Hoseya 2 – CCL & CCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Hoseya 2:1-23

1“Nena kwa abale ako kuti, ‘Ndinu anthu anga,’ kwa alongo ako kuti ‘Ndinu okondedwa anga.’ ”

Kulangidwa ndi Kubwezeretsedwa kwa Israeli

2“Dzudzulani amayi anu, adzudzuleni iwo,

pakuti si mkazi wanga,

ndipo ine sindine mwamuna wake.

Iyeyo achotse maonekedwe adama pa nkhope yake,

ndi kusakhulupirika pa mawere ake.

3Akapanda kutero ndidzamuvula,

ndipo adzakhala wamaliseche monga tsiku limene anabadwa;

ndidzamuwumitsa ngati chipululu,

adzakhala ngati dziko lopanda madzi,

ndi kumupha ndi ludzu.

4Sindidzaonetsa chikondi changa pa ana ake,

chifukwa ndi ana a mʼchiwerewere.

5Amayi awo akhala akuchita zachiwerewere

ndipo anawabereka anawo akuchita zinthu zochititsa manyazi.

Iwo anati, ‘Ine ndidzatsatira zibwenzi zanga,

zimene zimandipatsa chakudya ndi madzi,

ubweya ndi thonje, mafuta ndi chakumwa.’

6Choncho njira yake ndidzayitseka ndi minga;

ndidzamuzinga ndi khoma kotero kuti sadzapezanso njira yotulukira.

7Adzathamangira zibwenzi zake koma sadzazipeza;

adzazifunafuna koma sadzazipeza.

Pamenepo iye adzati,

‘Ndibwerera kwa mwamuna wanga woyamba uja,

pakuti ndinali pabwino ndi iyeyo kusiyanitsa ndi pano.’

8Iye sanazindikire kuti ndine amene

ndinkamupatsa tirigu, vinyo watsopano ndi mafuta.

Ndine amene ndinkamukhuthulira siliva ndi golide,

zimene ankapangira mafano a Baala.

9“Choncho Ine ndidzamulanda tirigu wanga pa nthawi yokolola,

ndi vinyo wanga watsopano pa nthawi yopsinya mphesa.

Ndidzamulanda ubweya ndi thonje langa,

zomwe akanaphimba nazo umaliseche wake.

10Motero tsopano ndidzaonetsa maliseche ake

pamaso pa zibwenzi zake;

palibe ndi mmodzi yemwe adzamupulumutse mʼmanja mwanga.

11Ndidzathetsa zikondwerero zake zonse:

zikondwerero zake za chaka ndi chaka, za mwezi watsopano,

za pa masiku a Sabata ndi maphwando ake onse a pa masiku okhazikitsidwa.

12Ndidzawononga mitengo yake ya mpesa ndi mitengo yake yamkuyu,

imene iye ankanena kuti inali malipiro ake ochokera kwa zibwenzi zake.

Ndidzayisandutsa chithukuluzi,

ndipo zirombo zakuthengo zidzadya zipatsozo.

13Ndidzamulanga chifukwa cha masiku

amene anafukiza lubani kwa Abaala;

anadzikongoletsa povala mphete ndi mikanda yamtengowapatali

ndipo anathamangira zibwenzi zake,

koma Ine anandiyiwala,”

akutero Yehova.

14“Koma tsopano ndidzamukopa mkaziyo;

ndidzapita naye ku chipululu

ndipo ndidzamuyankhula mwachikondi.

15Kumeneko ndidzamubwezera minda yake ya mpesa,

ndipo ndidzasandutsa Chigwa cha Akori kukhala khomo la chiyembekezo.

Kumeneko iye adzayimba nyimbo monga mʼmasiku a ubwana wake,

monga tsiku limene anatuluka ku Igupto.

16“Tsiku limeneli,” Yehova akuti,

“udzandiyitana kuti, ‘Amuna anga;’

sudzandiyitananso kuti, ‘Mbuye wanga.’

17Ndidzachotsa mayina a Abaala pakamwa pake;

sadzatchulanso mayina awo popemphera.

18Tsiku limenelo ndidzachita pangano

ndi zirombo zakuthengo ndi mbalame zamumlengalenga

ndiponso zolengedwa zokwawa pansi kuti ziyanjane ndi anthu anga.

Ndidzachotsa mʼdzikomo uta,

lupanga ndi zida zonse zankhondo,

kuti onse apumule mwamtendere.

19Ndidzakutomera kuti ukhale mkazi wanga mpaka muyaya;

ndidzakutomera mwachilungamo, mwaungwiro,

mwachikondi ndi mwachifundo.

20Ndidzakutomera mokhulupirika

ndipo udzadziwa Yehova.

21“Tsiku limenelo Ine ndidzayankha,”

akutero Yehova.

“Ndidzayankha mlengalenga pempho lake lofuna mitambo

ndipo mvula idzagwa pa dziko lapansi;

22ndipo nthaka idzamvera kupempha kwa tirigu,

vinyo ndi mafuta,

ndipo zidzamvera Yezireeli.

23Ndidzadzala Israeli mʼdziko kuti akhale wanga:

ndidzaonetsa chikondi changa kwa anthu amene ndinkawatchula dzina loti, ‘Sakondedwa.’

Ndidzawawuza amene ndinkawatchula dzina loti, ‘Si anthu anga,’ kuti, ‘Ndinu anthu wanga;’

ndipo adzanena kuti, ‘ndinu Mulungu wathu,’ ”

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

何西阿书 2:1-23

1“你们要称你们的弟兄为阿米2:1 阿米”意思是“我的子民”。,要称你们的姊妹为路哈玛2:1 路哈玛”意思是“得蒙怜悯”。

对不贞之妇的控诉

2“你们去跟你们的母亲理论吧!

因为她不再是我的妻子,

我也不再是她的丈夫。

叫她别再出卖色相,

别再露出乳间的淫态。

3不然,我要剥光她的衣服,

使她像初生之时一样赤身露体;

我要使她像沙漠,如旱地,

干渴而死。

4我也不怜悯她的儿女,

因为他们都是娼妓所生的儿女。

5他们的母亲淫乱放荡,厚颜无耻,

她说,‘我要跟随我的情人,

他们给我食物和水、羊毛和麻布、油和酒。’

6因此,我要用荆棘围堵她,

筑墙阻断她的去路。

7她要追随情人,却追不上;

寻找情人,却找不到。

于是,她说,‘我倒不如回到丈夫身边,

我从前的光景比现在还好。’

8她不知道是我给她五谷、新酒和油,

又赐给她大量金银——

她却用这些供奉巴力

9因此,到了收割和酿酒的季节,

我要收走我的五谷和新酒,

夺回我给她遮体的羊毛和麻布。

10我要当着她情人的面剥光她的衣服,

显出她的淫态,

无人能从我手中把她救出去。

11我要终止她一切的欢庆,

终止她的年节、朔日2:11 朔日”即每月初一。、安息日及其他节期。

12她说她的葡萄树和无花果树是情人给她的报酬,

我要摧毁它们,

使它们变为荒林,

被野兽吞吃。

13我要惩罚她,

因为她在节日向巴力烧香。

那时她戴耳环佩首饰,

追逐她的情人,把我忘记。

这是耶和华说的。

对不贞之妇的爱

14“然而,我要挽回她,

领她到旷野,

柔声安慰她。

15我要把葡萄园赐给她,

使灾祸之谷2:15 灾祸之谷”希伯来文是“亚割谷”,“亚割”意思是“灾祸”。参见约书亚记第七章。成为希望之门。

她要在那里快乐地歌唱,

如在妙龄时的日子,

如从埃及出来之时。”

16耶和华说:

“那时,你要称我为丈夫,

不再称我为主人2:16 此处的“主人”希伯来文是“巴力”。“巴力”意思是“主人或丈夫”,也是迦南人神明的名字。

17我要从你口中除掉巴力的名字,

再也不让你提起。

18那时,我要跟田间的走兽、空中的飞鸟及地上的爬虫立约,

使它们不再伤害你。

我要在你境内毁灭战弓和刀剑,止息战事,

使你安居乐业。

19我要聘你永远做我的妻,

以仁义、正直、慈爱、怜悯聘你。

20我要以信实聘你为妻,

这样你必认识耶和华。”

21耶和华说:

“那时,我要应允,

我要应允天的祈求,

天要应允地的祈求,

22地要应允五谷、新酒和油的祈求,

五谷、新酒和油要应允耶斯列的祈求。

23我要把你栽种在这片土地上,归我所有。

我要怜悯那不蒙怜悯的人,

对那不是我子民的人说,‘你是我的子民。’

他们也要对我说,‘你是我的上帝。’”