Ezekieli 5 – CCL & NIRV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ezekieli 5:1-17

Chizindikiro cha Chiweruzo

1Tsiku lina Yehova anandiwuza kuti, “Iwe mwana wa munthu, tsopano tenga lupanga lakuthwa ndipo uligwiritse ntchito ngati lumo lometera. Umete tsitsi ndi ndevu zako. Kenaka utenge sikelo ndipo ugawe tsitsilo patatu. 2Kuzinga mzinda kuja kukatha, chimodzi cha zigawo zitatu za tsitsilo uchitenthe pakati pa mzinda. Chigawo chachiwiri uchiduledule ndi lupanga, poyenda muzungulire mzinda wonsewo. Chigawo chachitatu uchimwazire ku mphepo, ndidzachitsata nditasolola lupanga. 3Koma utengeko tsitsi pangʼono, ulimange mu mpindiro wa mkanjo wako. 4Pa tsitsi limeneli utapepo lina, uliponye pa moto ndi kulitentha. Moto udzayambira pamenepo mpaka ku nyumba yonse ya Israeli.”

5Ambuye Yehova akunena kuti, “Uyu ndi Yerusalemu amene ndamuyika pakati pa mitundu ya anthu, ndipo mayiko onse amuzungulira. 6Koma anthu a Yerusalemu aphwanya malamulo anga pochita zoyipa kuposa anthu a mitundu ina. Iwo anandipandukira kupambana anthu ena amene awazungulira. Iwo anakana malamulo anga ndipo sanasunge malangizo anga.

7“Nʼchifukwa chake Ambuye Yehova akuti: Popeza mwakhala osamvera kupambana anthu a mitundu ina amene akuzungulirani, popeza simunatsate malamulo anga kapena kusunga malangizo anga, mʼmalo mwake mwakhala mukutsata makhalidwe a anthu a mitundu ina amene akuzungulirani.

8“Tsono Ambuye Yehova akuti: Ine mwini ndikutsutsana nawe, Yerusalemu, choncho Ine ndidzakulangani. Ine ndidzakulangani anthu a mitundu ina akuona. 9Chifukwa cha ntchito zanu zonyansa ndidzakulangani ndi chilango chimene sindinakulangeni nacho nʼkale lomwe ndipo sindidzakulangani ndi chofanana nacho mʼtsogolomo. 10Tsono pakati panu makolo adzadya ana awo, ndipo ana adzadya makolo awo. Ndidzakulanga ndipo otsala onse ndidzawabalalitsa ku mphepo zonse zinayi. 11Ndithu, pali Ine, akutero Ambuye Yehova Wamoyo, pakuti mwayipitsa Nyumba yanga ndi mafano ano oyipa ndi miyambo yanu yonyansa, Inenso ndidzakulangani. Sindidzakulekererani kapena kukumverani chisoni. 12Chimodzi mwa zigawo zitatu za anthu ako chidzafa ndi mliri, kapena chidzawonongeka ndi njala; chigawo china chidzaphedwa ndi lupanga kunja kwa mzinda, ndipo chigawo china ndidzachibalalitsira ku mphepo zonse zinayi pochita kuchithamangitsa.

13“Ndi mmene udzachitire mkwiyo wanga. Ndikadzatsiriza kuwalanga, pamenepo mtima wanga udzakhala pansi. Adzadziwa kuti Ine Yehova ndinawayankhula mwa nsanje ndikadzawalanga.

14“Ndidzakusandutsa iwe bwinja ndi chinthu chonyozeka pakati pa anthu a mitundu ina amene akuzungulira, ndi kwa onse odutsapo 15Udzakhala chinthu chonyozeka ndi chonyogodoledwa. Udzakhala chenjezo ndi chinthu choopsa kwa anthu a mitundu ina amene akuzungulira ndikadzakulanga mokwiya ndi mwaukali ndi kugamula mlandu wako mokwiya. Ine Yehova ndayankhula. 16Pamene ndidzakulasa ndi njala yolasa ngati mivi yoopsa ndi yosakaza ndidzatero nʼcholinga choti ndikuwonongeni. Ndidzagwetsa njalayo pa iwe mowirikiza pochepetsa chakudya chako cha tsiku ndi tsiku. 17Ndidzatumiza njala ndi zirombo za kuthengo, ndipo zidzakulanda ana ako. Mliri ndi kuphana zidzakhala pakati pako, ndipo ndidzakubweretsera nkhondo. Ine Yehova ndayankhula.”

New International Reader’s Version

Ezekiel 5:1-17

God’s Judgment Will Be Like a Barber’s Razor

1“Son of man, get a sharp sword. Use it as a barber’s razor. Shave your head and beard with it. Then get a set of scales and weigh the hair. Separate it into three piles. 2Burn up a third of the hair inside the city. Do this when you stop attacking the model of Jerusalem. Next, get another third of the hair. Strike it with a sword all around the city. Then scatter the last third to the winds. That is because I will chase the people with a sword that is ready to strike them down. 3But save a few hairs. Tuck them away in the clothes you are wearing. 4Next, get a few more hairs. Throw them into the fire. Burn them up. The fire will spread to all the people of Israel.”

5The Lord and King says, “What you do with the hair stands for what I will do with Jerusalem’s people. I have placed that city in the center of the nations. Countries are all around it. 6But its people are sinful. They have refused to obey my laws and rules. They have turned their backs on my laws. They have not followed my rules. These people are worse than the nations and countries around them.”

7The Lord and King continues, “You people have been worse than the nations around you. You have not lived by my rules or kept my laws. You have not even lived up to the standards of the nations around you.”

8The Lord and King continues, “Jerusalem, I myself am against you. I will punish you in the sight of the nations. 9I will do to you what I have never done before and will never do again. That is because you worship statues of gods. I hate them. 10So parents will eat their own children inside the city. And children will eat their parents. I will punish you. And I will scatter to the winds anyone who is left alive. 11You have made my temple ‘unclean.’ You have set up statues of all your evil gods. You have done other things I hate. So I will cut you off just like Ezekiel cut off his hair. I will not spare you or feel sorry for you. And that is just as sure as I am alive,” announces the Lord and King. 12A third of your people will die of the plague inside your walls. Or they will die of hunger there. Another third will be killed by swords outside your walls. And I will scatter the last third of your people to the winds. I will chase them with a sword that is ready to strike them down.

13“Then I will not be angry anymore. My great anger against them will die down. And I will be satisfied. Then they will know that I have spoken with strong feelings. And my great anger toward them will come to an end. I am the Lord.

14“I will destroy you. I will bring shame on you in the sight of the nations around you. All those who pass by will see it. 15You will be put to shame. The nations will make fun of you. You will serve as a warning to others. They will be shocked when they see you. So I will punish you because I am very angry with you. You will feel the sting of my warning. I have spoken. I am the Lord. 16I will shoot at you with my deadly, destroying arrows of hunger. I will shoot to kill. I will bring more and more hunger on you. I will cut off your food supply. 17I will send hunger and wild animals against you. They will destroy all your children. Plague and murder will sweep over you. And I will send swords to kill you. I have spoken. I am the Lord.”