Ezekieli 30 – CCL & KJV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ezekieli 30:1-26

Za Kulangidwa kwa Igupto

1Yehova anandiyankhula kuti: 2“Iwe mwana wa munthu, nenera ndipo ulengeze zimene Ine Ambuye Yehova ndikunena.

“ ‘Ufuwule mawu awa akuti,

‘Kalanga, tsiku lafika!’

3Pakuti tsiku layandikira,

tsiku la Yehova lili pafupi,

tsiku la mitambo yakuda,

tsiku lachiwonongeko cha mitundu ya anthu.

4Lupanga lidzabwera kudzalimbana ndi Igupto

ndipo mavuto adzafika pa Kusi.

Pamene anthu ambiri adzaphedwa mu Igupto,

chuma chake chidzatengedwa

ndipo maziko ake adzagumuka.

5Kusi, Puti, Ludi ndi Arabiya yense, Libiya ndiponso anthu a mʼdziko logwirizana naye adzaphedwa ndi lupanga pamodzi ndi Igupto.

6“ ‘Ine Ambuye Yehova ndikuti:

“ ‘Onse othandiza Igupto adzaphedwa

ndipo kunyadira mphamvu zake kudzatheratu.

Adzaphedwa ndi lupanga

kuyambira ku Migidoli mpaka ku mzinda wa Asiwani,’ ”

ndikutero Ine Ambuye Yehova.

7“ ‘Dziko la Igupto lidzasanduka bwinja

kupambana mabwinja ena onse opasuka,

ndipo mizinda yake idzakhala yopasuka

kupambana mizinda ina yonse.

8Nditatha kutentha Igupto

ndi kupha onse omuthandiza,

pamenepo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.

9“ ‘Nthawi imeneyo ikadzafika, amithenga adzapita mofulumira kuchokera kwa Ine kukaopseza Kusi, iwowo osadziwako kanthu. Ndipo adzada nkhawa pa tsiku limene Igupto adzawonongedwa, chifukwa tsikulo lidzafika ndithu.

10“ ‘Ine Ambuye Yehova ndikuti,

“ ‘Ndidzagwiritsa ntchito Nebukadinezara, mfumu ya ku Babuloni

kuti ndithetse gulu lankhondo la Igupto.

11Iye ndi gulu lake lankhondo, mtundu wa anthu ankhanza kwambiri aja

adzabwera kudzawononga dzikolo.

Adzasolola malupanga awo kulimbana ndi Igupto

ndipo dziko lidzadzaza ndi mitembo.

12Ndidzawumitsa mtsinje wa Nailo

ndi kugulitsa dziko la Igupto kwa anthu oyipa.

Ndidzagwiritsa ntchito anthu achilendo kuti ndiwononge dzikolo

pamodzi ndi zonse zili mʼmenemo.

Ine Yehova ndayankhula.

13“ ‘Ine Ambuye Yehova ndikuti,

“ ‘Ndidzawononga mafano

ndi kuthetsa milungu yosema ya ku Mefisi.

Simudzakhalanso mfumu mu Igupto,

ndipo ndidzaopseza dziko lonse.

14Ndidzasandutsa chipululu mzinda wa Patirosi,

ndi kutentha mzinda wa Zowani.

Ndidzalanga mzinda wa Thebesi.

15Ndidzakhuthulira ukali wanga pa mzinda wa Peluziumu,

linga lolimba la Igupto,

ndi kuwononga gulu lankhondo la Thebesi.

16Ndidzatentha ndi moto dziko la Igupto;

Peluziumu adzazunzika ndi ululu.

Malinga a Thebesi adzagumuka,

ndipo mzindawo udzasefukira ndi madzi.

17Anyamata a ku Oni ndi ku Pibeseti

adzaphedwa ndi lupanga

ndipo okhala mʼmizinda yake adzatengedwa ukapolo.

18Ku Tehafinehezi kudzakhala mdima

pamene ndidzathyola goli la Igupto;

motero kunyada kwake kudzatha.

Iye adzaphimbidwa ndi mitambo yakuda,

ndipo okhala mʼmizinda yake adzapita ku ukapolo.

19Kotero ndidzalanga dziko la Igupto,

ndipo iwo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.’ ”

Farao Watha Mphamvu

20Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri la mwezi woyamba wa chaka chakhumi ndi chimodzi, Yehova anandiyankhula kuti: 21“Iwe mwana wa munthu, ndathyola dzanja la Farao mfumu ya Igupto. Taona, silinamangidwe kuti lipole, ngakhale kulilimbitsa ndi nsalu kuti lithe kugwiranso lupanga. 22Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti, Ine ndikudana ndi Farao mfumu ya Igupto. Ndidzathyola manja ake onse; dzanja labwino pamodzi ndi lothyokalo, ndipo lupanga lidzagwa mʼmanja mwake. 23Ndidzamwaza Aigupto pakati pa mitundu ya anthu ndikuwabalalitsira ku mayiko ambiri. 24Ndidzalimbitsa manja a mfumu ya ku Babuloni, ndipo mʼmanja mwake ndidzayikamo lupanga langa. Koma ndidzathyola manja a Farao, ndipo adzabuwula ngati wolasidwa koopsa pamaso pa mfumu ya ku Babuloniyo. 25Ndidzalimbitsa manja a mfumu ya ku Babuloni, koma manja a Farao adzafowoka. Motero anthu adzadziwa kuti Ine ndine Yehova, ndikadzayika lupanga langa mʼmanja mwa mfumu ya ku Babuloni. Ndipo adzaligwiritsa ntchito pothira nkhondo dziko la Igupto. 26Ndidzamwaza Aigupto pakati pa mitundu ya anthu, ndikuwabalalitsira ku mayiko ambiri. Motero adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.”

King James Version

Ezekiel 30:1-26

1The word of the LORD came again unto me, saying, 2Son of man, prophesy and say, Thus saith the Lord GOD; Howl ye, Woe worth the day! 3For the day is near, even the day of the LORD is near, a cloudy day; it shall be the time of the heathen. 4And the sword shall come upon Egypt, and great pain shall be in Ethiopia, when the slain shall fall in Egypt, and they shall take away her multitude, and her foundations shall be broken down.30.4 pain: or, fear 5Ethiopia, and Libya, and Lydia, and all the mingled people, and Chub, and the men of the land that is in league, shall fall with them by the sword.30.5 Libya: Heb. Phut30.5 men: Heb. children 6Thus saith the LORD; They also that uphold Egypt shall fall; and the pride of her power shall come down: from the tower of Syene shall they fall in it by the sword, saith the Lord GOD.30.6 from…: or, from Migdol to Syene 7And they shall be desolate in the midst of the countries that are desolate, and her cities shall be in the midst of the cities that are wasted. 8And they shall know that I am the LORD, when I have set a fire in Egypt, and when all her helpers shall be destroyed.30.8 destroyed: Heb. broken 9In that day shall messengers go forth from me in ships to make the careless Ethiopians afraid, and great pain shall come upon them, as in the day of Egypt: for, lo, it cometh. 10Thus saith the Lord GOD; I will also make the multitude of Egypt to cease by the hand of Nebuchadrezzar king of Babylon. 11He and his people with him, the terrible of the nations, shall be brought to destroy the land: and they shall draw their swords against Egypt, and fill the land with the slain. 12And I will make the rivers dry, and sell the land into the hand of the wicked: and I will make the land waste, and all that is therein, by the hand of strangers: I the LORD have spoken it.30.12 dry: Heb. drought30.12 all…: Heb. the fulness thereof 13Thus saith the Lord GOD; I will also destroy the idols, and I will cause their images to cease out of Noph; and there shall be no more a prince of the land of Egypt: and I will put a fear in the land of Egypt. 14And I will make Pathros desolate, and will set fire in Zoan, and will execute judgments in No.30.14 Zoan: or, Tanis 15And I will pour my fury upon Sin, the strength of Egypt; and I will cut off the multitude of No.30.15 Sin: or, Pelusium 16And I will set fire in Egypt: Sin shall have great pain, and No shall be rent asunder, and Noph shall have distresses daily. 17The young men of Aven and of Pi-beseth shall fall by the sword: and these cities shall go into captivity.30.17 Aven: or, Heliopolis30.17 Pi-beseth: or, Pubastum 18At Tehaphnehes also the day shall be darkened, when I shall break there the yokes of Egypt: and the pomp of her strength shall cease in her: as for her, a cloud shall cover her, and her daughters shall go into captivity.30.18 darkened: or, restrained 19Thus will I execute judgments in Egypt: and they shall know that I am the LORD.

20¶ And it came to pass in the eleventh year, in the first month, in the seventh day of the month, that the word of the LORD came unto me, saying, 21Son of man, I have broken the arm of Pharaoh king of Egypt; and, lo, it shall not be bound up to be healed, to put a roller to bind it, to make it strong to hold the sword. 22Therefore thus saith the Lord GOD; Behold, I am against Pharaoh king of Egypt, and will break his arms, the strong, and that which was broken; and I will cause the sword to fall out of his hand. 23And I will scatter the Egyptians among the nations, and will disperse them through the countries. 24And I will strengthen the arms of the king of Babylon, and put my sword in his hand: but I will break Pharaoh’s arms, and he shall groan before him with the groanings of a deadly wounded man. 25But I will strengthen the arms of the king of Babylon, and the arms of Pharaoh shall fall down; and they shall know that I am the LORD, when I shall put my sword into the hand of the king of Babylon, and he shall stretch it out upon the land of Egypt. 26And I will scatter the Egyptians among the nations, and disperse them among the countries; and they shall know that I am the LORD.