Habakuku 3 – CCL & CST

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Habakuku 3:1-19

Pemphero la Habakuku

1Pemphero la mneneri Habakuku potsata mayimbidwe a Sigionoti.

2Inu Yehova, ndamva za kutchuka kwanu;

Inu Yehova, ntchito zanu zandiopsa.

Muzichitenso masiku athu ano,

masiku athu ano zidziwike;

mu ukali wanu mukumbukire kuchita chifundo.

3Mulungu anabwera kuchokera ku Temani,

Woyerayo kuchokera ku Phiri la Parani.

Sela

Ulemerero wake unaphimba mlengalenga

ndipo dziko lapansi linadzaza ndi matamando ake.

4Kuwala kwa ulemerero wake kunali ngati kutuluka kwa dzuwa;

kunyezimira kunkatuluka mʼdzanja lake,

mʼmene anabisamo mphamvu zake.

5Patsogolo pake pankagwa mliri;

nthenda yoopsa inkagwa kumbuyo kwake.

6Iye anayimirira ndi kugwedeza dziko lapansi;

anayangʼana ndipo mitundu ya anthu inanjenjemera.

Mapiri okhazikika anagumuka

ndipo zitunda zakalekale zinatitimira.

Njira zake ndi zachikhalire.

7Ndinaona matenti a ku Kusani ali pa mavuto,

mokhala a ku Midiyani muli ululu waukulu.

8Inu Yehova, kodi munakwiyira mitsinje?

Kodi munakalipira timitsinje?

Kodi munapsera mtima nyanja

pamene munakwera pa akavalo anu

ndiponso magaleta anu achipulumutso?

9Munasolola uta wanu mʼchimake,

munayitanitsa mivi yambiri.

Sela

Munagawa dziko lapansi ndi mitsinje;

10mapiri anakuonani ndipo anagwedezeka.

Madzi amphamvu anasefukira;

nyanja yozama inakokoma

ndipo mafunde ake anakwera kwambiri.

11Dzuwa ndi mwezi zinayima chilili mlengalenga,

pa kungʼanima kwa mivi yanu yowulukayo,

pa kunyezimira kwa mkondo wanu.

12Munayendayenda mʼdziko lapansi muli ndi ukali,

ndipo munapondereza mitundu ya anthu muli ndi mkwiyo.

13Munapita kukalanditsa anthu anu,

kukapulumutsa wodzozedwa wanu.

Munakantha mtsogoleri wa dziko la anthu oyipa,

munawononga anthu ake onse.

Sela

14Ndi mkondo wake womwe munalasa mtsogoleri wake

pamene ankhondo ake anabwera mwamphamvu kudzatibalalitsa,

ankasangalala ngati kuti akudzawononga

osauka amene akubisala.

15Munapondaponda pa nyanja ndi akavalo anu,

kuvundula madzi amphamvu.

16Ndinamva ndipo mtima wanga unagunda kwambiri,

milomo yanga inanjenjemera pakumva phokosolo;

mafupa anga anaguluka,

ndipo mawondo anga anawombana.

Komabe ndikuyembekezera mofatsa,

tsiku la masautso limene lidzafike pa mtundu wa anthu umene ukutithira nkhondo.

17Ngakhale mtengo wa mkuyu usachite maluwa,

ndipo mipesa ikhale yopanda mphesa.

Ngakhale mitengo ya olivi isabereke zipatso,

ndipo mʼminda musatuluke kanthu.

Ngakhale nkhosa

ndi ngʼombe zithe mʼkhola,

18komabe ine ndidzakondwera mwa Yehova,

ndidzasangalala mwa Mulungu Mpulumutsi wanga.

19Ambuye Yehova ndiye mphamvu yanga;

amalimbitsa miyendo yanga ngati ya mbawala yayikazi,

amandithandiza kukafika pamwamba pa phiri.

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Pa zoyimbira za nsambo.

Nueva Versión Internacional (Castilian)

Habacuc 3:1-19

La oración de Habacuc

1Oración del profeta Habacuc. Según sigionot.3:1 sigionot. Probablemente un término literario o musical.

2Señor, he sabido de tu fama;

tus obras, Señor, me dejan pasmado.

Realízalas de nuevo en nuestros días,

dalas a conocer en nuestro tiempo;

en tu ira, ten presente tu misericordia.

3De Temán viene Dios,

del monte de Parán viene el Santo.

Selah

Su gloria cubre el cielo

y su alabanza llena la tierra.

4Su brillantez es la del relámpago;

rayos brotan de sus manos;

¡tras ellos se esconde su poder!

5Una plaga mortal lo precede,

un fuego abrasador le sigue los pasos.

6Se detiene, y la tierra se estremece;

lanza una mirada, y las naciones tiemblan.

Se desmoronan las antiguas montañas

y se desploman las viejas colinas,

pero los caminos de Dios son eternos.

7He visto afligidos los campamentos de Cusán,

y angustiadas las moradas de Madián.

8¿Te enojaste, oh Señor, con los ríos?

¿Estuviste airado contra las corrientes?

¿Tan enfurecido estabas contra el mar

que cabalgaste en tus caballos

y montaste en tus carros victoriosos?

9Descubriste tu arco,

llenaste de flechas tu aljaba.3:9 llenaste de flechas tu aljaba (mss. de LXX); en TM, texto de difícil traducción. Selah

Tus ríos surcan la tierra;

10las montañas te ven y se retuercen.

Pasan los torrentes de agua,

y ruge el abismo, levantando sus manos.

11El sol y la luna se detienen en el cielo

por el fulgor de tus veloces flechas,

por el deslumbrante brillo de tu lanza.

12Indignado, marchas sobre la tierra;

lleno de ira, trillas las naciones.

13Saliste a liberar a tu pueblo,

saliste a salvar a tu ungido.

Aplastaste al rey de la perversa dinastía,

¡lo desnudaste de pies a cabeza! Selah

14Con tu lanza les partiste la cabeza a sus guerreros,

que enfurecidos querían dispersarme,

que con placer arrogante se lanzaron contra mí,

como quien se lanza contra un pobre indefenso.3:14 Versículo de difícil traducción.

15Pisoteaste el mar con tus corceles,

agitando las inmensas aguas.

16Al oírlo, se estremecieron mis entrañas;

a su voz, me temblaron los labios;

la carcoma me caló en los huesos,

y se me aflojaron las piernas.

Pero yo espero con paciencia

el día en que la calamidad

vendrá sobre la nación que nos invade.

17Aunque la higuera no florezca,

ni haya frutos en las vides;

aunque falle la cosecha del olivo,

y los campos no produzcan alimentos;

aunque en el aprisco no haya ovejas,

ni ganado alguno en los establos;

18aun así, yo me regocijaré en el Señor,

¡me alegraré en Dios, mi libertador!

19El Señor omnipotente es mi fuerza;

da a mis pies la ligereza de una gacela

y me hace caminar por las alturas.

Al director musical. Sobre instrumentos de cuerda.