Levitiko 23 – CCL & NSP

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Levitiko 23:1-44

1Yehova anawuza Mose kuti, 2“Yankhula ndi Aisraeli ndipo uwawuze kuti, ‘Awa ndi masiku anga osankhika a chikondwerero, masiku osankhika olemekeza Yehova amene uyenera kulengeza kuti akhale masiku opatulika a misonkhano.

Za Sabata

3“ ‘Pa masiku asanu ndi limodzi muzigwira ntchito, koma tsiku lachisanu ndi chiwiri ndi Sabata lopuma, tsiku la msonkhano wopatulika. Kulikonse kumene inu mukukhala musamagwire ntchito iliyonse tsiku limeneli popeza ndi tsiku la Sabata la Yehova.

Za Paska ndi za Buledi Wopanda Yisiti

4“ ‘Awa ndiwo masiku osankhidwa a zikondwerero za Yehova, masiku woyera a misonkhano amene muti mudzalengeze pa nthawi yake: 5Chikondwerero cha Paska chiziyamba madzulo a tsiku la 14 la mwezi woyamba. 6Tsiku la 15 la mwezi womwewo ndi tsiku lolemekeza Yehova ndipo muziyamba Chikondwerero cha Buledi Wopanda Yisiti. Muzidya buledi wopanda yisiti kwa masiku asanu ndi awiri. 7Pa tsiku loyamba muzichita msonkhano wopatulika. Musamagwire ntchito iliyonse. 8Pa masiku asanu ndi awiri muzipereka nsembe yopsereza kwa Yehova. Ndipo tsiku lachisanu ndi chiwiri muzikhala ndi msonkhano wopatulika ndipo musamagwire ntchito yolemetsa.’ ”

Za Zipatso Zoyambirira Kucha

9Yehova anawuza Mose kuti, 10“Yankhula ndi Aisraeli ndipo uwawuze kuti, ‘Mukakalowa mʼdziko limene ndikukupatsanilo ndi kukolola za mʼminda mwanu, mudzabwere kwa wansembe ndi mtolo wa tirigu woyambirira kucha wa mʼminda mwanu. 11Wansembeyo auweyule mtolowo pamaso pa Yehova kotero mtolowo udzalandiridwa mʼmalo mwanu. Wansembe auweyule tsiku lotsatana ndi la Sabata. 12Pa tsiku limene muweyula mtolowo, muperekenso mwana wankhosa wa mwamuna wa chaka chimodzi, wopanda chilema kuti akhale nsembe yopsereza ya kwa Yehova. 13Chopereka chachakudya chake chikhale cha makilogalamu awiri a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta kuti chikhale nsembe yopsereza yopereka kwa Yehova, ya fungo lokoma. Ndipo chopereka cha chakumwa chake chikhale vinyo wa malita anayi ndi theka. 14Musadye buledi aliyense kapena tirigu wokazinga, kapena wamuwisi mpaka tsiku limene mwabwera ndi chopereka ichi kwa Mulungu wanu. Limeneli ndi lamulo lamuyaya pa mibado yanu yonse, kulikonse kumene mukakhale.

Chikondwerero cha Masabata

15“ ‘Kuyambira tsiku lotsatana ndi la Sabata lija, tsiku limene munabwera ndi mtolo wa nsembe yoweyula, muziwerenga masabata asanu ndi awiri athunthu. 16Ndiye kuti muwerenge masiku makumi asanu kuchokera pa tsiku lotsatana ndi Sabata la chisanu ndi chiwiri, ndipo kenaka mupereke nsembe ya tirigu watsopano kwa Yehova. 17Kuchokera kulikonse kumene mukukhala, mubwere pamaso pa Yehova ndi buledi muwiri wa ufa wosalala wa makilogalamu awiri, ophikidwa ndi yisiti kuti akhale nsembe yoweyula ya zakudya zoyamba kucha. 18Pamodzi ndi bulediyu muperekenso ana ankhosa aamuna asanu ndi awiri, aliyense akhale wa chaka chimodzi ndi wopanda chilema. Pakhalenso ngʼombe yayingʼono yayimuna ndi nkhosa zazimuna ziwiri. Zimenezi zidzakhala nsembe zopsereza zopereka kwa Yehova pamodzi ndi nsembe za zakudya ndi nsembe za zakumwa. Zonsezi zikhale nsembe zopsereza za fungo lokomera Yehova. 19Kenaka mupereke mbuzi imodzi yayimuna kuti ikhale nsembe yopepesera machimo ndiponso ana ankhosa awiri, aliyense wa chaka chimodzi kuti akhale nsembe yachiyanjano. 20Wansembe aweyule ana ankhosa awiriwo pamaso pa Yehova monga nsembe yoweyula, pamodzi ndi buledi wa tirigu woyambirira kucha. Zimenezi ndi zopereka zopatulika za Yehova zopatsidwa kwa ansembe. 21Pa tsiku lomwelo mulengeze za msonkhano wopatulika ndipo musagwire ntchito zolemetsa. Limeneli ndi lamulo lamuyaya pa mibado yanu yonse, kulikonse kumene mukakhale.

22“ ‘Pamene mukukolola zinthu mʼmunda mwanu, musakolole munda wanu mpaka mʼmalire mwenimweni, ndipo musatole khunkha lake. Zimenezo musiyire anthu osauka ndi alendo. Ine ndine Yehova Mulungu wanu.’ ”

Chikondwerero cha Malipenga

23Yehova anawuza Mose kuti, 24“Uza Aisraeli kuti, ‘Tsiku loyamba la mwezi wachisanu ndi chiwiri, likhale tsiku lopumula, la msonkhano wopatulika, mulilengeze poyimba lipenga. 25Musagwire ntchito zolemetsa koma mupereke nsembe yopsereza kwa Yehova.’ ”

Tsiku Lopepesera Machimo

26Yehova anawuza Mose kuti, 27“Tsiku lakhumi la mwezi wachisanu ndi chiwiri ndi tsiku lochita Mwambo Wopepesera Machimo. Muzichita msonkhano wopatulika. Muzidzichepetsa pamaso pa Yehova ndi kupereka nsembe zopsereza kwa Yehova. 28Tsiku limeneli musamagwire ntchito chifukwa ndi tsiku la Mwambo Wopepesera Machimo, kupepesera machimo anu pamaso pa Yehova Mulungu wanu. 29Munthu aliyense amene sasala zakudya pa tsiku limeneli ayenera kuchotsedwa pakati pa anthu a mtundu wake. 30Aliyense wogwira ntchito tsiku limeneli ndidzamuwononga pakati pa anthu a mtundu wake. 31Inu musadzagwire ntchito iliyonse. Limeneli ndi lamulo lamuyaya pa mibado yanu yonse, kulikonse kumene mukakhale. 32Limeneli kwa inu ndi tsiku la Sabata lopumula, ndipo muyenera kusala zakudya. Kuyambira madzulo a tsiku lachisanu ndi chinayi la mwezi mpaka madzulo ena otsatirawo muzisunga tsikulo ngati Sabata lanu.”

Chikondwerero cha Misasa

33Yehova anawuza Mose kuti, 34“Uwawuze Aisraeli kuti pa masiku asanu ndi awiri kuyambira pa tsiku la 15 la mwezi wachisanu ndi chiwiri pazikhala Chikondwerero cha Misasa cholemekeza Yehova. 35Tsiku loyamba ndi la msonkhano wopatulika, musagwire ntchito zolemetsa. 36Pa masiku asanu ndi awiri muzipereka nsembe zopsereza kwa Yehova. Ndipo pa tsiku lachisanu ndi chitatu muzikhala ndi msonkhano wopatulika ndipo muzipereka nsembe yopsereza kwa Yehova. Kumeneku ndi kutsekera kwa msonkhano waukulu. Musagwire ntchito zolemetsa.

37(“ ‘Amenewa ndi masiku osankhika a chikondwerero cha Yehova, amene muziwalengeza kuti ndi nthawi ya msonkhano wopatulika. Masiku amenewa muzipereka nsembe zopsereza, nsembe za chakudya, nsembe zanyama ndi zopereka zachakumwa za tsiku ndi tsiku. 38Zopereka zimenezi ndi zowonjezera pa zopereka za Yehova za pa Sabata, zopereka zanu zolumbira ndiponso mphatso zanu zaufulu zopereka kwa Yehova.)

39“ ‘Choncho kuyambira pa tsiku la 15 la mwezi wachisanu ndi chiwiri, mutakolola zinthu mʼmunda mwanu, muchite chikondwerero cha Yehova kwa masiku asanu ndi awiri. Tsiku loyamba ndi tsiku lopumula, ndipo tsiku lachisanu ndi chitatu ndi lopumulanso. 40Pa tsiku loyamba muzitenga zipatso zabwino kwambiri zothyola mʼmitengo, nthambi za kanjedza, nthambi zazikulu za mitengo ya masamba ambiri, ndi za misondozi yakumtsinje, ndipo muzikondwera pamaso pa Yehova Mulungu wanu kwa masiku asanu ndi awiri. 41Chaka chilichonse muzichita chikondwerero cha Yehova kwa masiku asanu ndi awiri. Limeneli ndi lamulo lamuyaya pa mibado yanu yonse. Muzichita chikondwerero chimenechi mwezi wachisanu ndi chiwiri. 42Muzikhala mʼmisasa masiku asanu ndi awiri. Onse amene ali mbadwa mʼdziko la Israeli azikhala mʼmisasa 43kuti zidzukulu zanu zidzadziwe kuti ndine amene ndinakhazika Aisraeli mʼmisasa nditawatulutsa ku Igupto. Ine ndine Yehova Mulungu wanu.’ ”

44Choncho Mose analengeza kwa Aisraeli masiku osankhika a zikondwerero za Yehova.

New Serbian Translation

3. Мојсијева 23:1-44

Празници

1Господ рече Мојсију: 2„Говори народу израиљском. Реци им: ’Ово су Господњи празници, када ћете сазивати свете саборе. Ово су моји празници:

Субота

3Шест дана ради, а седмога дана је субота потпуног одмора, свети сабор. Не радите никаквог посла; нека Господња субота буде по свим вашим местима.

4Ово су Господњи празници, свети сабори, које ћеш прослављати у одређено време:

Пасха и празник Бесквасних хлебова

5Првога месеца, четрнаестог дана у месецу, увече, почиње Пасха Господња. 6А петнаестога дана истог месеца је Господњи празник Бесквасних хлебова. Једите бесквасне хлебове седам дана.

7Првога дана одржавајте свети сабор; не радите никаквог свакодневног посла. 8Седам дана приносите Господу паљене жртве. А седмога дана биће свети сабор: не радите никакав посао.’“

Прва жетва

9Господ рече Мојсију: 10„Говори Израиљцима. Реци им: ’Кад уђете у земљу коју вам ја дајем, и почнете од ње жети жетву, први сноп своје жетве донесите свештенику. 11Тада нека он подигне сноп пред Господом да будете примљени. Свештеник ће га подигнути наредног дана након суботе. 12На дан када подижете сноп, принесите јагње од годину дана, без мане, као жртву свеспалницу Господу, 13а уз њега десетину ефе брашна замешеног с уљем, као житну жртву. То је паљена жртва, угодни мирис Господу. Уз њега иде и жртва изливница од четвртине хина23,13 Око 1 l. вина. 14До тог дана, док не принесете принос свога Бога, не смете јести хлеб, пржено жито, или свеже класје. То је вечна уредба за ваше нараштаје по свим вашим местима.

Празник Седмица

15Наредног дана након суботе, пошто принесете клас за жртву дизаницу, набројте седам пуних недеља. 16Набројте педесет дана до првога дана након седме суботе, па принесите Господу жртву од новог жита. 17Донесите из својих места два хлеба за жртву дизаницу, сваки од по две десетине мере брашна. Нека буду печени с квасцем, као првина за Господа. 18Са хлебом принесите седам јагањаца без мане, од годину дана, једног јунца из крда, и два овна, за жртву свеспалницу Господу, заједно с њиховим житним жртвама и жртвама изливницама, као паљену жртву, угодан мирис Господу. 19Принесите и једног јарца као жртву за грех, и два јагњета од годину дана, као жртву мира. 20Нека их свештеник подигне пред Господом с хлебом од првина, као жртву дизаницу, и са она два јагњета. То је свети принос за Господа, који следује свештенику. 21Истог дана сазовите сабор. Нека вам то буде свети сабор. Не радите никакав свакодневни посао! Ово је трајна уредба за све ваше нараштаје по свим вашим местима.

22Кад почнете жети жетву са своје земље, немојте жети до самог краја свога поља, нити пабирчити после своје жетве. То оставите сиромаху и странцу. Ја сам Господ, Бог ваш.’“

Први дан седмог месеца

23Господ рече Мојсију: 24„Говори Израиљцима: ’Седмога месеца, првога дана у месецу, нека вам буде потпуни починак, спомен-дан објављен гласом трубе, свети сабор. 25Не радите никаквог свакодневног посла. Принесите Господу паљену жртву.’“

Дан откупљења

26Господ рече Мојсију: 27„А десетог дана седмога месеца је дан откупљења. Нека вам то буде свети сабор. Постите23,27 Дословно: Мучите или Понизити своју душу. и принесите паљену жртву Господу. 28Не радите никаквог посла на тај дан, јер је то дан откупљења, када ће се извршити ваше откупљење пред Господом, Богом вашим. 29Онај ко не буде постио на овај дан, нека се истреби из свог народа. 30Ко год се буде латио каквог посла на овај дан, њега ћу ја затрти усред његовог народа. 31Не радите никаквог посла! То је трајна уредба за ваше нараштаје, по свим вашим местима. 32Нека вам то буде субота потпуног одмора. Постите! Прослављајте своју суботу од вечери деветог дана у месецу до следеће вечери.“

Празник Сеница

33Господ рече Мојсију: 34„Говори Израиљцима: ’Петнаестог дана у седмом месецу је празник Сеница Господу, у трајању од седам дана. 35Првога дана је свети сабор: не радите никаквог свакодневног посла. 36Седам дана приносите Господу паљене жртве, а осмога дана нека вам буде свети сабор. Тада ћете приносити Господу паљене жртве. То је свечани сабор; не радите никаквог посла.

37То су Господњи празници, које ћете славити као свете саборе, приносећи Господу паљене жртве, жртве свеспалнице, житне жртве, приносе и жртве изливнице, сваку у одређени дан, 38осим Господњих субота и ваших дарова, и осим свих завета и добровољних прилога које приносите Господу.

39А петнаестог дана у седмом месецу, кад прикупите првине земље, седам дана славите Господњи празник. Први и осми дан нека буду дани потпуног одмора. 40На први дан узмите најбоље плодове, палмове гране, гране с лиснатог дрвећа, и врбе с потока, па се седам дана веселите пред Господом, Богом својим. 41Прослављајте Господњи празник седам дана у години. Ово је трајна уредба за ваше нараштаје: славите тај празник седмог месеца. 42Живите у сеницама седам дана; сви рођени у Израиљу нека живе у сеницама, 43да би ваши нараштаји знали да сам ја, Господ, Бог ваш, учинио да народ израиљски живи у сеницама, кад сам их извео из Египта.’“

44Тако је Мојсије саопштио Израиљцима Господње празнике.