Deuteronomo 8 – CCL & NIRV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Deuteronomo 8:1-20

Musayiwale Yehova

1Samalani potsata lamulo lililonse limene ndikukupatsani lero, kuti mukhale ndi moyo ndi kuchulukana kuti mulande ndi kulowa mʼdziko limene Yehova analumbira kuti adzapereka kwa makolo anu. 2Kumbukirani mmene Yehova Mulungu wanu anakutsogolerani njira yonse mʼchipululu kwa zaka makumi anayi, kukutsitsani ndi kukuyesani kuti adziwe chimene chinali mu mtima mwanu ngati mungathe kusunga malamulo ake kapena ayi. 3Iye anakutsitsani nakumvetsani njala kenaka nʼkukudyetsani mana amene anali osadziwika kwa inu kapena makolo anu, kuti akuphunzitseni kuti munthu sadzakhala ndi moyo ndi chakudya chokha koma ndi mawu aliwonse ochokera mʼkamwa mwa Yehova. 4Mʼzaka makumi anayi zimenezi, zovala zanu sizinangʼambike ndipo mapazi anu sanatupe. 5Tsono dziwani mu mtima mwanu kuti monga abambo amalanga mwana wawo, momwemonso Yehova Mulungu wanu amakulangani.

6Samalirani malamulo a Yehova Mulungu wanu, kuyenda mʼnjira yake ndi kumuopa Iye. 7Pakuti Yehova Mulungu wanu akukulowetsani mʼdziko labwino, dziko lokhala ndi mitsinje ndi mathawale a madzi, akasupe oyenderera mu zigwa ndi mʼmapiri, 8dziko lokhala ndi tirigu ndi barele, mpesa ndi mitengo ya mkuyu, makangadza, mafuta a olivi ndi uchi; 9dziko limene buledi sadzasowa ndipo simudzasowa chilichonse; dziko limene miyala yake ndi chitsulo ndipo ku mapiri ake mukhoza kukumbako mkuwa.

10Mukadya ndi kukhuta, yamikani Yehova Mulungu wanu chifukwa cha dziko labwino limene wakupatsani. 11Samalani kuopa kuti mungayiwale Yehova Mulungu wanu posasunga malamulo, zikhazikitso ndi malangizo ake amene ndikukupatsani lero, 12kuopa kuti mukadya ndi kukhuta, mukamanga nyumba zabwino ndi kukhalamo, 13ndi pamene ngʼombe zanu ndi nkhosa zanu zaswana, ndi siliva ndi golide wanu wachuluka ndiponso kuti zonse zimene muli nazo zachuluka, 14mtima wanu udzayamba kunyada ndi kuyiwala Yehova Mulungu wanu, amene anakutulutsani ku Igupto, kukuchotsani ku dziko la ukapolo. 15Iye anakutsogolerani kudutsa mʼchipululu chachikulu ndi chochititsa mantha, dziko lija la ludzu ndi lopanda madzi, lokhala ndi njoka zaululu ndi zinkhanira. Iye anatulutsa madzi kuchokera mʼthanthwe lowuma. 16Iye anakupatsani mana kuti mudye mʼchipululu, zinthu zoti ngakhale makolo anu sanazidziwe, kuti akuchepetseni ndi kukuyesani ndipo kuti pa mapeto pake zikuyendereni bwino. 17Mu mtima mwanu mukhoza kuganiza kuti, “Mphamvu zanga ndi kulimbika kwa dzanja langa ndi zimene zandilemeretsa chonchi.” 18Koma kumbukirani Yehova Mulungu chifukwa ndi amene amakupatsani mphamvu zopezera chuma chimenechi kuti atsimikize pangano limene analumbira kwa makolo anu, monga liliri lero lino.

19Ine ndine mboni yokutsutsani lero lino, kuti mukayiwala Yehova Mulungu wanu ndi kutsata milungu ina nʼkumayigwadira, mudzawonongeka ndithu. 20Monga mitundu ina ya anthu imene Yehova anayiwononga pamaso panu, inunso mudzawonongedwa chifukwa chosamvera Yehova Mulungu wanu.

New International Reader’s Version

Deuteronomy 8:1-20

Remember What the Lord Has Done

1Make sure you obey every command I’m giving you today. Then you will live, and there will be many of you. You will enter the land and take it as your own. It’s the land the Lord promised to your people of long ago. 2Remember how the Lord your God led you all the way. He guided you in the desert for these 40 years. He wanted to take your pride away. He wanted to test you to know what was in your hearts. He wanted to see whether you would obey his commands. 3He took your pride away. He let you go hungry. Then he gave you manna to eat. You and your parents had never even known anything about manna before. He tested you to teach you that man doesn’t live only on bread. He also lives on every word that comes from the mouth of the Lord. 4Your clothes didn’t wear out during these 40 years. Your feet didn’t swell. 5Here is what I want you to know in your hearts. The Lord your God guides you, just as parents guide their children.

6Obey the commands of the Lord your God. Live as he wants you to live. Have respect for him. 7The Lord your God is bringing you into a good land. It has brooks, streams and deep springs of water. Those springs flow in its valleys and hills. 8It has wheat, barley, vines, fig trees, pomegranates, olive oil and honey. 9There is plenty of food in that land. You will have everything you need. Its rocks have iron in them. And you can dig copper out of its hills.

10When you have eaten and are satisfied, praise the Lord your God. Praise him for the good land he has given you. 11Make sure you don’t forget the Lord your God. Don’t fail to obey his commands, laws and rules. I’m giving them to you today. 12But suppose you don’t obey his commands. And suppose you have plenty to eat. You build fine houses and live in them. 13The number of your herds and flocks increases. You also get more and more silver and gold. And everything you have multiplies. 14Then your hearts will become proud. And you will forget the Lord your God. The Lord brought you out of Egypt. That’s the land where you were slaves. 15He led you through that huge and terrible desert. It was a dry land. It didn’t have any water. It had poisonous snakes and scorpions. The Lord gave you water out of solid rock. 16He gave you manna to eat in the desert. Your people had never even known anything about manna before. The Lord took your pride away. He tested you. He did it so that things would go well with you in the end. 17You might say to yourself, “My power and my strong hands have made me rich.” 18But remember the Lord your God. He gives you the ability to produce wealth. That shows he stands by the terms of the covenant he made with you. He promised it to your people of long ago. And he’s still faithful to his covenant today.

19Don’t forget the Lord your God. Don’t serve other gods. Don’t worship them and bow down to them. I am a witness against you today that if you do, you will certainly be destroyed. 20You will be destroyed just like the nations the Lord your God is destroying to make room for you. That’s what will happen if you don’t obey him.