Maliro 1 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Maliro 1:1-22

1Haa! Mzinda uja wasiyidwa wokhawokha,

umene kale unali wodzaza ndi anthu!

Kale unali wotchuka pakati pa mitundu ya anthu!

Tsopano wasanduka ngati mkazi wamasiye.

Kale unali mfumukazi ya onse pa dziko lapansi,

tsopano wasanduka kapolo.

2Ukulira mowawidwa mtima usiku wonse,

misozi ili pa masaya pake.

Mwa abwenzi ake onse,

palibe ndi mmodzi yemwe womutonthoza.

Abwenzi ake onse amuchitira chiwembu;

onse akhala adani ake.

3Yuda watengedwa ku ukapolo,

kukazunzika ndi kukagwira ntchito yolemetsa.

Iye akukhala pakati pa anthu a mitundu ina;

ndipo alibe malo opumulira.

Onse omuthamangitsa iye amupitirira,

ndipo alibe kwina kothawira.

4Misewu yopita ku Ziyoni ikulira,

chifukwa palibe ndi mmodzi yemwe akubwera ku maphwando ake.

Zipata zake zonse zili pululu,

ansembe akubuwula.

Anamwali ake akulira,

ndipo ali mʼmasautso woopsa.

5Adani ake asanduka mabwana ake;

odana naye akupeza bwino.

Yehova wamubweretsera mavuto

chifukwa cha machimo ake ambiri.

Ana ake atengedwa ukapolo

pamaso pa mdani.

6Ulemerero wonse wa mwana wamkazi wa Ziyoni

wachokeratu.

Akalonga ake ali ngati mbawala

zosowa msipu;

alibe mphamvu zothawira

owathamangitsa.

7Pa masiku a masautso ndi kuzunzika kwake,

Yerusalemu amakumbukira chuma chonse

chimene mʼmasiku amakedzana chinali chake.

Anthu ake atagwidwa ndi adani ake,

panalibe aliyense womuthandiza.

Adani ake ankamuyangʼana

ndi kumuseka chifukwa cha kuwonongeka kwake.

8Yerusalemu wachimwa kwambiri

ndipo potero wakhala wodetsedwa.

Onse amene ankamulemekeza pano akumunyoza,

chifukwa aona umaliseche wake.

Iye mwini akubuwula

ndipo akubisa nkhope yake.

9Uve wake umaonekera pa zovala zake;

iye sanaganizire za tsogolo lake.

Nʼchifukwa chake kugwa kwake kunali kwakukulu;

ndipo analibe womutonthoza.

“Inu Yehova, taonani masautso anga,

pakuti mdani wapambana.”

10Adani amulanda

chuma chake chonse;

iye anaona mitundu ya anthu achikunja ikulowa mʼmalo ake opatulika,

amene Inu Mulungu munawaletsa

kulowa mu msonkhano wanu.

11Anthu ake onse akubuwula

pamene akufunafuna chakudya;

asinthanitsa chuma chawo ndi chakudya

kuti akhale ndi moyo.

“Inu Yehova, taonani ndipo ganizirani,

chifukwa ine ndanyozeka.”

12“Kodi zimenezi mukuziyesa zachabe, inu nonse mukudutsa?

Yangʼanani ndipo muone.

Kodi pali mavuto ofanana ndi

amene andigwerawa,

amene Ambuye anandibweretsera

pa tsiku la ukali wake?

13“Anatumiza moto kuchokera kumwamba,

unalowa mpaka mʼmafupa anga.

Anayala ukonde kuti ukole mapazi anga

ndipo anandibweza.

Anandisiya wopanda chilichonse,

wolefuka tsiku lonse.

14“Wazindikira machimo anga onse

ndipo ndi manja ake anawaluka pamodzi.

Machimowa afika pakhosi panga,

ndipo Ambuye wandithetsa mphamvu.

Iye wandipereka

kwa anthu amene sindingalimbane nawo.

15“Ambuye wakana

anthu anga onse amphamvu omwe ankakhala nane:

wasonkhanitsa gulu lankhondo kuti lilimbane nane,

kuti litekedze anyamata anga;

mʼmalo ofinyira mphesa Ambuye wapondereza

anamwali a Yuda.

16“Chifukwa cha zimenezi ndikulira

ndipo maso anga adzaza ndi misozi.

Palibe aliyense pafupi woti anditonthoze,

palibe aliyense wondilimbitsa mtima.

Ana anga ali okhaokha

chifukwa mdani watigonjetsa.

17“Ziyoni wakweza manja ake,

koma palibe aliyense womutonthoza.

Yehova walamula kuti abale ake

a Yakobo akhale adani ake;

Yerusalemu wasanduka

chinthu chodetsedwa pakati pawo.

18“Yehova ndi wolungama,

koma ndine ndinawukira malamulo ake.

Imvani inu anthu a mitundu yonse;

onani masautso anga.

Anyamata ndi anamwali anga

agwidwa ukapolo.

19“Ndinayitana abwenzi anga

koma anandinyenga.

Ansembe ndi akuluakulu anga

anafa mu mzinda

pamene ankafunafuna chakudya

kuti akhale ndi moyo.

20“Inu Yehova, onani mmene ine ndavutikira!

Ndikuzunzika mʼkati mwanga,

ndipo mu mtima mwanga ndasautsidwa

chifukwa ndakhala osamvera.

Mʼmisewu anthu akuphedwa,

ndipo ku mudzi kuli imfa yokhayokha.

21“Anthu amva kubuwula kwanga,

koma palibe wonditonthoza.

Adani anga onse amva masautso anga;

iwo akusangalala pa zimene Inu mwachita.

Lifikitseni tsiku limene munalonjeza lija

kuti iwonso adzakhale ngati ine.

22“Lolani kuti ntchito zawo zoyipa zifike pamaso panu;

muwalange

ngati mmene mwandilangira ine

chifukwa cha machimo anga onse.

Ndikubuwula kwambiri

ndipo mtima wanga walefuka.”

New Russian Translation

Плач Иеремии 1:1-22

Иерусалим – одинокая вдова

1Как одиноко стоит столица,

что некогда была многолюдной!

Она стала, как вдова,

а была великой среди народов,

была царицей над областями,

но стала рабыней.

2Горько плачет она ночью,

и слезы текут по ее щекам.

Нет у нее утешителя

среди всех возлюбленных1:2 возлюбленные – союзники Иудеи, которые предали ее, и их боги. Также в ст. 19. ее,

все друзья изменили ей

и стали врагами.

3Иудея пошла в изгнание,

после бед и тяжкого рабства.

Поселилась она среди других народов,

но не нашла покоя.

Все ее преследователи настигли ее

посреди бедствия.

4Дороги Сиона плачут,

потому что никто не идет на праздник.

Все ворота столицы опустели,

стонут священники ее,

девушки печальны,

горько и ей самой.

5Враги правят ею,

неприятели ее благоденствуют.

Горе послал ей Господь

из-за множества ее беззаконий.

Дети ее пошли в плен,

враг гонит их перед собой.

6Все великолепие покинуло дочь Сиона.

Вожди ее подобны оленям, не находящим пастбища;

обессиленные, они бегут впереди погонщика.

7В дни своих бедствий и скитаний

вспомнила столица о всех драгоценностях,

которые были у нее в прежние дни.

Когда народ ее попал в руки врага,

никто не помог ей;

враги смотрели на нее

и смеялись над ее поражением.

8Ужасно согрешила столица,

поэтому она и стала нечистой.

Все, кто прославлял ее, теперь презирают,

потому что увидели ее наготу.

Да и сама она вздыхает и отворачивается;

9ее нечистота замарала ей подол.

И так как она не задумывалась о будущем,

падение ее было ошеломительным,

и не было у нее утешителя.

– О Господь, взгляни на мое страдание,

ведь враг торжествует!

10Враг похитил у нее все самое ценное;

она видит, как в ее святилище входят язычники,

те, кому Ты запретил вступать в Твое собрание.

11Весь народ ее стонет в поисках хлеба,

отдает драгоценности свои за пищу,

лишь бы жизнь сохранить.

– О Господь, обрати Твой взор

и посмотри как я унижена!

Вопль Иерусалима

12Неужели это не трогает вас, все проходящие мимо?

Взгляните и посмотрите,

есть ли страдание, подобное моему страданию,

которое постигло меня,

которое Господь послал на меня

в день Своего пылающего гнева?

13Свыше Он послал огонь,

послал его в кости мои.

Он раскинул сеть для ног моих,

опрокинул меня.

Он опустошил меня

и наполнил дни мои болезнью.

14Беззакония мои Он взял

и, связав их, сделал из них ярмо.

Владыка возложил его на шею мою,

чем ослабил силы мои.

Он отдал меня в руки тех,

кому я не могу противостоять.

15Владыка низложил среди меня

всех сильных моих,

собрал против меня войска,

чтобы истребить моих юношей;

как в давильне, истоптал Владыка

девственную дочь Иуды1:15 То есть народ Иудеи..

16Вот почему я плачу,

и из глаз моих потоками льются слезы.

Рядом нет никого, кто бы утешил меня,

оживил бы душу мою.

Дети мои разорены,

потому что враг одолел их.

17Сион простирает руки свои,

но нет никого, кто бы утешил его.

Господь повелел окружающим народам

враждовать с Иаковом.

Иерусалим стал мерзостью среди них.

18– Праведен Господь,

а я была непокорна слову Его.

Послушайте, все народы,

и взгляните на страдание мое.

Девушки и юноши мои

пошли в плен.

19Звала я возлюбленных моих,

но они меня предали.

Священники и старцы мои

умирали в городе,

ища себе пищи,

чтобы сохранить себе жизнь.

20Взгляни, Господь, как я страдаю:

душа моя мается,

и сердце потеряло покой,

потому что я упорно противилась Тебе.

Снаружи меч лишил меня детей,

а внутри – поселилась смерть.

21Люди услышали стоны мои,

но нет мне утешителя.

Все враги мои услышали о бедствии моем

и были рады тому, что Ты сделал со мною.

Пусть же наступит день,

объявленный Тобой,

когда с ними случится то же,

что и со мной.

22Пусть все их злодеяния предстанут пред Тобой,

и поступи с ними так же,

как Ты поступил со мною

за все грехи мои,

потому что многочисленны стоны мои,

и изнемогает сердце мое.