Deuteronomo 9 – CCL & CARSA

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Deuteronomo 9:1-29

Osati Chifukwa cha Kulungama kwa Israeli

1Mvera Israeli. Watsala pangʼono kuwoloka Yorodani ndi kukathamangitsa mitundu ikuluikulu ndi yamphamvu kuposa iweyo, imene mizinda yake ndi ikuluikulu yokhala ndi makoma ofika mpaka kumwamba. 2Anthuwo ndi ataliatali, Aanaki! Ukudziwa za iwo ndipo unamvapo zikunenedwa kuti, “Ndani amene angalimbane ndi Aanaki?” 3Koma khulupirira lero kuti Yehova Mulungu wako amene ali patsogolo pako ali ngati moto wonyeketsa. Adzawononga iwowo ndipo adzawagonjetsa iweyo ukuona. Pamenepo udzawathamangitsa ndi kuwakantha mwamsanga, monga momwe Yehova wakulonjezera.

4Yehova Mulungu wako akadzawapirikitsa pamaso pako, usadzanene mu mtima mwako kuti, “Yehova wandibweretsa kuno kudzalanda dziko lino chifukwa cha kulungama kwanga.” Ayi, koma ndi chifukwa cha kuyipa kwa anthu amene Yehova ati awapirikitse pamaso pako. 5Sukalowa ndi kutenga dziko lawolo chifukwa cha kulungama kwako kapena kukhulupirika kwako koma chifukwa cha kuyipa kwa anthuwo. Yehova Mulungu wako awapirikitsa pamaso pako kuti akwaniritse zimene analumbira kwa makolo ako Abrahamu, Isake ndi Yakobo. 6Tsono zindikira kuti si chifukwa cha kulungama kwako kuti Yehova Mulungu wako akukupatsa dziko labwinoli kuti ulitenge popeza ndiwe wokanika.

Mwana Wangʼombe Wagolide

7Kumbukirani izi ndipo musayiwale mmene munaputira mkwiyo wa Yehova Mulungu mʼchipululu muja. Kuyambira tsiku limene munatuluka mu Igupto mpaka pamene munafika kuno, mwakhala owukira Yehova. 8Ku Horebu munaputa mkwiyo wa Yehova, kotero kuti anakwiya kwambiri nafuna kukuwonongani. 9Nditakwera ku phiri kuti ndikalandire miyala iwiri ya malamulo, ya pangano limene Yehova anachita ndi inu, ndinakhala ku phiriko kwa masiku makumi anayi usiku ndi usana, sindinadye buledi kapena kumwa madzi. 10Yehova anandipatsa miyala iwiri yolembedwa ndi chala chake. Pa miyalapo panali malamulo onse amene Yehova analengeza kwa inu pa phiri kuchokera mʼmoto pa tsiku la msonkhano.

11Pakutha pa masiku makumi anayi usiku ndi usana, Yehova anandipatsa miyala iwiri, miyala ya pangano. 12Tsono Yehova anandiwuza, “Tsikako kuno msanga, chifukwa anthu ako aja unawatulutsa ku Iguptowa adziyipitsa. Iwo apatukapo mofulumira pa zimene ndinawalamulira ndipo adzipangira fano lachitsulo.”

13Ndipo Yehova anati kwa ine, “Anthu awa ndawaona ndipo ndi anthu okanikadi! 14Ndilekeni ndiwawononge ndi kufafaniza mayina awo pa dziko lapansi. Ndipo ndidzakuyesa iwe mtundu wa anthu wamphamvu ndi wochuluka kuposa iwo.”

15Choncho ndinatembenuka ndi kutsika phiri moto ukanayakabe. Ndipo miyala iwiri ya pangano inali mʼmanja mwanga. 16Ine poyangʼana ndinaona kuti inu munachimwira Yehova Mulungu wanu. Munadzipangira fano lowumbidwa ngati mwana wangʼombe. Inuyo munapatuka msanga kuchoka pa njira imene Yehova anakulamulirani. 17Motero ine ndinaponya pansi miyala imene inali mʼmanja mwanga, ndi kuyiphwanya inu mukuona.

18Tsono nthawi yomweyo ndinagwa chafufumimba pamaso pa Yehova kwa masiku makumi anayi usiku ndi usana. Sindinadye buledi kapena kumwa madzi chifukwa cha machimo onse amene munawachita, kuchita zoyipa pamaso pa Yehova ndi kumukwiyitsa kwambiri. 19Ine ndinachita mantha ndi mkwiyo ndi ukali wa Yehova chifukwa anakwiya nanu kokwanira kukuwonongani. Koma Yehova anandimveranso. 20Ndipo Yehova anakwiya ndi Aaroni ndipo akanamuwononga, koma ine ndinamupemphereranso Aaroniyo. 21Ndiponso ndinatenga chinthu chanu choyipacho, mwana wangʼombe amene munapangayo, ndi kumuwotcha pa moto. Kenaka ndinamuphwanya ndi kumuperapera ndikukhala ngati fumbi ndipo ndinawaza fumbilo mu mtsinje umene unkayenda kuchokera mʼphiri.

22Inu munamukwiyitsanso Yehova ku Tabera, ku Masa ndi ku Kibiroti Hatava.

23Ndipo Yehova atakutulutsani ku Kadesi Barinea anati, “Pitani mukatenge dziko limene ndakupatsani.” Koma munawukira ulamuliro wa Yehova Mulungu wanu. Inu simunamukhulupirire kapena kumumvera. 24Kuyambira pamene ndinakudziwani, mwakhala owukira Yehova.

25Ine ndinagwa chafufumimba pamaso pa Yehova kwa masiku makumi anayi usana ndi usiku chifukwa Yehova ananena kuti akuwonongani. 26Ndinapemphera kwa Ambuye ndi kuti, “Haa Yehova Wamkulukulu, musawawononge anthu anu, chuma chanuchanu chimene munachipulumutsa ndi mphamvu yanu yayikulu ku Igupto ndi dzanja lanu la mphamvu. 27Kumbukirani atumiki anu Abrahamu, Isake ndi Yakobo. Musatengere kupulupudza, kuyipa ndi kuchimwa kwawo anthuwa. 28Kupanda kutero, ndiye kuti anthu a ku dziko lija munatitulutsaku adzati, ‘Yehova anawatulutsa kuti akawaphe mʼchipululu popeza sanathe kukawalowetsa mʼdziko limene anawalonjeza ndipo anadana nawo.’ 29Koma iwowa ndi anthu anu, chuma chanu chimene munachitulutsa ndi mphamvu yanu yayikulu ndi mkono wanu wotambasuka.”

Священное Писание (Восточный перевод), версия с «Аллахом»

Второзаконие 9:1-29

Земля как незаслуженный дар

1Слушай, Исраил, ты переходишь через Иордан, чтобы войти в землю и выселить народы, которые больше и сильнее тебя, с большими городами, чьи стены до неба. 2Люди те сильные и высокие – они анакиты! Ты знаешь о них и слышал, как говорят: «Кто может противостоять анакитам?» 3Но будь уверен, Вечный, твой Бог, пойдёт перед тобой, подобно пожирающему огню. Он истребит их; Он покорит их тебе. А ты прогонишь и уничтожишь их, как обещал тебе Вечный.

4После того как Вечный, твой Бог, прогонит их от тебя, не говори себе: «За мою праведность Вечный привёл меня сюда, чтобы я завладел этой землёй». Нет, из-за нечестия этих народов Вечный прогонит их от тебя. 5Не за праведность и чистоту своего сердца ты овладеешь их землёй, а из-за нечестия этих народов Вечный, твой Бог, прогонит их от тебя, чтобы исполнить то, о чём Он клялся твоим предкам: Ибрахиму, Исхаку и Якубу. 6Итак, пойми, что не за твою праведность Вечный, твой Бог, отдаёт тебе во владение эту благодатную землю, ведь ты – упрямый народ.

Золотой телец

(Исх. 32:1-35)

7Помните и никогда не забывайте, как в пустыне вы вызывали гнев Вечного, вашего Бога. Со дня, когда вы покинули Египет, и до вашего прихода сюда вы были мятежниками против Вечного. 8У горы Синай9:8 Букв.: «У Хорива». Хорив – другое название горы Синай. вы так разгневали Вечного, что Он готов был истребить вас. 9Когда я поднялся на гору, чтобы получить каменные плитки, плитки священного соглашения, которое Вечный заключил с вами, я провёл на горе сорок дней и сорок ночей; я не ел хлеба и не пил воды. 10Вечный дал мне две каменные плитки, написанные рукой Аллаха. На них были все повеления, которые Вечный объявил вам из пламени на горе, в день собрания.

11Через сорок дней и сорок ночей Вечный дал мне две каменные плитки, плитки священного соглашения. 12Вечный сказал мне: «Немедленно спускайся, потому что твой народ, который ты вывел из Египта, развратился. Они быстро отвернулись от того, что Я повелел им, и сделали себе литого идола».

13И Вечный сказал мне: «Я видел этот народ, и народ этот на самом деле упрямый! 14Оставь Меня, Я истреблю их и сотру память о них из-под небес. А от тебя Я произведу народ сильнее и многочисленнее этого».

15Я повернулся и спустился с горы, пылающей огнём. Две каменные плитки священного соглашения были у меня в руках. 16Взглянув, я увидел, что вы согрешили против Вечного, вашего Бога; вы сделали себе литого идола в виде тельца; быстро же вы свернули с пути, который указал вам Вечный. 17Я взял плитки, бросил их, и они разбились на куски у вас на глазах.

18Затем я снова простёрся перед Вечным и лежал так сорок дней и сорок ночей. Я не ел хлеба и не пил воды из-за греха, который вы совершили, сотворив зло в глазах Вечного и вызвав Его гнев. 19Я боялся гнева и ярости Вечного, потому что Он так гневался на вас, что готов был вас истребить. Но Вечный внял мне и на этот раз. 20И на Харуна Вечный гневался так, что готов был истребить его, но я молился и за Харуна. 21А греховного идола, тельца, которого вы сделали, я взял и расплавил в огне. Я разбил его, стёр в порошок, мелкий, как пыль, и бросил в реку, которая текла с горы.

22А ещё вы разгневали Вечного в Тавере, в Массе и в Киврот-Хатааве9:22 Тавера – см. Чис. 11:1-3; Масса – см. Исх. 17:1-7; Киврот-Таава – см. Чис. 11:4-34..

23И когда Вечный посылал вас из Кадеш-Барни, Он сказал: «Поднимитесь и захватите землю, которую Я отдал вам». Но вы взбунтовались против повеления Вечного, вашего Бога. Вы не доверились Ему и не послушались Его9:23 См. Чис. 13.. 24Вы были мятежниками против Вечного с тех самых пор, как я узнал вас.

25Сорок дней и сорок ночей я лежал, простёршись перед Вечным, потому что Вечный сказал, что истребит вас. 26Я молился Вечному и говорил: «Владыка Вечный, не губи Свой народ, Своё собственное наследие, которое Ты вызволил Своей великой властью и вывел из Египта могучей рукой. 27Вспомни Своих рабов: Ибрахима, Исхака и Якуба. Не смотри на упрямство этого народа, на его нечестие и грех. 28Иначе в стране, из которой Ты вывел нас, будут говорить: „Вечный вывел их, чтобы предать смерти в пустыне, потому что не смог привести их в землю, которую обещал им, и из-за ненависти к ним“. 29Но ведь они – Твоё наследие, Твой народ, который Ты вывел Своей великой силой и простёртой рукой».