Genesis 18 – CCL & CARST

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Genesis 18:1-33

Alendo Atatu a Abrahamu

1Yehova anadza kwa Abrahamu pafupi ndi mitengo ikuluikulu ya thundu ya ku Mamre. Abrahamu nʼkuti atakhala pansi pa khoma la tenti yake masana, dzuwa likutentha. 2Tsono Abrahamu atakweza maso ake patali anangoona anthu atatu atayima cha potero. Atawaona, ananyamuka mofulumira kuti awachingamire. Atafika anaweramitsa mutu pansi mwa ulemu nati, 3“Ngati mwandikomera mtima, mbuye wanga, musamulambalale mtumiki wanu. 4Ndikupatseniko timadzi pangʼono kuti nonse musambitse mapazi anu ndi kupumula pansi pa mtengo uwu. 5Tsono ndikutengereniko kachakudya kuti mudye kuti mwina nʼkupezako mphamvu zopitirizira ulendo wanu. Inu mwafika kumalo kwa mtumiki wanu.”

Ndipo iwo anamuyankha nati, “Zikomo kwambiri, chita monga wanenera.”

6Choncho Abrahamu anafulumira kupita kwa Sara mʼtenti nati, “Tafulumira, tenga mabeseni atatu a ufa wosalala, ukande ndi kupanga buledi.”

7Kenaka Abrahamu anakatenga mwana wangʼombe wonenepa ndi wofewa bwino ndi kupatsa wantchito wake amene anachita changu kukonza ndiwoyo. 8Tsono Abrahamu anatenga chambiko, mkaka ndi mwana wangʼombe wokonzedwa uja nazipereka kwa anthu aja. Alendowo akudya, Abrahamu ankawayangʼana atayimirira pansi pa mtengo.

9Anthuwo anafunsa Abrahamu kuti, “Mkazi wako Sara ali kuti?”

Iye anati, “Ali mu tentimu.”

10Tsono mmodzi mwa iwo anati, “Mosakayikira ndidzabweranso pa nthawi ngati yomwe ino chaka chamawa, ndipo Sara mkazi wako adzakhala ndi mwana wamwamuna.”

Koma Sara amene anali kumbuyo kwa Abrahamu pa khoma la tenti ankamva zonsezi. 11Abrahamu ndi Sara anali okalamba kale ndipo anali ndi zaka zambiri. Sara nʼkuti atapyola kale pa msinkhu oti nʼkubereka. 12Choncho anangoseka nati mu mtima mwake, “Kodi munthu wothayitha ngati ine ndingasangalalenso kugona pamodzi ndi mbuye wanga? Mwamuna wanga nayenso ndi wokalamba.”

13Ndipo Yehova anati kwa Abrahamu, “Nʼchifukwa chiyani Sara anaseka nʼkumati, ‘Moti ine nʼkudzakhaladi ndi mwana mmene ndakalambiramu?’ 14Kodi pali chimene chikhoza kumukanika Yehova? Pa nthawi yake, ngati yomwe ino chaka chamawa ndidzabweranso, ndipo Sara adzabala mwana wamwamuna.”

15Koma Sara ndi mantha ananama nati, “Sindinaseke.”

Koma Iye anati, “Inde iwe unaseka.”

Abrahamu Apembedzera Sodomu

16Kenaka anthu aja ananyamuka ndi kumapita, molunjika ku Sodomu. Ndipo Abrahamu anayenda nawo pamodzi kuwaperekeza. 17Tsono Yehova anati mu mtima mwake, “Kodi ndingamubisire Abrahamu chimene ndikuti ndichite posachedwa? 18Abrahamu adzakhaladi mtundu wa anthu waukulu ndi wamphamvu, ndipo mitundu yonse ya anthu pa dziko lapansi adzadalitsika kudzera mwa iye. 19Pakuti ndasankha iyeyu kuti adzatsogolere ana ake ndi a pa banja lake, kuti asunge mawu a Yehova pochita zoyenera ndi zachilungamo. Choncho Yehova adzachita kwa Abrahamu chimene anamulonjeza iye.”

20Ndipo Yehova anati kwa Abrahamu, “Kulirira Gomora kwakula ndipo tchimo lawo lafika poyipa kwambiri 21choncho ndikuti ndipiteko ndikaone ngati zimene achita zilidi zoyipa monga mmene madandawulo andipezera Ine. Ngati sizili choncho, ndikadziwa.”

22Anthu aja anatembenuka nʼkumapita, kulowera ku Sodomu, koma Abrahamu anali chiyimirire pamaso pa Yehova. 23Kenaka Abrahamu anasendera kufupi ndi Iye nati, “Kodi mudzawonongera kumodzi wolungama ndi woyipa? 24Nanga bwanji patakhala anthu makumi asanu olungama mu mzindamo? Kodi mudzawonongadi onse osausiyako mzindawo chifukwa cha anthu makumi asanu olungama omwe ali mʼmenemo? 25Ndithu simungachite zimenezi, kupha anthu olungama pamodzi ndi oyipa. Nʼzosatheka kuti inu nʼkufananitsa olungama ndi oyipa. Kodi woweruza wa dziko lapansi nʼkulephera kuchita chilungamo?”

26Yehova anati, “Nditapeza anthu makumi asanu olungama mu mzinda wa Sodomu, ndidzasiya malo onsewo osawawononga chifukwa cha iwo.”

27Ndipo Abrahamu anayankhulanso nati, “Tsono poti ndalimba mtima kuyankhula ndi Ambuye, ngakhale kuti ndine fumbi ndi phulusa chabe, 28bwanji anthu olungama atacheperapo ndi asanu pa anthu makumi asanu? Kodi mudzawononga mzinda wonse chifukwa cha asanuwo?”

Iye anati, “Nditapezamo anthu 45, sindidzawuwononga.”

29Kenakanso anayankhula kwa Iye nati, “Bwanji atangopezekamo anthu 40 okha?”

Iye anayankha, “Chifukwa cha anthu 40 amenewa, sindidzatero.”

30Ndipo Abrahamu anati, “Pepanitu musandipsere mtima Ambuye, koma mundilole kuti ndiyankhule. Nanga mutapezekamo anthu makumi atatu okha?”

Iye anayankha, “Sindidzatero ngati atapezekamo anthu makumi atatu.”

31Abrahamu anati, “Tsono poti ndalimba mtima chonchi kumayankhula ndi Ambuye, bwanji atangopezeka anthu makumi awiri okha?”

Iye anati, “Chifukwa cha anthu makumi awiriwo, sindidzawuwononga.”

32Kenaka Abrahamu anati, “Pepani Ambuye musandipsere mtima, ndingoyankhula kamodzi kokhaka basi. Bwanji atangopezeka khumi okha mʼmenemo?”

Iye anayankha nati, “Chifukwa cha khumiwo, sindidzawuwononga.”

33Yehova atatsiriza kuyankhula ndi Abrahamu, anachoka ndipo Abrahamu anabwerera ku nyumba yake.

Священное Писание (Восточный перевод), версия для Таджикистана

Начало 18:1-33

Три гостя Иброхима

1Вечный явился Иброхиму у великих деревьев Мамре, когда тот сидел у входа в свой шатёр во время дневного зноя. 2Иброхим поднял взгляд и увидел, что неподалёку стоят три человека; увидев их, он побежал от входа в шатёр им навстречу и поклонился до земли.

3Он сказал:

– Если я нашёл милость в Твоих глазах, Владыка, то не пройди мимо Твоего раба. 4Пусть принесут немного воды, чтобы вам вымыть ноги и отдохнуть под этим деревом, 5а я принесу вам что-нибудь поесть. Вы подкрепитесь и продолжите свой путь – раз уж вы пришли ко мне, вашему рабу.

– Очень хорошо, – ответили они. – Делай, как говоришь.

6И Иброхим поспешил в шатёр к Соро и сказал:

– Скорее, достань три меры18:6 Букв.: «три саты», что равняется 22 л (примерно 14 кг муки). лучшей муки, замеси тесто и испеки лепёшек.

7Затем он побежал к стаду, выбрал лучшего, нежного телёнка и отдал слуге, который быстро приготовил его. 8Потом он принёс творога, молока и приготовленного телёнка и поставил перед ними. Пока они ели, он стоял рядом с ними под деревом.

9– Где твоя жена Соро? – спросили они.

– Там, в шатре, – ответил он.

10Тогда Вечный сказал:

– Я непременно вернусь к тебе в следующем году, примерно в это же время, и у Соро, твоей жены, будет сын.

Соро слушала, стоя у Него за спиной, у входа в шатёр. 11Иброхим и Соро были уже стары и в преклонных годах, и то, что обычно бывает у женщин, у Соро прекратилось. 12Поэтому Соро рассмеялась про себя, подумав: «Я уже состарилась, и господин мой стар; мне ли иметь ещё такую радость?»

13Тогда Вечный сказал Иброхиму:

– Почему Соро смеётся и говорит: «Неужели у меня в самом деле будет ребёнок, ведь я стара?» 14Есть ли что-нибудь слишком трудное для Вечного? Я вернусь к вам через год в назначенное время, и у Соро будет сын.

15Соро испугалась и солгала, сказав:

– Я не смеялась.

Но Он сказал:

– Нет, ты смеялась.

Просьба Иброхима о сохранении города Содома

16Гости поднялись и пошли в сторону Содома. Иброхим отправился с ними, чтобы проводить их.

17Вечный сказал:

– Скрою ли Я от Иброхима то, что собираюсь сделать? 18От Иброхима непременно произойдёт великий и сильный народ, и все народы на земле получат благословение через него. 19Ведь Я избрал его, чтобы он заповедал своим детям и всем своим потомкам хранить путь Вечного, поступая правильно и справедливо, чтобы Вечный исполнил то, что обещал Иброхиму.

20Вечный сказал:

– Вопль против Содома и Гоморры так велик, их грех так тяжек, 21что Я сойду и посмотрю, верен ли вопль, достигший Меня, так ли скверно они поступают. Если нет, Я узнаю.

22Двое мужчин повернулись и пошли к Содому, но Вечный остался со стоящим перед Ним Иброхимом. 23Иброхим приблизился к Нему и сказал:

– Неужели Ты уничтожишь праведного вместе с грешным? 24Что, если в городе есть пятьдесят праведников? Неужели Ты уничтожишь и не пощадишь этого места ради пятидесяти праведников? 25Не можешь Ты сделать такое – погубить праведного вместе с нечестивым, обойтись с праведным и нечестивым одинаково. Не можешь Ты сделать так! Разве Судья всей земли может творить неправду?

26Вечный сказал:

– Если Я найду в Содоме пятьдесят праведников, то пощажу ради них всё это место.

27Тогда Иброхим сказал вновь:

– Вот я осмелился говорить с Владыкой, хотя я лишь прах и пепел; 28что, если число праведных на пять меньше пятидесяти? Уничтожишь ли Ты весь город из-за пяти человек?

– Если Я найду там сорок пять, – ответил Вечный, – то не уничтожу его.

29Иброхим обратился к Нему ещё раз:

– Что, если там найдутся лишь сорок?

Вечный ответил:

– Ради сорока Я не сделаю этого.

30Тогда тот сказал:

– Да не разгневается Владыка, но позволит мне сказать. Что, если найдутся там только тридцать?

Вечный ответил:

– Я не сделаю этого, если найду там тридцать.

31Иброхим сказал:

– Вот я был так смел, что решился говорить Владыке: что, если найдутся там лишь двадцать?

Вечный сказал:

– Ради двадцати Я не уничтожу его.

32Тогда Иброхим сказал:

– Да не разгневается Владыка, но позволит мне сказать ещё лишь один раз. Что, если найдутся там лишь десять?

Вечный ответил:

– Ради десяти Я не уничтожу его.

33Когда Вечный закончил говорить с Иброхимом, Он ушёл, а Иброхим вернулся домой.