Ezekieli 28 – CCL & CST

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ezekieli 28:1-26

Mawu Odzudzula Mfumu ya Turo

1Yehova anandiyankhula nati: 2“Iwe mwana wa munthu, iwuze mfumu ya ku Turo mawu a Ine Ambuye Yehova akuti,

“ ‘Iwe ndi mtima wako wodzikuza

umanena kuti, ‘Ine ndine mulungu;

ndimakhala pa mpando wa mulungu

pakati pa nyanja.’

Koma ndiwe munthu chabe osati mulungu,

ngakhale ukuganiza kuti ndiwe wanzeru ngati mulungu.

3Taona, ndiwedi wanzeru kupambana Danieli.

Ndipo palibe chinsinsi chobisika kwa iwe.

4Mwa nzeru zako ndi kumvetsa kwako

unadzipezera chuma

ndipo unasonkhanitsa golide ndi siliva

mʼnyumba zosungira chuma chako.

5Ndi nzeru zako zochitira malonda

unachulukitsa chuma chako

ndipo wayamba kunyada

chifukwa cha chuma chakocho.

6“ ‘Choncho Ine Ambuye Yehova ndikuti,

“ ‘Popeza umadziganizira

kuti ndiwe mulungu,

7Ine ndidzabwera ndi anthu achilendo, anthu ankhanza,

kuti adzalimbane nawe.

Adzakuthira nkhondo kuti awononge zonse zimene unazipeza ndi nzeru zako,

ndipo adzawononga kunyada kwakoko.

8Iwo adzakuponyera ku dzenje

ndipo udzafa imfa yoopsa

mʼnyanja yozama.

9Kodi udzanenabe kuti, ‘Ine ndine mulungu,’

pamaso pa iwo amene akukupha?

Iwe udzaoneka kuti ndiwe munthu chabe, osati mulungu,

mʼmanja mwa iwo amene akukuphawo.

10Udzafa imfa ya anthu osachita mdulidwe

mʼmanja mwa anthu achilendo.

Ine ndayankhula zimenezi, akutero Ambuye Yehova.’ ”

11Yehova anandiyankhula kuti: 12“Iwe mwana wa munthu, imba nyimbo yodandaulira mfumu ya Turo ndipo uyiwuze mawu a Ine Ambuye Yehova akuti,

“ ‘Iwe unali chitsanzo cha ungwiro weniweni,

wodzaza ndi nzeru ndi wokongola kwambiri.

13Iwe unkakhala ngati mu Edeni,

munda wa Mulungu.

Miyala yokongola ya mitundu yonse:

rubi, topazi ndi dayimondi,

kirisoliti, onikisi, yasipa,

safiro, kalineliyoni ndi berili ndiwo inali zofunda zako.

Ndipo zoyikamo miyalayo zinali zagolide.

Anakupangira zonsezi pa tsiku limene unalengedwa.

14Ndinayika kerubi kuti azikulondera.

Unkakhala pa phiri langa lopatulika,

ndipo unkayendayenda

pakati pa miyala ya moto.

15Makhalidwe ako anali abwino

kuyambira pamene unalengedwa

mpaka nthawi imene unayamba kuchita zoyipa.

16Unatanganidwa ndi zamalonda.

Zotsatira zake zinali zoti unachulukitsa zandewu

ndi kumachimwa.

Choncho ndinakuchotsa ku phiri langa lopatulika.

Mkerubi amene ankakulondera uja anakupirikitsa

kukuchotsa ku miyala yamoto.

17Unkadzikuza mu mtima mwako

chifukwa cha kukongola kwako,

ndipo unayipitsa nzeru zako

chifukwa chofuna kutchuka.

Kotero Ine ndinakugwetsa pansi

kuti ukhala chenjezo pamaso pa mafumu.

18Ndi malonda ako achinyengo unachulukitsa machimo ako.

Motero unayipitsa malo ako achipembedzo.

Choncho ndinabutsa moto pakati pako,

ndipo unakupsereza,

ndipo unasanduka phulusa pa dziko lapansi

pamaso pa anthu onse amene amakuona.

19Anthu onse amitundu amene ankakudziwa

akuchita mantha chifukwa cha iwe.

Watheratu mochititsa mantha

ndipo sudzakhalaponso mpaka muyaya.’ ”

Za Chilango cha Sidoni

20Yehova anandiyankhula nati: 21“Iwe mwana wa munthu, utembenukire ku mzinda wa Sidoni ndipo unenere mowudzudzula kuti, 22‘Ine Ambuye Yehova ndikuti,

“ ‘Ndine mdani wako, iwe Sidoni,

ndipo ndidzalemekezedwa chifukwa cha iwe.

Anthu adzadziwa kuti Ine ndine Yehova

ndikadzakulanga ndi kudzionetsa kuti

ndine woyera pakati pako.

23Ndidzatumiza mliri pa iwe

ndi kuchititsa magazi kuti ayende mʼmisewu yako.

Anthu ophedwa ndi lupanga

adzagwa mbali zonse.

Pamenepo iwo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.

24“ ‘Nthawi imeneyo Aisraeli sadzakhalanso ndi anthu pafupi achipongwe amene ali ngati nthula zowawa ndi ngati minga zopweteka. Pamenepo iwo adzadziwa kuti Ine ndine Ambuye Yehova.

25“ ‘Ine Ambuye Yehova mawu anga ndi awa: Nditasonkhanitsa Aisraeli kuchoka ku mayiko kumene anamwazikira, ndidzadzionetsa kuti ndine woyera pakati pawo pamaso pa anthu a mitundu ina. Adzakhala mʼdziko lawo, limene ndinalipereka kwa mtumiki wanga Yakobo. 26Adzakhala kumeneko mwamtendere ndipo adzamanga nyumba ndi kulima minda ya mpesa. Adzakhala kumeneko mwamtendere pamene ndidzalange anthu oyandikana nawo, amene ankawanyoza. Motero iwo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova Mulungu wawo.’ ”

Nueva Versión Internacional (Castilian)

Ezequiel 28:1-26

Profecía contra el rey de Tiro

1El Señor me habló diciendo: 2«Hijo de hombre, adviértele al rey de Tiro que así dice el Señor omnipotente:

»“En la intimidad de tu arrogancia dijiste:

‘Yo soy un dios.

Me encuentro en alta mar

sentado en un trono de dioses’.

¡Pero tú no eres un dios,

aunque te creas que lo eres!

¡Tú eres un simple mortal!

3¿Acaso eres más sabio que Daniel?28:3 Daniel. Alt. Danel.

¿Acaso conoces todos los secretos?

4Con tu sabiduría y tu inteligencia

has acumulado muchas riquezas,

y en tus cofres has amontonado

mucho oro y mucha plata.

5Eres muy hábil para el comercio;

por eso te has hecho muy rico.

A causa de tus grandes riquezas

te has vuelto muy arrogante.

6Por eso, así dice el Señor omnipotente:

»”Ya que pretendes ser

tan sabio como un dios,

7haré que vengan extranjeros contra ti,

los más feroces de las naciones:

desenvainarán la espada

contra tu hermosura y sabiduría,

y profanarán tu esplendor.

8Te hundirán en la fosa,

y en alta mar sufrirás una muerte violenta.

9Y aun así, en presencia de tus verdugos,

¿te atreverás a decir: ¡Soy un dios!?

¡Pues en manos de tus asesinos

no serás un dios, sino un simple mortal!

10Sufrirás a manos de extranjeros

la muerte de los incircuncisos,

porque yo lo he dicho.

Lo afirma el Señor omnipotente”».

11El Señor me habló diciendo: 12«Hijo de hombre, entona una elegía al rey de Tiro y adviértele que así dice el Señor omnipotente:

»“Eras un modelo de perfección,

lleno de sabiduría y de hermosura perfecta.

13Estabas en Edén, en el jardín de Dios,

adornado con toda clase de piedras preciosas:

rubí, crisólito, jade,

topacio, cornalina, jaspe,

zafiro, granate y esmeralda.

Tus joyas y encajes estaban cubiertos de oro,

y especialmente preparados para ti

desde el día en que fuiste creado.

14Fuiste elegido querubín protector,

porque yo así lo dispuse.28:14 Fuiste … dispuse. Texto de difícil traducción.

Estabas en el santo monte de Dios,

y caminabas sobre piedras de fuego.

15Desde el día en que fuiste creado

tu conducta fue irreprochable,

hasta que la maldad halló cabida en ti.

16Por la abundancia de tu comercio,

te llenaste de violencia, y pecaste.

Por eso te expulsé del monte de Dios,

como a un objeto profano.

A ti, querubín protector,

te borré de entre las piedras de fuego.

17A causa de tu hermosura

te llenaste de orgullo.

A causa de tu esplendor,

corrompiste tu sabiduría.

Por eso te arrojé por tierra,

y delante de los reyes

te expuse al ridículo.

18Has profanado tus santuarios,

por la gran cantidad de tus pecados,

¡por tu comercio corrupto!

Por eso hice salir de ti

un fuego que te devorara.

A la vista de todos los que te admiran

te eché por tierra y te reduje a cenizas.

19Al verte, han quedado espantadas

todas las naciones que te conocen.

Has llegado a un final terrible,

y ya no volverás a existir”».

Profecía contra Sidón

20El Señor me habló diciendo: 21«Hijo de hombre, encara a Sidón y profetiza contra ella. 22Adviértele que así dice el Señor omnipotente:

»“Aquí estoy, Sidón, para acusarte

y para ser glorificado en ti.

Cuando traiga sobre ti un justo castigo,

y manifieste sobre ti mi santidad,

se sabrá que yo soy el Señor.

23Mandaré contra ti una peste,

y por tus calles correrá la sangre;

por la espada que ataca por todos lados,

los heridos caerán en tus calles,

y se sabrá que yo soy el Señor.

24Los israelitas no volverán a sufrir

el desprecio de sus vecinos,

que duele como aguijones

y pincha como espinas,

¡y se sabrá que yo soy el Señor!”

25»Así dice el Señor omnipotente: “Cuando yo reúna al pueblo de Israel de entre las naciones donde se encuentra disperso, le mostraré mi santidad en presencia de todas las naciones. Entonces Israel vivirá en su propio país, el mismo que le di a mi siervo Jacob. 26Allí vivirán seguros, y se construirán casas y plantarán viñedos, porque yo ejecutaré un justo castigo sobre los vecinos que desprecian al pueblo de Israel. ¡Y se sabrá que yo soy el Señor su Dios!”»