Ezekieli 22 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ezekieli 22:1-31

Machimo a Yerusalemu

1Yehova anandiyankhula nati: 2“Iwe mwana wa munthu, kodi udzaweruza mzinda uwo wa anthu akupha anzawo? Tsono uwudzudzule chifukwa cha machitidwe ake onse onyansa 3ndipo unene kuti, ‘Ambuye akuti: Iwe mzinda umene wadzigwetsa wekha mʼtsoka pa kukhetsa magazi pakati pako ndi kudziyipitsa popanga mafano, 4wapezekatu wolakwa chifukwa cha magazi amene wakhetsa, ndipo wadziyipitsa chifukwa cha mafano amene wapanga. Choncho wachepetsa masiku ako, ndipo zaka zako zafika kumapeto. Nʼchifukwa chake ndalola kuti anthu a mitundu ina akunyoze ndiponso kuti anthu a mayiko onse akuseke. 5Mayiko amene ali pafupi ndi mayiko omwe ali kutali adzakunyoza, iwe mzinda wa mbiri yoyipa, wodzaza ndi chiwawa.

6“ ‘Taona momwe aliyense wa atsogoleri a Israeli amagwiritsira mphamvu zake kupha anthu. 7Mu mzindamo anthu amanyoza abambo ndi amayi awo. Iwo amapondereza alendo ndi kuzunza ana amasiye ndi akazi amasiye. 8Wanyoza zinthu zanga zopatulika ndi kuyipitsa Masabata anga. 9Mwa iwe muli anthu onenera anzawo zabodza kuti aphedwe. Mwa iwe mulinso amene amadyera zansembe pa mapiri a chipembedzo. Enanso amachita zonyansa. 10Mwa iwe muli ena ogonana ndi akazi a abambo awo, muli enanso amene amavuta akazi pamene ali woyipitsidwa ndi msambo. 11Ena amachita chigololo ndi akazi a anzawo, ndipo ena, mopanda manyazi, amayipitsa mkazi wa mwana wawo. Palinso ena amene amayipitsa alongo awo, ana aakazi a abambo awo. 12Mwa iwe muli anthu amene amalandira ziphuphu kuti aphe anzawo; ena amachita katapira ndi kupeza phindu loposera muyeso; enanso amapeza phindu mwachinyengo poopseza anzawo. Ndipo mwandiyiwala Ine, akutero Ambuye Yehova.

13“ ‘Koma Ine ndachita kuwomba mʼmanja kuti phuu nʼkudabwa chifukwa cha phindu lachinyengo limene mwapeza ndiponso chifukwa cha kuphana kumene kumachitika pakati panu. 14Kodi mtima wako udzakhala wolimbabe kapena manja ako adzakhalabe amphamvu ndikadzatsiriza kukulanga iwe? Ine Yehova ndayankhula, ndipo ndidzazichitadi. 15Ndidzakubalalitsani pakati pa anthu a mitundu ina ndi kukumwazirani ku mayiko onse. Umu ndi mmene ndidzachotsere zoyipa zako. 16Udzanyozedwa pamaso pa anthu a mitundu ina. Pambuyo pake udzadziwa kuti Ine ndine Yehova.’ ”

17Yehova anandiyankhula nati: 18“Iwe mwana wa munthu, Aisraeli asanduka chinthu cha chabechabe kwa Ine. Onse ali ngati mkuwa, chitini, chitsulo ndi mtovu zotsala mʼngʼanjo atayeretsa siliva. 19Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti: ‘Pakuti nonse mwasanduka chinthu cha chabechabe, Ine ndidzakusonkhanitsani mu Yerusalemu. 20Monga momwe anthu amasonkhanitsira siliva, mkuwa, chitsulo, mtovu ndi chitini mʼngʼanjo ndi kusonkhetsa moto kuti azisungunule, motero Inenso ndidzakusonkhanitsani ndili wokwiya ndi waukali, ndipo ndidzakuyikani mʼkati mwa mzinda, ndikukusungunurani. 21Ndidzakusonkhanitsani mu mzindamo ndi kukoleza moto wa mkwiyo wanga, ndipo inu mudzasungunuka mu mzindamo. 22Monga siliva amasungunulidwa mʼngʼanjo, kotero inunso mudzasungunuka mʼkati mwa mzinda ndipo Inu mudzadziwa kuti Ine Yehova ndakukwiyirani.’ ”

23Yehova anandiyankhulanso nati, 24“Iwe mwana wa munthu, uza dziko la Israeli kuti, ‘Iwe ndiwe dziko losayeretsedwa, ndiponso losavumbidwa ndi mvula chifukwa cha mkwiyo wanga.’ 25Atsogoleri ake mu mzindamo ali ngati mkango wobangula pogwira nyama. Apha anthu, alanda chuma ndi zinthu za mtengowapatali, ndiponso asandutsa amayi ambiri kukhala amasiye. 26Ansembe ake amaphwanya lamulo langa ndi kuyipitsa zinthu zanga zopatulika. Sasiyanitsa pakati pa zinthu zopatulika ndi zinthu wamba. Saphunzitsa anthu kusiyana kwa zinthu zoyenera pa chipembedzo ndi zinthu zosayenera. Sasamalira za kusunga masabata anga. Motero Ine ndimanyozedwa pakati pawo. 27Atsogoleri ake ali ngati mimbulu yokhadzula nyama; amakhetsa magazi ndi kupha anthu kuti apeze phindu loyipa. 28Aneneri ake amabisa zonsezi monga muja amachitira anthu popaka njereza. Amazimphimba ndi zabodza zimene aona mʼmasomphenya awo ndi zonama za mʼmawula awo. Iwo amati, ‘Ambuye Yehova akuti,’ pamene Ine Yehova sindinayankhule. 29Anthu a mʼdzikomo amasautsa anzawo ndi kulanda anthu osowa. Amazunza anthu osauka ndi amphawi. Amavutitsa alendo posawachitira zinthu mwachilungamo.

30“Ndinafunafuna munthu pakati pawo woti amange linga, woti ayimirire dziko pamaso panga kundipepesa kuti ndisaliwononge, koma sindinamupeze. 31Nʼchifukwa chake ndawakwiyira kwambiri. Ndawawonongeratu ndi mkwiyo wanga woyaka ngati moto. Ndawalanga molingana ndi zimene anachita. Akutero Ambuye Yehova.”

New Russian Translation

Иезекииль 22:1-31

Грехи Иерусалима

1Было ко мне слово Господа:

2– Сын человеческий, будешь ли судить его? Будешь ли судить этот кровавый город? Тогда укажи ему на все его омерзительные обычаи 3и скажи: «Так говорит Владыка Господь: О город, который, навлекая кару, проливает посреди себя кровь и оскверняется, делая идолов, 4ты стал виновен из-за крови, которую пролил, и осквернился идолами, которых сделал; ты приблизил свой день, и предел твоих лет настал. За это Я сделаю тебя поруганием для народов и посмешищем для всех стран. 5Те, кто далеко, и те, кто близко, будут глумиться над тобой, о бесславный город, объятый смутой.

6Вожди Израиля, что у тебя, каждый по мере своих сил, проливали чужую кровь. 7У тебя они с презрением обходились с отцами и матерями, у тебя притесняли чужеземцев, у тебя творили зло сиротам и вдовам. 8Ты пренебрегал Моими святынями и осквернял Мои субботы. 9У тебя клеветники проливали чужую кровь; у тебя находились те, кто ел в горных святилищах, и посреди тебя совершали непристойности. 10У тебя те, кто оскверняет отцовское ложе; у тебя – те, кто совокупляется с женщиной во время месячных, когда она ритуально нечиста. 11У тебя один совершает гнусное преступление с женой другого, второй бесстыдно оскверняет сноху, а третий насилует22:11 Или: «совокупляется с» сестру, дочь своего отца. 12У тебя берут взятки, чтобы лить чужую кровь; ты занимаешься ростовщичеством, берешь проценты и вымогательством наживаешься на ближнем. Ты оставляешь Меня, – возвещает Владыка Господь.

13Гляди, Я всплесну руками о твоей неправедной наживе, которую ты приобрел, и о крови, которую ты пролил посреди себя. 14Устоит ли твоя храбрость и останутся ли сильными твои руки в те дни, когда Я буду наказывать тебя? Я, Господь, сказал это и сделаю. 15Я рассею тебя между народами и раскидаю по странам; Я искореню в тебе твою нечистоту. 16Ты будешь осквернен в глазах народов. Тогда ты узнаешь, что Я – Господь».

17И было ко мне слово Господа:

18– Сын человеческий, дом Израиля стал у Меня бесполезной окалиной; все они как медь, олово, железо и свинец, которые остаются в плавильном горне, как изгарь серебра.

19Поэтому так говорит Владыка Господь:

– Так как вы стали окалиной, Я соберу вас в Иерусалиме. 20Как собирают в плавильный горн серебро, медь, железо, свинец и олово, чтобы, раздув огонь, расплавить их, так Я соберу вас в гневе и ярости, оставлю в городе и расплавлю. 21Я соберу вас, дохну на вас Моим огненным гневом, и вы расплавитесь в нем. 22Как серебро расплавляется в плавильном горне, так и вы расплавитесь в нем. Тогда вы узнаете, что Я, Господь, излил на вас Свою ярость.

23Вновь было ко мне слово Господа:

24– Сын человеческий, скажи земле: «Ты, земля, неочищенная и неорошенная в день гнева. 25Заговор ее пророков в ней подобен ревущему льву, что терзает добычу; они пожирают людей, отнимают сокровища и драгоценности и многих делают вдовами в этой земле. 26Ее священники преступают Мой Закон и оскверняют Мои святыни; они не делают различия между священным и несвященным; они учат, что нет разницы между нечистым и чистым; они закрывают глаза на соблюдение Моих суббот, так что Я оскверняюсь среди них. 27Ее приближенные в ней подобны волкам, терзающим добычу; они проливают кровь и убивают людей, чтобы приобрести неправедную поживу. 28Ее пророки закрашивают для них такие дела белилами пустых видений и лживых прорицаний. Они говорят: „Так говорит Владыка Господь“, когда Господь не говорил. 29Народ страны предан вымогательству и грабежу; они притесняют бедняков и нуждающихся и угнетают чужеземцев, отказывая им в правосудии.

30Я искал среди них человека, который починил бы стену и встал бы предо Мною в бреши, заступиться за страну, чтобы Мне ее не погубить, но не нашел. 31И вот, Я изолью на них Мою ярость и истреблю их пламенем Моего негодования, обрушив им на головы то, что они натворили», – возвещает Владыка Господь.