Genesis 21 – CCL & CCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Genesis 21:1-34

Kubadwa kwa Isake

1Yehova anakomera mtima Sara monga ananenera, ndipo Yehovayo anachita monga momwe analonjezera. 2Sara anakhala ndi pathupi ndipo anamuberekera Abrahamu mwana wamwamuna mu ukalamba wake, pa nyengo imene Mulungu anamulonjeza. 3Abrahamu anapereka dzina loti Isake kwa mwana wamwamuna amene Sara anamuberekera. 4Isake atakwanitsa masiku asanu ndi atatu, Abrahamu anamuchita mdulidwe monga Mulungu anamulamulira. 5Abrahamu anali ndi 100 pamene mwana wake Isake anabadwa.

6Sara anati, “Mulungu wandibweretsera mseko, ndipo aliyense amene adzamva zimenezi adzaseka nane pamodzi.” 7Ndipo anawonjezera kuti, “Ndani akanamuwuza Abrahamu kuti Sara nʼkudzayamwitsako ana? Chonsecho ndamubalira mwana wamwamuna kuwukalamba wake.”

Kuchotsedwa kwa Hagara ndi Ismaeli

8Mwana uja anakula mpaka kumuletsa kuyamwa. Tsiku lomuletsa Isake kuyamwa, Abrahamu anakonza phwando lalikulu. 9Koma Sara anaona kuti mwana wamwamuna amene Hagara Mwigupto anamuberekera Abrahamu amamuseka, 10ndipo anati kwa Abrahamu, “Muchotse mdzakazi ndi mwana wake wamwamunayu, pakuti mwana wa kapolo sadzagawana chuma ndi mwana wanga Isake.”

11Nkhaniyi inamumvetsa chisoni kwambiri Abrahamu chifukwa imakhudza mwana wake. 12Koma Mulungu anamuwuza Abrahamu kuti, “Usamve chisoni motero ndi mnyamatayu ndi mdzakazi wakoyu. Mvetsera chilichonse chomwe Sara akukuwuza, chifukwa zidzukulu zako zidzachokera mwa Isake. 13Mwana wa mdzakazi wakoyu ndidzamusandutsa mtundu wa anthu chifukwa ndi mwana wako.”

14Mmamawa wake, Abrahamu anatenga chakudya ndi botolo la madzi nazipereka kwa Hagara. Anasenzetsa Hagara nawaperekeza pangʼono ndi mnyamatayo. Hagara ananyamuka nayendayenda mʼchipululu cha Beeriseba.

15Madzi atatha mʼbotolo muja, anamuyika mnyamatayo pansi pa zitsamba. 16Kenaka Hagara anachoka nakakhala pansi cha pakatalipo, pafupifupi mamita makumi asanu ndi anayi, popeza mʼmaganizo mwake amati, “Sindingaonerere mwanayu akufa.” Ndipo anakhala pansi cha poteropo nʼkumalira.

17Mulungu anamva mnyamatayo akulira ndipo mngelo wa Mulungu anayankhula kwa Hagara kuchokera kumwamba nati, “Chavuta nʼchiyani Hagara? Usachite mantha; Mulungu wamva kulira kwa mnyamatayo pamene wagonapo. 18Munyamule mnyamatayo ndipo umugwire dzanja pakuti ndidzamupanga kukhala mtundu waukulu.”

19Kenaka Mulungu anatsekula maso a Hagara ndipo anaona chitsime cha madzi. Choncho anapita nadzaza botolo lija ndi madzi ndi kumupatsa mnyamatayo kuti amwe.

20Mulungu anali ndi mnyamatayo pamene ankakula. Anakhala ku chipululu nakhala katswiri wolasa uta. 21Akukhala ku chipululu cha Parani, mayi ake anamupezera mkazi wochokera ku Igupto.

Pangano la ku Beeriseba

22Pa nthawiyo, Abimeleki ndi Fikolo wamkulu wankhondo wake anati kwa Abrahamu, “Mulungu ali nawe pa chilichonse umachita. 23Tsopano undilumbirire ine pano pamaso pa Mulungu kuti sudzachita mwa chinyengo ndi ine kapena ana anga kapena zidzukulu zanga. Undionetse ine pamodzi ndi dziko limene ukukhalamo ngati mlendo, kukoma mtima kokhala ngati kumene ndinakuonetsa ine.”

24Abrahamu anati, “Ine ndikulumbira.”

25Kenaka Abrahamu anadandaula kwa Abimeleki pa za chitsime chimene antchito a Abimeleki analanda. 26Koma Abimeleki anati, “Ine sindikudziwa amene anachita zimenezi. Iwe sunandiwuze, ndipo ndazimva lero zimenezi.”

27Choncho Abrahamu anabweretsa nkhosa ndi ngʼombe nazipereka kwa Abimeleki, ndipo anthu awiriwo anachita pangano. 28Abrahamu anapatulako ana ankhosa aakazi asanu ndi awiri kuchoka pagulu la nkhosa zina, 29ndipo Abimeleki anafunsa Abrahamu, “Kodi tanthauzo lake la ana ankhosa aakazi asanu ndi awiri amene wawapatula pawokhawa nʼchiyani?”

30Iye anayankha kuti, “Landirani ana ankhosa aakazi kuchokera mʼdzanja langa ngati umboni kuti ndinakumba chitsime ichi.”

31Kotero malo amenewo anatchedwa Beeriseba, chifukwa anthu awiriwo analumbirirapo malumbiro.

32Atatha kuchita pangano pa Beeriseba, Abimeleki ndi Fikolo mkulu wankhondo wake anabwerera ku dziko la Afilisti. 33Abrahamu anadzala mtengo wa bwemba ku Beeriseba, ndipo anapemphera pamenepo mʼdzina la Yehova, Mulungu Wamuyaya. 34Ndipo Abrahamu anakhala mʼdziko la Afilisti kwa nthawi yayitali.

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

创世记 21:1-34

以撒出生

1耶和华按着自己说过的话眷顾撒拉,实现给她的应许。 2亚伯拉罕年老的时候,撒拉怀了孕,在上帝指定的日期为他生了一个儿子。 3亚伯拉罕为儿子取名叫以撒4以撒出生后第八天,亚伯拉罕就照着上帝的吩咐为他行了割礼。 5以撒出生时亚伯拉罕已经一百岁。 6撒拉说:“上帝使我欢笑,凡听见这事的人也必跟我一同欢笑。 7谁曾料到我会为亚伯拉罕哺养孩子呢?我竟然在丈夫年老的时候给他生了儿子。”

夏甲和以实玛利被逐

8以撒渐渐长大,亚伯拉罕在他断奶的那天摆设宴席。 9撒拉埃及夏甲亚伯拉罕生的儿子以实玛利嘲笑以撒10就对亚伯拉罕说:“赶走这婢女和她的儿子,因为这婢女的儿子不可和我的儿子以撒一同承受产业。” 11亚伯拉罕因儿子以实玛利的事非常烦恼。 12上帝对亚伯拉罕说:“你不要再为这孩子和你的婢女烦恼,只管照撒拉的意思去做,因为以撒生的才可算为你的后代。 13至于那婢女的儿子以实玛利,我也会使他自成一国,因为他也是你的儿子。”

14第二天,亚伯拉罕清早起来,把食物和一皮袋水放在夏甲肩上,让她和孩子离开。夏甲别示巴的旷野流浪。 15皮袋的水喝光了,夏甲把儿子留在一丛灌木下, 16自己走到离孩子约一箭之远的地方,对着孩子坐下,说:“我不忍心看着他死啊!”夏甲坐在那里放声大哭起来。 17上帝听见孩子的哭声,就差遣天使从天上安慰夏甲说:“夏甲,你怎么了?不要害怕,上帝已经听见孩子的哭声了。 18你去扶他起来,安慰他,我必使他成为大国。” 19上帝使夏甲的眼睛明亮,让她看见一口水井,她就上前把皮袋装满水拿给儿子喝。 20在上帝的看顾下,孩子在旷野渐渐长大,成为一个射箭能手。 21他住在巴兰旷野,他母亲为他娶了一个埃及女子。

亚伯拉罕与亚比米勒立约

22有一次,亚比米勒和他的将领非各亚伯拉罕说:“你做的一切都有上帝保佑。 23现在请你在这里当着上帝的面向我起誓,你不会欺骗我和我的子孙后代。我怎样善待你,请你也同样善待我以及你所寄居之地的百姓。” 24亚伯拉罕说:“我愿起誓。”

25由于亚比米勒的仆人霸占了一口水井,亚伯拉罕就指责亚比米勒26亚比米勒说:“我不知道是谁做的,你以前没有告诉我,我今天才听说这事。” 27亚伯拉罕把牛羊送给亚比米勒,他们二人立了约。 28亚伯拉罕又从羊群中分出七只母羊羔。 29亚比米勒亚伯拉罕:“你分出七只母羊羔是什么意思?” 30亚伯拉罕回答说:“你要从我手中接受这七只母羊羔,表示你承认这口井是我挖的。” 31所以,那地方被称为别示巴21:31 别示巴”意思是“盟誓之井”。,因为他们二人在那里起了誓。

32他们立约以后,亚比米勒和他的将领非各便回非利士去了。 33亚伯拉罕别示巴栽了一棵红柳,又在那里呼求耶和华——永恒上帝的名。 34亚伯拉罕非利士住了很长时间。