Deuteronomo 7 – CCL & NIRV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Deuteronomo 7:1-26

Apirikitsa Mitundu Ina ya Anthu

1Pamene Yehova Mulungu wanu wakufikitsani mʼdziko limene mukukalowa ndi kulilanda ndi kuthamangitsa pamaso panu mitundu ya anthu iyi: Ahiti, Agirigasi, Aamori, Akanaani, Aperezi, Ahivi ndi Ayebusi; yomwe ndi mitundu isanu ndi iwiri yayikulu ndi yamphamvu kuposa inu; 2Yehova Mulungu wanu akadzawapereka mʼmanja mwanu, ndipo inu mukadzawagonjetsa, mudzawawononge kwathunthu. Musadzachite mgwirizano ndi anthuwo ndiponso musadzawachitire chifundo. 3Musadzakwatirane nawo. Musadzapereke ana anu aakazi kwa ana awo aamuna kapena kutenga ana anu aamuna ndi kuwapereka kwa ana awo aakazi. 4Mukadzatero, iwo adzasocheretsa ana anu aamuna kuti asanditsatire ndi kutumikira milungu ina. Motero Yehova adzakukwiyirani ndi kukuwonongani mwachangu. 5Koma mukachite izi: Mukagumule maguwa awo ansembe, mukaswe miyala yawo yachipembedzo, mukadule mitengo yawo ya Asera, ndi kutentha mafano awo pa moto. 6Pakuti inu ndinu anthu opatulika kwa Yehova Mulungu wanu. Yehova Mulungu wanu anakusankhani pakati pa anthu onse pa dziko lapansi kuti mukhale ake, chuma chake cha mtengo wapatali.

7Yehova sanakukondeni chifukwa choti munali ochuluka kuposa ena pakuti inuyo ndiye munali ochepetsetsa mwa anthu onse. 8Koma chifukwa chakuti Yehova anakukondani nasunga lumbiro lake limene analumbira kwa makolo anu. Ndi chifukwa chake anakutulutsani ndi mphamvu yake yopanda malire ndi kukupulumutsani ku dziko la ukapolo, kuchoka mʼmanja mwa Farao mfumu ya ku Igupto. 9Choncho dziwani kuti Yehova Mulungu wanu, ndi Mulungu. Iye ndi Mulungu wokhulupirika, wosunga pangano lake la chikondi chosasinthika ku mibadomibado, kwa iwo amene amamukonda nasunga malamulo ake. 10Koma

iwo amene amamuda adzawabwezera powawononga pamaso pawo;

sadzachedwa kuwabwezera iwo amene amadana naye.

11Choncho muziyesetsa kusunga malamulo, malangizo ndi maphunziro amene ndikukulamulani lero lino kuti muchite.

12Mukamvera malamulo amenewa, ndi kusamala kuwatsata, ndiye kuti Yehova Mulungu wanu adzasunga pangano lake la chikondi chosasinthika ndi inu, monga analumbira kwa makolo anu. 13Iye adzakukondani nakudalitsani ndi kukuchulukitsani. Adzadalitsa chipatso cha mʼmimba mwanu, zokolola za mʼdziko mwanu, tirigu wanu, vinyo wanu ndi mafuta anu, ana angʼombe zanu ndi ana ankhosa zanu mʼdziko limene analumbirira kwa makolo anu kuti akupatseni inu. 14Inu mudzadalitsika kuposa mtundu wina uliwonse wa anthu ndipo palibe mwamuna kapena mkazi aliyense pakati panu amene adzakhale wosabereka. Ziweto zanu nazonso, sipadzapezeka zosabereka. 15Yehova adzakupewetsani ku matenda aliwonse. Sadzakugwetserani matenda owopsa aja munawadziwa ku Igupto, koma adzawagwetsera pa odana nanu. 16Muwononge anthu onse amene Yehova Mulungu wanu awapereka kwa inu. Musawamvere chisoni ndipo musatumikire milungu yawo pakuti umenewo udzakhala msampha kwa inu.

17Mukhoza kunena kuti, “Anthu awa ndi amphamvu kuposa ifeyo. Nanga tingawapirikitse bwanji?” 18Koma musachite nawo mantha, kumbukirani bwino zimene Yehova Mulungu wanu anachita ndi Farao pamodzi ndi Igupto yense. 19Munadzionera nokha ndi maso anu mayesero aakulu, zizindikiro zozizwitsa ndi zodabwitsa, mphamvu yake yopanda malire imene Yehova Mulungu wanu anakutulutsirani. Yehova Mulungu adzachita zimenezo ndi anthu onse amene muwaopa tsopano. 20Kuwonjezera apo, Yehova Mulungu wanu adzatumiza mavu pakati pawo mpaka atamaliza onse amene adzakubisalirani. 21Musaopsedwe nawo pakuti Yehova Mulungu wanu, amene ali pakati panu, ndi Mulungu wamkulu ndi woopsa. 22Yehova Mulungu wanu adzapirikitsa anthu a mitundu yonse pamaso panu, pangʼonopangʼono. Sadzakulolani kuti muwathe nthawi imodzi, kuti nyama zakuthengo zingadzaswane mokuzungulirani. 23Koma Yehova Mulungu wanu adzawapereka kwa inu, adzawasokoneza kufikira atawonongedwa. 24Iye adzapereka mafumu awo mʼdzanja lanu, ndipo adzafafaniza mayina awo pa dziko lapansi. Palibe amene adzalimbana nanu, inu mudzawawononga. 25Muwawotche pa moto mafano a milungu yawo. Musasirire siliva ndi golide amene ali pa mafanoyo. Musamutenge kuti akhale wanu chifukwa mukatero mudzakodwa naye ngati msampha, pakuti Yehova Mulungu wanu amanyansidwa nazo. 26Musabweretse chinthu chonyansa mʼnyumba mwanu kuopa kuwonongedwa ngati chonyasacho. Muziyipidwa ndi kunyansidwa nacho kwambiri pakuti chidzawonongedwanso.

New International Reader’s Version

Deuteronomy 7:1-26

The Lord Will Drive Out Many Nations

1The Lord your God will bring you into the land. You are going to enter it and take it as your own. He’ll drive out many nations to make room for you. He’ll drive out the Hittites, Girgashites, Amorites, Canaanites, Perizzites, Hivites and Jebusites. Those seven nations are larger and stronger than you are. 2The Lord your God will hand them over to you. You will win the battle over them. You must completely destroy them. Don’t make a peace treaty with them. Don’t show them any mercy. 3Don’t marry any of their people. Don’t give your daughters to their sons. And don’t take their daughters for your sons. 4If you do, those people will turn your children away from serving the Lord. Then your children will serve other gods. The Lord will be very angry with you. He will quickly destroy you. 5So here is what you must do to those people. Break down their altars. Smash their sacred stones. Cut down the poles they use to worship the female god named Asherah. Burn the statues of their gods in the fire. 6You are a holy nation. The Lord your God has set you apart for himself. He has chosen you to be his special treasure. He chose you out of all the nations on the face of the earth to be his people.

7The Lord chose you because he loved you very much. He didn’t choose you because you had more people than other nations. In fact, you had the smallest number of all. 8The Lord chose you because he loved you. He wanted to keep the promise he had made to your people of long ago. That’s why he used his mighty hand to bring you out of Egypt. He bought you back from the land where you were slaves. He set you free from the power of Pharaoh, the king of Egypt. 9So I want you to realize that the Lord your God is God. He is the faithful God. He keeps his covenant for all time to come. He keeps it with those who love him and obey his commandments. He shows them his love. 10But he will pay back those who hate him. He’ll destroy them. He’ll quickly pay back those who hate him. 11So be careful to obey the commands, rules and laws I’m giving you today.

12Pay attention to the laws of the Lord your God. Be careful to obey them. Then he will keep his covenant of love with you. That’s what he promised to your people of long ago. 13The Lord will love you and bless you. He’ll cause there to be many of you. He’ll give you many children. He’ll bless the crops of your land. He’ll give you plenty of grain, olive oil and fresh wine. He’ll bless your herds with many calves. He’ll give your flocks many lambs. He’ll do all these things for you in the land of Canaan. It’s the land he promised your people of long ago that he would give you. 14He will bless you more than any other nation. All your men and women will have children. All your livestock will have little ones. 15The Lord will keep you from getting sick. He won’t send on you any of the horrible sicknesses you saw all around you in Egypt. But he’ll send them on everyone who hates you. 16You must destroy all the nations the Lord your God hands over to you. Don’t feel sorry for them. Don’t serve their gods. If you do, they will be a trap for you.

17You might say to yourselves, “These nations are stronger than we are. How can we drive them out?” 18But don’t be afraid of them. Be sure to remember what the Lord your God did to Pharaoh and all the Egyptians. 19With your own eyes you saw what the Lord did to them. You saw the signs and amazing things he did. He reached out his mighty hand and powerful arm. The Lord your God used all those things to bring you out. You are now afraid of the nations that are in the land the Lord promised you. But the Lord your God will do to them the same things he did to Egypt. 20The Lord your God will also send hornets among those nations. Some of the people left alive will hide from you. But even they will die. 21So don’t be terrified by them. The Lord your God is with you. He is a great and wonderful God. 22The Lord your God will drive out those nations to make room for you. But he will do it little by little. You won’t be allowed to get rid of them all at once. If you did, wild animals would multiply all around you. 23But the Lord your God will hand those nations over to you. He will throw them into a panic until they are destroyed. 24He will hand their kings over to you. You will wipe out their names from the earth. No one will be able to stand up against you. You will destroy them. 25Burn the statues of their gods in the fire. Don’t wish for the silver and gold on those statues. Don’t take it for yourselves. If you do, it will be a trap for you. The Lord your God hates it. 26Don’t bring anything he hates into your house. If you do, you will be completely destroyed along with it. So hate it with all your heart. It is set apart to be destroyed.