Genesis 22 – CCL & CCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Genesis 22:1-24

Kuyesedwa kwa Abrahamu

1Nthawi ina zitatha izi, Mulungu anamuyesa Abrahamu. Iye anati, “Abrahamu!”

Ndipo iye anayankha kuti, “Ee Ambuye.”

2Ndipo Mulungu anati, “Tenga Isake, mwana wako yekhayo amene umamukonda ndi kupita naye ku dziko la Moriya. Ukamupereke iye ngati nsembe yopsereza pa limodzi la mapiri a kumeneko limene ndidzakuwuza.”

3Abrahamu anadzuka mmamawa wake namangirira chokhalira pa bulu. Atadula nkhuni zokwanira zowotchera nsembe yopsereza, Abrahamu, antchito ake awiri pamodzi ndi Isake ananyamuka kupita kumalo kumene Mulungu anamuwuza Abrahamu. 4Pa tsiku lachitatu, Abrahamu anakweza maso ake ndipo anaona malowo chapatali. 5Ndipo Abrahamu anati kwa antchito ake aja, “Bakhalani pano ndi buluyu. Ine ndi mnyamatayu tipita uko kukapemphera, koma tibweranso.”

6Abrahamu anatenga nkhuni za nsembe yopsereza zija namusenzetsa mwana wake Isake, ndipo iye mwini anatenga moto ndi mpeni. Pamene awiriwo amayendera pamodzi, 7Isake anati kwa abambo ake Abrahamu, “Abambo?”

Abrahamu anayankha, “Ee mwana wanga.”

Isake anafunsa, “Moto ndi nkhuni zilipo, koma nanga mwana wankhosa wa nsembe yopsereza ali kuti?”

8Abrahamu anayankha, “Mwana wanga, Mulungu adzipezera yekha mwana wankhosa wa nsembe yopsereza.” Ndipo awiriwo anapitiriza ulendo.

9Atafika pamalo pamene Mulungu anamuwuza paja, Abrahamu anamangapo guwa lansembe nayika nkhuni pamwamba pa guwapo. Kenaka anamumanga mwana wake Isake namugoneka paguwapo, pamwamba pa nkhuni paja. 10Kenaka Abrahamu anatambasula dzanja lake natenga mpeni kuti aphe mwana wake. 11Koma mngelo wa Yehova anayitana Abrahamu kuchokera kumwamba nati, “Abrahamu! Abrahamu!”

Iye anayankha kuti, “Ee Ambuye.”

12Mngeloyo anati, “Usatambasulire mwanayo dzanja lako kuti umuphe, pakuti tsopano ndadziwa kuti iwe umaopa Mulungu. Iwe sunandimane mwana wako mmodzi yekhayo.”

13Abrahamu anatukula maso ake ndipo anaona nkhosa yamphongo itakoledwa ndi nyanga zake mu ziyangoyango. Iye anapita nakatenga nkhosa ija ndikuyipha ngati nsembe yopsereza mʼmalo mwa mwana wake. 14Choncho Abrahamu anatcha malo amenewa kuti Yehova-Yire (Wopereka). Ndipo mpaka lero amatchula malowo kuti ndi “Pa phiri la Yehova wopereka.”

15Mngelo wa Yehova anayitana Abrahamu kuchokera kumwamba kachiwiri 16ndipo anati, “Ndikulumbira mwa Ine ndekha kuti popeza wachita zimenezi, wosandikaniza mwana wako mmodzi yekhayu, 17ndidzakudalitsa ndithu ndipo ndidzakupatsa zidzukulu zochuluka ngati nyenyezi zamlengalenga komanso ngati mchenga wa mʼmphepete mwa nyanja. Zidzukulu zako zidzalanda mizinda ya adani awo, 18ndipo kudzera mwa chidzukulu chako, mitundu yonse ya anthu pa dziko lapansi idzadalitsika, chifukwa iwe wandimvera.”

19Kenaka Abrahamu anabwerera kumene anasiya antchito ake kuja nanyamukira nawo pamodzi kupita ku Beeriseba. Ndipo Abrahamu anakhala ku Beeriseba.

Ana Aamuna a Nahori

20Patapita nthawi, Abrahamu anamva kuti, “Milika nayenso anaberekera Nahori, mʼbale wake ana. 21Woyamba anali Huzi ndipo kenaka mʼbale wake Buzi. Anaberekanso Kemueli, amene anali abambo ake a Aramu. 22Ana ena ndi Kesede Hazo, Pilidasi, Yidilafi ndi Betueli.” 23Betueli anabereka Rebeka. Milika anaberekera Nahori, mʼbale wake wa Abrahamu, ana aamuna asanu ndi atatu amenewa. 24Mkazi wake wachiwiri, dzina lake Reuma, anamubaliranso Nahori ana awa: Teba, Gahamu, Tahasi ndi Maaka.

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

创世记 22:1-24

上帝考验亚伯拉罕

1这些事以后,上帝要考验亚伯拉罕,就呼唤他:“亚伯拉罕!”他回答说:“我在这里。” 2上帝说:“带着你的儿子,你的独生子,你疼爱的以撒前往摩利亚,在我指示你的山上把他献为燔祭。” 3亚伯拉罕清早起来,准备好驴,劈好献燔祭用的柴,带着两个仆人和儿子以撒动身前往上帝指示他的地方。 4到了第三天,亚伯拉罕远远看见那地方, 5就对仆人说:“你们和驴在这里等着,我和孩子到那边敬拜上帝,然后便回来。”

6于是,亚伯拉罕把献燔祭用的柴放在儿子以撒肩上,自己手里拿着火种和刀。父子二人一同向前走。 7以撒说:“父亲。”亚伯拉罕说:“孩子,什么事?”以撒说:“你看,火种和柴都有了,但献燔祭用的羊羔在哪里呢?” 8亚伯拉罕说:“孩子,上帝自己会预备献燔祭的羊羔。”二人就继续向前走。

9他们到了上帝指示的地方,亚伯拉罕就筑起祭坛,把柴摆在上面,然后把以撒捆起来放在柴上。 10亚伯拉罕伸手拿起刀来,要杀他的儿子。 11耶和华的天使从天上呼唤他说:“亚伯拉罕亚伯拉罕!”他回答说:“我在这里。” 12天使说:“不要动孩子,不可伤害他!现在我知道你敬畏上帝,因为你不惜献上你的儿子——你的独生子。” 13这时亚伯拉罕抬起头来,突然看见有一只公绵羊两角卡在稠密的树丛中,于是把羊取来代替他的儿子献为燔祭。 14亚伯拉罕称那地方为“耶和华以勒22:14 耶和华以勒”或译“耶和华必预备”。。直到今天人们还说:“在耶和华的山上必有预备。”

15耶和华的天使再次从天上呼唤亚伯拉罕16对他说:“耶和华说,‘你既然愿意把你的儿子,你的独生子献给我,我凭自己向你起誓, 17我必赐福给你,使你的后裔多如天上的星和海边的沙。你的后裔必占领仇敌的城池, 18天下万国必因你的后裔而蒙福,因为你听从了我的话。’” 19于是,亚伯拉罕回到仆人等候的地方,他们一同返回亚伯拉罕居住的别示巴

拿鹤的后代

20后来,有人告诉亚伯拉罕:“密迦为你的兄弟拿鹤生了几个儿子, 21长子乌斯乌斯的弟弟布斯亚兰的父亲基姆利22基薛哈琐必达益拉利百加的父亲彼土利。” 23密迦亚伯拉罕的兄弟拿鹤生了八个儿子。 24拿鹤的妾流玛生了提八迦含他辖玛迦