Ezara 3 – CCL & CCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ezara 3:1-13

Kumangidwanso kwa Guwa la Nsembe

1Utafika mwezi wa chisanu ndi chiwiri Aisraeli atakhala kale mʼmidzi yawo, anthu anasonkhana ku Yerusalemu ndi cholinga chimodzi. 2Kenaka Yesuwa mwana wa Yozadaki ndi ansembe anzake pamodzi ndi Zerubabeli mwana wa Sealatieli ndi abale ake anayamba kumanga guwa lansembe la Mulungu wa Israeli. Anatero pofuna kuti aziperekapo nsembe zopsereza monga analembera mʼbuku la Mose, munthu wa Mulungu uja. 3Ndi mantha ndi mantha chifukwa cha anthu a mʼmayikomo, iwo anamanga guwalo pa maziko ake akale, ndipo anapereka nsembe zopsereza kwa Mulungu pa guwapo mmawa ndi madzulo. 4Ankasunga tsiku la chikondwerero cha misasa monga momwe zinalembedwera. Ankaperekanso nsembe za tsiku ndi tsiku monga mwa chiwerengero chake potsata mwambo wake wa tsiku ndi tsiku monga zinalembedwa. 5Pambuyo pake, ankapereka nsembe zopsereza, nsembe zopereka pa nthawi ya mwezi watsopano ndi za pa masiku onse a chikondwerero oyikidwa kutamandira Yehova, kudzanso nsembe zaufulu zopereka kwa Yehova. 6Kuyambira pa tsiku loyamba la mwezi wachisanu ndi chiwiri, iwo anayambanso kupereka nsembe zopsereza kwa Yehova, ngakhale kuti maziko a Nyumba ya Yehova anali asanamangidwe.

Kumangidwanso kwa Nyumba ya Mulungu

7Ndipo anapereka ndalama kwa amisiri a miyala ndi kwa amisiri a matabwa, ndi chakudya, chakumwa ndi mafuta kwa anthu a ku Sidoni ndi a ku Turo, kuti abweretse mitengo ya mkungudza pa nyanja kuchokera ku Lebanoni mpaka ku Yopa. Zonsezi anachita malinga ndi chilolezo chimene analandira kuchokera kwa Koresi, mfumu ya Peresiya.

8Tsono mu chaka chachiwiri atabwera ku Yerusalemu, ku malo akale a Nyumba ya Yehova, mwezi wachiwiri Zerubabeli mwana wa Sealatieli, Yesuwa mwana wa Yozadaki pamodzi ndi abale awo onse, ansembe, Alevi ndi onse amene anabwera ku Yerusalemu kuchokera ku ukapolo, anayamba kugwira ntchito. Iwo anasankha Alevi a zaka zoyambira makumi awiri kuti aziyangʼanira ntchito ya kumanga Nyumba ya Yehova. 9Yesuwa ndi ana ake aamuna kudzanso abale ake, Kadimieli ndi ana ake (ana a Yuda) onse pamodzi anasenza udindo woyangʼanira antchito ku Nyumba ya Mulungu, kuphatikizanso ana a Henadadi komanso Alevi, ana awo ndi abale awo.

10Amisiri omanga nyumba atamanga maziko a Nyumba ya Yehova, ansembe anabwera akuyimba malipenga, atavala zovala zaunsembe. Ndipo Alevi, zidzukulu za Asafu, anadza akuyimba matambolini ndi kutenga udindo wawo wotamanda Yehova, potsata malangizo a Davide mfumu ya Aisraeli. 11Iwo ankayimba motamanda ndi mothokoza Yehova nyimbo iyi:

“Yehova ndi wabwino;

chikondi chake pa Israeli ndi chamuyaya.”

Ndipo anthu onse ankafuwula kwambiri kumutamanda Yehova, chifukwa maziko a Nyumba ya Yehova anali kumangidwa. 12Koma ambiri mwa ansembe, Alevi ndiponso atsogoleri amabanja, akuluakulu amene anaona Nyumba ya Yehova yakale, analira mokweza pamene anaona maziko a nyumbayi akumangidwa. Komanso ena ambiri ankafuwula mosangalala. 13Choncho panalibe amene ankatha kusiyanitsa liwu lofuwula mokondwerera ndi liwu la anthu olira, chifukwa anthuwo ankafuwula kwambiri. Ndipo liwu lofuwulalo limamveka kutali.

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

以斯拉记 3:1-13

重建祭坛

1到了七月,以色列人已安居各城,他们万众一心地聚集在耶路撒冷2约萨达的儿子耶书亚及其他祭司、撒拉铁的儿子所罗巴伯及其亲属,一起重新筑造以色列上帝的祭坛,为要照上帝的仆人摩西在律法书上的记载在坛上献燔祭。 3他们虽然惧怕当地的居民,还是在原来的根基上重建祭坛,并早晚在上面向耶和华献燔祭。 4他们照律法书的记载守住棚节,每天按规定的数目献上燔祭。 5之后,他们献上日常的燔祭,并在朔日3:5 朔日”即每月初一。和耶和华所定的一切节期献祭,又向耶和华献上自愿献的祭。 6尽管耶和华殿的根基还没有立好,从七月一日起,他们就开始向耶和华献燔祭。 7他们付给石匠和木匠银子,并经波斯塞鲁士批准,供给泰尔人和西顿人食物、酒和油,换取他们把香柏木从黎巴嫩经海路运到约帕

开始重建圣殿

8在回到耶路撒冷上帝殿的第二年二月,撒拉铁的儿子所罗巴伯约萨达的儿子耶书亚及其祭司和利未亲族,以及所有从流亡之地回到耶路撒冷的人,开始重建耶和华的殿,并派二十岁以上的利未人做督工。 9何达威雅3:9 何达威雅”希伯来文是“犹大”,参考2:40的后裔,即耶书亚及其子孙和弟兄、甲篾及其子孙,与利未希拿达的子孙及其弟兄同心协力地监督在上帝殿里做工的人。

10工人立耶和华殿的根基时,祭司身穿礼服拿着号角,利未亚萨的子孙拿着钹各就各位,照以色列大卫所定的规矩赞美耶和华。 11他们彼此唱和,赞美、称谢耶和华,说:

“祂是美善的,

因为祂向以色列人永施慈爱!”

所有人都高声欢呼赞美耶和华,因为耶和华殿的根基已经立好。 12许多曾见过旧殿的年长的祭司、利未人和族长看见这殿的根基,不禁放声大哭,也有很多人高声欢呼。 13人们无法分辨是痛哭声还是欢呼声,因为众人都大声呼喊,声音传到远处。