Mawu Odzudzula Mfumu ya Turo
1Yehova anandiyankhula nati: 2“Iwe mwana wa munthu, iwuze mfumu ya ku Turo mawu a Ine Ambuye Yehova akuti,
“ ‘Iwe ndi mtima wako wodzikuza
umanena kuti, ‘Ine ndine mulungu;
ndimakhala pa mpando wa mulungu
pakati pa nyanja.’
Koma ndiwe munthu chabe osati mulungu,
ngakhale ukuganiza kuti ndiwe wanzeru ngati mulungu.
3Taona, ndiwedi wanzeru kupambana Danieli.
Ndipo palibe chinsinsi chobisika kwa iwe.
4Mwa nzeru zako ndi kumvetsa kwako
unadzipezera chuma
ndipo unasonkhanitsa golide ndi siliva
mʼnyumba zosungira chuma chako.
5Ndi nzeru zako zochitira malonda
unachulukitsa chuma chako
ndipo wayamba kunyada
chifukwa cha chuma chakocho.
6“ ‘Choncho Ine Ambuye Yehova ndikuti,
“ ‘Popeza umadziganizira
kuti ndiwe mulungu,
7Ine ndidzabwera ndi anthu achilendo, anthu ankhanza,
kuti adzalimbane nawe.
Adzakuthira nkhondo kuti awononge zonse zimene unazipeza ndi nzeru zako,
ndipo adzawononga kunyada kwakoko.
8Iwo adzakuponyera ku dzenje
ndipo udzafa imfa yoopsa
mʼnyanja yozama.
9Kodi udzanenabe kuti, ‘Ine ndine mulungu,’
pamaso pa iwo amene akukupha?
Iwe udzaoneka kuti ndiwe munthu chabe, osati mulungu,
mʼmanja mwa iwo amene akukuphawo.
10Udzafa imfa ya anthu osachita mdulidwe
mʼmanja mwa anthu achilendo.
Ine ndayankhula zimenezi, akutero Ambuye Yehova.’ ”
11Yehova anandiyankhula kuti: 12“Iwe mwana wa munthu, imba nyimbo yodandaulira mfumu ya Turo ndipo uyiwuze mawu a Ine Ambuye Yehova akuti,
“ ‘Iwe unali chitsanzo cha ungwiro weniweni,
wodzaza ndi nzeru ndi wokongola kwambiri.
13Iwe unkakhala ngati mu Edeni,
munda wa Mulungu.
Miyala yokongola ya mitundu yonse:
rubi, topazi ndi dayimondi,
kirisoliti, onikisi, yasipa,
safiro, kalineliyoni ndi berili ndiwo inali zofunda zako.
Ndipo zoyikamo miyalayo zinali zagolide.
Anakupangira zonsezi pa tsiku limene unalengedwa.
14Ndinayika kerubi kuti azikulondera.
Unkakhala pa phiri langa lopatulika,
ndipo unkayendayenda
pakati pa miyala ya moto.
15Makhalidwe ako anali abwino
kuyambira pamene unalengedwa
mpaka nthawi imene unayamba kuchita zoyipa.
16Unatanganidwa ndi zamalonda.
Zotsatira zake zinali zoti unachulukitsa zandewu
ndi kumachimwa.
Choncho ndinakuchotsa ku phiri langa lopatulika.
Mkerubi amene ankakulondera uja anakupirikitsa
kukuchotsa ku miyala yamoto.
17Unkadzikuza mu mtima mwako
chifukwa cha kukongola kwako,
ndipo unayipitsa nzeru zako
chifukwa chofuna kutchuka.
Kotero Ine ndinakugwetsa pansi
kuti ukhala chenjezo pamaso pa mafumu.
18Ndi malonda ako achinyengo unachulukitsa machimo ako.
Motero unayipitsa malo ako achipembedzo.
Choncho ndinabutsa moto pakati pako,
ndipo unakupsereza,
ndipo unasanduka phulusa pa dziko lapansi
pamaso pa anthu onse amene amakuona.
19Anthu onse amitundu amene ankakudziwa
akuchita mantha chifukwa cha iwe.
Watheratu mochititsa mantha
ndipo sudzakhalaponso mpaka muyaya.’ ”
Za Chilango cha Sidoni
20Yehova anandiyankhula nati: 21“Iwe mwana wa munthu, utembenukire ku mzinda wa Sidoni ndipo unenere mowudzudzula kuti, 22‘Ine Ambuye Yehova ndikuti,
“ ‘Ndine mdani wako, iwe Sidoni,
ndipo ndidzalemekezedwa chifukwa cha iwe.
Anthu adzadziwa kuti Ine ndine Yehova
ndikadzakulanga ndi kudzionetsa kuti
ndine woyera pakati pako.
23Ndidzatumiza mliri pa iwe
ndi kuchititsa magazi kuti ayende mʼmisewu yako.
Anthu ophedwa ndi lupanga
adzagwa mbali zonse.
Pamenepo iwo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.
24“ ‘Nthawi imeneyo Aisraeli sadzakhalanso ndi anthu pafupi achipongwe amene ali ngati nthula zowawa ndi ngati minga zopweteka. Pamenepo iwo adzadziwa kuti Ine ndine Ambuye Yehova.
25“ ‘Ine Ambuye Yehova mawu anga ndi awa: Nditasonkhanitsa Aisraeli kuchoka ku mayiko kumene anamwazikira, ndidzadzionetsa kuti ndine woyera pakati pawo pamaso pa anthu a mitundu ina. Adzakhala mʼdziko lawo, limene ndinalipereka kwa mtumiki wanga Yakobo. 26Adzakhala kumeneko mwamtendere ndipo adzamanga nyumba ndi kulima minda ya mpesa. Adzakhala kumeneko mwamtendere pamene ndidzalange anthu oyandikana nawo, amene ankawanyoza. Motero iwo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova Mulungu wawo.’ ”
Profecía contra el rey de Tiro
1El Señor me habló diciendo: 2«Hijo de hombre, adviértele al rey de Tiro que así dice el Señor omnipotente:
»“En la intimidad de tu arrogancia dijiste:
‘Yo soy un dios.
Me encuentro en alta mar
sentado en un trono de dioses’.
¡Pero tú no eres un dios,
aunque te creas que lo eres!
¡Tú eres un simple mortal!
3¿Acaso eres más sabio que Daniel?28:3 Daniel. Alt. Danel.
¿Acaso conoces todos los secretos?
4Con tu sabiduría y tu inteligencia
has acumulado muchas riquezas,
y en tus cofres has amontonado
mucho oro y mucha plata.
5Eres muy hábil para el comercio;
por eso te has hecho muy rico.
A causa de tus grandes riquezas
te has vuelto muy arrogante.
6Por eso, así dice el Señor omnipotente:
»”Ya que pretendes ser
tan sabio como un dios,
7haré que vengan extranjeros contra ti,
los más feroces de las naciones:
desenvainarán la espada
contra tu hermosura y sabiduría,
y profanarán tu esplendor.
8Te hundirán en la fosa,
y en alta mar sufrirás una muerte violenta.
9Y aun así, en presencia de tus verdugos,
¿te atreverás a decir: ¡Soy un dios!?
¡Pues en manos de tus asesinos
no serás un dios, sino un simple mortal!
10Sufrirás a manos de extranjeros
la muerte de los incircuncisos,
porque yo lo he dicho.
Lo afirma el Señor omnipotente”».
11El Señor me habló diciendo: 12«Hijo de hombre, entona una elegía al rey de Tiro y adviértele que así dice el Señor omnipotente:
»“Eras un modelo de perfección,
lleno de sabiduría y de hermosura perfecta.
13Estabas en Edén, en el jardín de Dios,
adornado con toda clase de piedras preciosas:
rubí, crisólito, jade,
topacio, cornalina, jaspe,
zafiro, granate y esmeralda.
Tus joyas y encajes estaban cubiertos de oro,
y especialmente preparados para ti
desde el día en que fuiste creado.
14Fuiste elegido querubín protector,
porque yo así lo dispuse.28:14 Fuiste … dispuse. Texto de difícil traducción.
Estabas en el santo monte de Dios,
y caminabas sobre piedras de fuego.
15Desde el día en que fuiste creado
tu conducta fue irreprochable,
hasta que la maldad halló cabida en ti.
16Por la abundancia de tu comercio,
te llenaste de violencia, y pecaste.
Por eso te expulsé del monte de Dios,
como a un objeto profano.
A ti, querubín protector,
te borré de entre las piedras de fuego.
17A causa de tu hermosura
te llenaste de orgullo.
A causa de tu esplendor,
corrompiste tu sabiduría.
Por eso te arrojé por tierra,
y delante de los reyes
te expuse al ridículo.
18Has profanado tus santuarios,
por la gran cantidad de tus pecados,
¡por tu comercio corrupto!
Por eso hice salir de ti
un fuego que te devorara.
A la vista de todos los que te admiran
te eché por tierra y te reduje a cenizas.
19Al verte, han quedado espantadas
todas las naciones que te conocen.
Has llegado a un final terrible,
y ya no volverás a existir”».
Profecía contra Sidón
20El Señor me habló diciendo: 21«Hijo de hombre, encara a Sidón y profetiza contra ella. 22Adviértele que así dice el Señor omnipotente:
»“Aquí estoy, Sidón, para acusarte
y para ser glorificado en ti.
Cuando traiga sobre ti un justo castigo,
y manifieste sobre ti mi santidad,
se sabrá que yo soy el Señor.
23Mandaré contra ti una peste,
y por tus calles correrá la sangre;
por la espada que ataca por todos lados,
los heridos caerán en tus calles,
y se sabrá que yo soy el Señor.
24Los israelitas no volverán a sufrir
el desprecio de sus vecinos,
que duele como aguijones
y pincha como espinas,
¡y se sabrá que yo soy el Señor!”
25»Así dice el Señor omnipotente: “Cuando yo reúna al pueblo de Israel de entre las naciones donde se encuentra disperso, le mostraré mi santidad en presencia de todas las naciones. Entonces Israel vivirá en su propio país, el mismo que le di a mi siervo Jacob. 26Allí vivirán seguros, y se construirán casas y plantarán viñedos, porque yo ejecutaré un justo castigo sobre los vecinos que desprecian al pueblo de Israel. ¡Y se sabrá que yo soy el Señor su Dios!”»