Eksodo 2 – CCL & NIRV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Eksodo 2:1-25

Kubadwa kwa Mose

1Ndipo munthu wina wa fuko la Levi anakwatira mkazi wa fuko lomwelo. 2Mkaziyo anatenga pathupi ndipo anabereka mwana wamwamuna. Ataona kuti mwanayo anali wokongola, anamubisa kwa miyezi itatu. 3Koma mwanayo atafika pa msinkhu woti sakanathanso kubisidwa, amayi ake anatenga kadengu kopangidwa ndi bango nakamata phula. Kenaka anayika mwanayo mʼmenemo ndi kukamuyika pa mabango mu mtsinje wa Nailo. 4Mlongo wake wa mwanayo anayima pataliko kuti aone chimene chidzamuchitikira mwanayo.

5Mwana wamkazi wa Farao anapita ku mtsinje wa Nailo kukasamba ndipo adzakazi ake ankayenda mʼmbali mwa mtsinjewo. Tsono mwana wa Farao uja anaona kadenguko pakati pa mabango ndipo anatuma mdzakazi wake kuti akakatenge. 6Iye atavundukula anaona mwana wamwamuna akungolira. Iye anamva naye chisoni mwana uja, nati, “Ameneyu ndi mmodzi mwa ana a Chihebri.”

7Kenaka mlongo wake wa mwanayo anafunsa mwana wa Farao kuti, “Ndingapite kukakupezerani mmodzi mwa amayi a Chihebri kuti azikakulererani mwanayu?”

8Iye anayankha kuti, “Inde, pita.” Ndipo mtsikanayo anapita nakayitana amayi a mwanayo. 9Mwana wa Farao anati, “Tengani mwanayu mukandilerere, ndidzakulipirani.” Mayiyo anatenga mwanayo kukamulera. 10Mwanayo atakula anakamupereka kwa mwana wa Farao ndipo anakhala mwana wake. Iye anamutcha dzina lake Mose, popeza anati, “Ndinamuvuwula mʼmadzi.”

Mose Athawira ku Midiyani

11Tsiku lina, Mose atakula, anapita kumene kunali anthu a mtundu wake ndipo anawaona akugwira ntchito yowawa. Iye anaona Mwigupto akumenya Mhebri, mmodzi mwa anthu a mtundu wake. 12Atayangʼana uku ndi uku, naona kuti panalibe wina aliyense, Mose anamupha Mwiguptoyo ndipo anamukwirira mu mchenga. 13Mmawa mwake Mose anapita ndipo anaona anthu awiri a Chihebri akumenyana. Iye anafunsa amene anali wolakwa kuti, “Chifukwa chiyani ukumenya Mhebri mnzako?”

14Munthu uja anati, “Kodi ndani anakuyika kuti ukhale wotilamulira ndi wotiweruza? Kodi ukufuna kundipha monga momwe unaphera Mwigupto uja?” Mose anachita mantha ndipo anati mu mtima mwake, “Chimene ndinachita chija chadziwika.”

15Farao atamva zimenezi anafuna kuti aphe Mose, koma Mose anathawa ndipo anapita kukakhala ku Midiyani. Ali kumeneko, tsiku lina anakhala pansi pafupi ndi chitsime. 16Wansembe wa ku Midiyaniko anali ndi ana aakazi asanu ndi awiri. Iwowa anabwera kudzatunga madzi ndi kudzaza mu zomwera kuti amwetse nkhosa za abambo awo. 17Koma kunabwera abusa ena amene anathamangitsa atsikana aja. Ndiye Mose anayimirira nawathandiza atsikana aja ndi kumwetsa nkhosa zawo.

18Atsikana aja atabwerera kwa abambo awo Reueli, iye anawafunsa kuti, “Chifukwa chiyani lero mwabwera msanga?”

19Atsikanawo anayankha kuti, “Mwigupto wina ndiye watilanditsa kwa abusa. Ndiponso anatitungira madzi ndi kumwetsa ziweto zathu.”

20Tsono Reueli anafunsa ana ake kuti, “Ndiye ali kuti munthuyo? Chifukwa chiyani mwamusiya? Kamuyitaneni kuti adzadye.”

21Mose anavomera kukhala ndi Reueli, ndipo anamupatsa Zipora kuti akhale mkazi wake. 22Zipora anabereka mwana wa mwamuna amene Mose anamutcha Geresomu, popeza anati, “Ndakhala mlendo mʼdziko la eni.”

23Nthawi yonseyo nʼkuti ana a Israeli akulira chifukwa cha ukapolo wawo uja. Iwo anafuwula kupempha thandizo, ndipo kulira kwawoko kunafika kwa Mulungu. 24Mulungu anamva kubuwula kwawo ndipo anakumbukira pangano lake ndi Abrahamu, Isake ndi Yakobo. 25Mulungu ataona Aisraeli aja ndi masautso awo, Iye anawamvera chifundo.

New International Reader’s Version

Exodus 2:1-25

Moses Is Born

1A man and a woman from the tribe of Levi got married. 2She became pregnant and had a son by her husband. She saw that her baby was a fine child. And she hid him for three months. 3After that, she couldn’t hide him any longer. So she got a basket made out of the stems of tall grass. She coated the basket with tar. She placed the child in the basket. Then she put it in the tall grass that grew along the bank of the Nile River. 4The child’s sister wasn’t very far away. She wanted to see what would happen to him.

5Pharaoh’s daughter went down to the Nile River to take a bath. Her attendants were walking along the river bank. She saw the basket in the tall grass. So she sent her female slave to get it. 6When she opened it, Pharaoh’s daughter saw the baby. He was crying. She felt sorry for him. “This is one of the Hebrew babies,” she said.

7Then his sister spoke to Pharaoh’s daughter. She asked, “Do you want me to go and get one of the Hebrew women? She could breast-feed the baby for you.”

8“Yes. Go,” she answered. So the girl went and got the baby’s mother. 9Pharaoh’s daughter said to her, “Take this baby and feed him for me. I’ll pay you.” So the woman took the baby and fed him. 10When the child grew older, she took him to Pharaoh’s daughter. And he became her son. She named him Moses. She said, “I pulled him out of the water.”

Moses Escapes to Midian

11Moses grew up. One day, he went out to where his own people were. He watched them while they were hard at work. He saw an Egyptian hitting a Hebrew man. The man was one of Moses’ own people. 12Moses looked around and didn’t see anyone. So he killed the Egyptian. Then he hid his body in the sand. 13The next day Moses went out again. He saw two Hebrew men fighting. He asked the one who had started the fight a question. He said, “Why are you hitting another Hebrew man?”

14The man said, “Who made you ruler and judge over us? Are you thinking about killing me as you killed the Egyptian?” Then Moses became afraid. He thought, “People must have heard about what I did.”

15When Pharaoh heard about what had happened, he tried to kill Moses. But Moses escaped from Pharaoh and went to live in Midian. There he sat down by a well. 16A priest of Midian had seven daughters. They came to fill the stone tubs with water. They wanted to give water to their father’s flock. 17Some shepherds came along and chased the girls away. But Moses got up and helped them. Then he gave water to their flock.

18The girls returned to their father Reuel. He asked them, “Why have you returned so early today?”

19They answered, “An Egyptian saved us from the shepherds. He even got water for us and gave it to the flock.”

20“Where is he?” Reuel asked his daughters. “Why did you leave him? Invite him to have something to eat.”

21Moses agreed to stay with the man. And the man gave his daughter Zipporah to Moses to be his wife. 22Zipporah had a son by him. Moses named him Gershom. That’s because Moses said, “I’m an outsider in a strange land.”

23After a long time, the king of Egypt died. The people of Israel groaned because they were slaves. They also cried out to God. Their cry for help went up to him. 24God heard their groans. He remembered his covenant with Abraham, Isaac and Jacob. 25So God looked on the Israelites with concern for them.