Estere 2 – CCL & NUB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Estere 2:1-23

Mfumu Ikwatira Estere

1Pambuyo pake mtima wa Ahasiwero utatsika, Ahasiwero anakumbukira Vasiti ndi zimene anachita Vasitiyo. Anakumbukiranso lamulo lomukhudza limene anasindikiza. 2Tsono anyamata a mfumu amene ankamutumikira anati, “Mfumu, akufunireni anamwali okongola. 3Mfumu isankhe oyangʼanira pa chigawo chilichonse cha ufumu wake kuti abwere nawo pamodzi anamwali onse okongola ku nyumba yosungira akazi ku Susa. Hegai, mdindo wofulidwa wa mfumu, amene amayangʼanira amayi, akhale wosamalira anamwaliwa ndipo aziwapatsa mafuta odzola. 4Ndipo namwali amene mfumu yakondwera naye akhale mfumukazi mʼmalo mwa Vasiti.” Mfumu inakondwera ndi uphunguwu, ndipo inachita momwemo.

5Myuda wina wa fuko la Benjamini, dzina lake Mordekai, mwana wa Yairi, mwana wa Simei, mwana wa Kisi, anali mu mzinda wa Susa. 6Iyeyu anali mmodzi mwa anthu amene anatengedwa ukapolo ndi Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni kuchokera ku Yerusalemu pamodzi ndi Yekoniya mfumu ya Yuda. 7Mordekai nʼkuti atalera Hadasa, amene ankatchedwanso Estere, mwana wamkazi wa amalume ake chifukwa analibe abambo kapena amayi. Mtsikanayu anali wokongola ndi wooneka bwino ndipo Mordekai ankamutenga ngati mwana wake weniweni pamene abambo ndi amayi ake anamwalira.

8Lamulo la mfumu atalilengeza ndi kubwera nawo pamodzi anamwali ambiri ku mzinda wa Susa kuti akasamalidwe ndi Hegai, Estere nayenso anatengedwa kupita naye ku nyumba ya mfumu kuti akasamalidwe ndi Hegai woyangʼanira nyumba yosungiramo akazi uja. 9Hegai anasangalatsidwa naye namwaliyo ndipo anamukomera mtima. Mosataya nthawi anamupatsa mafuta ake odzola ndi chakudya chapadera. Anamusankhiranso anamwali asanu ndi awiri a ku nyumba ya mfumu kuti azimutumikira, ndipo iye pamodzi ndi anamwali omutumikira aja anawapatsa malo abwino koposa mʼnyumba yosungira akazi.

10Estere sanawulule mtundu wake ndi abale ake chifukwa Mordekai anamuletsa kutero. 11Tsiku ndi tsiku Mordekai ankayendayenda pafupi ndi bwalo la nyumba yosungiramo akazi ija kuti adziwe za moyo wa Estere ndi kuti zinthu zikumuyendera bwanji.

12Tsono nthawi inkafika kuti namwali aliyense akaonekere kwa mfumu Ahasiwero, pakutha pa miyezi khumi ndi iwiri yomwe inakhazikitsidwa kuti amayi azidzikongoletsa. Pa miyezi isanu ndi umodzi ankadzola mafuta a mure ndipo pa miyezi isanu ndi umodzi inayo ankadzola zonunkhira ndi zokongoletsa. 13Ndipo namwali ankapita kwa mfumu motere: Ankaloledwa kutenga chilichonse angafune mʼnyumba yosungiramo akazi kupita nacho ku nyumba ya mfumu. 14Ankalowa madzulo kwa mfumu ndi kutuluka mmawa kupita ku nyumba ina yosungira akazi yomwe ankayangʼanira ndi Saasigazi, mdindo wofulidwa wa mfumu amene amayangʼanira akazi a mfumu. Namwali sankabwerera kwa mfumu pokhapokha amukomere mtima ndi kumuyitana potchula dzina lake.

15Tsono inafika nthawi kuti Estere, mwana wamkazi wa Abihaili amenenso analeredwa ndi Mordekai amalume ake, alowe kwa mfumu. Iye sanapemphe kanthu kalikonse, koma anatenga zokhazo zimene ananena Hegai mdindo wofulidwa wa mfumu woyangʼanira nyumba yosungiramo akazi. Ndipo aliyense amene anamuona Estere, anasangalatsidwa naye. 16Anapita naye kwa mfumu Ahasiwero ku nyumba ya ufumu pa mwezi wa khumi, mwezi wa Tebete, chaka cha chisanu ndi chiwiri cha ufumu wake.

17Ndipo mfumu inamukonda Estere koposa wina aliyense wa akazi aja, kotero inamukonda ndi kumukomera mtima koposa wina aliyense wa anamwali aja. Choncho anamumveka chipewa chaufumu pa mutu pake nakhala mfumukazi mʼmalo mwa Vasiti. 18Ndipo mfumu inakonza phwando lalikulu, phwando la Estere, kukonzera anthu olemekezeka ndi nduna zake zonse. Analamuliranso kuti anthu mʼzigawo zonse asapereke msonkho ndipo anapereka mphatso monga mwakukoma mtima kwa mfumu.

Mordekai Awulula Chiwembu

19Anamwali atasonkhanitsidwa pamodzi, Mordekai anakhala pansi pa chipata cha mfumu. 20Koma Estere anali asanawululebe za mtundu wake ndi anthu a pa banja lake monga momwe analamulira Mordekai, chifukwa anapitirira kutsata malangizo a Mordekai monga ankachitira pamene ankamulera.

21Pa nthawi imene Mordekai ankalondera pa chipata cha mfumu, Bigitana ndi Teresi, awiri mwa adindo ofulidwa amfumu, olondera pa khomo la nyumba yake, anayipidwa mtima ndipo anakonza chiwembu chofuna kupha mfumu Ahasiwero. 22Koma Mordekai atazindikira za chiwembuchi anawuza mfumukazi Estere ndipo iye anakawuza mfumu mʼmalo mwa Mordekai. 23Ndipo pamene anafufuza za chiwembuchi kuti zinali zoona, adindo awiriwa anaphedwa monyongedwa. Zinthu izi zinalembedwa mʼbuku la Mbiri ndi kusungidwa ndi Mfumu.

Swedish Contemporary Bible

Ester 2:1-23

Kungen väljer Ester

1Efter en tid, när kung Xerxes vrede hade lagt sig, kom han att tänka på vad Vashti hade gjort och vad man beslutat om henne.

2”Låt oss leta reda på vackra, orörda flickor åt kungen”, föreslog hans tjänare. 3”Kungen bör utse i varje provins tjänstemän som kan samla alla orörda vackra unga flickor till kungens harem i Susas borg. Kungens hovman Hegaj, som har ansvaret för kvinnorna, får ta hand om dem och se till att de får sin skönhetsbehandling. 4Sedan får den flicka som behagar kungen mest bli drottning i Vashtis ställe.”

Kungen gillade förslaget och följde det genast.

5I borgen i Susa fanns det en jude som hette Mordokaj, son till Jair, son till Shimi, son till Kish från Benjamins stam. 6Han hade deporterats från Jerusalem samtidigt med de fångar som tillfångatogs med Juda kung Jekonja av Nebukadnessar, kungen av Babylonien. 7Mordokaj var fosterfar till sin kusin Hadassa, eller Ester, som hon också kallades, och som var föräldralös. Hon var välväxt och vacker, och efter hennes föräldrars död hade Mordokaj adopterat henne som sin egen dotter.

8När nu kungens befallning och förordning tillkännagavs och många flickor fördes till kungens harem i Susas borg och togs om hand av Hegaj, hämtades också Ester till kungapalatset och togs om hand av Hegaj, som hade ansvaret för kvinnorna. 9Flickan behagade honom och vann hans välvilja. Han såg genast till att hon fick sina skönhetsbehandlingar och den mat hon skulle ha och sju tjänsteflickor, som valts ut åt henne från kungapalatset. Han flyttade in henne med hennes tjänsteflickor i haremets främsta del.

10Ester hade inte avslöjat något om sin nationalitet eller sin släkt, eftersom Mordokaj hade förbjudit henne att göra det. 11Han promenerade varje dag utanför haremsgården för att ta reda på hur Ester hade det och hur hon behandlades.

12Innan en flickas tur kom att komma in till kung Xerxes, fick hon under tolv månader gå igenom skönhetsbehandlingar, som det var föreskrivet för kvinnorna – först sex månader med myrraolja och sedan sex månader med välluktande kryddor och andra skönhetsmedel för kvinnor. 13När det sedan var hennes tur att gå till kungen, fick hon ta med sig vad hon ville från haremet till kungapalatset. 14Hon gick dit på kvällen och återvände nästa morgon till en annan del av haremet och lämnades i hovmannen Shaasgas omsorg, som hade ansvaret för konkubinerna. Sedan kom hon inte in till kungen fler gånger, om hon inte hade behagat honom så mycket att han personligen kallade på henne.

15När turen att gå in till kungen kom till Ester, Avichajils dotter, som Mordokaj hade adopterat efter sin farbror, begärde hon inget annat än det som kungens hovman Hegaj, som hade ansvaret för kvinnorna, föreslog henne. Hon vann välvilja hos alla som såg henne.

16Ester blev hämtad till kung Xerxes i palatset i den tionde månaden, tevet, under hans sjunde regeringsår.

17Kungen blev mer förtjust i Ester än i någon annan kvinna, och hon vann hans välvilja och kärlek mer än någon av de andra flickorna. Han satte den kungliga kronan på hennes huvud och gjorde henne till drottning i stället för Vashti. 18Kungen anordnade ett stort gästabud för alla sina furstar och tjänare till Esters ära. Han utlyste en allmän ledighet2:18 Eller efterskänkte skatt, eller möjligen beviljade amnesti. i provinserna och gav kungligt generösa gåvor.

Mordokaj avslöjar ett mordförsök

19När man samlade ihop unga flickor en andra gång, satt Mordokaj vid kungens port.

20Ester hade inte avslöjat något om sin släkt och nationalitet, precis som Mordokaj hade sagt till henne. Hon lydde honom alltjämt, som om hon fortfarande var i hans vård.

21En dag, när Mordokaj satt i kungens port, blev Bigtan och Teresh, två av de hovmän som höll vakt vid porten, förbittrade på kung Xerxes och sökte efter tillfälle att döda honom. 22Mordokaj fick reda på det och berättade det för drottning Ester, som i sin tur talade om det för kungen å Mordokajs vägnar. 23En undersökning av saken visade att det var sant, och då spetsades de två männen på pålar. Detta blev antecknat i krönikan i kungens närvaro.