Genesis 47 – CCL & CARST

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Genesis 47:1-31

1Yosefe anapita kukamuwuza Farao kuti, “Abambo anga, abale anga pamodzi ndi nkhosa, ngʼombe zawo, ndi antchito awo abwera kuchokera ku dziko la Kanaani ndipo tsopano ali ku Goseni.” 2Iye anapita kwa Farao kuja ndi abale ake asanu, kukawaonetsa.

3Farao anafunsa abale akewo kuti, “Mumagwira ntchito yanji?”

Iwo anamuyankha kuti, “Ife, bwana ndife oweta ziweto, monga ankachitira makolo athu. 4Ife tabwera kudzakhala kuno kwa kanthawi chifukwa njala yafika poopsa ku Kanaani motero kuti kulibe msipu wodyetsera ziweto. Ndiye bwana tiloleni kuti tikhale ku Goseni.”

5Farao anati kwa Yosefe, “Abambo ako ndi abale ako abwera kwa iwe. 6Dziko lonse la Igupto lili mʼdzanja lako. Uwakhazike abambo ako ndi abale ako mʼmalo achonde kwambiri. Akhale ku Goseni. Ndipo ngati ukudziwapo ena mwa iwo amene ali akatswiri pa kuweta ziweto, uwapatse udindo woyangʼanira ziweto zanga.”

7Kenaka Yosefe anapita ndi abambo ake kwa Farao kukawaonetsa, ndipo Yakobo anadalitsa Faraoyo. 8Atatero, Farao anafunsa Yakobo kuti, “Muli ndi zaka zingati?”

9Yakobo anayankha kuti, “Zaka za maulendo anga zakwana 130. Zaka za moyo wanga ndi zowerengeka, komanso zakhala zaka za masautso. Zaka za moyo wanga sizingafanane ndi zaka za moyo wa makolo anga.” 10Atatha kumudalitsa Farao uja, Yakobo anatsanzika nʼkunyamuka.

11Choncho Yosefe anakhazika abambo ake aja ndi abale ake mʼdziko la Igupto. Iye anawapatsa dera la Ramesesi limene linali dziko lachonde kwambiri monga analamulira Farao. 12Yosefe anaperekanso chakudya kwa abambo ake, kwa abale ake ndi kwa onse a mʼnyumba ya abambo ake monga mwa chiwerengero cha ana awo.

Yosefe pa Nthawi ya Njala

13Njala inakula kwambiri motero kuti chakudya chinasowa mʼdziko lonse. Anthu a ku Igupto ndi ku Kanaani analefuka nayo njalayo. 14Yosefe anasonkhanitsa ndalama zonse zimene anthu a mu Igupto ndi Kanaani ankapereka pogula tirigu, ndipo anabwera nazo ku nyumba kwa Farao. 15Anthu a ku Igupto ndi Kanaani ndalama zitawathera, Aigupto onse anabwera kwa Yosefe nati, “Tipatseni chakudya. Nanga tiferenji pamaso panu? Ndalama zathu zatha.”

16Ndipo Yosefe anawayankha kuti, “Bwerani ndi ziweto zanu ndipo tidzasinthana ndi chakudya poti mukuti ndalama zanu zatha.” 17Choncho anthu anabwera ndi ziweto zawo monga akavalo, nkhosa, mbuzi, ngʼombe ndi abulu ndipo Yosefe anawapatsa zakudya.

18Chitatha chaka chimenecho, anthu anapitanso kwa Yosefe chaka chinacho nati, “Ife sitingakubisireni mbuye wathu kuti ndalama zathu zatithera ndipo ziweto zathu zili ndi inu, palibenso choti nʼkukupatsani mbuye wathu kupatula matupi athu ndi dziko lathu. 19Tiferenji ife ndi dziko lathu inu mukuona? Mutipatse chakudya ndipo tidzigulitsa ife ndi minda yathu yomwe. Ife tidzakhala akapolo a Farao. Tipatseni mbewuzo kuti tikhale ndi moyo tisafe ndipo dziko lisachite bwinja.”

20Choncho Yosefe anamugulira Farao dziko lonse la Igupto. Aliyense mu Igupto anagulitsa munda wake chifukwa njala inakula kwambiri. Dziko lonse linasanduka la Farao, 21ndipo Yosefe anawasandutsa anthu onse kukhala akapolo a Farao, kuchokera ku malire a mbali ina ya Igupto kukafika ku malire a mbali ina ya dzikolo. 22Komabe, sanagule minda ya ansembe chifukwa Farao ankawapatsa thandizo lokwanira. Nʼchifukwa chake sanagulitse minda yawo.

23Yosefe anati kwa anthuwo, “Tsono poti ndakugulani inu ndi minda yanu, kugulira Farao. Nayi mbewu kuti mudzale mʼminda yanu. 24Koma podzakolola, mudzapereka gawo limodzi la magawo asanu aliwonse kwa Farao. Magawo anayi enawo adzakhala anu. Zina mudzasunge mbewu ndi zina mudzadye inuyo, mabanja anu ndi ana anu.”

25Iwo anati, “Mwatipulumutsa potichitira zabwinozi, mbuye wathu, tsono tidzakhala akapolo a Farao.”

26Choncho Yosefe anakhazikitsa lamulo limene lilipobe mpaka lero mʼdziko lonse la Igupto kuti limodzi la magawo asanu a zokolola ndi la Farao. Ndi minda ya ansembe yokha imene sinatengedwe kukhala ya Farao.

27Tsono Aisraeli anakhazikika mʼdziko la Igupto ku chigawo cha Goseni. Kumeneko anapeza chuma ndipo anaberekana nachuluka kwambiri.

28Yakobo anakhala ku Igupto zaka 17 ndipo zaka za moyo wake zinali 147. 29Nthawi itayandikira yoti Israeli amwalire, anayitanitsa mwana wake Yosefe nati kwa iye, “Ngati ukundikondadi monga abambo ako, ika dzanja lako pansi pa ntchafu yanga ndipo ulonjeze kuti udzaonetsa kukoma mtima ndi kukhulupirika kwako kwa ine kuti sudzayika mtembo wanga kuno ku Igupto. 30Ine ndikagona pamodzi ndi makolo anga. Choncho ndikadzamwalira udzanditulutse mu Igupto muno ndipo ukayike mtembo wanga kumene anayikidwa makolo anga.”

Yosefe anati, “Ndidzachita monga mwanenera.”

31Yakobo anati, “Lumbira kwa ine.” Yosefe analumbira kwa iye, ndipo Israeli anapembedza Mulungu atatsamira ndodo yake.

Священное Писание (Восточный перевод), версия для Таджикистана

Начало 47:1-31

Встреча фараона с семьёй Юсуфа

1Юсуф пошёл к фараону и сказал ему:

– Мой отец и братья со своими стадами крупного и мелкого скота и всем имуществом пришли из земли Ханона и сейчас находятся в Гошене.

2Он выбрал пятерых из своих братьев и представил их фараону.

3Фараон спросил братьев:

– Чем вы занимаетесь?

Они ответили фараону:

– Твои рабы – пастухи, как и наши отцы, – 4ещё они сказали: – Мы пришли сюда жить, потому что в земле Ханона жестокий голод и твоим рабам негде пасти свои отары. Поэтому позволь твоим рабам поселиться в Гошене.

5Фараон сказал Юсуфу:

– Твой отец и братья пришли к тебе. 6Земля Египта – перед тобой; посели отца и братьев в лучшей части этой земли. Пусть живут в Гошене. А если ты знаешь среди них способных к тому людей, поставь их смотреть за моим собственным скотом.

7Юсуф привёл своего отца Якуба и представил его фараону, и Якуб благословил47:7 Или: «приветствовал». фараона. 8Фараон спросил его:

– Сколько тебе лет?

9Якуб ответил фараону:

– Я прожил на свете сто тридцать лет. Жизнь моя была короткой и трудной, и я не достиг возраста моих отцов.

10Якуб благословил фараона47:10 Или: «простился с фараоном». и покинул его дворец.

11Юсуф поселил отца и братьев в Египте и дал им в собственность лучшую часть земли в округе Раамсес, как повелел фараон. 12Юсуф обеспечил едой отца, и братьев, и весь свой род, дав каждому по числу членов его семьи.

Юсуф управляет Египтом во время голода

13Потом нигде не стало еды, потому что был жестокий голод; и Египет, и Ханон были истощены от голода. 14Юсуф собрал все деньги, какие только были в Египте и Ханоне, в уплату за зерно, которое у него покупали; он хранил их во дворце фараона. 15Когда кончились деньги и в Египте, и в Ханоне, все египтяне пришли к Юсуфу и сказали:

– Дай нам хлеба; зачем нам умирать у тебя на глазах? Наши деньги кончились.

16Юсуф сказал:

– Приведите свой скот, а я дам вам хлеба в обмен на него, раз у вас кончились деньги.

17Они привели к Юсуфу скот, и он дал им хлеба в обмен на лошадей, овец и коз, быков, коров и ослов. Он кормил их хлебом в тот год, в обмен на весь их скот.

18Когда год прошёл, они пришли к нему и сказали:

– Мы не станем таить от нашего господина, что наши деньги кончились и наш скот принадлежит тебе, так что у нас ничего не осталось для нашего господина, кроме наших тел и нашей земли. 19Зачем нам гибнуть у тебя на глазах, и нам самим, и нашей земле? Купи нас и нашу землю в обмен на хлеб, а мы с нашей землёй будем в рабстве у фараона; и дай нам семян, чтобы нам остаться в живых, и чтобы эта земля не опустела.

20Так Юсуф купил всю землю в Египте для фараона. Египтяне продали каждый своё поле, потому что голод одолел их, и земля стала собственностью фараона, 21а народ Юсуф сделал рабами, от одного конца Египта до другого. 22Он не купил только землю жрецов, потому что они получали постоянную долю от фараона, и этой доли, которую дал им фараон, им хватало на пропитание; вот почему они не продали свою землю.

23Юсуф сказал народу:

– Теперь, когда я купил вас и вашу землю для фараона, вот вам семена, чтобы засеять землю. 24Когда поспеет урожай, отдайте одну пятую от него фараону, а остальные четыре пятых будут вам на семена для полей и на пропитание для вас самих, для ваших домашних и для детей.

25Они сказали:

– Ты спас нам жизнь. Да найдём мы расположение в глазах нашего господина: мы будем рабами фараона.

26Так Юсуф установил в Египте закон о земле, который и сегодня в силе: одна пятая всего урожая принадлежит фараону, кроме урожая с земель жрецов, которая не стала собственностью фараона.

Последнее желание Якуба

27Исроильтяне жили в Египте в области Гошен; они приобрели там собственность и были плодовиты; число их возрастало.

28Якуб прожил в Египте семнадцать лет, так что всего он жил сто сорок семь лет. 29Когда пришло ему время умирать, он позвал своего сына Юсуфа и сказал ему:

– Если я нашёл расположение в твоих глазах, положи руку мне под бедро47:29 Таков был обычай принесения торжественной клятвы (см. 24:2). и обещай, что явишь мне милость и верность. Не хорони меня в Египте, 30но когда я сойду к моим отцам, вынеси меня из Египта и похорони там, где похоронены они.

Юсуф ответил:

– Я сделаю так, как ты говоришь.

31– Поклянись, – сказал он.

Юсуф поклялся ему, и Исроил поклонился, оперевшись на свой посох47:31 Или: «Исроил склонился на изголовье своей постели»..