Levitiko 2 – CCL & NIRV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Levitiko 2:1-16

Nsembe Zachakudya

1“ ‘Munthu wina aliyense akabwera ndi nsembe ya chakudya kwa Yehova, chopereka chake chizikhala ufa wosalala. Ufawo ausakanize ndi mafuta ndi lubani, 2ndipo apite nawo kwa ansembe, ana a Aaroni. Atapeko modzazitsa dzanja ufa wosalala uja kuti ukhale wachikumbutso pamodzi ndi mafuta ndi lubani ndipo atenthe zonsezi pa guwa lansembe kuti zilandiridwe ndi Yehova mʼmalo mwa chopereka chonse. Iyi ndi nsembe yotentha pa moto ndiponso fungo lokomera Yehova. 3Zotsala za nsembe ya chakudyazo ndi za Aaroni pamodzi ndi ana ake. Chimenechi ndi chigawo chopatulika kwambiri chifukwa chatapidwa pa chopereka chotentha pa moto cha Yehova.

4“ ‘Ukabweretsa nsembe ya chakudya chophika mu uvuni, ikhale ya buledi wa ufa wosalala wopanda yisiti koma wosakaniza ndi mafuta, kapena timitanda ta buledi topyapyala, topanda yisiti koma topaka mafuta. 5Ngati nsembe yako yachakudya ndi yophika pa chitsulo chamoto, ikhale ya buledi wa ufa wosalala wopanda yisiti koma wosakaniza ndi mafuta. 6Umuduledule bulediyo ndi kumupaka mafuta; imeneyo ndi nsembe yachakudya. 7Ngati nsembe yako yachakudya ndi yophikidwa pa chiwaya, ikhale ya buledi wa ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta. 8Munthu azibwera ndi nsembe za chakudya zimene wapanga ndi zinthu zimenezi. Atachipereka kwa wansembe, iyeyu adzipita nacho ku guwa. 9Wansembeyo atengeko gawo lina la nsembeyo kukhala ufa wachikumbutso kuti ilandiridwe ndi Yehova mʼmalo mwa nsembe yonse ndipo ayitenthe pa moto monga nsembe yopsereza ya fungo lokomera Yehova. 10Zotsala za nsembe ya chakudyayo zikhale za Aaroni ndi ana ake. Chimenechi ndi chigawo chopatulika kwambiri chifukwa chatapidwa pa chopereka chotentha pa moto cha Yehova.

11“ ‘Nsembe ya chakudya chilichonse imene ubweretsa kwa Yehova ikhale yopanda yisiti, pakuti suyenera kupereka kwa Yehova nsembe yotentha pa moto imene ili ndi yisiti kapena uchi. 12Ziwirizi ungathe kubwera nazo kwa Yehova ngati chopereka cha zokolola zoyambirira. Koma usazitenthe pa guwa kuti zikhale fungo lokomera Yehova. 13Zopereka zako zonse zachakudya uzithire mchere. Usayiwale kuthira mchere pa chopereka chako popeza mcherewo ukusonyeza pangano pakati pa iwe ndi Mulungu wako. Tsono uzinthira mchere pa chopereka chako chilichonse.

14“ ‘Mukamapereka kwa Yehova chopereka cha chakudya choyamba kucha, choperekacho chikhale cha chipatso chatsopano chokazinga pa moto ndi chopunthapuntha. 15Uchithire mafuta ndi lubani pakuti ndi chopereka cha chakudya. 16Tsono wansembe atenthe gawo la chopereka chopunthapuntha chija kuti chikhala ufa wachikumbutso ndi cha mafuta pamodzi ndi lubani yense kuti Yehova alandire mʼmalo mwa zopereka zonse. Ichi ndi chopereka chotentha pa moto cha Yehova.

New International Reader’s Version

Leviticus 2:1-16

Rules for Grain Offerings

1“ ‘Suppose anyone brings a grain offering to the Lord. Then their offering must be made out of the finest flour. They must pour olive oil on it. They must also put incense on it. 2They must take it to the priests in Aaron’s family line. A priest must take a handful of the flour and oil. He must mix them with all the incense. Then he must burn that part on the altar. It will be a reminder that all good things come from the Lord. It is a food offering. Its smell pleases the Lord. 3The rest of the grain offering belongs to Aaron and to the priests in his family line. It is a very holy part of the food offerings presented to the Lord.

4“ ‘If you bring a grain offering baked in an oven, make it out of the finest flour. It can be thick loaves of bread made without yeast. Mix them with olive oil. Or it can be thin loaves of bread that are made without yeast. Spread olive oil on them. 5If your grain offering is cooked on a metal plate, make your offering out of the finest flour. Mix it with oil. Make it without yeast. 6Break it into pieces. Pour oil on it. It is a grain offering. 7If your grain offering is cooked in a pan, make your offering out of the finest flour and some olive oil. 8Bring to the Lord your grain offering made out of all these things. Give it to the priest. He must take it to the altar. 9All good things come from the Lord. The priest must take out the part of the grain offering that reminds you of this. He must burn it on the altar. It is a food offering. Its smell pleases the Lord. 10The rest of the grain offering belongs to Aaron and the priests in his family line. It is a very holy part of the food offerings presented to the Lord.

11“ ‘Every grain offering you bring to the Lord must be made without yeast. You must not add any yeast or honey to a food offering presented to the Lord. 12You can bring them to the Lord as an offering of the first share of food you gather or produce. But they must not be offered on the altar as a pleasant smell. 13Put salt on all your grain offerings. Salt stands for the lasting covenant between you and your God. So do not leave it out of your grain offerings. Add salt to all your offerings.

14“ ‘Suppose you bring to the Lord a grain offering of the first share of your food. Then offer crushed heads of your first grain that have been cooked in fire. 15Put olive oil and incense on the grain. It is a grain offering. 16The priest must burn part of the crushed grain and the oil. It will remind you that all good things come from the Lord. The priest must burn it together with all the incense. It is a food offering presented to the Lord.