Ezekieli 29 – CCL & CST

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ezekieli 29:1-21

Za Chilango cha Igupto

1Pa tsiku lakhumi ndi chiwiri la mwezi wakhumi, chaka chakhumi, Yehova anandiyankhula kuti: 2“Iwe mwana wa munthu, tembenukira kwa Farao, mfumu ya Igupto, ndipo unenere modzudzula mfumuyo pamodzi ndi dziko lake. 3Uyiwuze mfumuyo kuti, ‘Ine Ambuye Yehova ndikuti,

“ ‘Ndine mdani wako, iwe Farao mfumu ya Igupto,

iwe ngʼona yayikulu yogona pakati pa mitsinje yako.

Umanena kuti, ‘Mtsinje wa Nailo ndi wanga;

ndinadzipangira ndekha.’

4Koma ndidzakukola ndi mbedza mʼkamwa mwako

ndipo nsomba za mʼmitsinje yako zidzakangamira ku mamba ako.

Tsono ndidzakutulutsa mu mtsinje mwakomo

pamodzi ndi nsomba zimene zakangamira ku mamba ako.

5Ndidzakutaya ku chipululu,

iwe pamodzi ndi nsomba zonse za mʼmitsinje yako.

Udzagwera pamtetete kuthengo

popanda munthu woti akutole kuti akayike maliro ako.

Ndidzakusandutsa chakudya

cha zirombo za pa dziko lapansi ndi mbalame za mlengalenga.

6Motero aliyense amene amakhala mu Igupto adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.

“ ‘Iwe unakhala ngati ndodo yabango ku Aisraeli. 7Pamene anakugwira unathethekera mʼmanja mwawo ndi kucheka mapewa awo. Pamene anakutsamira, unathyoka ndipo misana yawo inagwedezeka.

8“ ‘Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti, ndikubweretsera lupanga kuti lidzaphe anthu pamodzi ndi nyama zomwe. 9Dziko la Igupto lidzasanduka lopanda anthu. Pamenepo iwo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.

“ ‘Popeza iwe unati, ‘Mtsinje wa Nailo ndi wanga; ndinawupanga ndine,’ 10nʼchifukwa chake Ine ndikudana nawe pamodzi ndi mitsinje yakoyo, ndipo ndidzasandutsa dziko la Igupto bwinja kuyambira chipululu cha Migidoli mpaka ku mzinda wa Asiwani, kukafika ku malire a Kusi. 11Palibe phazi la munthu kapena la nyama limene lidzapondepo. Kudzakhala kopanda anthu kwa zaka makumi anayi. 12Ndidzasandutsa dziko la Igupto kukhala chipululu ngati zipululu za mayiko ena. Kwa zaka makumi anayi mizinda yakenso idzakhala yopasuka pakati pa mizinda yopasuka. Ndipo ndidzathamangitsira Aigupto pakati pa mitundu ya anthu ndi kuwabalalitsira mʼmayiko.

13“ ‘Komabe Ine Ambuye Yehova ndikuti: Pakutha pa zaka makumi anayi ndidzasonkhanitsa Aigupto onse kuchokera ku mayiko amene ndinawabalalitsirako. 14Ndidzachotsa Aiguptowo ku ukapolo ndipo ndidzawabwezera ku Patirosi kumene anachokera. Kumeneko iwo adzakhala ufumu wotsika. 15Udzakhala ufumu wotsika kwambiri kupambana maufumu ena onse ndipo sudzadzitukumula pakati pa mitundu ina. Ndidzawufowoketsa kwambiri kotero kuti sudzathanso kulamulira mitundu ya anthu. 16Aisraeli sadzadaliranso Aigupto. Koma kuti chilango chawo chidzawakumbutsa tchimo lawo lija lofunafuna thandizo kuchokera ku Igupto. Pamenepo iwo adzadziwa kuti Ine ndine Ambuye Yehova.’ ”

Mphotho ya Nebukadinezara

17Pa tsiku loyamba la mwezi woyamba, chaka cha 27, Yehova anandiyankhula kuti: 18“Iwe mwana wa munthu, kale Nebukadinezara mfumu ya Babuloni inagwiritsa ntchito ankhondo ake kukathira nkhondo mzinda wa Turo, mpaka munthu aliyense anachita dazi chifukwa chosenza katundu, ndipo ananyuka pa phewa. Komabe ngakhale iyeyo, kapena gulu lake lankhondo sanaphulepo kanthu pa ntchito yonse imene anayigwira polimbana ndi mzindawo. 19Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti, Ine ndidzapereka Igupto kwa Nebukadinezara mfumu ya Babuloni, ndipo iyo idzatenga chuma chake ndi kuchifunkha ngati malipiro a gulu lake lankhondo. 20Ndamupatsa Nebukadinezara Igupto ngati mphotho ya kulimbika kwake chifukwa iyo ndi gulu lake lankhondo anandigwirira ntchito, akutero Ambuye Yehova.

21“Pa nthawi imeneyo ndidzapereka mphamvu yatsopano pa Aisraeli, ndipo ndidzatsekula pakamwa pako, iwe, Ezekieli kuti uthe kuyankhula pakati pawo. Pamenepo iwo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.”

Nueva Versión Internacional (Castilian)

Ezequiel 29:1-21

Profecía contra Egipto

1A los doce días del mes décimo del año décimo, el Señor me habló diciendo: 2«Hijo de hombre, encara al faraón, rey de Egipto, y profetiza contra él y contra todo Egipto. 3Adviértele que así dice el Señor omnipotente:

»“A ti, Faraón, rey de Egipto,

gran monstruo que yaces

en el cauce de tus ríos,

que dices: ‘El Nilo es mío,

el Nilo es mi creación’,

¡te declaro que estoy en tu contra!

4Te pondré garfios en las mandíbulas,

y haré que los peces del río

se te peguen a las escamas.

Y con todos los peces pegados a tus escamas

te sacaré de la corriente.

5Te abandonaré a tu suerte en el desierto,

junto con todos los peces de tu río.

Caerás en campo abierto,

y no serás recogido ni enterrado.29:5 enterrado (mss. hebreos y Targum); juntado (TM).

Las bestias de la tierra y las aves del cielo

te las daré como alimento.

6Entonces todos los habitantes de Egipto

sabrán que yo soy el Señor.

No fuiste para el pueblo de Israel

más que un bastón de caña.

7Cuando se agarraron de tu mano,

te quebraste, y les desgarraste las manos;29:7 manos (LXX y Siríaca); hombros (TM).

cuando en ti se apoyaron te rompiste,

y sus espaldas se estremecieron.29:7 se estremecieron (Siríaca; véanse LXX y Vulgata); hiciste que se pararan (TM).

8»”Por eso, así dice el Señor omnipotente: Contra ti traeré la espada, y haré que mate a hombres y animales. 9La tierra de Egipto se convertirá en desolación. Entonces sabrán que yo soy el Señor. Tú dijiste: ‘El Nilo es mío, el Nilo es mi creación’. 10Por eso me declaro en contra tuya y en contra de tus ríos. Desde Migdol hasta Asuán, y hasta la frontera con Etiopía, convertiré la tierra de Egipto en ruina y desolación total. 11Durante cuarenta años quedará completamente deshabitada, y ni hombres ni animales pasarán por allí. 12Haré de Egipto la más desolada de todas las tierras, y durante cuarenta años sus ciudades quedarán en ruinas y en medio de gran desolación. Yo dispersaré a los egipcios entre las naciones, y los esparciré por los países.

13»”Así dice el Señor omnipotente: Al cabo de los cuarenta años reuniré a los egipcios de entre los pueblos donde fueron dispersados. 14Cambiaré la suerte de Egipto y los haré volver a Patros, tierra de sus antepasados. Allí formarán un reino humilde. 15Será el reino de menor importancia, y nunca podrá levantarse por encima de las demás naciones. Yo mismo los haré tan pequeños que no podrán dominar a las otras naciones. 16El pueblo de Israel no confiará más en Egipto. Al contrario, será Egipto quien les sirva para recordar el pecado que cometieron los israelitas al seguirlo. Así sabrán que yo soy el Señor”».

17El día primero del mes primero del año veintisiete, el Señor me habló diciendo: 18«Ten en cuenta, hijo de hombre, que el rey de Babilonia, Nabucodonosor, y su ejército llevaron a cabo una gran campaña contra Tiro. Todos ellos quedaron con la cabeza rapada y con llagas en la espalda. Pero, a pesar del tremendo esfuerzo, ni él ni su ejército sacaron provecho alguno de la campaña emprendida contra Tiro. 19Por eso, así dice el Señor omnipotente: Pondré a Egipto en manos de Nabucodonosor, rey de Babilonia, quien se apoderará de sus riquezas, saqueará sus despojos y se llevará el botín que servirá de recompensa para su ejército. 20Al rey de Babilonia le entregaré Egipto como recompensa por lo que hizo contra Tiro, porque ellos lo hicieron por mí. Lo afirma el Señor omnipotente.

21»En aquel día acrecentaré la fuerza del pueblo de Israel, y entonces tú, Ezequiel, les hablarás con libertad. Entonces sabrán que yo soy el Señor».