Ezekieli 26 – CCL & CARST

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ezekieli 26:1-21

Za Chilango cha Turo

1Pa chaka cha khumi ndi chimodzi, tsiku loyamba la mwezi, Yehova anandiyankhula kuti: 2“Iwe mwana wa munthu, anthu a ku Turo ananyogodola Yerusalemu kuti ‘Hii! Uja amene anali chipata choloweramo anthu a mitundu ina wawonongeka. Zitseko zake zatsekukira ife. Tidzalemera popeza wasanduka bwinja.’ 3Nʼchifukwa chake, Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ndidzakulangani, inu anthu a ku Turo. Ndidzakuyitanirani anthu a mitundu ina kuti adzakulangeni monga momwe mafunde amawombera pa Nyanja. 4Anthuwo adzawononga makoma a Turo ndi kugwetsa nsanja zake. Ndidzapala dothi lake ndipo ndidzamusandutsa thanthwe losalala. 5Udzakhala poyanikapo makoka pakati pa nyanja. Ine Ambuye Yehova ndayankhula zimenezo. Udzasanduka chofunkha cha anthu a mitundu ina. 6Anthu okhala ku mtunda adzasakazidwa ndi lupanga. Pamenepo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.

7“Ine Ambuye Yehova ndikuti: Iwe Turo, ndidzakubweretsera Nebukadinezara, mfumu ya ku Babuloni mfumu ya mafumu, kuchokera kumpoto pamodzi ndi akavalo ndiponso magaleta, anthu okwera pa akavalo ndi gulu lalikulu la ankhondo. 8Anthu okhala ku mtunda adzawapha ndi lupanga. Adzapanga mitumbira yankhondo ndi kukukwezera zishango kuti alimbane nawe. 9Adzagwetsa makoma ako ndi zida zogumulira khoma ndi kugwetsa nsanja zako ndi nkhwangwa zake. 10Akavalo ake adzakhala ochuluka kwambiri kotero kuti adzakukwirira ndi fumbi lawo. Makoma ako adzagwedezeka ndi mdidi wa akavalo, ngolo ndi magaleta pamene iye adzalowa pa zipata monga mmene amalowera mu mzinda umene makoma ake agwetsedwa. 11Akavalo ake adzapondaponda mʼmisewu yako yonse ndi ziboda zawo. Adzapha anthu ako ndi lupanga. Mizati yako yolimba idzagwetsedwa. 12Iwo adzafunkha chuma chako ndipo adzalanda zinthu zako za malonda. Adzagwetsa makoma ako ndi kuwononga nyumba zako zabwino. Adzaponya miyala yako, matabwa ako ndi dothi lako mʼnyanja. 13Choncho ndidzathetsa phokoso la nyimbo zanu, ndipo kulira kwa apangwe ako sikudzamvekanso. 14Ndidzakusandutsa thanthwe losalala, ndipo udzakhala malo woyanikapo makoka a nsomba. Sudzamangidwanso, pakuti Ine Yehova ndayankhula, akutero Ambuye Yehova.

15“Ine Ambuye Yehova ndikukuwuza, iwe mzinda wa Turo, kuti zilumba zidzagwedezeka pakumva za kugwa kwako ndiponso poona anthu opweteka akubuwula ndipo anthu akuphedwa pakati pako. 16Pamenepo mafumu a mʼmbali mwa nyanja adzatsika pa mipando yawo yaufumu. Adzayika pambali mikanjo yawo ndi kuvala zovala zawo zamakaka. Adzachita mantha ndipo adzakhala pansi akunjenjemera kosalekeza. Adzathedwa nzeru poona zimene zakugwera. 17Pamenepo adzayimba nyimbo yokudandaula ndipo adzati kwa iwe:

“ ‘Nʼkuchita kuwonongeka chotere, iwe mzinda wotchuka,

wodzaza ndi anthu a ku nyanja!

Unali wamphamvu pa nyanja,

iwe ndi nzika zako;

unkaopseza anthu onse amene

ankakhala kumeneko.

18Tsopano mayiko a mʼmbali mwa nyanja akunjenjemera

chifukwa cha kugwa kwako;

okhala pa zilumba nawonso agwidwa ndi mantha aakulu

chifukwa cha kugwa kwako.’

19“Mawu a Ine Ambuye Yehova ndi awa: Ndidzakusandutsa bwinja, ngati mizinda imene anthu sangathe kukhalamo. Ndidzakuphimba ndi madzi ozama a mʼnyanja, madzi amphamvu woti akumize. 20Ndidzakugwetsa pansi kuti ukhale pamodzi ndi anthu amvulazakale amene akutsikira ku manda. Ine ndidzakusunga ku dzenjeko ngati ku bwinja losiyidwa kalekale, pamodzi ndi anthu amene anafa kale motero sudzabwererako kukhala pakati pa anthu amoyo. 21Ine ndidzakuthetsa mochititsa mantha, ndipo sudzakhalaponso. Anthu adzakufunafuna, koma sudzapezekanso, akutero Ambuye Yehova.”

Священное Писание (Восточный перевод), версия для Таджикистана

Езекиил 26:1-21

Пророчество о Тире

1В одиннадцатом году, в первый день месяца (587 (586) г. до н. э.), было ко мне слово Вечного:

2– Смертный, за то, что Тир, насмехаясь, сказал об Иерусалиме: «Вот! Врата народов разрушены, распахнуты для меня. Он опустошён, и теперь я буду благоденствовать», 3Владыка Вечный говорит: «Я твой противник, Тир. Я подниму против тебя многие народы, подобно тому, как море вздымает волны. 4Они сломают твои стены и разрушат твои башни, а Я вымету из тебя пыль и сделаю голой скалой. 5Посреди моря ты станешь местом, где раскидывают рыбацкие сети, потому что Я так сказал, – возвещает Владыка Вечный. Ты будешь разграблен народами, 6а твои селения на земле будут преданы мечу. Тогда ты узнаешь, что Я – Вечный».

7Ведь так говорит Владыка Вечный: «Смотрите, Я веду с севера на Тир Навуходоносора, царя Вавилона, царя царей, с конями и колесницами, всадниками и огромным, могучим войском. 8Он опустошит твои селения на земле мечом. Он возведёт против тебя осадные валы, сделает насыпь у твоих стен и обратит против тебя щиты. 9Он прикажет бить в твои стены таранами и разрушить твои башни кирками. 10Коней у него будет так много, что поднятая ими пыль покроет тебя. Твои стены дрогнут от топота его боевых коней, повозок и колесниц, когда он войдёт в твои ворота, как входят в город, стены которого были пробиты. 11Копыта его коней будут попирать твои улицы. Он перебьёт твоих жителей мечом, и твои мощные колонны рухнут на землю. 12Твои богатства разграбят, твои товары расхитят. Твои стены сломают, роскошные дома разрушат, а камни, дерево и мусор бросят в море. 13Я положу конец твоим шумным песням, и музыка твоих арф смолкнет. 14Я сделаю тебя голой скалой; ты станешь местом, где раскидывают рыбацкие сети. Ты никогда не будешь вновь отстроен, потому что Я, Вечный, так сказал», – возвещает Владыка Вечный.

15Так говорит Тиру Владыка Вечный:

– Неужели побережье не вздрогнет от шума твоего падения, когда застонут раненые, когда в тебе начнётся резня? 16Тогда властители побережья сойдут с престолов, сбросят мантии и снимут расшитые одежды. Охваченные трепетом, они будут сидеть на земле, вздрагивая каждый миг и ужасаясь твоей доле. 17Они поднимут о тебе плач; они скажут тебе:

«Как сгинул ты, славный город,

мореходами населённый!

Ты был силою на морях,

ты и твои горожане,

что наводили страх

на всё побережье.

18Ныне, в день твоего падения,

содрогаются берега;

острова, что на море,

ужасаются твоей гибели».

19Так говорит Владыка Вечный:

– Когда Я сделаю тебя опустошённым городом, подобным тем городам, где никто больше не живёт, когда Я сомкну над тобой океанскую бездну, и её великие воды покроют тебя, 20тогда Я сведу тебя с теми, кто спускается в пропасть, к тем, кто жил в древности. Я поселю тебя в нижнем мире, среди вековечных развалин, с теми, кто спускается в пропасть, чтобы ты больше не был населён и не занял места26:20 Или: «…населён, и Я дам красоту». на земле живых. 21Я пошлю тебе страшный конец, и тебя не станет. Тебя будут искать, но не найдут, – возвещает Владыка Вечный.