

65Et ils l’accablaient d’injures.

Jésus devant le Grand-Conseil

(Mt 26.59-65 ; 27.1 ; Mc 14.55-64 ; 15.1 ; Jn 18.19-24)

66Dès le point du jour, les responsables du peuple, les chefs des prêtres et les spécialistes de la Loi se réunirent et firent amener Jésus devant leur Grand-Conseil. 67L’interrogatoire commença : Si tu es le Messie, déclare-le-nous.

Jésus leur dit : Si je vous réponds, vous ne croirez pas, 68et si je vous pose des questions, vous ne me répondrez pas. 69Mais à partir de maintenant, le Fils de l’homme siégera à la droite du Dieu tout-puissant22.69 Ps 110.1 ; Dn 7.13..

70Alors ils se mirent à crier tous ensemble : Tu es donc le Fils de Dieu !

– Vous dites vous-mêmes que je le suis, répondit Jésus.

71Là-dessus ils s’écrièrent : Qu’avons-nous encore besoin de témoignages ? Nous venons de l’entendre nous-mêmes de sa bouche.