Genesis 30 – CCL & CCBT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Genesis 30:1-43

1Rakele ataona kuti sakumuberekera Yakobo ana, anayamba kumuchitira nsanje mʼbale wake. Choncho anati kwa Yakobo, “Undipatse ana kapena apo ayi ndingofa!”

2Yakobo anapsera mtima Rakele ndipo nati, “Kodi ine ndalowa mʼmalo mwa Mulungu amene wakulepheretsa iwe kukhala ndi ana?”

3Pamenepo Rakele anati kwa Yakobo, “Mdzakazi wanga Biliha nayu. Lowana naye kuti mwina nʼkundibalira mwana, ndipo kudzera mwa iyeyu nanenso nʼkukhala ndi ana.”

4Ndipo anamupatsa Yakobo wantchito wake Biliha kuti alowane naye. Choncho Yakobo analowana ndi Biliha, 5ndipo Bilihayo anatenga pathupi namubalira Yakobo mwana wamwamuna. 6Pamenepo Rakele anati, “Mulungu waweruza mondikomera mtima, wamva kupempha kwanga ndipo wandipatsa mwana wa mwamuna.” Choncho anamutcha Dani.

7Biliha, wantchito wa Rakele, anatenganso pathupi nabalira Yakobo mwana wa mwamuna wachiwiri. 8Pamenepo Rakele anati, “Ndakhala ndikulimbana kwambiri ndi mʼbale wanga ndipo ndapambana.” Choncho anamutcha Nafutali.

9Pamene Leya anaona kuti waleka kubereka ana, iye anatenga wantchito wake Zilipa namupereka kwa Yakobo kuti alowane naye. 10Zilipa, wantchito wa Leya, anaberekera Yakobo mwana wamwamuna. 11Pamenepo Leya anati, “Mwayi wangawo!” Choncho anamutcha Gadi.

12Zilipa, wantchito wa Leya anamubalira Yakobo mwana wa mwamuna wachiwiri. 13Pamenepo Leya anati, “Ndakondwa bwanji! Amayi adzanditcha ine wokondwa.” Choncho anamutcha Aseri.

14Pa nthawi yokolola tirigu, Rubeni anapita ku munda ndipo anapezako zipatso za mankhwala wobereketsa. Tsono anatengerako mayi wake Leya. Rakele anati kwa Leya, “Chonde patseko mankhwala wakupezera mwana wakowo.”

15Koma iye anati kwa Rakele, “Kodi sizinakukwanire kulanda mwamuna wanga? Ukuti utengenso mankhwala a mwana wangawa.”

Iye anati, “Chabwino, agone ndi iwe usiku uno kuti tisinthane ndi mankhwala a mwana wakowo.”

16Choncho pamene Yakobo ankabwera kuchokera ku munda madzulo, Leya anapita kukakumana naye nati, “Lero mukagona ku nyumba chifukwa ndakubwerekani ndi mankhwala wobereketsa a mwana wanga.” Choncho usiku umenewo Yakobo anakalowa kwa Leya.

17Mulungu anamva pemphero la Leya ndipo anatenga pathupi nabalira Yakobo mwana wa mwamuna wachisanu. 18Pamenepo Leya anati, “Mulungu wandipatsa mphotho chifukwa chopereka wantchito wanga kwa mwamuna wanga.” Choncho anamutcha Isakara.

19Leya anatenganso pathupi nabalira Yakobo mwana wa mwamuna wachisanu ndi chimodzi. 20Pamenepo Leya anati, “Mulungu wandipatsa mphatso yapamwamba. Tsopano mwamuna wanga adzandilemekeza chifukwa ndamubalira ana aamuna asanu ndi mmodzi.” Choncho anamutcha Zebuloni.

21Patapita nthawi Leya anabereka mwana wamkazi ndipo anamutcha Dina.

22Kenaka, Mulungu anakumbukira Rakele namva pemphero lake ndi kulola kuti akhale ndi mwana. 23Rakele anatenga pathupi nabala mwana wamwamuna ndipo anati, “Mulungu wandichotsera manyazi anga.” 24Iye anamutcha mwanayo Yosefe, ndipo anati, “Mulungu andipatsenso mwana wina.”

Nkhosa za Yakobo Zichuluka

25Rakele atabereka Yosefe, Yakobo anati kwa Labani, “Ndimasuleni kuti ndizipita ku dziko la kwathu. 26Patseni akazi anga ndi ana anga, amene ndinakugwirirani ntchito, ndipo ndidzanyamuka ulendo. Inu mukudziwa ntchito imene ndakugwirirani.”

27Koma Labani anati kwa iye, “Chonde, ngati mungandikomere mtima musapite chifukwa ndadziwa kudzera mwa kuwombeza kwanga kuti Yehova wandidalitsa chifukwa cha inu.” 28Anapitiriza kunena kuti, “Tchula malipiro ako ndipo ndidzakupatsa.”

29Koma Yakobo anati kwa iye, “Inu mukudziwa mmene ine ndakugwirirani ntchito ndi mmene ziweto zanu zaswanira pamene ine ndimazisamalira. 30Poyamba munali nazo zochepa ine ndisanabwere, koma tsopano zachuluka. Yehova wakudalitsani chifukwa cha ine. Ndi nthawi tsopano kuti nane ndisamalire banja langa.”

31Labani anafunsa, “Ndikupatse chiyani?”

Yakobo anayankha, “Musandipatse kanthu. Koma mungondichitira izi ndipo ndidzapitiriza kusamalira nkhosa zanu ndi kuziyangʼanira: 32Mundilole ndiyendeyende pakati pa ziweto zanu lero ndi kuchotsamo mwana wankhosa wamkazi aliyense wakuda, mbuzi iliyonse yamathothomathotho ndi yamawangamawanga. Zimenezi ndiye zikhale malipiro anga. 33Ndipo chilungamo changa chidzaoneka mʼtsogolo, pamene inu mudzabwere kudzaona malipiro angawo. Ngati mudzapeza mbuzi mʼgulu langa imene si yamawangamawanga, kapena mwana wankhosa wamkazi amene si wakuda ndiye kuti zimenezo zidzakhala kuti ndinakuberani.”

34Labani anati, “Ndavomera, zikhale monga mmene wayankhuliramu.” 35Tsiku lomwelo Labani anachotsa atonde onse ndi mbuzi zazikazi zonse zimene zinali ndi mawangamawanga kapena zamathothomathotho, ndiponso zonse zabanga loyera. Anachotsa ana onse ankhosa aakazi akuda, napereka ziweto zonsezi kwa ana ake aamuna kuti aziweta. 36Kenaka Labani anayenda mtunda wa masiku atatu kutalikirana ndi Yakobo koma Yakobo anapitiriza kuweta nkhosa zina zonse za Labani.

37Tsono Yakobo anatenga nthambi zaziwisi za mitengo ya mkundi, alimoni ndi puleni nazisenda kuchotsa makungwa ake mpaka mtengo woyera wamʼkati kuonekera. 38Atatero anayika nthambi zija mʼmagome omwera madzi molunjika ziweto zija kuti pakumwa madziwo ziweto zazikazi ziziyangʼana nthambi zija popeza kuti pakumwa madzi ziweto zija zinkakwerana. 39Ndiye kuti nkhosa zija zinkatenga mawere pakumwa madzi molunjika nthambi zija, ndipo zinkaswa ana a mawangamawanga kapena a mathothomathotho. 40Yakobo anayika padera ana a ziweto zija. Koma ziweto zina anaziyika kuti ziyangʼanane ndi za Labani, zimene zinali za mawangamawanga ndi zakuda. Motero anapeza ziweto zakezake, ndipo sanazisakanize ndi za Labani. 41Yakobo ankayika nthambi zija momwera madzi pamene ziweto zamphamvu zazikazi zinkakweredwa pofuna kuti zitenge mawere pakumwa madzi moyangʼanana ndi nthambi zija. 42Koma sankayika nthambizo pamene ziweto zofowoka zazikazi zinkakweredwa pakumwa madzi. Choncho ziweto zofowoka zonse zinakhala za Labani, ndi ziweto zamphamvu zinakhala za Yakobo. 43Mwa njira imeneyi, Yakobo analemera kwambiri ndipo anali ndi ziweto zochuluka kwambiri, antchito aakazi ndi aamuna, ngamira ndi abulu.

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

創世記 30:1-43

1拉結見自己沒有給雅各生孩子,就嫉妒姐姐。她對雅各說:「你給我孩子,不然我還不如死了!」 2雅各氣憤地說:「使你不能生育的是上帝,難道我能代替上帝嗎?」 3拉結說:「你去跟我的婢女辟拉同房吧,這樣她可以為我生孩子,我也可以留下後代。」 4於是拉結把婢女辟拉給丈夫做妾,雅各辟拉同房。 5辟拉懷了孕,為雅各生下一個兒子。 6拉結說:「上帝為我申了冤,也聽了我的懇求,賜給我一個兒子。」拉結就給孩子取名叫30·6 」意思是「伸冤」。7拉結的婢女辟拉又懷孕,為雅各生了第二個兒子。 8拉結說:「我跟姐姐相爭,我得勝了。」她就給這孩子取名叫拿弗他利30·8 拿弗他利」意思是「相爭」。

9利亞見自己不再生育,就把婢女悉帕雅各做妾。 10悉帕雅各生了一個兒子。 11利亞說:「真幸運!」她便給孩子取名叫迦得30·11 迦得」意思是「幸運」。12悉帕又給雅各生了第二個兒子, 13利亞說:「我真有福啊!婦女們會說我有福!」她就為孩子取名亞設30·13 亞設」意思是「有福」。

14在收麥子的季節,呂便在田間找到一些風茄,拿回家給母親利亞拉結知道後,對利亞說:「請給我一些你兒子找到的風茄。」 15利亞說:「你搶了我丈夫還不夠嗎?現在還要搶我兒子的風茄嗎?」拉結回答說:「你給我風茄,今夜雅各就跟你同房。」 16那天晚上,雅各從田間回來,利亞就出來迎接他說:「你要來跟我同房,因為我已經用兒子的風茄把你雇下來了。」於是,那天晚上雅各便跟利亞同房。 17上帝答應利亞的祈求,使她懷孕,為雅各生了第五個兒子。 18利亞說:「我把婢女送給丈夫做妾,現在上帝給我報酬了。」因此,她就為孩子取名叫以薩迦30·18 以薩迦」意思是「報酬」。

19後來,利亞又懷孕,給雅各生下第六個兒子。 20她說:「上帝賜給我珍貴的禮物,現在我丈夫會尊重我,因為我給他生了六個兒子。」於是,她就給這個兒子取名叫西布倫30·20 西布倫」意思是「尊重」。21後來,利亞又生了一個女兒,給她取名叫底娜

22上帝眷顧拉結,聽了她的禱告,使她可以生育。 23她就懷孕,生了一個兒子,說:「上帝除去了我的羞辱。」 24她給孩子取名叫約瑟30·24 約瑟」意思是「增添」。,又說:「願上帝再給我添一個兒子!」

雅各與拉班的協議

25拉結約瑟以後,雅各拉班說:「請讓我走吧!我想回故鄉, 26請你讓我和妻兒一同回去吧!她們都是我替你工作得來的,你知道我怎樣努力為你工作。」

27拉班卻挽留他,說:「如果你肯賞光,請你留下來!因為我占卜得知上帝為了你的緣故才賜福給我。 28你要多少酬勞,只管說出來,我一定會給你。」

29雅各回答說:「你知道我怎樣努力地服侍你,照顧你的牲畜。 30我來以前,你的財產很少。上帝因為我的到來而賜福給你,使你財產大增。但我自己什麼時候才能興家立業呢?」

31拉班問:「我該給你什麼呢?」雅各說:「你不用給我什麼,只要你答應一件事,我就繼續照料你的羊群。 32今天讓我從你的羊群中挑出黑色或有斑點的綿羊,以及有斑點的山羊作為我的薪酬。 33以後,如果你在給我作薪酬的羊群中發現白色的綿羊或沒有斑點的山羊,就算是我偷的。這樣你可以知道我是否誠實。」

34拉班說:「好,就照你的話做!」 35當天,拉班把有條紋或斑點的公山羊以及有斑點或夾雜白紋的母山羊,連同黑色的綿羊都挑出來,交給自己的兒子們看管。 36然後,他離開雅各,彼此相隔三天的路程。雅各繼續為他照料其餘的羊。

37雅各折下一些楊樹、杏樹和楓樹的嫩枝,削掉部分樹皮,露出白色的條紋, 38然後把這些嫩枝插在羊喝水的水槽和水溝裡。羊群來喝水時互相交配。 39牠們對著這些樹枝交配,就生下有條紋和有斑點的羊羔。 40雅各把這些羊羔分出來,使牠們與拉班的羊各在一處。他把自己的羊安置在一處,不與拉班的羊攙雜在一起。 41每當肥壯的羊交配時,雅各就把有條紋的枝子插在水溝裡,使羊對著樹枝交配。 42但如果交配的羊是瘦弱的,他就不插枝子。這樣,瘦弱的羊歸拉班,肥壯的羊歸雅各43因此,雅各變得極其富有,擁有很多羊、駱駝、驢和僕婢。