Genesis 4 – CCL & KJV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Genesis 4:1-26

Kaini ndi Abele

1Adamu anagona malo amodzi ndi Hava mkazi wake ndipo mkaziyo anakhala woyembekezera nabala Kaini, ndipo anati, “Ndi thandizo la Yehova ndapeza mwana wamwamuna.” 2Kenaka anabereka mʼbale wake Abele.

Abele anali woweta nkhosa ndipo Kaini anali mlimi. 3Patapita nthawi, Kaini anatenga zipatso za ku munda nakazipereka kwa Yehova monga nsembe. 4Nayenso Abele anatenga ana ankhosa oyamba kubadwa pamodzi ndi mafuta ake nakazipereka ngati nsembe kwa Yehova. Yehova anakondwera ndi Abele ndi nsembe yake. 5Koma sanakondwere ndi Kaini ndi nsembe yake. Kotero Kaini anakwiya kwambiri ndipo nkhope yake inagwa.

6Choncho Yehova anati kwa Kaini, “Chifukwa chiyani wakwiya ndipo bwanji nkhope yako yagwa? 7Ukanachita zabwino sindikanakulandira kodi? Koma tsopano wachita zoyipa ndipo tchimo likukudikira pa khomo pako, likufuna kukugwira; koma iwe uyenera kugonjetsa tchimolo.”

8Tsiku lina Kaini anati kwa mʼbale wake Abele, “Tiye tipite ku munda.” Ndipo ali ku mundako, Kaini anawukira mʼbale wake namupha.

9Ndipo Yehova anamufunsa Kaini kuti, “Ali kuti mʼbale wako Abele?”

Iye anayankha kuti, “Sindikudziwa. Kodi ine ndine wosunga mʼbale wanga?”

10Yehova anati, “Kodi wachita chiyani? Tamvera! Magazi a mʼbale wako akulirira kwa Ine kuchokera mʼnthaka. 11Ndipo tsopano ndiwe wotembereredwa ndipo wachotsedwa mʼdziko limene nthaka yake inatsekula pakamwa pake kulandira magazi a mʼbale wako amene unakhetsa. 12Udzalima munda koma nthakayo sidzakupatsanso zokolola zake. Udzakhala wosakhazikika; womangoyendayenda pa dziko lapansi.”

13Kaini anati kwa Yehova, “Chilango changa ndi chachikulu kuposera mphamvu zanga. 14Lero mukundipirikitsa pa dziko ndi pamaso panu; ndidzakhala wosakhazikika, woyendayenda, ndipo aliyense amene adzandipeze adzandipha.”

15Koma Yehova anamuwuza kuti, “Sizidzatero ayi; aliyense amene adzaphe Kaini adzalangidwa ndi kulipiritsidwa kasanu ndi kawiri.” Pamenepo Yehova anayika chizindikiro pa Kaini kuti aliyense womupeza asamuphe. 16Ndipo Kaini anachoka pamaso pa Yehova nakakhala ku dziko la Nodi, kummawa kwa Edeni.

Banja la Kaini

17Kaini anagona malo amodzi ndi mkazi wake ndipo mkaziyo anakhala woyembekezera nabala Enoki. Kaini nthawi imeneyo nʼkuti akumanga mzinda ndipo anawutcha dzina la mwana wake Enoki. 18Enoki anabereka Iradi; Iradi anabereka Mehuyaeli, ndipo Mehuyaeli anabereka Metusela, ndipo Metusela anabereka Lameki.

19Lameki anakwatira akazi awiri, wina dzina lake linali Ada ndi winayo dzina lake linali Zila. 20Ada anabereka Yabala; iyeyu anali kholo la onse okhala mʼmatenti ndi oweta ziweto. 21Dzina la mʼbale wake linali Yubala; iyeyu anali kholo la onse oyimba zeze ndi chitoliro. 22Zila nayenso anali ndi mwana wamwamuna, dzina lake Tubala-Kaini. Iyeyu anali kholo la amisiri onse osula zida za mkuwa ndi chitsulo. Mlongo wake wa Tubala-Kaini anali Naama.

23Lameki anawuza akazi akewo kuti,

“Ada ndi Zila, ndimvereni;

inu akazi anga imvani mawu anga.

Ine ndinapha munthu chifukwa anandipweteka.

Ndinapha mnyamatayo chifukwa anandimenya.

24Ngati wopha Kaini amulipsira kasanu nʼkawiri,

ndiye kuti wopha ine Lameki adzamulipsira kokwanira 77.”

25Adamu anagonanso malo amodzi ndi mkazi wake, ndipo anabereka mwana wamwamuna namutcha Seti, kutanthauza kuti, “Mulungu wandipatsa mwana wina mʼmalo mwa Abele, popeza Kaini anamupha.” 26Seti naye anali ndi mwana wa mwamuna, ndipo anamutcha Enosi.

Pa nthawi imeneyi anthu anayamba kupemphera mʼdzina la Yehova.

King James Version

Genesis 4:1-26

1And Adam knew Eve his wife; and she conceived, and bare Cain, and said, I have gotten a man from the LORD.4.1 Cain: that is, Gotten, or, Acquired 2And she again bare his brother Abel. And Abel was a keeper of sheep, but Cain was a tiller of the ground.4.2 Abel: Heb. Hebel4.2 a keeper: Heb. a feeder

3And in process of time it came to pass, that Cain brought of the fruit of the ground an offering unto the LORD.4.3 in process…: Heb. at the end of days 4And Abel, he also brought of the firstlings of his flock and of the fat thereof. And the LORD had respect unto Abel and to his offering:4.4 flock: Heb. sheep, or, goats 5But unto Cain and to his offering he had not respect. And Cain was very wroth, and his countenance fell.

6And the LORD said unto Cain, Why art thou wroth? and why is thy countenance fallen? 7If thou doest well, shalt thou not be accepted? and if thou doest not well, sin lieth at the door. And unto thee shall be his desire, and thou shalt rule over him.4.7 be accepted: or, have the excellency4.7 unto…: or, subject unto thee 8And Cain talked with Abel his brother: and it came to pass, when they were in the field, that Cain rose up against Abel his brother, and slew him.

9¶ And the LORD said unto Cain, Where is Abel thy brother? And he said, I know not: Am I my brother’s keeper? 10And he said, What hast thou done? the voice of thy brother’s blood crieth unto me from the ground.4.10 blood: Heb. bloods 11And now art thou cursed from the earth, which hath opened her mouth to receive thy brother’s blood from thy hand; 12When thou tillest the ground, it shall not henceforth yield unto thee her strength; a fugitive and a vagabond shalt thou be in the earth.

13And Cain said unto the LORD, My punishment is greater than I can bear.4.13 My…: or, Mine iniquity is greater than that it may be forgiven 14Behold, thou hast driven me out this day from the face of the earth; and from thy face shall I be hid; and I shall be a fugitive and a vagabond in the earth; and it shall come to pass, that every one that findeth me shall slay me. 15And the LORD said unto him, Therefore whosoever slayeth Cain, vengeance shall be taken on him sevenfold. And the LORD set a mark upon Cain, lest any finding him should kill him.

16¶ And Cain went out from the presence of the LORD, and dwelt in the land of Nod, on the east of Eden. 17And Cain knew his wife; and she conceived, and bare Enoch: and he builded a city, and called the name of the city, after the name of his son, Enoch.4.17 Enoch: Heb. Chanoch 18And unto Enoch was born Irad: and Irad begat Mehujael: and Mehujael begat Methusael: and Methusael begat Lamech.4.18 Lamech: Heb. Lemech

19¶ And Lamech took unto him two wives: the name of the one was Adah, and the name of the other Zillah. 20And Adah bare Jabal: he was the father of such as dwell in tents, and of such as have cattle. 21And his brother’s name was Jubal: he was the father of all such as handle the harp and organ. 22And Zillah, she also bare Tubal-cain, an instructer of every artificer in brass and iron: and the sister of Tubal-cain was Naamah.4.22 instructer: Heb. whetter

23And Lamech said unto his wives, Adah and Zillah, Hear my voice; ye wives of Lamech, hearken unto my speech: for I have slain a man to my wounding, and a young man to my hurt.4.23 I have…: or, I would slay a man in my wound, etc.4.23 to my hurt: or, in my hurt 24If Cain shall be avenged sevenfold, truly Lamech seventy and sevenfold.

25¶ And Adam knew his wife again; and she bare a son, and called his name Seth: For God, said she, hath appointed me another seed instead of Abel, whom Cain slew.4.25 Seth: Heb. Sheth: that is Appointed, or, Put 26And to Seth, to him also there was born a son; and he called his name Enos: then began men to call upon the name of the LORD.4.26 Enos: Heb. Enosh4.26 to call…: or, to call themselves by the name of the Lord