Ezekieli 6 – CCL & NIRV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ezekieli 6:1-14

Uneneri Wotsutsa Mapiri a Israeli

1Yehova anandipatsa uthenga uwu kuti, 2“Iwe mwana wa munthu, yangʼana ku mapiri a Israeli; yankhula nawo modzudzula 3kuti, ‘Inu mapiri a ku Israeli, imvani mawu a Ambuye Yehova. Iye akuwuza mapiri, magomo, mitsinje ndi zigwa kuti: Ine ndizakuthirani nkhondo ndipo ndidzawononga nyumba zanu mʼmene mukupembedzeramo mafano. 4Maguwa anu ansembe adzagumulidwa ndipo maguwa anu ofukizira lubani adzaphwanyidwa; ndipo ndidzapha anthu anu pamaso pa mafano anu. 5Ine ndidzagoneka mitembo ya Aisraeli pamaso pa mafano awo, ndipo ndidzamwaza mafupa anu mozungulira maguwa anu ansembe. 6Konse kumene mumakhala, mizinda yanu idzasanduka bwinja. Nyumba zanu zopembedzera mafano zidzagumulidwa kotero kuti maguwa anu adzawonongedwa ndi kusakazidwa, mafano anu adzaphwanyidwa ndi kuwonongedwa. Maguwa anu ofukizirapo lubani adzagwetsedwa pansi ndipo zonse zimene munapanga zidzatheratu. 7Anthu anu adzaphedwa pakati panu, ndipo mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.’

8“Komabe ndidzasiya ena pangʼono opulumuka ku nkhondo. Iwowa ndidzawamwazira ku mayiko ena pakati pa anthu a mitundu ina. 9Pamenepo opulumuka mwa inu adzandikumbukira ku mayiko kumene anatengedwa ukapolo. Ndidzawamvetsa chisoni chifukwa cha kusakhulupirika kwawo ndi kundipandukira kuja ndiponso chifukwa kuti anayika mtima wawo pa mafano. Choncho adzachita okha manyazi chifukwa cha zoyipa zimene ankachita ndi miyambo yonyansa imene ankatsata. 10Ndipo iwo adzadziwa kuti ndine Yehova ndi kuti sindinkawaopseza chabe pamene ndinanena kuti ndidzawawononga.

11“Ambuye Yehova akuti: Womba mʼmanja mwako ndipo uponde mapazi ako pansi mwamphamvu ndipo ufuwule kuti, ‘Mayo!’ chifukwa cha zonyansa ndi zoyipa zonse zimene Aisraeli achita, pakuti adzaphedwa ndi lupanga, njala ndi mliri. 12Amene ali kutali adzafa ndi mliri, ndipo amene ali pafupi adzafa pa nkhondo, ndipo amene adzapulumuke ndi kusaphedwa adzafa ndi njala. Kotero ndidzakwaniritsa ukali wanga pa iwo. 13Ndipo iwo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova, pamene anthu awo adzagona atafa pakati pa mafano awo mozungulira maguwa awo ansembe, pamwamba pa magomo ndi mapiri onse, pansi pa mtengo uliwonse watambalala ndi wa thundu uliwonse wamasamba ambiri, kumalo kumene ankapereka nsembe zonunkhira kwa mafano awo onse. 14Choncho ndidzawalanga ndi mkono wanga ndi kusandutsa dziko kukhala bwinja. Dziko lonse kumene akukhala kuyambira ku chipululu mpaka ku mzinda wa Ribula ndidzalisandutsa bwinja. Pamenepo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.”

New International Reader’s Version

Ezekiel 6:1-14

Ezekiel Prophesies Against the Mountains of Israel

1A message from the Lord came to me. The Lord said, 2“Son of man, turn your attention to the mountains of Israel. Prophesy against them. 3Say, ‘Mountains of Israel, listen to the message of the Lord and King. Here is what he says to the mountains and hills. And here is what he says to the canyons and valleys. He tells them, “I will send swords to kill your people. I will destroy the high places where you worship other gods. 4Your altars will be torn down. Your incense altars will be smashed. And I will kill your people in front of the statues of your gods. 5I will put the dead bodies of Israelites in front of those statues. I will scatter your bones around your altars. 6No matter where you live, the towns will be destroyed. The high places will be torn down. So your altars will be completely destroyed. The statues of your gods will be smashed to pieces. Your incense altars will be broken down. And everything you have made will be wiped out. 7Your people will fall down dead among you. Then you will know that I am the Lord.

8“ ‘ “But I will spare some of you. Some will escape from being killed by swords. You will be scattered among other lands and nations. 9You will be taken away to those nations as prisoners. Those of you who escape will remember me. You will recall how much pain your unfaithful hearts gave me. You turned away from me. Your eyes longed to see the statues of your gods. You will hate yourselves because of all the evil things you have done. I hate those things too. 10You will know that I am the Lord. I said I would bring trouble on you. And my warning came true.” ’ ”

11The Lord and King said to me, “Clap your hands. Stamp your feet. Cry out, ‘How sad!’ Do this because the people of Israel have done so many evil things. I hate those things. Israel will be destroyed by war, hunger and plague. 12The one who is far away will die of the plague. The one who is near will be killed by swords. Anyone who is left alive and is spared will die of hunger. And in this way I will pour out my great anger on them. 13Then they will know that I am the Lord. Their people will lie dead among the statues of their gods around their altars. Their bodies will lie on every high hill and every mountaintop. They will lie under every green tree and leafy oak tree. They used to offer sweet-smelling incense to all their gods at those places. 14I will reach out my powerful hand against them. The land will become dry and empty. Those people will live from the desert all the way to Diblah. They will know that I am the Lord.”