Estere 1 – CCL & NUB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Estere 1:1-22

Vasiti Mkazi wa Mfumu Achotsedwa

1Izi ndi zimene zinachitika pa nthawi ya ufumu wa Ahasiwero, amene analamulira zigawo 127 kuyambira ku India mpaka ku Kusi. 2Pa nthawi imeneyi nʼkuti mfumu Ahasiwero atakhazikika pa mpando wake wa ufumu mu mzinda wa Susa, 3ndipo mʼchaka chachitatu cha ufumu wake anakonza phwando la olemekezeka ndi nduna zake. Atsogoleri a nkhondo a ku Peresiya ndi Mediya, anthu olemekezeka pamodzi ndi nduna za mʼzigawo zonse anasonkhana kwa iye.

4Pa nthawi yomweyi kwa masiku 180 a phwando mfumu inkaonetsa kulemera kwa ulemerero wa ufumu wake ndiponso kukongola ndi kukula kwa ufumu wake. 5Atatha masiku amenewa, kwa masiku ena asanu ndi awiri mfumu inakonzanso phwando la anthu onse okhala mu mzinda wa Susa kuyambira anthu olemekezeka mpaka anthu wamba ku bwalo la munda la nyumba yake yaufumu. 6Bwalo la mundali analikongoletsa ndi makatani a nsalu zoyera ndi za mtundu wamtambo zimene anazimangirira ndi zingwe za nsalu zoyera ndi zapepo ku mphete za siliva zimene anazikoloweka pa nsanamira za maburo. Anayika mipando yopumirapo yagolide ndi siliva pabwalo la miyala yoyala yamtengowapatali yofiira, ya marabulo, ndi yonyezimira. 7Anapereka zakumwa mʼchikho zagolide zamitundumitundu, ndipo vinyo waufumu anali wochuluka kwambiri monga mwa kukoma mtima kwa mfumu. 8Monga mwa lamulo la mfumu aliyense anamwa mʼmene anafunira, pakuti mfumu inawuza otumikira ake kuti apatse aliyense monga mwa kukonda kwake.

9Mkazi wa mfumu Vasiti nayenso anakonzera phwando amayi ku nyumba ya ufumu ya mfumu Ahasiwero.

10Pa tsiku la chisanu ndi chiwiri, pamene mfumu Ahasiwero inaledzera ndi vinyo, inalamula adindo ofulidwa asanu ndi awiri amene ankamutumikira: Mehumani, Bizita, Haribona, Bigita, Abagita, Zetara, ndi Karikasi 11kuti abwere naye mfumukazi Vasiti pamaso pa mfumu atavala chipewa chaufumu. Cholinga cha mfumu chinali choti adzamuonetse kwa anthu onse ndi olemekezeka, chifukwa anali wokongola kwambiri. 12Koma antchito atapereka uthenga wa mfumu kwa mfumukazi, Vasiti anakana kubwera. Tsono mfumu inakwiya ndi kupsa mtima.

13Mfumu inayankhula ndi anthu anzeru ndi ozindikira choyenera kuchita popeza chinali chikhalidwe chake kufunsa uphungu kwa akatswiri pa nkhani za malamulo ndi kuweruza kolungama. 14Anthu amene ankakhala pafupi ndi mfumu anali awa: Karisena, Setara, Adimata, Tarisisi, Meresi, Marisena ndi Memukani, olemekezeka asanu ndi awiri a ku Peresiya ndi Medina amene ankaloledwa mwapadera kuonana ndi mfumu ndipo anali pamwamba kwambiri mu ufumuwo.

15Mfumu inafunsa kuti, “Kodi titani naye mfumukazi Vasiti mwa lamulo, popeza sanamvere lamulo la ine mfumu Ahasiwero limene adindo ofulidwa anakamuwuza?”

16Ndipo Memukani anayankha pa maso pa mfumu ndi olemekezeka anzake kuti, “Mfumukazi Vasiti sanalakwire mfumu yokha, koma walakwiranso olemekezeka onse ndi anthu onse okhala mʼzigawo zonse za mfumu Ahasiwero. 17Pakuti amayi onse adzadziwa zimene wachita mfumukazi ndipo kotero adzapeputsa amuna awo ndi kunena kuti, ‘Mfumu Ahasiwero analamulira kuti abwere naye mfumukazi Vasiti kwa iye koma sanapite.’ 18Lero lomwe lino amayi olemekezeka a ku Peresiya ndi Mediya amene amva zimene wachita mfumukazi adzaganiza zochita chimodzimodzi kwa nduna zonse za mfumu. Ndipo kupeputsana ndi kukongola zidzapitirira.”

19“Choncho, ngati chikukomerani mfumu, lamulirani kuti Vasiti asadzaonekerenso pamaso pa mfumu Ahasiwero. Lamuloli lilembedwe mʼmabuku a malamulo a Aperezi ndi Amedi kuti lisadzasinthike. Pamalo pa Vasiti ngati mfumukazi payikidwepo mkazi wina amene ali bwino kuposa iye. 20Ndipo lamulo la mfumuli lilengezedwa mʼdziko lake lonse ngakhale lili lalikulu, amayi onse adzapereka ulemu kwa amuna awo, amuna olemekezeka mpaka amuna wamba.”

21Mfumu ndi nduna zake anakondwera ndi uphungu uwu, kotero mfumu inachita monga momwe ananenera Memukani. 22Mfumu inatumiza makalata ku madera onse a ufumu wake, chigawo chilichonse mʼzilembo zawo ndi ku mtundu uliwonse mʼchiyankhulo chawochawo kulengeza kuti mwamuna ayankhule chilichonse chimene chikumukomera.

Swedish Contemporary Bible

Ester 1:1-22

Ester blir drottning

(1:1—2:23)

Drottning Vashti blir avsatt

1Detta hände under kung Xerxes1:1 Ahasveros enligt det hebreiska sättet att återge det persiska namnet. tid, som härskade över 127 provinser från Indien ända till Kush. 2Han regerade från sin tron i borgen i Susa. 3Under sitt tredje regeringsår ordnade han en stor fest för alla sina furstar och tjänare. Persiens och Mediens militära ledning, adeln och furstarna från provinserna samlades alla hos honom. 4Under en så lång tid som 180 dagar visade han den enorma rikedom och all den kungliga glans och prakt som fanns i hans rike.

5När dessa dagar var över anordnade kungen en sju dagar lång fest för alla i borgen i Susa, från den högste till den lägste, i kungapalatsets inhägnade trädgård. 6Där hängde draperier av vitt och blått linne, fästa med vita och purpurröda snören i ringar av silver på pelare av marmor. Soffor av guld och silver stod på golvet, som var lagt av grön och vit marmor, pärlemor och annan värdefull sten. 7Vinet serverades i guldbägare av olika form, ingen lik den andra, och det fanns gott om vin, för kungen var mycket generös. 8Kungen hade befallt att det inte fick vara något dryckestvång, utan var och en fick dricka så mycket eller lite han själv önskade. Servitörerna hade fått order om detta.

9Samtidigt höll drottning Vashti en fest för kvinnorna inne i kung Xerxes palats. 10På den sjunde dagen, när kungen var upprymd av vinet, befallde han sina sju personliga hovmän – Mehuman, Bisseta, Harvona, Bigta, Avagta, Setar och Karkas –  11att föra drottning Vashti till honom med krona på huvudet. Hon var mycket vacker, och han ville visa upp hennes skönhet för folken och furstarna. 12Men när hovmännen framförde kungens befallning, vägrade drottning Vashti att komma.

Kungen blev då rasande och brann av vrede. 13Han brukade rådgöra med sina visaste experter om saker som gällde lagar och förordningar, och nu vände han sig till dem. 14Det var de sju furstarna i Persien och Medien: Karshena, Shetar, Admata, Tarshish, Meres, Marsena och Memukan. Alla dessa var högt uppsatta män i landet och stod kungen mycket nära.

15”Vad ska man enligt lagen göra med drottning Vashti?” frågade han dem. ”Hon har ju vägrat lyda kung Xerxes order som hans hovmän framfört.”

16Memukan svarade då inför kungen och furstarna: ”Drottning Vashti har handlat fel, inte bara i kungens närvaro, utan också mot alla furstar och allt folk i kung Xerxes provinser. 17Nu kommer alla kvinnorna att få kännedom om vad drottningen gjort och förakta sina män och säga: ’Kung Xerxes befallde att drottning Vashti skulle föras till honom, men hon kom inte!’ 18Innan den här dagen är slut kommer hustrurna till alla furstarna i Persien och Medien att ha hört talas om vad drottningen har gjort, och sedan kommer de att tala till sina män på samma sätt. Följden blir förakt och bråk utan ände.

19Om du nu, o kung, finner det för gott, så låt det utfärdas en kunglig befallning i Persiens och Mediens lagar, som inte kan ändras, att drottning Vashti aldrig mer får komma inför kung Xerxes. Sedan ska hennes kungliga ställning ges åt någon som är bättre än hon. 20När denna kungliga befallning blir känd i hans väldiga rike kommer varje kvinna att visa respekt för sin man, från den högste till den lägste.”

21Kungen och furstarna samtyckte till Memukans råd, och kungen gjorde som han föreslagit. 22Han skickade brev till alla sina provinser, till varje provins med dess egen skrift och till varje folk på dess eget språk, att varje man skulle vara herre i sitt hus och tala sitt folks språk.