Genesis 46 – CCL & CARST

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Genesis 46:1-34

Yakobo Apita ku Igupto

1Israeli anasonkhanitsa zonse anali nazo napita ku Beeriseba kukapereka nsembe kwa Mulungu wa abambo ake Isake.

2Ndipo Mulungu anayankhula ndi Israeli mʼmasomphenya usiku nati, “Yakobo! Yakobo!”

Iye anayankha, “Ee, Ambuye.”

3Mulungu anati, “Ine ndine Mulungu. Mulungu wa abambo ako. Usachite mantha kupita ku Igupto, pakuti ndidzachulukitsa zidzukulu zako kumeneko moti zidzakhala mtundu waukulu. 4Ine ndidzapita ku Igupto pamodzi ndi iwe ndipo mosakayika konse zidzukulu zako ndidzazibweretsa konkuno. Yosefe adzakhalapo pa nthawi yako yomwalira.”

5Yakobo anachoka ku Beeriseba, ndipo ana ake anakweza abambo awo, ana awo, pamodzi ndi akazi awo pa ngolo zimene Farao anatumiza kuti adzakwerepo. 6Iwo anatenganso ziweto zawo ndi katundu wawo amene anali naye ku Kanaani, ndipo Yakobo pamodzi ndi ana ndi zidzukulu zake anapita ku Igupto. 7Ndiye kuti popita ku Igupto Yakobo anatenga ana aamuna, zidzukulu zazimuna, ana aakazi ndi zidzukulu zazikazi.

8Nawa ana a Israeli (ndiye kuti Yakobo ndi ana ake) amene anapita ku Igupto:

Rubeni mwana woyamba wa Yakobo.

9Ana aamuna a Rubeni ndi awa:

Hanoki, Palu, Hezironi ndi Karimi.

10Ana aamuna a Simeoni ndi awa:

Yemueli, Yamini, Ohadi, Yakini, Zohari ndi Shaulo amene mayi wake anali wa ku Kanaani.

11Ana aamuna a Levi ndi awa:

Geresoni, Kohati ndi Merari.

12Ana aamuna a Yuda ndi awa:

Eri, Onani, Sela, Perezi ndi Zera. Koma Eri ndi Onani anamwalira mʼdziko la Kanaani.

Ana a Perezi anali

Hezironi ndi Hamuli.

13Ana aamuna a Isakara ndi awa:

Tola, Puwa, Yobi ndi Simironi.

14Ana aamuna a Zebuloni ndi awa:

Seredi, Eloni ndi Yahaleeli.

15Amenewa ndi ana aamuna a Leya amene anamubalira Yakobo ku Padanaramu. Panali mwana wamkazi dzina lake Dina. Ana onse analipo 33.

16Ana aamuna a Gadi ndi awa:

Zifioni, Hagi, Suni, Eziboni, Eri, Arodi ndi Areli.

17Ana aamuna a Aseri ndi awa:

Imuna, Isiva, Isivi, Beriya

ndi Sera mlongo wawo.

Ana aamuna a Beriya ndi awa:

Heberi ndi Malikieli.

18Amenewa ndi zidzukulu za Yakobo mwa Zilipa amene Labani anapereka kwa mwana wake, Leya. Onse pamodzi analipo 16.

19Ana aamuna a Rakele mkazi wa Yakobo anali:

Yosefe ndi Benjamini. 20Ku Igupto, Asenati mwana wa Potifara wansembe wa Oni, anamuberekera Yosefe ana awa: Manase ndi Efereimu.

21Ana aamuna a Benjamini ndi awa:

Bela, Bekeri, Asibeli, Gera, Naamani, Ehi, Rosi, Mupimu, Hupimu ndi Aridi.

22Amenewa ndi zidzukulu za Yakobo mwa mkazi wake Rakele. Onse analipo khumi ndi anayi.

23Mwana wa mwamuna wa Dani anali:

Husimu.

24Ana aamuna a Nafutali ndi awa:

Yahazeeli, Guni, Yezeri ndi Silemu.

25Amenewa ndi zidzukulu za Yakobo mwa Biliha amene Labani anapereka kwa mwana wake Rakele. Onse pamodzi analipo asanu ndi awiri.

26Onse amene anapita ndi Yakobo (iwo amene anali akeake, osawerengera akazi a ana ake), analipo 66. 27Pophatikiza ana awiri a Yosefe obadwira ku Igupto, anthu a pa banja la Yakobo amene anapita ku Igupto, onse pamodzi analipo 70.

28Tsopano Yakobo anatumiza Yuda kwa Yosefe kukamupempha kuti akakumane naye ku Goseni. Iwo atafika ku chigawo cha Goseni, 29Yosefe anakonza galeta nakwerapo ndi kupita ku Goseni kukakumana ndi abambo ake, Israeli. Yosefe atangofika pamaso pa abambo ake, anawakumbatira nalira kwa nthawi yayitali.

30Israeli anati kwa Yosefe, “Tsopano ndikhoza kumwalira poti ndaona nkhope yako kuti ukanali ndi moyo.”

31Ndipo Yosefe anati kwa abale ake pamodzi ndi a pa banja la abambo ake, “Ndipita kwa Farao ndipo ndikamuwuza kuti, ‘Abale anga pamodzi ndi onse a mʼnyumba ya abambo anga amene amakhala mʼdziko la Kanaani abwera kuno kwa ine. 32Anthuwa ndi abusa; amaweta ziweto zawo ndipo abwera ndi nkhosa ndi ngʼombe zawo, pamodzi ndi antchito awo.’ 33Tsono Farao akakuyitanani nakufunsani kuti, ‘Kodi mumagwira ntchito yanji?’ 34Muyankhe kuti, ‘Ife, bwana ndife oweta ziweto kuyambira ubwana wathu mpaka tsopano. Takhala tikuweta ziweto monga mmene ankachitira makolo athu.’ Mukadzayankha choncho, ndiye kuti mudzakhala mʼdziko la Goseni chifukwa anthu a ku Igupto amanyansidwa nawo anthu oweta ziweto.”

Священное Писание (Восточный перевод), версия для Таджикистана

Начало 46:1-34

Якуб со всей семьёй переселяется в Египет

1Исроил отправился в путь со всем, что у него было, пришёл в Беэр-Шеву и принёс там жертвы Богу своего отца Исхока. 2Всевышний говорил с Исроилом в ночном видении и сказал:

– Якуб! Якуб!

– Вот я, – ответил Якуб.

3И сказал Всевышний:

– Я Всевышний, Бог твоего отца. Не бойся пойти в Египет, потому что Я произведу от тебя там великий народ. 4Я пойду в Египет вместе с тобой, и Я же приведу тебя обратно. И глаза тебе закроет рука Юсуфа.

5Якуб отправился в путь из Беэр-Шевы. Сыновья Исроила посадили отца, детей и жён в колесницы, которые фараон прислал, чтобы перевезти его. 6Они взяли с собой скот и имущество, которое нажили в Ханоне; и Якуб со всем своим потомством пришёл в Египет. 7Он взял с собой в Египет сыновей и внуков, дочерей и внучек – всё своё потомство.

Список потомков Якуба

8Вот имена сыновей Исроила, которые пришли в Египет; Якуб и его потомки:

Рувим, первенец Якуба.

9Сыновья Рувима:

Ханох, Фаллу, Хецрон и Харми.

10Сыновья Шимона:

Иемуил, Иамин, Охад, Иахин, Цохар и Шаул, сын ханонеянки.

11Сыновья Леви:

Гершон, Кааф и Мерари.

12Сыновья Иуды:

Ир, Онан, Шела, Фарец и Зерах (но Ир и Онан умерли в Ханоне).

Сыновьями Фареца были Хецрон и Хамул.

13Сыновья Иссокора:

Тола, Пуа, Иашув46:13 Букв.: «Иов»; в Книге Пророков, 1 Лет. 7:1 он назван Иашувом. и Шимрон.

14Сыновья Завулона:

Серед, Елон и Иахлеил.

15Это сыновья Лии, которых она родила Якубу в Паддан-Араме; она родила и дочь Дину; всего их было тридцать три человека.

16Сыновья Гада:

Цефон, Хагги, Шуни, Эцбон, Ери, Ароди и Арели.

17Сыновья Ошера:

Имна, Ишва, Ишви и Брия. Их сестра Серах. Сыновья Брии: Хевер и Малкиил.

18Это дети, рождённые Якубу Зелфой, которую Лобон дал в служанки своей дочери Лии; всего шестнадцать человек.

19Сыновья жены Якуба Рахили:

Юсуф и Вениамин. 20В Египте Асенефа, дочь Потифера, жреца города Она, родила Юсуфу Манассу и Ефраима.

21Сыновья Вениамина:

Бела, Бехер, Ашбел, Гера, Нааман, Ехи, Рош, Муппим, Хуппим и Ард.

22Это сыновья Рахили, которых она родила Якубу; всего четырнадцать человек.

23Сын Дона:

Хушим.

24Сыновья Неффалима:

Иахцеил, Гуни, Иецер и Шиллем.

25Это сыновья, рождённые Якубу Билхой, которую Лобон дал в служанки своей дочери Рахиле; всего семь человек.

26Всех, кто пришёл в Египет с Якубом, – его прямых потомков, не считая жён его сыновей, – было шестьдесят шесть человек. 27Сыновей Юсуфа, которые были рождены ему в Египте, было двое. Всего членов семьи Якуба, пришедших в Египет, было семьдесят человек.

Встреча Якуба с Юсуфом

28Якуб послал перед собой к Юсуфу Иуду, чтобы узнать путь в Гошен. И они прибыли туда. 29Юсуф запряг колесницу и поехал в Гошен, чтобы встретить своего отца Исроила. Он предстал перед отцом, обнял его и долго плакал.

30Исроил сказал Юсуфу:

– Теперь я могу и умереть, потому что увидел своими глазами, что ты жив.

31Юсуф сказал своим братьям и домашним отца:

– Я пойду к фараону и скажу ему: «Мои братья и дом моего отца, которые жили в земле Ханона, пришли ко мне. 32Эти люди – пастухи; они разводят скот и привели с собой свои стада и принесли всё своё имущество». 33Когда фараон вызовет вас и спросит: «Чем вы занимаетесь?» – 34вы должны ответить: «Рабы твои с отрочества своего и доныне разводят скот, как делали и наши отцы». Тогда вам будет позволено поселиться в земле Гошен, потому что египтянам отвратительны пастухи.