Eksodo 37 – CCL & KLB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Eksodo 37:1-29

Bokosi la Chipangano

1Bezaleli anapanga Bokosi la Chipangano lamatabwa amtengo wa mkesha. Kutalika kwake kunali masentimita 114, mulifupi mwake munali masentimita 69, msinkhu wake masentimita 69. 2Iye analikuta bokosilo ndi golide wabwino kwambiri mʼkati mwake ndi kunja komwe. Anapanganso mkombero wagolide kuzungulira bokosilo. 3Iye anapanga mphete zinayi zagolide ndi kuzimangirira ku miyendo yake inayi ija, mbali ina ziwiri ndi mbali inanso ziwiri. 4Kenaka anapanga mizati yamtengo wa mkesha ndi kuzikuta ndi golide. 5Ndipo analowetsa nsichizo mʼmphete zija za mbali zonse ziwiri za bokosilo kuti azinyamulira.

6Iye anapanga chivundikiro cha bokosilo cha golide wabwino kwambiri, kutalika kwake masentimita 114, mulifupi mwake masentimita 69. 7Ndipo anapanga Akerubi awiri agolide osula ndi nyundo ndi kuwayika mbali ziwiri za chivundikirocho. 8Iye anapanga kerubi mmodzi mbali ina ndi wina mbali inayo. Akerubiwa anawapangira limodzi ndi chivundikirocho mʼmapeto mwa mbali ziwirizo. 9Mapiko a Akerubiwo anatambasukira pamwamba pa chivundikiro cha bokosilo kuti achiphimbe. Akerubiwo anakhala choyangʼanana, aliyense kuyangʼana chivundikirocho.

Mapangidwe a Tebulo

10Iwo anapanga tebulo la matabwa amtengo wa mkesha, mulitali mwake masentimita 91, mulifupi mwake masentimita 46, msinkhu wake masentimita 69. 11Kenaka analikuta ndi golide wabwino kwambiri, ndipo anapanga mkombero wagolide mʼmbali mwake. 12Iwo anapanga feremu yozungulira tebulo, mulifupi mwake ngati chikhatho cha dzanja, ndipo anayika mkombero wagolide kuzungulira feremuyo. 13Iwo anapanga mphete zinayi zagolide ndipo anazilumikiza ku ngodya zake zinayi, kumene kunali miyendo yake inayi. 14Mphetezo anaziyika kufupi ndi feremu kuti azikolowekamo nsichi zonyamulira tebuloyo. 15Anapanga nsichi zamtengo wa mkesha ndi kuzikuta ndi golide kuti azinyamulira tebulolo. 16Ndipo anapanga ziwiya za pa tebulolo zagolide wabwino, mbale ndi zipande, mitsuko ndi mabeseni zogwiritsa ntchito popereka nsembe za chakumwa.

Mapangidwe a Choyikapo Nyale

17Iwo anapanga choyikapo nyale chagolide wabwino kwambiri. Tsinde lake ndi mphanda zake zinasulidwa ndi nyundo. Zikho zake zokhala ndi mphukira ndi maluwa ake zinapangidwa kumodzi. 18Mʼmbali mwake munali mphanda zisanu ndi imodzi, zitatu mbali iliyonse. 19Zikho zitatu zokhala ngati za maluwa amtowo, mphukira ndi duwa zinali pa mphanda yoyamba. Pa mphanda yachiwiri panalinso zikho zitatu zokhala ngati za maluwa amtowo, mphukira ndi duwa. Ndipo mphanda zonse zisanu ndi imodzi zinali chimodzimodzi ndipo zinatuluka mʼchoyikapo nyalecho. 20Pa choyikapo nyalecho panali zikho zinayi zokhala ngati maluwa amtowo, mphukira ndi maluwa ake. 21Mphukira yoyamba inali mʼmunsi mwa nthambi ziwiri zoyamba za pa choyikapo nyale. Mphukira yachiwiri inali mʼmunsi mwa nthambi ziwiri zinazo. Mphukira yachitatu inali mʼmunsi mwa nthambi zina ziwirinso. Zonse pamodzi zinali nthambi zisanu ndi imodzi 22Mphukira ndi nthambi zonse zinasulidwa kumodzi ndi choyikapo nyalecho ndi golide wabwino kwambiri.

23Iwo anapanga nyale zisanu ndi ziwiri, mbaniro ndi zowolera phulusa, zonse zinali zagolide wabwino kwambiri. 24Iwo anapanga choyikapo nyale ndi zipangizo zake zonse zagolide wabwino kwambiri wolemera makilogalamu 34.

Guwa Lofukizirapo Lubani

25Iwo anapanga guwa lamatabwa amtengo wa mkesha lofukizirapo lubani. Linali lofanana mbali zonse, mulitali masentimita 46, mulifupi masentimita 46, ndipo msinkhu masentimita 91, ndipo nyanga zake zinapangidwa kumodzi ndi guwalo. 26Iwo anakuta guwa lonse ndi golide wabwino kwambiri, pamwamba pake, mbali zonse ndi nyanga zake, ndipo anapanga mkombero wagolide kuzungulira guwalo. 27Anapanga mphete ziwiri pansi pa mkomberowo ndi kulumikiza ku mbali zonse ziwiri kuti apisemo nsichi zonyamulira. 28Anapanga mizati yamtengo wa mkesha ndipo anayikuta ndi golide.

29Iwo anapanganso mafuta opatulika odzozera ndi zofukiza za fungo lokoma kwambiri. Iyi inali ntchito ya mʼmisiri waluso lopanga zonunkhiritsa.

Korean Living Bible

출애굽기 37:1-29

법궤

1브사렐은 아카시아나무로 가로 113센티미터, 세로 68센티미터, 높이 68센티미터의 궤를 만들었다.

2그는 순금으로 그 궤의 안팎을 싸고 윗 언저리에 금테를 둘렀으며

3또 금고리 네 개를 만들어 양쪽에 각각 두 개씩 네 발에 달았다.

4그는 또 아카시아나무로 운반채를 만들어 금으로 싸고

5그 운반채를 궤 양쪽 고리에 꿰어 궤를 운반할 수 있도록 하였다.

6그리고 순금으로 그 궤의 뚜껑인 37:6 또는 ‘시은좌’속죄소를 만들었는데 그 크기는 길이 113센티미터, 너비 68센티미터였다.

7그런 다음 그는 금을 두들겨 두 그룹 천사를 만들어

8그 뚜껑과 한 덩어리가 되게 뚜껑 양쪽 끝에 각각 하나씩 세웠으며

9그 그룹 천사들은 날개를 위로 펴서 속죄소를 덮고 그 얼굴은 속죄소를 향하여 서로 마주 보게 하였다.

차림상

10그는 또 아카시아나무로 길이 90센티미터, 너비 45센티미터, 높이 68센티미터의 상을 만들었다.

11그는 그 상을 순금으로 싸고 가장자리에 금테를 둘렀으며

12상 둘레에 손바닥 넓이만한 턱을 만들고 그 턱 주위에 금테를 둘렀다.

13그리고 금고리 네 개를 만들어 상 다리가 붙은 네 모퉁이

14턱 곁에 달아 운반채를 꿸 수 있게 하였다.

15그는 또 아카시아나무로 상의 운반채를 만들어 금으로 쌌으며

16상의 기구인 대접과 국자와 잔과 제사 술을 따르는 주전자를 순금으로 만들었다.

순금 등대

17또 그는 순금을 두들겨 등대를 만들었는데 밑받침과 줄기와 등잔과 꽃 모양의 장식을 모두 하나로 연이어 만들었다.

18-19그 등대 줄기에서는 양쪽으로 가지가 세 개씩 뻗어 나오게 하고 각 가지마다 세 개의 살구꽃 모양을 장식하였다.

20-21그리고 등대 줄기에는 네 개의 살구꽃 모양을 장식하였다. 두 개는 윗가지와 아랫가지 사이에 각각 하나씩 만들고 하나는 제일 윗가지 바로 위에, 하나는 제일 아랫가지 바로 밑에 만들었다.

22이런 꽃 모양의 장식과 가지와 줄기는 모두 순금을 두들겨 하나로 연이어 만들었으며

23일곱 개의 등잔과 심지 자르는 가위와 불똥 그릇도 순금으로 만들었다.

24이와 같이 그는 37:24 히 ‘정금 한 달란트’순금 34킬로그램으로 등대와 그 모든 기구를 만들었다.

향단

25그는 또 아카시아나무로 분향할 단을 만들었다. 그것은 가로 세로가 각각 45센티미터로 네모가 반듯하며 높이는 90센티미터였다. 그리고 네 뿔을 단과 한 덩이로 연이어 만들고

26그 단의 윗면과 전후 좌우 면과 그 뿔을 순금으로 쌌으며 윗 가장자리에 금테를 둘렀다.

27그런 다음 금테 아래 양쪽에 운반채를 꿸 금고리 두 개씩을 만들어 달고

28아카시아나무로 그 운반채를 만들어 금으로 쌌다.

29그는 또 거룩한 의식에 쓸 기름을 만들고 전문적인 향 제조법으로 향기로운 순수한 향을 만들었다.