Hoseya 3 – CCL & CCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Hoseya 3:1-5

Hoseya Ayanjana ndi Mkazi Wake

1Yehova anati kwa ine, “Pita kamukondenso mkazi wako, ngakhale ali pa chibwenzi ndi wina ndi kuti ndi wachigololo. Mukonde iyeyo monga momwe Yehova amakondera Aisraeli, ngakhale iwo amapita kukapembedza milungu ina ndi kukonda nsembe za keke zamphesa zowuma.”

2Motero ndinamukwatira popereka ndalama khumi ndi zisanu zasiliva, ndiponso mitanga isanu ndi iwiri ya barele. 3Kenaka ndinamuwuza mkaziyo kuti, “Ukhale nane masiku ambiri; usachitenso zachiwerewere kapena chigololo ndi munthu wina, ndipo ine ndidzakhala nawe.”

4Pakuti Aisraeli adzakhala masiku ambiri opanda mfumu kapena kalonga, osapereka nsembe kapena kuyimika miyala yachipembedzo, wopanda efodi kapena fano. 5Pambuyo pake Aisraeli adzabwerera ndi kufunafuna Yehova Mulungu wawo ndi Davide mfumu yawo. Adzabwera kwa Yehova akunjenjemera ndipo adzalandira madalitso mʼmasiku awo otsiriza.

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

何西阿书 3:1-5

何西阿赎回不贞之妻

1耶和华对何西阿说:“你要再去爱那个另有新欢的淫妇,像耶和华爱以色列人一样爱她。尽管他们祭拜别的神明,喜爱葡萄饼,耶和华仍然爱他们。” 2于是,我用一百七十克银子和一百五十公斤大麦赎回她, 3对她说:“你要和我住许多日子。这期间不可行淫,不可亲近别的男人,我也不与你同房。” 4以色列人也要有许多日子没有君王和首领,没有祭祀和神柱,也没有以弗得和家庭神像。 5之后,以色列人将回心转意,寻求他们的上帝耶和华,归向他们的君王大卫。在末后的日子,他们将怀着敬畏的心归向耶和华,领受祂的恩惠。