Eksodo 38 – CCL & KLB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Eksodo 38:1-31

Guwa Lansembe Yopsereza

1Anapanga guwa lansembe zopsereza lamatabwa amtengo wa mkesha. Linali lofanana mbali zonse. Msinkhu wake masentimita 137, mulitali mwake masentimita 229, mulifupi masentimita 229. 2Anapanga nyanga imodziimodzi pa ngodya zake zinayizo, kotero kuti nyangazo ndi guwalo zinali chinthu chimodzi, ndipo anakuta guwalo ndi mkuwa. 3Anapanganso ziwiya zamkuwa izi zogwirira ntchito pa guwalo: miphika, mafosholo, mabeseni owazira magazi, ngowe zokowera nyama ndi zosonkhezera moto. 4Anapanga sefa yachitsulo chamkuwa ya guwa lansembelo kuti ikhale mmunsi mwa khoma la guwa lansembelo, kuchokera pansi mpaka pakati pa khoma la guwalo. 5Anapanga mphete zamkuwa zinayi ndipo anazilumikiza ku ngodya zinayi za sefa ija kuti zigwire nsichi zonyamulira. 6Anapanga nsichi zamtengo wa mkesha ndipo anazikuta ndi mkuwa. 7Iwo analowetsa nsichizo mʼmphetemo mbali zonse ziwiri za guwalo kuti azinyamulira. Guwalo linali lamatabwa ndi logoba mʼkati mwake.

Beseni Losambira

8Anapanga beseni lamkuwa lokhala ndi miyendo yamkuwanso kuchokera ku magalasi oyangʼanira nkhope a amayi amene ankatumikira pa chipata cha tenti ya msonkhano.

Bwalo la Chihema

9Kenaka anapanga bwalo la chihema. Mbali yakummwera inali yotalika mamita 46 ndipo kunali nsalu yotchinga yofewa yosalala yolukidwa bwino. 10Anapanganso mizati makumi awiri, matsinde makumi awiri amkuwa ndi ngowe zasiliva ndi zingwe za mizatiyo. 11Mbali yakumpoto inalinso yotalika mamita 46 ndipo inali ndi mizati makumi awiri, matsinde amkuwa makumi awiri, ngowe zasiliva ndi zingwe za mizatiyo.

12Mbali yakumadzulo inali yotalika mamita 23 ndipo inali ndi nsalu yotchinga, mizati khumi ndi matsinde khumi. Inalinso ndi ngowe zasiliva ndi zingwe za mizatiyo. 13Mbali yakummawa, kotulukira dzuwa, inalinso yotalika mamita 23. 14Mbali imodzi yachipata kunali nsalu yotchinga yotalika mamita asanu ndi awiri, mizati itatu ndi matsinde atatu, 15polowera mʼbwalo panali nsalu yotchinga ya mamita asanu ndi awiri pamodzi ndi mizati itatu ndi matsinde atatu. 16Katani yonse yotchinga kuzungulira chihema inali yofewa, yosalala ndi yolukidwa bwino. 17Matsinde amizati anali amkuwa. Ngowe ndi zingwe za mizati zinali zasiliva, ndipo pamwamba pa mizatiyo anakutapo siliva. Choncho mizati yonse ya bwalolo inalumikizidwa ndi zingwe zasiliva.

18Nsalu yotchinga ya pa chipata inali yamtundu wa mtambo, yapepo ndi yofiira, yofewa yosalala ndi yopangidwa ndi anthu aluso. Nsaluyo inali yotalika mamita asanu ndi anayi, molingana ndi nsalu zotchinga bwalo. Msinkhu wake unali masentimita 229, 19pamodzi ndi mizati yake inayi ndi matsinde amkuwa anayi. Ngowe ndi zingwe zake zinali za siliva, ndipo pamwamba pake pa mzati anakutapo ndi siliva. 20Zikhomo za chihema ndi zina zonse zozungulira chihemacho zinali zamkuwa.

Zipangizo Zachitsulo za ku Malo Opatulika

21Chiwerengero cha zipangizo zimene anagwiritsa ntchito popanga chihema, chihema chaumboni, zimene Mose analamulira Alevi kuti alembe motsogozedwa ndi Itamara mwana wa Aaroni, wansembe, chinali ichi: 22Bezaleli mwana wa Uri, mwana wa Huzi wa fuko la Yuda anapanga chilichonse Yehova analamulira Mose, 23pamodzi ndi Oholiabu mwana wa Ahisamaki, wa fuko la Dani, wa luso la zopangapanga ndi kulemba mapulani, ndi wopanga nsalu zolukidwa bwino za mtundu wa mtambo, yapepo ndi zofiira, zofewa ndi zosalala. 24Golide yense wochokera ku nsembe yoweyula amene anagwiritsa ntchito pa ntchito yonse yopanga malo wopatulika anali wolemera makilogalamu 1,000 potsata miyeso ya kumalo wopatulika.

25Siliva wochokera ku gulu lonse la anthu anali wolemerera makilogalamu 3,430, potsata miyeso ya ku malo wopatulika. 26Munthu aliyense amapereka beka imodzi, kufanana ngati makilogalamu 6, potsata muyeso wa ku malo wopatulika. Kuchokera kwa aliyense amene anawerengedwa kuyambira zaka 20 kapena kuposerapo, amuna onse analipo 603,550. 27Anagwiritsa ntchito siliva wolemera makilogalamu 3,400 kupanga matsinde 100 a ku malo wopatulika ndi makatani, ndipo makilogalamu 34 kupanga tsinde limodzi. 28Makilogalamu otsalawo anagwiritsa ntchito popanga ngowe zamzati kukutira pamwamba pa mizati ndiponso kupanga zingwe zake.

29Mkuwa ochokera ku nsembe yoweyula unali makilogalamu 2,425. 30Iwo anawugwiritsa ntchito popanga matsinde a pa chipata cha tenti ya msonkhano, guwa la mkuwa pamodzi ndi sefa yake ndiponso ziwiya zonse, 31matsinde ozungulira bwalo ndiponso a pa chipata pake, ndi zikhomo zonse za tentiyo ndi matsinde a malo wozungulirapo.

Korean Living Bible

출애굽기 38:1-31

번제단

1그는 아카시아나무로 제물을 태워 바칠 제단을 만들었다. 그것은 가로 세로가 각각 2.3미터로 네모가 반듯하고 높이는 1.4미터였다.

2그리고 제단 네 모퉁이에 뿔이 하나씩 나오도록 만들고 그 제단을 놋으로 쌌다.

3그런 다음 그는 그 단의 모든 기구, 곧 재를 담는 통과 부삽과 피를 담는 그릇과 고기 갈고리와 불 옮기는 그릇을 다 놋으로 만들었으며

4또 단에 쓸 놋그물을 만들어 단의 아래 언저리 밑에 놓아 그것이 단의 절반 높이로 올라오게 하고

5그 놋그물 네 모퉁이에 운반채를 꿸 고리 네 개를 만들었다.

6그리고 운반채는 아카시아나무로 만들어 놋으로 싸고

7그것을 단의 양쪽 고리에 꿰어 단을 운반할 수 있게 하였으며 그 단은 널빤지로 속이 비게 만들었다.

8그는 또 회막 입구에서 섬기는 여자들이 바친 놋거울로 넓적한 물통과 그 받침을 만들었다.

성막 뜰

9다음으로 그는 성막 뜰을 위해 고운 모시 포장을 만들었는데 뜰 남쪽을 위해서 포장의 길이를 45미터로 하고

1020개의 기둥을 만들었다. 그리고 그 기둥 받침은 놋으로 만들고 기둥의 갈고리와 가로대는 은으로 만들었다.

11또 맞은편인 북쪽을 위해서도 이와 똑같이 만들고

12서쪽을 위해서는 포장 길이를 22.5미터로 하였으며 10개의 기둥과 받침을 만들고 기둥의 갈고리와 가로대를 은으로 만들었다.

13그리고 출입구를 낼 뜰 동쪽 길이도 22.5미터가 되게 하였다.

14-15출입구 양쪽을 위해 각각 3개의 기둥 과 받침을 만들고 거기에 칠 6.8미터 길이의 포장을 만들었다.

16이와 같이 뜰 사면의 포장은 모두 고운 모시로 만들었으며

17기둥 받침은 놋으로 만들고 기둥의 갈고리와 가로대와 기둥머리 덮개는 은으로 만들었으며 뜰의 모든 기둥에는 은가로대를 꿸 수 있게 하였다.

18그리고 청색, 자색, 홍색 실과 가늘게 꼰 베실로 수놓아 짜서 뜰의 출입구 막을 만들었으며 그 길이는 9미터, 높이는 뜰의 포장과 마찬가지로 2.3미터로 하였다.

19또 출입구 막을 달 수 있도록 4개의 기둥과 기둥 받침과 기둥머리 덮개, 그리고 가로대와 갈고리를 만들었는데 그 기둥 받침은 놋이며 갈고리와 기둥머리 덮개와 가로대는 은이었다.

20그리고 성막 말뚝과 뜰 사면의 포장 말뚝은 다 놋으로 만들었다.

성막을 만드는 데 쓰인 재료

21법궤를 안치할 성막을 세우는 데 쓴 재료의 품목은 모세의 명령을 받아 제사장 아론의 아들인 이다말이 계산하였으며

22유다 지파 사람 훌의 손자이며 우리의 아들인 브사렐은 여호와께서 모세에게 명령하신 모든 것을 만들었다. 그리고

23그의 조력자인 단 지파 사람 아히사막의 아들 오홀리압은 재능이 있어서 조각하고 정교한 일을 하며 청색, 자색, 홍색 실과 가늘게 꼰 베실로 수놓는 일을 하였다.

24성소를 짓고 그 모든 기구를 만드는 데 사용된 금은 38:24 히 ‘성소의 세겔대로 29달란트와 730세겔’약 톤이었다.

25그리고 인구 조사를 받은 백성들이 바친 은은 38:25 히 ‘성소의 세겔대로 100달란트와 1,775세겔’약 3,420킬로그램이었다.

2620세 이상 인구 조사를 받은 사람이 전부 603,550명이므로 인당 38:26 히 ‘성소의 세겔대로 은 한 베가 곧 반 세겔’약 6그램씩 낸 셈이었다.

27그 중에서 38:27 히 ‘은 100달란트’은 3,400킬로그램으로 성막 벽이 될 기둥과 지성소 앞의 휘장 기둥에 받칠 밑받침 100개를 만들었으며 그 밑받침 하나에는 은 34킬로그램씩 들었다.

28그리고 나머지 은 20킬로그램으로 기둥 갈고리와 기둥머리와 기둥 가로대를 만들었다.

29그 밖에 백성들이 바친 놋은 38:29 히 ‘70달란트와 2,400세겔’약 2,400킬로그램인데

30이것으로 성막 출입구 기둥 받침, 놋제단과 놋그물과 그 모든 기구,

31뜰 사면의 기둥 받침과 뜰 출입구 기둥 받침, 그리고 성막의 말뚝과 뜰 사면의 모든 말뚝을 만들었다.