Ezekieli 35 – CCL & CCBT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ezekieli 35:1-15

Za Chilango cha Edomu

1Yehova anandiyankhula kuti: 2“Iwe mwana wa munthu, yangʼana phiri la Seiri; yankhula moliyimba mlandu ndipo 3awawuze anthu a kumeneko kuti zimene ndikuyankhula Ine Ambuye Yehova ndi izi: Inu anthu a ku mapiri a Seiri ndikudana nanu. Ndidzatambasula dzanja langa kulimbana nanu, ndipo ndidzasandutsa dziko lanu kukhala chipululu. 4Mizinda yanu ndidzayisandutsa mabwinja, ndipo dziko lanu lidzasanduka chipululu. Zikadzachitika izi mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.

5“Munali adani a Israeli nthawi zonse, ndipo munkalola kuti Aisraeli aphedwe pa nkhondo pa nthawi ya mavuto awo, pa nthawi imene chilango chawo chinafika pachimake. 6Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti: Pali Ine wamoyo, ndithu ndidzakukanthani. Imfa idzakulondolani. Popeza sunadane nako kukhetsa magazi, imfa idzakulondola. 7Phiri la Seiri ndidzalisandutsa chipululu ndipo ndidzapha onse amene amapita nabwerera kumeneko. 8Ndidzaza mapiri ake ndi mitembo. Ophedwa pa nkhondo adzagwera pa zitunda zanu, zigwa zanu ndi mʼmitsinje yanu yonse. 9Ndidzasandutsa dziko lanu kukhala chipululu mpaka muyaya, ndipo mʼmizinda yanu simudzakhalanso anthu. Zikadzachitika izi mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.

10“Inu munanena kuti, ‘Mitundu iwiri iyi ya anthu, Yuda ndi Israeli, pamodzi ndi mayiko awo omwe idzakhala yathu.’ Munanena chomwechi ngakhale kuti Ine Yehova ndinali momwemo. 11Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti: Pali Ine wamoyo, ndithu ndidzachita nanu monga munachita ndi anthu a ku Yuda ndi Israeli poonetsa mkwiyo wanu, nsanje yanu ndi chidani chanu pa iwo. Ndikadzakulangani mudzandidziwadi pakati panupo. 12Ndipo mudzadziwa kuti Ine Yehova ndinamva mawu anu onse onyoza amene munanena molimbana ndi mapiri a Israeli. Inu munati, ‘Mapiri a Israeli asanduka bwinja, ndipo aperekedwa kwa ife kuti tiwawononge.’ 13Mawu anu amene munayankhula monyada kundinyoza Ine ndinawamva. 14Ine Ambuye Yehova ndikuti: Dziko lonse lapansi lidzasangalala pamene ndidzakusandutsani bwinja. 15Monga momwe inu munasangalala pamene anthu anga Aisraeli anagwa, Inenso ndidzakuchitani chimodzimodzi. Udzasanduka bwinja, iwe Phiri la Seiri, iwe ndi dziko lonse la Edomu. Zikadzatero anthu onse adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.”

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

以西結書 35:1-15

預言以東受懲罰

1耶和華對我說: 2「人子啊,你要面向西珥山,發預言斥責它, 3告訴它,主耶和華這樣說,『西珥山啊,我要與你為敵,伸手攻擊你,使你荒涼不堪。 4我要使你的城邑淪為廢墟,一片荒涼,這樣你就知道我是耶和華。 5因為你永懷仇恨,在以色列人遭遇危難、因罪惡受盡刑罰的時候,把他們交在刀下。 6所以主耶和華說,我憑我的永恆起誓,你既然不憎恨殺人流血之事,殺人流血之事必臨到你。 7我要使西珥山荒涼不堪,消滅一切來往此地的人, 8我要使喪身刀下的人遍佈你的高山、丘陵、山谷和溪流。 9我要使你永遠荒廢,你的城邑杳無人跡,這樣你就知道我是耶和華。

10「『因為你曾說,猶大以色列必歸我,即使上帝在那裡,我們也要吞併他們。 11所以主耶和華說,我憑我的永恆起誓,你憎恨他們,滿腹怒氣和嫉妒,我也必這樣對待你。我審判你的時候,以色列人就會認識我。 12那時,你必知道我耶和華聽見了你譭謗以色列山嶺的一切話,你說,這些山嶺荒廢了,歸我們所有了。 13你妄自尊大,肆意譭謗我,我都聽見了。 14主耶和華這樣說,普天下歡樂的時候,我要使你荒涼。 15你既因以色列的荒涼而幸災樂禍,我要讓你遭受同樣的下場。西珥山啊,你和以東都要荒涼。這樣,你們就知道我是耶和華。』