Yoswa 1 – CCL & CARSA

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yoswa 1:1-18

Yehova Asankha Yoswa Kukhala Mtsogoleri

1Atamwalira Mose mtumiki wa Mulungu, Yehova anati kwa Yoswa mwana wa Nuni mthandizi wa Mose: 2“Mose mtumiki wanga wamwalira. Ndipo iwe ndi anthu onsewa, tsopano konzekani kuwoloka mtsinje wa Yorodani kupita ku dziko limene ndiwapatse Aisraeli onse. 3Paliponse pamene phazi lanu liponde, ndikupatsani monga momwe ndinalonjezera Mose. 4Dziko lanu lidzayambira ku chipululu kummwera mpaka ku mapiri a Lebanoni kumpoto, kuchokeranso ku mtsinje waukulu wa Yufurate kummawa, mpaka dziko lonse la Ahiti, kukafika ku Nyanja Yayikulu ya kumadzulo. 5Palibe munthu amene adzatha kukugonjetsa masiku onse a moyo wako. Monga Ine ndinakhalira ndi Mose, chomwechonso ndidzakhala nawe. Sindidzakusiya kapena kukataya.

6“Ukhale wamphamvu ndi wolimba mtima, chifukwa iwe udzatsogolera anthu awa kukalandira dziko limene Ine ndinalonjeza makolo awo kuti ndidzawapatsa. 7Ukhale wamphamvu ndi wolimba mtima kwambiri. Usamale ndithu kuti umvere malamulo onse amene mtumiki wanga Mose anakupatsa. Usachoke pa malamulo anga ndipo kulikonse kumene udzapite udzapambana. 8Uziwerenga Buku la Malamuloli, uzilingalira zolembedwa mʼmenemo usana ndi usiku, kuti uchite zonse zimene zinalembedwamo. Ukamatero udzapeza bwino ndi kupambana. 9Paja ndinakulamula kuti ukhale wamphamvu ndi wolimba mtima. Choncho usamachite mantha kapena kutaya mtima popeza Ine Yehova Mulungu wako ndidzakhala nawe kulikonse kumene udzapite.”

10Tsono Yoswa analamula atsogoleri a Aisraeli nawawuza kuti, 11“Pitani ku misasa yonse ndipo muwuze anthu kuti, ‘Konzekani, mangani katundu wanu, popeza pakapita masiku atatu kuyambira lero mudzawoloka Yorodani kupita kukatenga dziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani.’ ”

12Koma Yoswa anawuza fuko la Rubeni, fuko la Gadi ndi theka la fuko la Manase kuti, 13“Kumbukirani zimene Mose mtumiki wa Yehova anakulamulani kuti, ‘Yehova Mulungu wanu akukupatsani mpumulo, ndi dziko ili kuti likhale lanu.’ 14Tsono akazi anu, ana anu ndi ziweto zanu zitsale mʼdziko lino limene Mose anakupatsani kummawa kwa Yorodani. Koma ankhondo anu okha ndiwo awoloke atatenga zida zawo ndi kupita patsogolo pa abale anu kukawathandiza. 15Abale anuwo akadzalandira dziko limene Yehova Mulungu wanu akuwapatsa monga inu mwachitira, inu mudzabwerera kudzakhazikika mʼdziko lanu limene Mose mtumiki wa Yehova anakupatsani tsidya la kummawa kwa Yorodani.”

16Kenaka iwo anayankha Yoswa kuti, “Ife tidzachita chilichonse chimene mwatilamula, ndipo kulikonse kumene mudzatitume tidzapita. 17Monga momwe tinamvera Mose kwathunthu, chomwechonso tidzakumvera iwe. Yehova Mulungu wanu akhale nanu monga momwe anachitira ndi Mose. 18Aliyense wotsutsana ndi inu kapena wosamvera zimene mutilamula adzaphedwa. Inu mukhale wamphamvu ndi wolimba mtima!”

Священное Писание (Восточный перевод), версия с «Аллахом»

Иешуа 1:1-18

Вечный повелевает Иешуа завоевать Ханаан

1После смерти Мусы, раба Вечного1:1 Вечный – на языке оригинала: «Яхве». Под этим именем Всевышний открылся Мусе и народу Исраила (см. Исх. 3:13-15). См. пояснительный словарь., Вечный сказал Иешуа, сыну Нуна, помощнику Мусы:

2– Мой раб Муса умер. Итак, приготовься вместе со всем этим народом переправиться через реку Иордан в землю, которую Я даю им – исраильтянам. 3Я отдам вам всякое место, на которое ступит ваша нога, как Я обещал Мусе. 4Ваша земля будет простираться от пустыни до Ливана, от великой реки Евфрат (включая всю землю хеттов) до Средиземного моря1:4 Букв.: «до Великого моря». на западе. 5Никто не сможет противостоять тебе во все дни твоей жизни. Как Я был с Мусой, так буду и с тобой. Я никогда тебя не оставлю и никогда не покину.

6Будь твёрд и мужествен, потому что ты поведёшь этих людей, чтобы им унаследовать землю, которую Я клялся дать их предкам. 7Будь твёрд и очень мужествен. Тщательно исполняй весь Закон, который дал тебе Мой раб Муса. Не уклоняйся от него ни вправо, ни влево, чтобы тебе иметь успех везде, куда бы ты ни пошёл. 8Пусть слова Таурата, книги Закона, всегда будут у тебя на устах, размышляй над ними день и ночь, чтобы в точности исполнять всё, что написано. Тогда ты будешь иметь успех в своих делах и поступать благоразумно. 9Итак, Я повелеваю тебе: будь твёрд и мужествен. Не бойся и не падай духом, потому что Вечный, твой Бог, будет с тобой, куда бы ты ни пошёл.

10И приказал Иешуа вождям народа:

11– Пройдите по лагерю и скажите народу: «Запаситесь едой, потому что через три дня вы переправитесь здесь через Иордан, чтобы пойти и завладеть землёй, которую Вечный, ваш Бог, даёт вам во владение».

12Но родам Рувима, Гада и половине рода Манассы Иешуа сказал:

13– Помните повеление, которое дал вам Муса, раб Вечного: «Вечный, ваш Бог, дал вам покой и даровал эту землю». 14Ваши жёны, дети и скот могут остаться в земле, которую Муса дал вам к востоку от Иордана, но все ваши воины в полном вооружении должны переправиться впереди ваших братьев. Вы должны помогать вашим братьям, 15пока Вечный не даст им покой, как Он сделал это для вас самих, и пока они тоже не завладеют землёй, которую Вечный, ваш Бог, даёт им. После этого вы сможете вернуться и занять свою землю, которую Муса, раб Вечного, дал вам к востоку от Иордана.

16Они ответили Иешуа:

– Всё, что бы ты ни приказал нам, мы исполним, и куда бы ты ни направил нас, мы пойдём. 17Как мы слушались Мусу, так будем слушаться и тебя. Только пусть Вечный, твой Бог, будет с тобой, как Он был с Мусой. 18Всякий, кто воспротивится твоему приказу и не послушается твоих слов – что бы ты ни приказал, будет предан смерти. Только будь твёрд и мужествен!