Eksodo 1 – CCL & KJV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Eksodo 1:1-22

Aisraeli Azunzidwa ku Igupto

1Awa ndi mayina a ana a Israeli amene anapita ku Igupto pamodzi ndi Yakobo abambo awo, aliyense ndi banja lake: 2Rubeni, Simeoni, Levi, Yuda; 3Isakara, Zebuloni, Benjamini; 4Dani, Nafutali; Gadi ndi Aseri. 5Anthu onse obadwa mwa Yakobo analipo 70. Yosefe nʼkuti ali kale ku Igupto.

6Tsono Yosefe ndi abale ake onse ndiponso mʼbado wawo wonse anamwalira. 7Koma Aisraeli anaberekana ndi kuchuluka kwambiri nakhala amphamvu kwambiri, kotero kuti anadzaza dzikolo.

8Pambuyo pake mfumu yatsopano imene sinkamudziwa Yosefe, inayamba kulamulira dziko la Igupto. 9Iyo inati kwa anthu ake, “Taonani, Aisraeli achuluka ndipo ndi amphamvu kwambiri kuposa ife. 10Tiyeni tiwachenjerere. Tikapanda kutero adzachuluka kuposa ife, ndipo ngati kutakhala nkhondo, adzadziphatika kwa adani athu nadzamenyana nafe, kenaka nʼkudzachoka mʼdziko muno.”

11Kotero anayika akapitawo kuti aziwazunza ndi kuwagwiritsa ntchito yolemetsa mokakamiza. Iwo anamangira Farao mizinda ya Pitomu ndi Ramesesi kumene ankasungirako chakudya. 12Koma pamene ankawazunza kwambiri, Aisraeli ndiye ankachulukirachulukira mpaka kubalalikira mʼdziko lonse. Kotero Aigupto anayamba kuopa Aisraeliwo 13ndipo anawagwiritsa ntchito mwankhanza kwambiri. 14Aigupto anachititsa moyo wa Aisraeli kukhala owawa kwambiri powagwiritsa ntchito yakalavulagaga yowumba njerwa ndi kuponda dothi lomangira, pamodzi ndi ntchito zina zosiyanasiyana zamʼminda. Iwo anakakamiza Aisraeli mwankhanza kuti agwire ntchito yowawayi.

Azamba Akana Kumvera Mfumu

15Mfumu ya Igupto inati kwa azamba a Chihebri omwe mayina awo anali Sifira ndi Puwa, 16“Mukamathandiza amayi a Chihebri pa mwala wochirira, muzionetsetsa kuti akabadwa mwana wamwamuna muzipha, koma akakhala wamkazi muzimuleka akhale ndi moyo.” 17Koma azambawo ankaopa Mulungu ndipo sanachite zimene mfumu ya Igupto inawawuza kuti achite. Iwo analeka ana aamuna kuti akhale ndi moyo. 18Kenaka mfumu ya Igupto inayitanitsa azamba aja ndi kuwafunsa kuti, “Chifukwa chiyani mwachita zimenezi? Bwanji mwasiya ana aamuna kuti akhale ndi moyo?”

19Azambawo anamuyankha Farao kuti, “Amayi a Chihebri sali ngati amayi a Chiigupto; Iwo ndi amphamvu ndipo amachira azamba asanafike.”

20Kotero Mulungu anawakomera mtima azambawo, ndipo Aisraeli anapitirirabe kuchulukana nakhala amphamvu kwambiri. 21Pakuti azambawo ankaopa Mulungu, Iye anawapatsa mabanja awoawo.

22Pamenepo Farao analamulira anthu ake onse kuti, “Mwana wamwamuna aliyense akabadwa, mukamuponye mu mtsinje wa Nailo, koma wamkazi mulekeni akhale ndi moyo.”

King James Version

Exodus 1:1-22

1Now these are the names of the children of Israel, which came into Egypt; every man and his household came with Jacob. 2Reuben, Simeon, Levi, and Judah, 3Issachar, Zebulun, and Benjamin, 4Dan, and Naphtali, Gad, and Asher. 5And all the souls that came out of the loins of Jacob were seventy souls: for Joseph was in Egypt already.1.5 loins: Heb. thigh 6And Joseph died, and all his brethren, and all that generation.

7¶ And the children of Israel were fruitful, and increased abundantly, and multiplied, and waxed exceeding mighty; and the land was filled with them.

8Now there arose up a new king over Egypt, which knew not Joseph. 9And he said unto his people, Behold, the people of the children of Israel are more and mightier than we: 10Come on, let us deal wisely with them; lest they multiply, and it come to pass, that, when there falleth out any war, they join also unto our enemies, and fight against us, and so get them up out of the land. 11Therefore they did set over them taskmasters to afflict them with their burdens. And they built for Pharaoh treasure cities, Pithom and Raamses. 12But the more they afflicted them, the more they multiplied and grew. And they were grieved because of the children of Israel.1.12 But…: Heb. And as they afflicted them, so they multiplied, etc 13And the Egyptians made the children of Israel to serve with rigour: 14And they made their lives bitter with hard bondage, in morter, and in brick, and in all manner of service in the field: all their service, wherein they made them serve, was with rigour.

15¶ And the king of Egypt spake to the Hebrew midwives, of which the name of the one was Shiphrah, and the name of the other Puah: 16And he said, When ye do the office of a midwife to the Hebrew women, and see them upon the stools; if it be a son, then ye shall kill him: but if it be a daughter, then she shall live. 17But the midwives feared God, and did not as the king of Egypt commanded them, but saved the men children alive. 18And the king of Egypt called for the midwives, and said unto them, Why have ye done this thing, and have saved the men children alive? 19And the midwives said unto Pharaoh, Because the Hebrew women are not as the Egyptian women; for they are lively, and are delivered ere the midwives come in unto them. 20Therefore God dealt well with the midwives: and the people multiplied, and waxed very mighty. 21And it came to pass, because the midwives feared God, that he made them houses. 22And Pharaoh charged all his people, saying, Every son that is born ye shall cast into the river, and every daughter ye shall save alive.