Ezekieli 39 – CCL & BPH

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ezekieli 39:1-29

1“Iwe mwana wa munthu, nenera modzudzula Gogi ndi kumuwuza kuti Ine Ambuye Yehova ndikuti: ‘Ine ndikudana nawe, iwe Gogi, kalonga wamkulu wa Mesaki ndi Tubala. 2Ine ndidzakuzunguza ndi kukupirikitsira kutsogolo. Ndidzakutenga kuchokera kutali kumpoto ndi kukutumiza kuti ukalimbane ndi anthu a ku mapiri a Israeli. 3Kenaka Ine ndidzathyola uta wa mʼdzanja lako lamanzere ndipo ndidzagwetsa mivi ya mʼdzanja lako lamanja. 4Udzagwa ku mapiri a ku Israeli, iwe ndi magulu ako onse ankhondo ndiponso mitundu ya anthu imene ili nawe. Ndidzakusandutsa chakudya cha mitundu yonse ya mbalame zodya nyama, ndiponso cha zirombo zakuthengo. 5Udzafera pa mtetete kuthengo, pakuti Ine ndayankhula. Ndikutero Ine Ambuye Yehova. 6Ndidzatumiza moto pa Magogi ndi pa onse amene amakhala mwamtendere mʼmbali mwa nyanja. Choncho adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.’

7“Ndidzachititsa kuti dzina langa loyera lidziwike pakati pa anthu anga Israeli. Sindidzalola kuti dzina langa liyipitsidwenso, ndipo mitundu ya anthu idzadziwa kuti Ine Yehova ndine Woyera mu Israeli. 8Zikubwera! Ndipo zidzachitikadi, ndikutero Ine Ambuye Yehova. Ndiye tsiku limene ndinanena lija.

9“Pamenepo okhala mʼmizinda ya Israeli adzatuluka ndipo adzasonkhanitsa zida zankhondo kuti zikhale nkhuni ndipo adzazitentha; zishango ndi lihawo, mauta ndi mivi, zibonga za nkhondo ndi mikondo. Adzazisonkhera moto kwa zaka zisanu ndi ziwiri. 10Iwo sadzatolera nkhuni kuthengo kapena kukadula ku nkhalango, chifukwa adzasonkhera moto zidazo. Ndipo iwo adzafunkha amene anawafunkhawo, ndi kulanda chuma cha amene anawalanda, ndikutero Ine Ambuye Yehova.

11“Pa tsiku limenelo ndidzamupatsa Gogi manda mu Israeli, mʼchigwa cha apaulendo, kummawa kwa Nyanja Yakufa. Mandawo adzatseka njira ya apaulendo, chifukwa Gogi ndi gulu lake lankhondo adzayikidwa kumeneko. Ndipo chigwacho chidzatchedwa chigwa cha gulu lankhondo la Gogi.

12“Nyumba ya Israeli idzakhala ikukwirira mitembo kwa miyezi isanu ndi iwiri ndi cholinga choyeretsa dziko. 13Anthu onse a mʼdzikomo adzakwirira nawo mitembo. Ntchito imeneyo adzatchuka nayo pa tsiku limene ndidzaonetsa ulemerero wanga. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.

14“Patapita miyezi isanu ndi iwiri adzalemba ntchito anthu ena odzayenda mʼdziko lonse kufunafuna mitembo imene inatsalira nʼkumayikwirira. Choncho adzayeretseratu dzikolo. 15Poyenda mʼdzikomo azidzati akaona fupa la munthu azidzayikapo chizindikiro pambali pake mpaka okumba manda atakalikwirira fupalo ku chigwa cha gulu lankhondo la Gogi. 16(Komwekonso kudzakhala mzinda wotchedwa Gulu la nkhondo). Ndipo potero adzayeretsa dziko.

17“Tsono iwe mwana wa munthu, Ine Ambuye Yehova ndikuti: Itana mbalame za mitundu yonse ndi zirombo zonse zakuthengo ndipo uziwuze kuti, ‘Sonkhanani ndipo bwerani kuchokera ku mbali zonse ku nsembe imene ndikukonzerani inu, nsembe yayikulu pa mapiri a Israeli. Kumeneko inu mudzadya mnofu ndi kumwa magazi. 18Mudzadya mnofu wa anthu ankhondo amphamvu ndi kumwa magazi a akalonga a dziko lapansi. Onsewo anaphedwa ngati nkhosa zazimuna, ana ankhosa onenepa, mbuzi ndiponso ngati ngʼombe zazimuna zonenepa za ku Basani. 19Ku phwando lansembe limene ndikukonzera inulo, mudzadya zonona mpaka kukhuta ndi kumwa magazi mpaka kuledzera. 20Pa tebulo langa mudzakhuta pakudya akavalo ndi okwerapo ake, anthu amphamvu ndi asilikali amitundumitundu,’ ndikutero Ine Ambuye Yehova.

21“Ine ndidzaonetsa ulemerero wanga pakati pa anthu a mitundu ina, ndipo adzaona mmene ndidzawalangire ndikadzayika dzanja langa pa iwo. 22Kuyambira tsiku limenelo mpaka mʼtsogolo Aisraeli adzadziwa kuti Ine ndine Yehova Mulungu wawo. 23Ndipo anthu a mitundu ina adzadziwa kuti anthu a Israeli anatengedwa ukapolo chifukwa cha tchimo lawo, chifukwa anali osakhulupirika kwa Ine. Choncho Ine ndinawabisira nkhope yanga ndi kuwapereka kwa adani awo. Motero anaphedwa pa nkhondo. 24Ndinawachita zimenezi chifukwa cha kunyansa kwawo ndi zolakwa zawo, ndipo ndinawabisira nkhope yanga.

25“Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti: Tsopano ndidzakhazikanso pa bwino banja la Yakobo. Ndidzachitira chifundo Aisraeli onse, ndipo ndidzateteza dzina langa loyera. 26Anthuwo akadzakhala mwamtendere mʼdziko lawo popanda wina wowaopseza, pamenepo adzayiwala zamanyazi zawo zimene zinawachitikira chifukwa chosandikhulupirira Ine. 27Ndidzawabwezeranso kwawo kuchokera pakati pa anthu a mitundu ina ndipo ndidzawasonkhanitsa kuchokera ku mayiko a adani awo. Poteropo ndidzaonetsa pamaso pa anthu a mitundu yambiri kuti ndine Woyera. 28Pamenepo iwo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova Mulungu wawo, ngakhale kuti ndinawapereka ku ukapolo pakati pa anthu a mitundu ina. Ine ndidzawasonkhanitsanso ku dziko lawo osasiyako wina mʼmbuyo. 29Ine sindidzawabisiranso nkhope yanga, pakuti ndidzathira Mzimu wanga pa Aisraeli. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.”

Bibelen på hverdagsdansk

Ezekiels Bog 39:1-29

Gogs fald og Israels frelse

1Herren fortsatte: „Du menneske, profetér videre imod Gog og sig til ham: ‚Du fyrste over Meshek og Tubal, jeg kæmper imod dig. 2Jeg vender dig om og trækker dig fra det høje nord ned til Israels højland. 3Der slår jeg buen ud af din venstre hånd og pilene ud af din højre. 4Derpå skal I alle dø, både du selv, dine hære og dine allierede, og I skal blive til føde for rovfugle og vilde dyr. 5Aldrig skal du nå frem til Israels byer, for du skal falde på åben mark. Jeg har talt, siger Gud Herren. 6Jeg vil lade ild regne ned over Magog og dem, som lever i tryghed langs kysterne, så de indser, at jeg er Herren.’

7På den måde skal min hellighed blive kendt i hele Israel. Jeg vil ikke længere acceptere, at mit navn bliver vanæret. Alle nationer skal erkende at jeg, Herren, er Israels hellige Gud. 8Det vil ske, som jeg har sagt.

9Da skal indbyggerne i Israels byer gå ud og indsamle alle deres fjenders våben: skjolde, buer og pile, kastespyd og lanser, og bruge dem til brændsel. Der bliver brændsel nok til syv års forbrug. 10I den periode behøver de ikke bekymre sig om at samle brænde på markerne eller fælde træer i skoven, for der er rigeligt med brændsel fra våbnene. Sådan skal Israels folk plyndre de folk, der kom for at plyndre dem, siger Herren.

11Til den tid vil jeg berede en gravplads for Gog i Israel, i den dal der bruges til gennemrejse, øst for havet.39,11 Formodentlig Det Døde Hav. Der skal Gog og alle hans hære begraves, så dalen bliver spærret for gennemrejse. Dalen vil derefter blive kaldt ‚Gogs Massegrav’. 12-13Det vil tage Israels folk syv måneder at begrave alle ligene, selv om alle hjælper til. Først da kan landet blive renset. Det bliver en herlig dag for Israel, når jeg viser min herlighed og magt. 14Når de syv måneder er gået, skal man udpege folk til systematisk at gennemsøge landet for eventuelle døde, som endnu ikke er blevet begravet. 15-16Hvis de så finder nogle skeletrester, skal de afmærke stedet, så graverne kan få dem begravet i ‚Gogs Massegrav’. Selv en af byerne i dalen vil få navn efter massegraven. Sådan skal landet omsider blive renset fra al den urenhed, som ligene var årsag til.

17Du menneske, kald alle rovfuglene og de vilde dyr sammen til en mægtig offerfest. Lad dem komme fra nær og fjern til Israels bjergland og tage del i festen, hvor de skal æde menneskekød og drikke menneskeblod. 18-19Sig til fuglene og dyrene: ‚Kom til den offerfest, jeg holder for jer i Israels bjergland. Spis kød fra helte og drik blod fra fyrster, som var det fede væddere, lam, geder eller okser fra Bashan. Æd, til I revner, og drik jer berusede i blod. 20Kom til festen og spis jer mætte i heste og ryttere, helte og krigere.’ ”

21Herren fortsatte: „Jeg vil demonstrere min magt og herlighed over for nationerne. De bliver alle vidne til, hvordan jeg straffer Gog og hele hans hær.

22Fra den dag og i al fremtid vil Israels folk erkende, at jeg er Herren, deres Gud, 23og nationerne vil forstå, hvorfor Israels folk blev sendt i landflygtighed. Jeg måtte straffe dem for deres oprør og utroskab imod mig. Derfor vendte jeg ryggen til dem og lod deres fjender ødelægge dem. 24De fik den straf, de havde fortjent på grund af alle deres synder.

25Men nu vil jeg genoprette mit folk, siger Gud Herren. Jeg forbarmer mig over Israels folk for mit navns æres skyld. 26Da skal de få lov til at bo trygt og fredeligt i deres eget land uden at frygte for at blive jaget bort, og de skal med skam mindes deres tidligere oprør og utroskab overfor mig. 27Når jeg fører dem hjem fra fjendeland og på den måde demonstrerer min hellighed over for verden, 28vil de indse, at jeg er Herren, deres Gud, som sendte dem i landflygtighed, og som førte dem hjem igen til deres land uden at glemme en eneste af dem. 29Jeg vil aldrig igen vende ryggen til mit folk, når jeg først har udgydt min Ånd over dem, siger Gud Herren.”