Hoseya 2 – CCL & NASV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Hoseya 2:1-23

1“Nena kwa abale ako kuti, ‘Ndinu anthu anga,’ kwa alongo ako kuti ‘Ndinu okondedwa anga.’ ”

Kulangidwa ndi Kubwezeretsedwa kwa Israeli

2“Dzudzulani amayi anu, adzudzuleni iwo,

pakuti si mkazi wanga,

ndipo ine sindine mwamuna wake.

Iyeyo achotse maonekedwe adama pa nkhope yake,

ndi kusakhulupirika pa mawere ake.

3Akapanda kutero ndidzamuvula,

ndipo adzakhala wamaliseche monga tsiku limene anabadwa;

ndidzamuwumitsa ngati chipululu,

adzakhala ngati dziko lopanda madzi,

ndi kumupha ndi ludzu.

4Sindidzaonetsa chikondi changa pa ana ake,

chifukwa ndi ana a mʼchiwerewere.

5Amayi awo akhala akuchita zachiwerewere

ndipo anawabereka anawo akuchita zinthu zochititsa manyazi.

Iwo anati, ‘Ine ndidzatsatira zibwenzi zanga,

zimene zimandipatsa chakudya ndi madzi,

ubweya ndi thonje, mafuta ndi chakumwa.’

6Choncho njira yake ndidzayitseka ndi minga;

ndidzamuzinga ndi khoma kotero kuti sadzapezanso njira yotulukira.

7Adzathamangira zibwenzi zake koma sadzazipeza;

adzazifunafuna koma sadzazipeza.

Pamenepo iye adzati,

‘Ndibwerera kwa mwamuna wanga woyamba uja,

pakuti ndinali pabwino ndi iyeyo kusiyanitsa ndi pano.’

8Iye sanazindikire kuti ndine amene

ndinkamupatsa tirigu, vinyo watsopano ndi mafuta.

Ndine amene ndinkamukhuthulira siliva ndi golide,

zimene ankapangira mafano a Baala.

9“Choncho Ine ndidzamulanda tirigu wanga pa nthawi yokolola,

ndi vinyo wanga watsopano pa nthawi yopsinya mphesa.

Ndidzamulanda ubweya ndi thonje langa,

zomwe akanaphimba nazo umaliseche wake.

10Motero tsopano ndidzaonetsa maliseche ake

pamaso pa zibwenzi zake;

palibe ndi mmodzi yemwe adzamupulumutse mʼmanja mwanga.

11Ndidzathetsa zikondwerero zake zonse:

zikondwerero zake za chaka ndi chaka, za mwezi watsopano,

za pa masiku a Sabata ndi maphwando ake onse a pa masiku okhazikitsidwa.

12Ndidzawononga mitengo yake ya mpesa ndi mitengo yake yamkuyu,

imene iye ankanena kuti inali malipiro ake ochokera kwa zibwenzi zake.

Ndidzayisandutsa chithukuluzi,

ndipo zirombo zakuthengo zidzadya zipatsozo.

13Ndidzamulanga chifukwa cha masiku

amene anafukiza lubani kwa Abaala;

anadzikongoletsa povala mphete ndi mikanda yamtengowapatali

ndipo anathamangira zibwenzi zake,

koma Ine anandiyiwala,”

akutero Yehova.

14“Koma tsopano ndidzamukopa mkaziyo;

ndidzapita naye ku chipululu

ndipo ndidzamuyankhula mwachikondi.

15Kumeneko ndidzamubwezera minda yake ya mpesa,

ndipo ndidzasandutsa Chigwa cha Akori kukhala khomo la chiyembekezo.

Kumeneko iye adzayimba nyimbo monga mʼmasiku a ubwana wake,

monga tsiku limene anatuluka ku Igupto.

16“Tsiku limeneli,” Yehova akuti,

“udzandiyitana kuti, ‘Amuna anga;’

sudzandiyitananso kuti, ‘Mbuye wanga.’

17Ndidzachotsa mayina a Abaala pakamwa pake;

sadzatchulanso mayina awo popemphera.

18Tsiku limenelo ndidzachita pangano

ndi zirombo zakuthengo ndi mbalame zamumlengalenga

ndiponso zolengedwa zokwawa pansi kuti ziyanjane ndi anthu anga.

Ndidzachotsa mʼdzikomo uta,

lupanga ndi zida zonse zankhondo,

kuti onse apumule mwamtendere.

19Ndidzakutomera kuti ukhale mkazi wanga mpaka muyaya;

ndidzakutomera mwachilungamo, mwaungwiro,

mwachikondi ndi mwachifundo.

20Ndidzakutomera mokhulupirika

ndipo udzadziwa Yehova.

21“Tsiku limenelo Ine ndidzayankha,”

akutero Yehova.

“Ndidzayankha mlengalenga pempho lake lofuna mitambo

ndipo mvula idzagwa pa dziko lapansi;

22ndipo nthaka idzamvera kupempha kwa tirigu,

vinyo ndi mafuta,

ndipo zidzamvera Yezireeli.

23Ndidzadzala Israeli mʼdziko kuti akhale wanga:

ndidzaonetsa chikondi changa kwa anthu amene ndinkawatchula dzina loti, ‘Sakondedwa.’

Ndidzawawuza amene ndinkawatchula dzina loti, ‘Si anthu anga,’ kuti, ‘Ndinu anthu wanga;’

ndipo adzanena kuti, ‘ndinu Mulungu wathu,’ ”

New Amharic Standard Version

ሆሴዕ 2:1-23

1“ወንድሞቻችሁን ‘ሕዝቤ’፣ እኅቶቻችሁንም ‘ተወዳጆቼ’ ብላችሁ ጥሯቸው።

የእስራኤል መቀጣትና መመለስ

2“እናታችሁን ምከሯት፤ ምከሯት፤

እርሷ ሚስቴ አይደለችም፤

እኔም ባሏ አይደለሁምና።

ከፊቷ የዘማዊነት አስተያየትን፣

ከጡቶቿም መካከል ምንዝርናዋን ታስወግድ።

3አለዚያ ገፍፌ ዕርቃኗን አስቀራታለሁ፤

እንደ ተወለደችበትም ቀን አደርጋታለሁ፤

እንደ ምድረ በዳ፣

እንደ ደረቅም ምድር አደርጋታለሁ፤

በውሃ ጥምም እገድላታለሁ።

4ለልጆቿ አልራራላቸውም፤

የምንዝርና ልጆች ናቸውና።

5እናታቸው አመንዝራ ነች፤

በውርደትም ፀንሳቸዋለች፤

እርሷም፣ ‘እንጀራዬንና ውሃዬን ይሰጡኛል፤

ሱፌንና የሐር ልብሴን፣ ዘይቴንና መጠጤን ይሰጡኛል፤

ስለዚህ ውሽሞቼን ተከትዬ እሄዳለሁ’ አለች።

6በዚህ ምክንያት መንገዷን በእሾኽ እዘጋለሁ፤

መውጫ መንገድ እንዳታገኝም ዙሪያዋን በግንብ ዐጥራለሁ።

7ውሽሞቿን ተከትላ ትሄዳለች፤ ነገር ግን አትደርስባቸውም፤

ትፈልጋቸዋለች፤ ሆኖም አታገኛቸውም።

ከዚያም እንዲህ ትላለች፤

‘ወደ ቀድሞ ባሌ እመለሳለሁ፤

የፊተኛው ኑሮዬ ከአሁኑ ይሻለኛልና።’

8እርሷም እህል፣ ዘይትና አዲስ የወይን ጠጅ የሰጠኋት፣

ለበኣል አምልኮ ያደረጉትን፣

ብርንና ወርቅን ያበዛሁላት፣

እኔ እንደ ሆንሁ አላወቀችም።

9“ስለዚህ እህሌን በመከር ጊዜ፣

አዲሱም የወይን ጠጅ በደረሰ ጊዜ እወስዳለሁ፤

ዕርቃኗንም እንዳትሸፍንበት፣

ሱፍና የሐር ልብሴን መልሼ እወስድባታለሁ።

10አሁንም በውሽሞቿ ፊት፣

ነውሯን እገልጣለሁ፤

ከእጄም የሚያድናት የለም።

11የደስታ በዓሎቿን ሁሉ፣

የዓመት በዓሎቿንና፣ የወር መባቻዎቿን

ሰንበቶቿንና የተመረጡ በዓሎቿን ሁሉ አስቀራለሁ።

12ከውሽሞቼ የተቀበልሁት ዋጋ ነው የምትለውን

የወይን ተክሎቿንና የበለስ ዛፎቿን አጠፋለሁ፤

ጫካ አደርገዋለሁ፤

የዱር አራዊትም ይበሉታል።

13ለበኣል አማልክት ዕጣን ስላጠነችባቸው ቀናት

እቀጣታለሁ፤

በጌጣጌጥና በቀለበቶች ራሷን አስጊጣለች፤

ውሽሞቿንም ተከትላ ሄዳለች፤

እኔን ግን ረስታለች”

ይላል እግዚአብሔር

14“ስለዚህ እነሆ፤ አባብላታለሁ፤

ወደ ምድረ በዳም እወስዳታለሁ፤

በፍቅር ቃል አነጋግራታለሁ።

15በዚያም የወይን ተክሏን እመልስላታለሁ፤

የአኮርንም2፥15 አኮር ማለት ችግር ማለት ነው ሸለቆ የተስፋ በር እንዲሆናት አደርጋለሁ።

በዚያም ከግብፅ እንደ ወጣችበት ቀን፣

እንደ ልጅነቷም ጊዜ ትዘምራለች።2፥15 ወይም ትሆናለች

16“በዚያ ቀን፣ ‘ባሌ’ ብለሽ፣

ትጠሪኛለሽ” ይላል እግዚአብሔር

“ከእንግዲህም፣ ‘ጌታዬ’2፥16 ዕብራይስጡ በኣል ይላል ብለሽ አትጠሪኝም።

17የበኣል አማልክትን ስም ከአንደበቷ አስወግዳለሁ፤

ከእንግዲህም ስሞቻቸው አይነሡም።

18በዚያን ቀን ከምድር አራዊትና ከሰማይ ወፎች፣

በምድርም ላይ ከሚንቀሳቀሱ ፍጥረት ጋር፣

ቃል ኪዳን አደርግላቸዋለሁ፤

ሁሉም በሰላም እንዲኖሩ፣

ቀስትን፣ ሰይፍንና ጦርነትን፣

ከምድሪቱ አስወግዳለሁ።

19ለእኔ እንድትሆኚ ለዘላለም ዐጭሻለሁ፤

በጽድቅና በፍትሕ፣

በፍቅርና በርኅራኄም ዐጭሻለሁ።

20በታማኝነት ዐጭሻለሁ፤

አንቺም እግዚአብሔርን ታውቂያለሽ።”

21እግዚአብሔር እንዲህ ይላል፤

“በዚያ ቀን እኔ እመልሳለሁ፤

ለሰማያት እመልሳለሁ፤

እነርሱም ለምድር ምላሽ ይሰጣሉ፤

22ምድርም ለእህል፣

ለአዲስ የወይን ጠጅና ለዘይት ምላሽ ትሰጣለች፤

እነርሱም ለኢይዝራኤል2፥22 ኢይዝራኤል ማለት እግዚአብሔር ይተክላል ማለት ነው ምላሽ ይሰጣሉ።

23ስለ ራሴ ስል በምድሪቱ እተክላታለሁ፤

‘ምሕረትን ያላገኘ’2፥23 ዕብራይስጡ ሎሩሃማ ይላል ብዬ የጠራሁትንም እምረዋለሁ፤

‘ሕዝቤ አይደላችሁም’2፥23 ዕብራይስጡ ሎዓሚ ይላል ተብለው የተጠሩትንም፣ ‘ሕዝቤ’ እላቸዋለሁ፤

እነርሱም፣ ‘አንተ አምላኬ ነህ’ ይላሉ።”