Ezekieli 10 – CCL & BPH

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ezekieli 10:1-22

Ulemerero Uchoka ku mʼNyumba ya Mulungu

1Ine nditayangʼana ku thambo limene lili pamwamba pa mitu ya akerubi ndinangoona chinthu chooneka ngati mpando waufumu wa mwala wa safiro. 2Tsono Yehova anawuza munthu wovala chovala chabafuta uja kuti, “Pita pakati pa mikombero kunsi kwa akerubi. Udzaze manja ako ndi makala oyaka amene ali pakati pa akerubiwo ndipo uwawaze mu mzinda.” Iye anachita zimenezi ine ndikuona.

3Apa akerubiwo anali atayima mbali ya kummwera kwa Nyumba ya Mulungu pamene munthuyo ankalowa. Tsono mtambo unadzaza bwalo lamʼkati. 4Ndipo ulemerero wa Yehova unachoka pamwamba pa akerubi ndipo unafika ku chiwundo cha Nyumba ya Mulungu. Mtambo unadzaza Nyumba ya Mulungu, ndipo kuwala kwa ulemerero wa Yehova kunadzaza bwalolo. 5Phokoso la mapiko a akerubi limamveka mpaka ku bwalo lakunja, monga momwe linamvekera liwu la Mulungu Wamphamvuzonse akamayankhula.

6Kenaka Yehova analamula munthu wovala chovala chabafuta uja kuti, “Pala moto pakati pa mikombero, pakati pa akerubi.” Munthu uja anapitadi nakayima pa mbali pa mkombero umodzi. 7Ndipo mmodzi wa akerubi anatambalitsa dzanja lake mpaka pa moto umene unali pakati pawo. Iye anapalako motowo ndipo anapatsa munthu wovala chovala chabafuta uja. Tsono iye anawulandira natuluka. 8Ndiye kuti kunsi kwa mapiko akerubi kumaoneka zinthu zooneka ngati manja a munthu.

9Ine nditayangʼanitsitsa ndinaona mikombero inayi pambali pa akerubi. Pambali pa kerubi aliyense panali mkombero umodzi; mikomberoyo inkanyezimira ngati miyala yokongola ya krizoliti. 10Maonekedwe a mikombero inayi ija anali ofanana. Mkombero uliwonse umaoneka ngati mkombero wolowana ndi unzake. 11Poyenda akerubiwo, amapita mbali iliyonse ya mbali zinayizo kumene akerubiwo amayangʼana. Mikomberoyo simatembenuka pamene akerubiwo ankayenda. Kulikonse kumene mutu walunjika nʼkumene ankapita popanda kutembenuka. 12Matupi awo onse, misana yawo, manja awo ndi mapiko awo zinali ndi maso okhaokha, monganso mʼmene inalili mikombero yawo inayi ija. 13Ine ndinamva mikombero ikutchedwa kuti, “mikombero yakamvuluvulu.” 14Kerubi aliyense anali ndi nkhope zinayi. Nkhope yoyamba inali ya Kerubi, nkhope yachiwiri inali ya munthu, nkhope yachitatu inali ya mkango ndipo nkhope yachinayi inali ya chiwombankhanga.

15Tsono akerubi aja anawuluka. Izi zinali zamoyo zija zimene ndinaziona ku mtsinje wa Kebara. 16Pamene akerubi ankayenda, nayonso mikombero ya mʼmbali mwawo inkayenda. Akerubiwo ankati akatambasula mapiko awo kuti auluke mikombero sinkachoka mʼmbali mwawo. 17Akerubiwo ankati akayima, mikombero inkayimanso. Ngati akerubiwo auluka, mikomberoyo inkapita nawo chifukwa mzimu wa zamoyozo ndiwo unkayendetsa mikomberoyo.

18Pamenepo ulemerero wa Yehova unachoka pa chiwundo cha Nyumba ya Mulungu ndi kukakhala pamwamba pa akerubi. 19Ine ndikuona akerubi, anatambasula mapiko awo ndi kuwuluka. Pamene ankapita, mikombero inapita nawo pamodzi. Akerubi anakayima pa khomo la chipata cha kummawa cha Nyumba ya Yehova. Tsono ulemerero wowala wa Mulungu wa Israeli unali pamwamba pawo.

20Izi ndizo zamoyo ndinaziona pansi pa Mulungu wa Israeli ku mtsinje wa Kebara, ndipo ndinazindikira kuti anali akerubi. 21Kerubi aliyense anali ndi nkhope zinayi ndi mapiko anayi, ndipo kunsi kwa mapiko awo kunali chinthu chimene chimaoneka ngati manja a munthu. 22Nkhope zawo zinali zofanana ndi zomwe ndinaziona ku mtsinje wa Kebara. Kerubi aliyense amayenda molunjika.

Bibelen på hverdagsdansk

Ezekiels Bog 10:1-22

Herrens herlighed forlader templet

1Derefter så jeg i mit syn noget, der lignede en trone af safir, som stod på den lysende hvælving over kerubernes hoveder. 2Jeg hørte Herren sige til manden, der var klædt i linned: „Gå ind mellem hjulene under keruberne og tag en håndfuld af de glødende kul og strø dem ud over byen.”

3Da manden fik besked på at gå hen til keruberne, stod de ved templets sydside, og den strålende sky af Herrens herlighed fyldte den indre forgård. 4Herrens stråleglans havde løftet sig fra keruberne og flyttet sig hen over templets indgang, så hele templet fyldtes af skyen, og hele forgården fyldtes af skæret fra Herrens herlighed. 5Lyden af kerubernes vingeslag kunne høres helt ud i den ydre forgård, og det lød, som når Gud, den Almægtige, taler.

6Da Herren befalede manden at gå ind mellem hjulene under keruberne og tage en håndfuld glødende kul, gik han hen og stillede sig ved et af hjulene. 7Derefter rakte en af keruberne hånden ud, tog nogle af de glødende kul fra ilden og gav dem til ham. Han tog imod kullene og gik tilbage, hvor han kom fra.

8Under kerubernes vinger var der nemlig noget, der lignede menneskehænder. 9Under hver af de fire keruber var der et hjul, der funklede som ædelsten. 10Alle hjulene var ens og inden i hvert hjul sad der et andet hjul på tværs. 11Keruberne og hjulene kunne bevæge sig i alle fire retninger uden at vende sig. De fulgte efter den ledende kerub uden at vende sig. 12Kerubernes krop, ryg, hænder og vinger var fulde af øjne, og det samme gjaldt hjulene. 13Jeg hørte, at hjulene blev kaldt „hvirvelhjul”.

14Hver af keruberne havde fire ansigter: et kerubansigt, et menneskeansigt, et løveansigt og et ørneansigt.

15Derpå bevægede de sig op i luften. De var ligesom de levende væsener, jeg tidligere havde set ved Kebarfloden. 16Når keruberne flyttede sig, gjorde hjulene det også. Når keruberne hævede sig i vejret, fulgte hjulene med dem og blev hos dem, mens de fløj. 17Hvor som helst de bevægede sig hen, fulgte hjulene med, for deres ånd var i hjulene.

18Derefter flyttede Herrens herlighed sig fra templets indgang til tronen over keruberne, 19og jeg så keruberne sprede vingerne ud og løfte sig fra jorden sammen med hjulene. De fløj væk fra templet, men gjorde ophold ved den østlige port, og Israels Guds herlighed hvilede hele tiden over dem.

20Jeg var klar over, at disse keruber var de samme som de levende væsener, jeg tidligere havde set under Israels Guds trone ved Kebarfloden. 21Hver af dem havde fire ansigter og fire vinger, og under deres vinger var der noget, som lignede menneskehænder. 22Deres ansigter var som dem, jeg havde set ved Kebarfloden, og de bevægede sig også på samme måde.