Genesis 16 – CCL & CCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Genesis 16:1-16

Sarai ndi Hagara

1Tsono Sarai, mkazi wa Abramu anali asanamuberekere ana Abramuyo. Koma anali ndi wantchito wamkazi wa ku Igupto dzina lake Hagara; 2ndipo Sarai anati kwa Abramu, “Yehova sanalole kuti ine ndikhale ndi ana. Bwanji mulowe mwa wantchito wanga wamkaziyu kuti mwina ndingaone ana kudzera mwa iyeyu.”

Abramu anamvera Sarai. 3Tsono Sarai anatenga Hagara wantchito wake wamkazi wa ku Igupto uja namupereka kwa Abramu mwamuna wake kuti akhale mkazi wake. Izi zinachitika Abramu atakhala ku Kanaani zaka khumi. 4Abramu atalowana ndi Hagara, Hagara uja anatenga mimba.

Pamene Hagara anadziwa kuti anali woyembekezera anayamba kunyoza mbuye wake Sarai. 5Pamenepo Sarai anati kwa Abramu, “Inu ndinu amene mwandiputira nkhanza zikundichitikirazi. Ndinakupatsani wantchito wanga wamkazi kuti akhale mkazi wanu, ndiye tsopano wayamba kundinyoza ine chifukwa wadziwa kuti ndi woyembekezera. Yehova ndiye amene aweruze pakati pa inu ndi ine.”

6Abramu anati, “Wantchito wakoyu ali mʼmanja mwako. Chita naye chilichonse chimene ukuganiza kuti ndi chokukomera.” Tsono Sarai anazunza Hagara mpaka anathawa.

7Mngelo wa Yehova anamupeza Hagara pafupi ndi chitsime mʼchipululu. Chinali chitsime chimene chili mʼmphepete mwa msewu wopita ku Suri. 8Ndipo mngeloyo anati, “Hagara, iwe wantchito wa Sarai, ukuchokera kuti ndipo ukupita kuti?”

Iye anayankha, “Ndikuthawa mbuye wanga Sarai.”

9Mngelo wa Yehova anamuwuza kuti, “Bwerera kwa mbuye wako ndipo ukamugonjere. 10Ndidzakupatsa zidzukulu zambiri zoti munthu sangaziwerenge.”

11Mngelo wa Yehova uja anamuwuzanso kuti,

“Ndiwe woyembekezera

ndipo udzabala mwana wamwamuna.

Udzamutcha dzina lake Ismaeli,

pakuti Yehova wamva kulira chifukwa cha kuzunzika kwako.

12Iye adzakhala munthu wa khalidwe ngati mʼmbulu wamisala;

adzadana ndi aliyense

ndipo anthu onse adzadana naye,

adzakhala mwaudani pakati pa abale ake

onse.”

13Hagara anatcha Yehova amene anamuyankhula uja dzina loti: “Ndinu Mulungu amene mumandiona,” popeza anati, “Ndakumana ndi Yehova atatha kundikomera mtima.” 14Nʼchifukwa chake chitsime chija chimene chili pakati pa Kadesi ndi Beredi chinatchedwa Beeri-lahai-roi.

15Tsono Hagara anamuberekera Abramu mwana wamwamuna ndipo Abramu anamutcha mwanayo Ismaeli. 16Pamene Hagara anamubalira Ismaeli nʼkuti Abramuyo ali ndi zaka 86.

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

创世记 16:1-16

夏甲与以实玛利

1亚伯兰的妻子撒莱没有生育,她有个婢女名叫夏甲,是埃及人。 2撒莱亚伯兰说:“耶和华不让我生育,请你与我的婢女同房,也许我可以借着她生子立后。”亚伯兰同意了撒莱的话。 3于是,撒莱埃及婢女夏甲亚伯兰做妾。那时亚伯兰已经在迦南住了十年。 4亚伯兰夏甲同房,她就怀了孕。夏甲知道自己怀了孕,就轻视女主人撒莱5撒莱亚伯兰说:“我受气都是因为你。我把婢女放在你怀里,她仗着自己怀了孕就轻视我,愿耶和华在你我之间主持公道。” 6亚伯兰撒莱说:“婢女在你手中,随你处置。”于是,撒莱苦待夏甲夏甲就逃走了。

7耶和华的天使在旷野中通往书珥之路的水泉旁找到了夏甲8便问她:“撒莱的婢女夏甲,你从哪里来?要到哪里去?”她回答说:“我是从女主人撒莱那里逃出来的。” 9耶和华的天使对她说:“你要回到女主人那里顺服她。” 10又说:“我必使你的后代多得不可胜数。” 11接着又说:“你现在怀了孕,将来会生一个男孩,你要给他取名叫以实玛利16:11 以实玛利”意思是“上帝听见了”。,因为耶和华已经听见你痛苦的哀声。 12这孩子性情必像野驴,他要跟人作对,人也要跟他作对。他必与他所有的弟兄为敌。” 13夏甲称对她说话的耶和华为“看顾人的上帝”,她说:“我竟然在这里看见了看顾我的上帝。” 14因此,她称加低斯巴列之间的那口井为庇耳·拉海·莱16:14 庇耳·拉海·莱”意思是“看顾我的永恒上帝之井”。

15后来夏甲亚伯兰生了一个儿子,亚伯兰给他取名叫以实玛利16夏甲以实玛利时,亚伯兰八十六岁。