Levitiko 24 – CCL & NSP

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Levitiko 24:1-23

Mafuta ndi Buledi wa Pamaso pa Yehova

1Yehova anawuza Mose kuti, 2“Lamula Aisraeli kuti akupatse mafuta anyale, a olivi wabwino kwambiri kuti nyalezo ziziyaka nthawi zonse. 3Kunja kwa nsalu yotchinga Bokosi la Chipangano, mʼchihema cha msonkhano, Aaroni azionetsetsa kuti nyale ikukhala chiyakire pamaso pa Yehova kuyambira madzulo mpaka mmawa, nthawi zonse. Limeneli ndi lamulo lamuyaya pa mibado yonse. 4Aaroni ayatse nyale zimene zili pa choyikapo nyale chagolide wabwino kwambiri kuti zikhale zoyaka nthawi zonse pamaso pa Yehova.

5“Mutenge ufa wosalala ndipo muphike makeke khumi ndi awiri ndipo keke iliyonse ikhale ya ufa wa makilogalamu awiri. 6Muwayike pa tebulo la golide wabwino kwambiri pamaso pa Yehova mʼmizere iwiri. Mzere uliwonse ukhale wa makeke asanu ndi imodzi. 7Pa mzere uliwonse muyikepo lubani wafungo lokoma kuti pamodzi ndi bulediyo akhale wachikumbutso cha nsembe yopsereza yopereka kwa Yehova. 8Sabata ndi sabata nthawi zonse Aaroni aziyika makeke amenewa pamaso pa Yehova mʼmalo mwa Aisraeli onse kuti akhale pangano lamuyaya. 9Chakudyacho ndi cha Aaroni ndi ana ake ndipo azidyera ku malo wopatulika chifukwa kwa iye chakudyacho ndi chopatulika kwambiri chochokera pa chopereka chopsereza cha Yehova.”

Woyankhula Monyoza Mulungu Aphedwa ndi Miyala

10Tsiku lina munthu wina wamwamuna amene amayi ake anali Mwisraeli koma abambo ake anali Mwigupto anapita kwa Aisraeli ndipo anakangana ndi Mwisraeli wina ku msasa. 11Munthu uja ananyoza dzina la Yehova ndi kulitemberera. Choncho anabwera naye kwa Mose. Dzina la amayi ake linali Selomiti, mwana wa Dibiri, wa fuko la Dani. 12Anamuyika mʼndende mpaka atadziwa bwino chofuna cha Yehova.

13Ndipo Yehova anawuza Mose kuti, 14“Pita naye kunja kwa msasa munthu wotembererayo. Onse amene anamumva akutemberera asanjike manja awo pamutu pake ndipo gulu lonse la anthu limugende miyala. 15Choncho uza Aisraeli kuti, ‘Aliyense wotemberera Mulungu wake alangidwe. 16Aliyense wonyoza dzina la Yehova, mlendo ngakhale mbadwa, aphedwe. Gulu lonse la anthu limuponye miyala.

17“ ‘Ngati munthu wina aliyense achotsa moyo wa munthu mnzake, munthuyo ayenera kuphedwa. 18Aliyense wopha chiweto cha mnzake ayenera kulipira china. Moyo kulipa moyo. 19Ngati munthu avulaza mnzake, nayenso amuchite zomwe wachitira mnzakeyo: 20kuthyola fupa kulipira kuthyola fupa, diso kulipira diso, dzino kulipira dzino. Monga momwe anavulazira mnzake, amuvulaze chimodzimodzinso. 21Aliyense wopha chiweto cha mnzake, alipire chiweto china, koma aliyense wopha munthu ayenera kuphedwa. 22Lamulo la mlendo ndi mbadwa ndi limodzi lomweli. Ine ndine Yehova Mulungu wanu.’ ”

23Pamenepo Mose anawuza Aisraeli zimenezi, ndipo iwo anatulutsira munthu wotembererayo kunja kwa msasa ndi kumugenda miyala. Aisraeli anachita zimene Yehova analamula Mose.

New Serbian Translation

3. Мојсијева 24:1-23

Пламен у свећњаку

1Господ рече Мојсију: 2„Заповеди Израиљцима да ти донесу чистог, свеже исцеђеног, маслиновог уља за свећњак, да светло стално гори. 3Нека га Арон постави у Шатору од састанка, изван завесе Сведочанства, да непрестано гори пред Господом, од вечери до јутра. То је трајна уредба за све ваше нараштаје. 4Нека Арон непрестано одржава жишке на свећњаку од чистог злата пред Господом.

Посвећени хлебови

5Узми брашна и испеци дванаест погача. Нека свака погача тежи две десетине ефе24,5 Око 2,6 kg.. 6Постави их у два реда, по шест у сваком, на сто од чистог злата пред Господом. 7На сваки ред стави чистог тамјана, да хлеб буде за спомен, паљену жртву Господу. 8Нека их Арон сваке суботе поставља пред Господом, као вечни савез ради Израиљаца. 9Нека их Арон и његови синови једу на светом месту, јер је то најсветији део од паљених жртава Господњих. То је вечна уредба.“

Казна за богохулство

10А син једне Израиљке и Египћанина, дође међу Израиљце, и потуче се у табору са једним Израиљцем. 11Међутим, син те жене, Израиљке, погрди име Господње проклињући га. Доведу га Мојсију. Његова мајка се звала Селомита, ћерка Давријина, из Дановог племена. 12Ставили су га у притвор, док им се не обзнани Господња одлука.

13Господ рече Мојсију: 14„Изведи изван табора богохулника, а сви који су га чули нека положе руке на његову главу. Затим нека га цела заједница каменује. 15А Израиљцима реци: ’Ако неки човек прокуне свога Бога, одговараће за свој грех. 16Онај који погрди име Господње, нека се свакако погуби; нека га цела заједница заспе камењем. Био он странац или домаћи, ако погрди име Господње, нека умре!

17Ако неко одузме живот човеку, нека се свакако погуби.

18Ако неко усмрти живинче, нека плати одштету: живот за живот.

19Ако неко нанесе повреду своме ближњему, нека му се уради оно што је он урадио њему. 20Прелом за прелом, око за око, зуб за зуб. Како је он другоме нанео повреду, тако нека се њему нанесе повреда.

21Ако неко убије живинче, нека плати одштету, а ко убије човека, нека се погуби. 22Исти закон важи за вас, како за странца, тако за домаћег. Ја сам Господ, Бог ваш.’“

23Пошто је Мојсије саопштио Израиљцима ово, они изведу богохулника изван табора и заспу га камењем. Тако су Израиљци учинили како је Господ заповедио Мојсију.