Genesis 17 – CCL & CCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Genesis 17:1-27

Pangano la Mdulidwe

1Pamene Abramu anali ndi zaka 99, Yehova anamuonekera nati, “Ine ndine Mulungu Wamphamvuzonse. Ukhale munthu wochita zolungama nthawi zonse. 2Ndipo Ine ndikulonjeza kuti ndidzakupatsa zidzukulu zambiri.”

3Pomwepo Abramu anadziponya pansi ndipo Mulungu anati kwa iye, 4“Pangano langa ndi iwe ndi ili: Udzakhala kholo la mitundu yambiri ya anthu. 5Sudzatchedwanso Abramu; dzina lako lidzakhala Abrahamu, chifukwa ndakusandutsa kukhala kholo la mitundu yambiri ya anthu. 6Ndidzakupatsa zidzukulu zambiri motero kuti mitundu yambiri ya anthu idzatuluka mwa iwe. Mafumunso adzatuluka mwa iwe. 7Pangano langa ndi iwe pamodzi ndi zidzukulu za mibado ya mʼtsogolo lidzakhala la muyaya. Ndidzakhala Mulungu wako ndi Mulungu wa zidzukulu zako. 8Dziko lonse la Kanaani, limene iwe ukukhala tsopano, ndalipereka kwa iwe ndi kwa zidzukulu zako kuti likhale chuma chanu mpaka muyaya. Ndipo Ine ndidzakhala Mulungu wa zidzukulu zako.”

9Kenaka Mulungu anati kwa Abrahamu, “Koma iwe pamodzi ndi zidzukulu zako zobwera pambuyo pako mʼmibado ya mʼtsogolomo, sungani pangano langali. 10Iwe pamodzi ndi zidzukulu zako zobwera pambuyo pako muzisunga pangano ili loti mwamuna aliyense pakati panupa azichita mdulidwe. 11Kuyambira tsopano muzichita mdulidwe ndipo ichi chidzakhala chizindikiro cha pangano langa ndi iwe. 12Kuyambira tsopano mpaka mibado ya mʼtsogolomo mwana wamwamuna aliyense pakati panu amene wakwana masiku asanu ndi atatu ayenera kuchita mdulidwe. Awa ndi ana obadwa mʼbanja lako, kapena akapolo ochita kugula ndi ndalama, mlendo osakhala wa mʼmbumba yako. 13Achite mdulidwe ndithu mwana wamwamuna aliyense, mbadwa ngakhale kapolo wochita kugula ndi ndalama, ndipo ichi chidzakhala chizindikiro pa thupi lanu cha pangano langa lamuyaya. 14Mwamuna aliyense amene adzakhala wosachita mdulidwe adzachotsedwa pakati pa anthu ake chifukwa sanasunge pangano langa.”

15Mulungu anatinso kwa Abrahamu, “Sarai mkazi wako, sudzamutchanso Sarai; dzina lake lidzakhala Sara. 16Ndidzamudalitsa ndipo adzakubalira mwana wamwamuna. Ndidzamudalitsa kuti akhale mayi wa mitundu ya anthu; mafumu a anthuwo adzachokera mwa iye.”

17Abrahamu anadzigwetsa pansi pamaso pa Yehova, Iye anaseka nati, “Kodi munthu wa zaka 100 nʼkubala mwana? Kodi Sara adzabereka mwana pa msinkhu wa zaka makumi asanu ndi anayi?” 18Ndipo Abrahamu anati kwa Mulungu, “Bwanji mumudalitse Ismaeli.”

19Koma Mulungu anati, “Ayi, koma mkazi wako Sara adzakubalira mwana wamwamuna, ndipo udzamutcha Isake. Ndidzasunga pangano langa losatha ndi iyeyu komanso ndi zidzukulu zobwera pambuyo pake. 20Koma za Ismaeli, ndamva. Ndidzamudalitsadi, ndipo adzakhala ndi zidzukulu zambiri. Iye adzakhala kholo la mafumu khumi ndi awiri ndipo mwa iye mudzatuluka mtundu waukulu wa anthu. 21Koma ndidzasunga pangano langali ndi Isake amene Sara adzakubalira pofika nthawi ngati ino chaka chamawa.” 22Atatha kuyankhula, Mulungu anamuchokera Abrahamu.

23Tsono Abrahamu anachita mdulidwe mwana wake Ismaeli ndi onse amene anali mʼbanja lake, mbadwa ngakhale kapolo ochita kugula ndi ndalama, monga mmene Mulungu analamulira. 24Abrahamu anali ndi zaka 99 pamene anachita mdulidwe, 25ndipo mwana wake Ismaeli anali ndi zaka khumi ndi zitatu; 26Onse, Abrahamu ndi mwana wake Ismaeli, anachita mdulidwe tsiku limodzi. 27Aliyense wamwamuna wa pa banja pa Abrahamu, kuphatikizapo iwo amene anabadwira pa banja pomwepo kapena akapolo ogula ndi ndalama kwa alendo, anachita mdulidwe.

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

创世记 17:1-27

上帝再次与亚伯兰立约

1亚伯兰九十九岁那年,耶和华向他显现说:“我是全能的上帝。你要遵行我的旨意,做纯全无过的人。 2我要与你立约,我要使你子孙极其兴旺。” 3亚伯兰就俯伏在地,上帝又对他说: 4“我要与你立约,你必成为许多民族的始祖。 5以后你的名字不再叫亚伯兰,要改为亚伯拉罕17:5 亚伯拉罕”意思是“万族之父”。,因为我要立你为万族之父。 6我要使你的子孙极其兴旺,许多民族和君王必从你而出。 7我要和你并你的子子孙孙立永恒的约,我要做你和你子孙的上帝。 8我要把你现在寄居的整个迦南赐给你和你的后裔永远作产业,我也必做他们的上帝。”

9上帝又对亚伯拉罕说:“你和你的子孙世世代代都要遵守我的约。 10你们所有的男子都要受割礼,这是我与你和你的子孙所立的约,你们要遵守。 11你们都要割包皮,作为我与你们立约的记号。 12你们世世代代的男子在出生后的第八日都要接受割礼。在你家里出生的和用钱从外族人那里买来的奴仆也要受割礼。 13不论是在你家里生的,还是你用钱买来的男子,都要接受割礼,这样你们的肉体上就有我永恒之约的记号。 14任何没有接受割礼的男子,要将他从民中铲除,因为他违背了我的约。”

15上帝对亚伯拉罕说:“你的妻子以后不要叫撒莱,她的名字要叫撒拉16我必赐福给她,让她为你生一个儿子。她必成为万族的母亲,万民的君王必从她而出。” 17亚伯拉罕就俯伏在地,笑了起来,心想:“我一百岁了,还能有孩子吗?撒拉已经九十岁了,还能生养吗?” 18亚伯拉罕对上帝说:“愿以实玛利蒙你赐福。” 19上帝说:“不,你妻子撒拉必为你生一个儿子,你要给他取名叫以撒,我必向他和他的后代坚守我的约,直到永远。 20至于以实玛利,我已听见你的祈求,我必赐福给他,使他的后代极其兴旺昌盛。他必做十二个族长的父亲,我必使他成为大国。 21撒拉必在明年这时候给你生以撒,我必向他坚守我的约。” 22上帝说完以后,便离开亚伯拉罕上升而去。

23亚伯拉罕就在那天照着上帝的吩咐,为儿子以实玛利和家中所有的男子,不论是在家中出生的,还是买回来的,都行了割礼。 24亚伯拉罕接受割礼的时候九十九岁。 25他的儿子以实玛利接受割礼的时候十三岁。 26他们父子二人就在那天接受了割礼。 27亚伯拉罕家里所有的男子,包括家中出生的和买回来的,都一起接受了割礼。