Genesis 19 – CCL & CARST

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Genesis 19:1-38

Kuwonongedwa kwa Sodomu ndi Gomora

1Angelo awiri aja anafika ku Sodomu madzulo ndipo Loti anali atakhala pansi pa chipata cha mzindawo. Loti atawaona, anayimirira ndi kukakumana nawo ndipo anaweramitsa mutu wake pansi mwaulemu. 2Iye anati, “Ambuye wanga, chonde patukirani ku nyumba kwa mtumiki wanu. Mukhoza kusambitsa mapazi anu ndi kugona usiku uno kenaka nʼkumapitirira ndi ulendo wanu mmamawa.”

Iwo anati, “Ayi, tigona panja.”

3Koma iye anawawumiriza kwambiri kotero kuti anapita naye pamodzi ku nyumba kwake. Anawakonzera chakudya buledi wopanda yisiti ndipo anadya. 4Alendo aja asanapite kogona, amuna onse achinyamata ndi achikulire ochokera mbali zonse za mzinda wa Sodomu anazinga nyumba ya Loti. 5Iwo anayitana Loti namufunsa kuti, “Ali kuti amuna aja amene afika kuno usiku womwe uno? Atulutse, utipatse kuti tigone nawo malo amodzi.”

6Loti anatuluka panja kukakumana nawo natseka chitseko 7ndipo anati, “Ayi anzanga, musachite zinthu zoyipa zotere. 8Taonani, ine ndili ndi ana anga akazi awiri amene sanagonepo ndi mwamuna. Mundilole ndikutulutsireni amenewo ndipo muchite nawo zimene mungafune. Koma musachite chilichonse ndi anthuwa, pakuti iwowa ndi alendo anga ndipo ndiyenera kuwatchinjiriza.”

9Iwo anayankha kuti, “Tachoka apa tidutse.” Ndipo anati, “Munthu uyu anabwera kuno ngati mlendo chabe, tsono lero akufuna kuti akhale wotiweruza! Tikukhawulitsa kuposa iwowa.” Anapitiriza kumuwumiriza Loti uja nʼkumasunthira kutsogolo kuti athyole chitseko.

10Koma anthu aja anali mʼkatiwa anasuzumira namukokera Loti uja mʼkati mwa nyumba nʼkutseka chitseko. 11Kenaka anawachititsa khungu anthu amene anali panja pa nyumba aja, aangʼono ndi aakulu omwe, kuti asaone pa khomo.

12Anthu awiri aja anati kwa Loti, “Kodi uli ndi wina aliyense pano, kaya ndi akamwini ako, kaya ndi ana ako aamuna kapena aakazi, kapena aliyense mu mzindamu amene ndi anzako? Atulutse onse muno, 13chifukwa tiwononga malo ano. Yehova waona kuti kuyipa kwa anthu a mu mzindawu kwakulitsa. Choncho watituma kuti tiwuwononge.”

14Choncho Loti anatuluka nayankhula ndi akamwini ake amene anali kuyembekezera kukwatira ana ake akazi nati, “Fulumirani, tiyeni tichoke pa malo ano chifukwa Yehova watsala pangʼono kuwononga mzindawu.” Koma akamwini akewo ankayesa kuti akungoselewula.

15Mmene kumacha, angelo aja anamufulumizitsa Loti nati, “Nyamuka, tenga mkazi wako ndi ana ako aakazi awiriwo, ndipo mutuluke mu mzindawo kuopa kuti mungaphedwe pamodzi nawo.”

16Koma Loti ankakayikabe. Koma Yehova anawachitira chifundo motero kuti anthu aja anagwira mkazi wake ndi ana ake aakazi aja nawatsogolera bwinobwino kuwatulutsa mu mzindawo. 17Atangowatulutsa, mmodzi wa angelowo anati, “Thawani kuti mudzipulumutse, musachewuke, musayime pena paliponse mʼchigwamo! Thawirani ku mapiri kuopa kuti mungawonongeke!”

18Koma Loti anawawuza kuti, “Ayi, ambuye anga chonde musatero! 19Taonani, Inu mwachitira mtumiki wanu chifundo, ndipo mwaonetsa kukoma mtima kwanu pondipulumutsa. Sindingathawire ku mapiri chifukwa chiwonongekochi chikhoza kundipeza ndisanafike ku mapiriko ndipo ndingafe. 20Koma, chapafupi pomwepa pali mudzi woti ndikhoza kuthamanga nʼkukafikako. Mundilole ndithawireko, ndi waungʼono kwambiri, si choncho? Mukatero, moyo wanga upulumuka.”

21Mngeloyo anati kwa iye, “Chabwino, ndavomeranso pempho lako, sindiwononga mudzi ukunenawo. 22Koma uthawireko mofulumira chifukwa sindichita kena kalikonse mpaka utafikako.” (Nʼchifukwa chake mudziwo unatchedwa Zowari).

23Pamene Loti amafika ku Zowari, nʼkuti dzuwa litatuluka. 24Ndiye Yehova anathira sulufule wamoto wochokera kumwamba kwa Yehova pa Sodomu ndi Gomora. 25Kotero, anawononga mizindayo, chigwa chonse pamodzi ndi onse okhala mʼmizindayo. Anawononganso zomera zonse za mʼdzikolo. 26Koma mkazi wa Loti anachewuka ndipo anasanduka mwala wa mchere.

27Mmawa mwake, Abrahamu ananyamuka nabwerera kumalo kumene anakumana ndi Yehova kuja. 28Anayangʼana kumunsi ku Sodomu, Gomora ndi ku dziko lonse la ku chigwa, ndipo anaona chiwutsi chikufuka mʼdzikolo ngati chikuchokera mʼngʼanjo.

29Choncho Mulungu anawononga mizinda ya ku chigwa, koma anakumbukira pemphero la Abrahamu natulutsa Loti ku sulufule ndi moto zimene zinawononga mizinda ya kumene Loti amakhalako.

Loti ndi Ana ake Aakazi

30Loti ndi ana ake awiri aakazi anachoka ku Zowari nakakhala ku mapiri, chifukwa amachita mantha kukhala ku Zowari. Iye ndi ana ake awiri ankakhala mʼphanga. 31Tsiku lina mwana wake wamkazi wamkulu anawuza mngʼono wake kuti, “Abambo athu ndi wokalamba ndipo palibe mwamuna aliyense pano woti atikwatire ndi kubereka ana monga mwa chikhalidwe cha pa dziko lonse lapansi. 32Tiye tiwamwetse vinyo ndipo tigone nawo. Tikatero mtundu wathu udzakhalapobe.”

33Usiku umenewo analedzeretsa vinyo abambo awo, ndipo wamkuluyo analowa nagona naye. Abambo awo samadziwa kanthu pamene mwanayo anagona naye kapena pamene anadzuka.

34Tsiku linali mwana wamkazi wamkulu uja anati kwa mngʼono wake, “Usiku wathawu ine ndinagona ndi abambo anga. Tiye tiwaledzeretsenso vinyo usiku uno ndipo iwe upite ndi kugona nawo ndipo mtundu wathu udzakhalapobe.” 35Choncho analedzeranso vinyo abambo awo usiku umenewonso, ndipo mwana wamkazi wamngʼono anapita nagona nawo. Abambo awo sanadziwenso kanthu pamene mwanayo anagona naye kapena pamene anadzuka.

36Choncho ana onse awiri a Loti aja anatenga pathupi pa abambo awo. 37Mwana wamkazi wamkulu uja anabereka mwana wa mwamuna ndipo anamutcha Mowabu. Iyeyo ndiye kholo la Amowabu onse. 38Mwana wamkazi wamngʼono naye anabereka mwana wamwamuna, ndipo anamutcha iye Beni-Ammi. Iyeyu ndiye kholo la Aamoni onse.

Священное Писание (Восточный перевод), версия для Таджикистана

Начало 19:1-38

Спасение Лута и разрушение городов Содома и Гоморры

1Когда к вечеру два ангела пришли в Содом, Лут сидел у ворот города. Увидев их, он встал им навстречу и поклонился лицом до земли.

2– Господа мои, – сказал он, – пожалуйста, зайдите в дом вашего раба. Вы сможете помыть ноги и переночевать, а ранним утром продолжите свой путь.

– Нет, – ответили они, – мы переночуем на площади.

3Но он так настаивал, что они последовали за ним и вошли в дом. Он приготовил для них еду, испёк пресные лепёшки, и они поели. 4Но прежде чем они легли, все мужчины Содома, молодые и старые, окружили дом.

5Они кричали Луту:

– Где люди, которые пришли к тебе вечером? Выведи их к нам, мы хотим надругаться над ними.

6Лут вышел к ним и запер за собой дверь. 7Он сказал:

– Нет, друзья мои, не делайте такого зла. 8Послушайте, у меня есть две дочери, которые никогда ещё не были с мужчиной. Давайте я выведу их к вам, и делайте с ними, что хотите. Но не делайте ничего этим людям, которые пришли под защиту моего крова.

9Они ответили:

– Прочь с дороги!

И сказали:

– Этот человек пришёл сюда как чужеземец, а теперь хочет быть нам судьёй! Мы поступим с тобой ещё хуже, чем с ними.

Они стали оттеснять Лута и подошли, чтобы выломать дверь. 10Но гости, которые оставались внутри, протянули руки, втащили Лута в дом и заперли дверь. 11А тех, кто были у двери дома, и молодых и старых, они поразили слепотой, так что те не могли найти дверь.

12И гости сказали Луту:

– Кто ещё у тебя здесь есть – зятья, сыновья, дочери, кто-нибудь ещё в городе? Выведи их отсюда, 13потому что мы собираемся уничтожить это место. Вопль к Вечному против этого народа так велик, что Он послал нас уничтожить его.

14Лут вышел и сказал своим будущим зятьям, женихам его дочерей:

– Скорее, уходите отсюда: Вечный собирается уничтожить город!

Но те подумали, что он шутит.

15Когда взошла заря, ангелы стали торопить Лута, говоря:

– Торопись! Уводи отсюда свою жену и двух дочерей, а не то ты погибнешь, когда наказание падёт на город.

16Он медлил, но те двое взяли его за руку, и его жену, и двух дочерей, потому что Вечный был к ним милостив, и вывели их за пределы города. 17Уже за пределами города один из них сказал:

– Бегите отсюда! Не оглядывайтесь назад и не останавливайтесь нигде в долине! Бегите в горы, а не то вы погибнете!

18Но Лут сказал им:

– Нет, господа, прошу вас! 19Раб ваш нашёл в ваших глазах расположение, и вы явили мне великую милость, спасая мою жизнь. Но в горы мне не добежать: бедствие настигнет меня, и я погибну. 20Вон тот городок недалеко, туда я успею добежать, и он невелик. Позвольте мне бежать туда – ведь он совсем мал, не так ли? – и моя жизнь будет спасена.

21Ангел ответил:

– Хорошо, я выполню и эту просьбу: я не разрушу города, о котором ты говоришь. 22Беги туда быстрее, потому что я ничего не могу сделать, пока ты не доберёшься до него. (Вот почему тот город был назван Цоар («малый»).)

23Солнце уже встало, когда Лут добрался до Цоара. 24Тогда Вечный пролил дождём горящую серу с небес19:24 Букв.: «Тогда Вечный пролил дождём горящую серу от Вечного с небес». на Содом и Гоморру: 25Он разрушил города и всю долину, и всех, кто жил в городах, и всё, что росло на земле. 26А жена Лута оглянулась назад и превратилась в соляной столб.

27На другое утро Иброхим поднялся рано и вернулся к тому месту, где он стоял перед Вечным. 28Он посмотрел на Содом и Гоморру и на всю долину и увидел: густой дым поднимается от земли, как дым из печи.

29Так, когда Всевышний уничтожил города долины, Он вспомнил Иброхима и спас Лута от бедствия, разрушившего города, в которых жил Лут.

Ужасный грех в семье Лута

30Лут вместе с двумя своими дочерьми покинул Цоар и поселился в горах, так как он боялся оставаться в Цоаре. Он и его дочери жили в пещере.

31Старшая дочь сказала младшей:

– Наш отец стар, а здесь нигде нет мужчины, чтобы лечь с нами по обычаю всей земли. 32Давай напоим отца вином и ляжем с ним, чтобы сохранить наш род через нашего отца.

33В ту ночь они напоили отца вином, и старшая дочь вошла и легла с ним. Он и не знал, когда она легла и когда встала. 34На другой день старшая дочь сказала младшей:

– Прошлой ночью я легла с отцом. Давай опять напоим его вином сегодня вечером, и ты войдёшь и ляжешь с ним, чтобы мы могли сохранить наш род через нашего отца.

35Они напоили отца вином и в эту ночь, и младшая дочь вошла и легла с ним. Он и не знал, когда она легла и когда встала.

36Так обе дочери Лута забеременели от отца. 37Старшая дочь родила сына и назвала его Моав («от отца»); он отец нынешних моавитян. 38Младшая дочь тоже родила сына и назвала его Бен-Амми («сын моего народа»); он отец нынешних аммонитян.