Levitiko 10 – CCL & CCBT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Levitiko 10:1-20

Imfa ya Nadabu ndi Abihu

1Ana a Aaroni, Nadabu ndi Abihu, aliyense anatenga chofukizira lubani chake nayikamo makala a moto ndi kuthiramo lubani. Iwo anapereka pamaso pa Yehova moto wachilendo, moto umene Yehova sanawalamule. 2Choncho moto unatuluka pamaso pa Yehova ndi kuwapsereza, ndipo anafa pamaso pa Yehova. 3Pamenepo Mose anawuza Aaroni kuti, “Pajatu Yehova ananena kuti,

“ ‘Kwa iwo amene amandiyandikira

ndidzaonetsa ulemerero wanga;

pamaso pa anthu onse

ndidzalemekezedwa.’ ”

Aaroni anakhala chete wosayankhula.

4Mose anayitana Misaeli ndi Elizafani, ana a Uzieli, abambo angʼono a Aaroni, ndipo anawawuza kuti, “Bwerani kuno mudzachotse abale anuwa pa malo wopatulika ndi kuwatulutsira kunja kwa msasa.” 5Choncho anabwera atavala minjiro yawo ndipo anawatenga ndi kuwatulutsa kunja kwa msasawo monga momwe Mose analamulira.

6Ndipo Mose anawuza Aaroni ndi ana ake Eliezara ndi Itamara kuti, “Musalileke tsitsi lanu nyankhalala ndipo musangʼambe zovala zanu kuti mungafe, ndi mkwiyo wa Yehova ungagwere anthu onsewa. Koma abale anu okha, kutanthauza fuko lonse la Israeli ndiwo ayenera kulira omwalira aja amene Yehova wawapsereza ndi moto. 7Musatuluke kunja kwa tenti ya msonkhano, mungafe, chifukwa munadzozedwa ndi mafuta a Yehova kukhala ansembe.” Choncho iwo anachita monga Mose ananenera.

8Pambuyo pake Yehova anayankhula ndi Aaroni nati, 9“Iwe ndi ana ako musamamwe vinyo kapena chakumwa chilichonse choledzeretsa pamene mukulowa mu tenti ya msonkhano kuti mungafe. Ili ndi lamulo lamuyaya pa mibado yanu yonse. 10Muzisiyanitsa pakati pa zinthu zopatulika ndi zinthu wamba, pakati pa zinthu zodetsedwa ndi zinthu zoyeretsedwa, 11ndipo muyenera kuphunzitsa Aisraeli onse malamulo amene Yehova wakupatsani kudzera mwa Mose.”

12Mose anawuza Aaroni ndi ana ake otsalawo, Eliezara ndi Itamara kuti, “Tengani zopereka zachakudya zopanda yisiti zimene zatsala pa nsembe zopsereza za kwa Yehova ndipo muzidye pafupi ndi guwa pakuti ndi zopatulika kwambiri. 13Muzidye pa malo wopatulika chifukwa zimenezi ndi gawo lako ndi la ana ako pa zopereka zopsereza kwa Yehova. Izitu ndi zimene Yehova anandilamulira. 14Koma iwe pamodzi ndi ana ako aamuna ndi aakazi muzidya chidale chimene chinaweyulidwa ndi ntchafu zimene zinaperekedwa nsembe. Muzidye pamalo woyeretsedwa. Zimenezi zaperekedwa kwa iwe ndi ana ako monga gawo lanu pa zopereka zachiyanjano zimene apereka Aisraeli. 15Ntchafu imene inaperekedwayo ndi chidale chomwe chinaweyulidwacho abwere nazo pamodzi ndi nsembe ya mafuta ya Yehova yotentha pa moto, ndipo uziweyule kuti zikhale zopereka zoweyula pamaso pa Yehova. Zimenezi zizikhala zako ndi ana ako nthawi zonse monga walamulira Yehova.”

16Pambuyo pake Mose anafunafuna mbuzi ya nsembe yopepesera machimo koma anapeza kuti anayitentha kale. Apa Mose anakalipira Eliezara ndi Itamara, ana a Aaroni otsala aja nati, 17“Chifukwa chiyani simunadyere pamalo wopatulika nsembe yopepesera machimo ija? Kodi imene ija siyopatulika? Kodi Yehova sanapereke nyamayo kwa inu kuti muchotse machimo a mpingo wonse powachitira mwambo wa nsembe yopepesera machimo pamaso pa Yehova? 18Pakuti magazi ake sanalowe nawo ku Malo Wopatulika, mukanadya nyama ya mbuziyo pa malo wopatulikawo monga Yehova analamulira.”

19Aaroni anamuyankha Mose kuti, “Lero anthu apereka nsembe yawo yopepesera machimo ndiponso nsembe yawo yopsereza pamaso pa Yehova komabe zinthu zoterezi zandichitikira. Kodi Yehova akanakondwa ndikanadya nsembe yopepesera machimo lero?” 20Pamene Mose anamva zimenezi, anakhutira.

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

利未記 10:1-20

拿答和亞比戶之死

1亞倫的兒子拿答亞比戶各拿自己的香爐,點火加香,在耶和華面前獻上凡火。他們這樣做不合耶和華的吩咐。 2於是,有火從耶和華面前出來吞噬了他們,他們就死在耶和華面前。 3摩西告訴亞倫:「耶和華曾說過,『我要在事奉我的人10·3 事奉我的人」希伯來文是「靠近我的人」。中顯明我的聖潔,在所有子民面前彰顯我的榮耀。』」亞倫默默無言。 4摩西叫來亞倫的叔父烏薛的兒子米沙利以利撒反,對他們說:「過來,把你們弟兄的屍體從聖所前抬到營外去。」 5他們就遵照摩西的吩咐,把仍穿著內袍的屍體抬到營外。 6摩西亞倫和他剩下的兩個兒子以利亞撒以他瑪說:「你們不要蓬頭散髮,也不要撕裂衣服,免得你們死亡,也免得耶和華向全體會眾發怒。不過,你們的所有以色列同胞都可以為耶和華用火燒死的人哀傷。 7你們不可走出會幕門口,否則你們都會死,因為耶和華的膏油在你們身上。」他們就遵照摩西的話去做。

有關祭司的條例

8耶和華對亞倫說: 9「你和你兒子們進會幕前,淡酒烈酒都不可喝,否則你們都會死。你們世世代代都要遵守這永遠的條例。 10你們必須明辨什麼是聖潔的、什麼是世俗的,什麼是潔淨的、什麼是不潔淨的。 11你們必須將我藉摩西賜給以色列人的一切律例教導他們。」

12摩西亞倫及其兩個兒子以利亞撒以他瑪說:「你們要把獻給耶和華的火祭中剩下的素祭做成無酵餅,在壇邊吃,因為這是至聖之物。 13你們要在聖潔之處吃,因為在獻給耶和華的火祭中,這是你們和你們的子孫應得之份。這是耶和華對我的吩咐。 14至於作搖祭的胸肉和作舉祭的腿肉,你們和你們的子孫可以在潔淨的地方吃。因為在以色列人所獻的平安祭中,這是你們應得之份。 15在獻火祭的脂肪時,要把作舉祭的腿肉和作搖祭的胸肉一起帶到耶和華面前,這些永遠是你們和你們的子孫應得之份,正如耶和華的吩咐。」

16摩西到處尋找那隻作贖罪祭的公山羊,卻發現那隻羊已經被焚燒了。他憤怒地對亞倫剩下的兩個兒子以利亞撒以他瑪說: 17「你們為什麼不在聖潔之處吃這贖罪祭?這是至聖之物,耶和華賜給你們是要叫你們為會眾擔罪,在耶和華面前為他們贖罪。 18既然這祭牲的血沒有被帶進聖所,你們本應按照我的吩咐在聖潔之處吃這祭肉。」 19亞倫摩西說:「看啊,他們今天向耶和華獻贖罪祭和燔祭,卻有這樣的災禍發生在我身上。今天我如果吃了這贖罪祭的祭肉,耶和華會悅納嗎?」 20摩西亞倫的回答感到滿意。