Genesis 2 – CCL & KJV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Genesis 2:1-25

1Motero kumwamba, dziko lapansi ndi zonse za mʼmenemo zinatha kulengedwa monga mwa kuchuluka kwawo.

2Pofika tsiku lachisanu ndi chiwiri Mulungu anamaliza ntchito zonse zimene ankagwira ndipo pa tsiku lachisanu ndi chiwiri anapumula ku ntchito zake zonse. 3Ndipo Mulungu anadalitsa tsiku lachisanu ndi chiwiri nalipatula, chifukwa pa tsiku limeneli Iye anapumula ku ntchito yonse yolenga imene anayigwira.

Adamu ndi Hava

4Mbiri ya momwe kumwamba ndi dziko lapansi zinalengedwera pa tsiku lija Yehova Mulungu ankazilenga ndi iyi:

Yehova Mulungu atapanga dziko lapansi ndi kumwamba, 5zitsamba zinali zisanamere ndipo chomera chilichonse chinali chisanamerenso popeza Yehova Mulungu anali asanagwetse mvula pa dziko lapansi. Panalibe munthu wolima nthaka, 6koma kasupe ankatuluka mʼnthaka ndi kuthirira pa dziko lonse. 7Tsono Yehova Mulungu anawumba munthu kuchokera ku dothi nawuziramo mpweya wamoyo mʼmphuno mwake ndipo munthuyo anakhala wamoyo.

8Kenaka Yehova Mulungu anatsekula munda wa Edeni chakummawa; kumeneko anayikako munthu amene anamupanga uja. 9Ndipo Yehova Mulungu anameretsa mʼmundamo mitengo ya mitundu yonse. Inali mitengo yokongola ndi ya zipatso zokoma. Pakati pa munda uja panali mtengo wopatsa moyo ndi mtengo wopatsa nzeru zodziwitsa chabwino ndi choyipa.

10Mtsinje wothirira mundawo unkatuluka mu Edeni; kuchokera apo unkagawikana kukhala mitsinje inayi. 11Dzina la mtsinje woyamba ndi Pisoni; uwu umazungulira dziko lonse la Havila, kumene kuli golide. 12(Golide wa ku dziko ili ndi wabwino. Kulinso miyala yokongola ya bedola ndi onikisi). 13Dzina la mtsinje wachiwiri ndi Gihoni; uwu umazungulira dziko lonse la Kusi. 14Dzina la mtsinje wachitatu ndi Tigirisi; umayenda chakummawa kwa Asiriya. Ndipo mtsinje wachinayi ndi Yufurate.

15Yehova Mulungu anatenga munthu uja ndi kumuyika mʼmunda wa Edeni kuti awulime ndi kuwusamalira. 16Ndipo Yehova Mulungu analamula munthu uja kuti, “Uzidya zipatso za mu mtengo wina uliwonse mʼmundamu; 17koma usadye zipatso za mu mtengo wodziwitsa chabwino ndi choyipa, popeza ukadzadya za mu mtengowu udzafa ndithu.”

18Ndipo Yehova Mulungu anati, “Sibwino kuti munthu akhale yekha. Ndidzamupangira mnzake womuthandiza.”

19Kenaka Yehova Mulungu anawumba ndi dothi nyama zonse zakuthengo ndi mbalame zonse zamlengalenga. Ndipo Iye anapita nazo kwa munthu uja kuti akazipatse mayina; ndipo dzina lililonse limene Adamu anapereka ku chamoyo chilichonse, lomwelo linakhala dzina lake. 20Choncho Adamu anazitcha mayina ziweto zonse, mbalame zamlengalenga ndi nyama zakuthengo zonse.

Komabe munthu uja analibe mnzake womuthandiza. 21Tsono Yehova Mulungu anamugonetsa munthu uja tulo tofa nato; ali mtulo chomwecho, Mulungu anachotsa imodzi mwa nthiti zake ndi kutseka pamalopo ndi mnofu. 22Motero Yehova Mulungu anapanga mkazi ndi nthiti ija imene anatenga kwa munthu uja nabwera naye kwa iye.

23Munthu uja anati,

“Uyu ndiye fupa lochokera ku mafupa anga

ndi mnofu wochokera ku mnofu wanga;

adzatchedwa ‘mkazi,’

popeza wachokera mwa mwamuna.”

24Nʼchifukwa chake, mwamuna amasiya abambo ndi amayi ake nakaphatikana ndi mkazi wake ndipo awiriwo amakhala thupi limodzi.

25Munthu uja ndi mkazi wakeyo, onse awiri anali maliseche ndipo analibe manyazi.

King James Version

Genesis 2:1-25

1Thus the heavens and the earth were finished, and all the host of them. 2And on the seventh day God ended his work which he had made; and he rested on the seventh day from all his work which he had made. 3And God blessed the seventh day, and sanctified it: because that in it he had rested from all his work which God created and made.2.3 created…: Heb. created to make

4¶ These are the generations of the heavens and of the earth when they were created, in the day that the LORD God made the earth and the heavens, 5And every plant of the field before it was in the earth, and every herb of the field before it grew: for the LORD God had not caused it to rain upon the earth, and there was not a man to till the ground. 6But there went up a mist from the earth, and watered the whole face of the ground.2.6 there…: or, a mist which went up from, etc. 7And the LORD God formed man of the dust of the ground, and breathed into his nostrils the breath of life; and man became a living soul.2.7 of the dust…: Heb. dust of the ground

8¶ And the LORD God planted a garden eastward in Eden; and there he put the man whom he had formed. 9And out of the ground made the LORD God to grow every tree that is pleasant to the sight, and good for food; the tree of life also in the midst of the garden, and the tree of knowledge of good and evil. 10And a river went out of Eden to water the garden; and from thence it was parted, and became into four heads. 11The name of the first is Pison: that is it which compasseth the whole land of Havilah, where there is gold; 12And the gold of that land is good: there is bdellium and the onyx stone. 13And the name of the second river is Gihon: the same is it that compasseth the whole land of Ethiopia.2.13 Ethiopia: Heb. Cush 14And the name of the third river is Hiddekel: that is it which goeth toward the east of Assyria. And the fourth river is Euphrates.2.14 toward…: or, eastward to Assyria 15And the LORD God took the man, and put him into the garden of Eden to dress it and to keep it.2.15 the man: or, Adam

16And the LORD God commanded the man, saying, Of every tree of the garden thou mayest freely eat:2.16 thou…: Heb. eating thou shalt eat 17But of the tree of the knowledge of good and evil, thou shalt not eat of it: for in the day that thou eatest thereof thou shalt surely die.2.17 thou shalt surely…: Heb. dying thou shalt die

18¶ And the LORD God said, It is not good that the man should be alone; I will make him an help meet for him.2.18 meet…: Heb. as before him 19And out of the ground the LORD God formed every beast of the field, and every fowl of the air; and brought them unto Adam to see what he would call them: and whatsoever Adam called every living creature, that was the name thereof.2.19 Adam: or, the man 20And Adam gave names to all cattle, and to the fowl of the air, and to every beast of the field; but for Adam there was not found an help meet for him.2.20 gave: Heb. called

21And the LORD God caused a deep sleep to fall upon Adam, and he slept: and he took one of his ribs, and closed up the flesh instead thereof; 22And the rib, which the LORD God had taken from man, made he a woman, and brought her unto the man.2.22 made: Heb. builded 23And Adam said, This is now bone of my bones, and flesh of my flesh: she shall be called Woman, because she was taken out of Man.2.23 Woman: Heb. Isha2.23 Man: Heb. Ish 24Therefore shall a man leave his father and his mother, and shall cleave unto his wife: and they shall be one flesh. 25And they were both naked, the man and his wife, and were not ashamed.