Deuteronomo 4 – CCL & CARSA

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Deuteronomo 4:1-49

Alamulidwa Kukhala Womvera

1Mverani inu Aisraeli, malangizo ndi malamulo amene ndikuphunzitseni. Muwatsatire kuti mukhale ndi moyo ndi kuti mulowe ndi kutenga dziko limene Yehova Mulungu wa makolo anu akukupatsani. 2Musawonjezere pa zimene ndikukulamulirani ndipo musachotserepo, koma muwasunge malamulo a Yehova Mulungu wanu amene ndikukupatsani.

3Inu munaona ndi maso anu zimene Yehova anachita ku Baala-Peori. Yehova Mulungu wanu anawononga aliyense amene anatsata Baala wa ku Peori pakati panu. 4Koma inu nonse amene munagwiritsitsa Yehova Mulungu wanu mukanali ndi moyo mpaka lero.

5Taonani, ndakuphunzitsani malangizo ndi malamulo monga Yehova Mulungu wanga anandilamulira kuti inuyo muwatsatire mʼdziko limene mukulowa ndi kulitengali. 6Muwasunge mosamalitsa pakuti zimenezi zidzaonetsa nzeru zanu ndi kuzindikira kwanu kwa anthu a mitundu ina, amene adzamva za malangizo onsewa nati, “Ndithudi, mtundu waukulu uwu ndi wa anthu anzeru ndi ozindikira.” 7Mtundu wina wa anthu ndi uti umene uli waukulu chomwechi, woti ukhoza kukhala ndi milungu yawo pafupi monga mmene alili Yehova Mulungu wathu ndi ife nthawi zonse pamene tipemphera kwa Iye? 8Ndipo ndi mtundu uti mwa mitundu ya anthu umene ndi waukulu chotere kuti nʼkukhala ndi malangizo ndi malamulo olungama ngati malamulo amene ndikuyika pamaso panu lero?

9Inu mungosamala ndi kudziyangʼanira kwambiri nokha kuti musayiwale zimene maso anu aona. Musalole kuti zichoke mʼmitima mwanu pa moyo wanu wonse. Zimenezi muziphunzitse kwa ana anu ndi zidzukulu zanu ngakhale mʼtsogolo. 10Kumbukirani tsiku limene munayimirira pamaso pa Yehova Mulungu wanu ku Horebu, pamene anati kwa ine, “Sonkhanitsa anthu pamaso panga kuti amve mawu anga ndi kuti aphunzire kundilemekeza mʼmoyo wawo onse mʼdzikomo ndi kuti ana awo aziwaphunzitsa zimenezi.” 11Munabwera pafupi ndi kuyima pa tsinde pa phiri pamene phirilo limayaka moto umene umafika mpaka kumwamba. Panalinso mtambo wakuda ndi mdima wambiri. 12Kenaka Yehova anayankhula nanu kuchokera mʼmotowo. Inu munamva mawu ake okha koma simunamuone pakuti panali mawu chabe. 13Iye anakuwuzani Malamulo Khumi omwe ndi pangano lake limene anakulamulirani kuti mutsatire. Ndipo anawalemba malamulowo pa mapale awiri a miyala. 14Ndipo Yehova anandilamula nthawi imene ija kuti ndikuphunzitseni malangizo ndi malamulo amene muyenera kutsata mʼdziko limene mutenge mukawoloka Yorodani.

Mafano Aletsedwa

15Tsiku limene Yehova anayankhula nanu ku Horebu mʼmoto uja, simunaone thupi lake. Choncho mudziyangʼanire nokha mosamalitsa, 16kuti musasokonezeke ndi kudzipangira nokha fano kapena chifanizo cha mtundu uliwonse, kaya chokhala ngati mwamuna kapena ngati mkazi, 17kaya chokhala ngati nyama iliyonse ya pa dziko lapansi kapena mbalame iliyonse yowuluka mlengalenga. 18Kapena cholengedwa chilichonse choyenda pa nthaka kapena nsomba ya mʼmadzi akuya. 19Ndipo pamene muyangʼana kumwamba muona dzuwa, mwezi ndi nyenyezi, zonse zakumwambazo musakopeke kuti muzigwadire ndi kumapembedza zinthu zimene Yehova wapereka kwa anthu a mitundu yonse pa dziko lapansi. 20Koma inuyo, Yehova anakutengani ndi kukutulutsani mʼngʼanjo yosungunulira zitsulo, ku Igupto kuti mukhale anthu olandira chuma chake monga mmene mulili tsopano.

21Yehova anakwiya nane chifukwa cha inu, ndipo analumbira kwathunthu kuti sindidzawoloka Yorodani ndi kulowa mʼdziko labwinolo limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani inu ngati cholowa chanu. 22Ine ndifera mʼdziko lino, sindiwoloka Yorodani. Koma inu mwatsala pangʼono kuwoloka ndi kukatenga dziko labwinolo. 23Samalani, musayiwale pangano limene Yehova Mulungu wanu anapangana nanu ndipo musadzipangire nokha fano la chinthu chilichonse chimene Yehova Mulungu wanu waletsa. 24Pakuti Yehova Mulungu wanu ndi moto wonyeketsa ndipo ndi Mulungu wansanje.

25Mukadzakhala nthawi yayitali mʼdzikomo ndi kubereka ana ndi kukhala ndi zidzukulu ndipo mukadzasokonekera ndi kupanga fano la mtundu uliwonse, nʼkumachita zoyipa pamaso pa Yehova Mulungu wanu ndi kumukwiyitsa, 26ine ndi kuti kumwamba ndi dziko lapansi zikhale mboni lero zokutsutsani kuti mudzawonongedwa msanga ndipo mudzachotsedwa mʼdziko limene mutenge mukawoloka Yorodani. Simudzakhalitsa kumeneko koma mudzawonongedwa ndithu. 27Yehova adzakubalalitsani pakati pa anthu ena. Ochepa okha pakati panu ndi amene adzapulumuke pakati pa anthu a mitundu ina kumene Yehova adzakupirikitsireniko. 28Kumeneko mudzapembedza milungu ya mitengo ndi miyala yopangidwa ndi anthu, imene singaone kapena kumva kapena kudya kapena kununkhiza. 29Mukanali komweko, ngati mudzamufunafuna Yehova Mulungu wanu mudzamupeza koma ngati mutamufunafuna ndi mtima wanu wonse ndi moyo wanu wonse. 30Mukadzakhala pa chipsinjo ndipo zonsezi zikadzakuchitikirani, ndi pamene pambuyo pake mudzabwerera kwa Yehova Mulungu wanu ndi kumumvera Iye. 31Pakuti Yehova Mulungu wanu ndi Mulungu wachifundo, Iye sadzakutayani kapena kukuwonongani kapena kuyiwala pangano lake ndi makolo anu, limene analitsimikiza mwa lumbiro.

Yehova Ndiye Mulungu

32Tsopano tafunsani za masiku a mʼmbuyomu, zakale inu musanabadwe, kuyambira tsiku limene Mulungu analenga munthu pa dziko lapansi. Tafufuzani kuyambira kumapeto mpaka mapeto anzake a thambo. Kodi chinachitikako china chachikulu ngati ichi, kapena chinayamba chamvekako chokhala ngati ichi? 33Kodi uliponso mtundu wina wa anthu umene unamva mawu a Mulungu akuyankhula kuchokera mʼmoto nʼkukhala ndi moyo monga mwachitira inumu? 34Kodi alipo mulungu amene anayeserapo kudzitengera mtundu wa anthu kuwachotsa mu mtundu unzake mwa mayesero, zizindikiro zozizwitsa, nkhondo, komanso mwa mphamvu zake zopanda malire, kapena mwa zochita zazikulu ndi zochititsa mantha, monga zimene Yehova Mulungu wanu anakuchitirani ku Igupto inu mukupenya?

35Iye anakuonetsani zonsezi kuti inu muzindikire kuti Yehova ndiye Mulungu, palibenso wina wofanana naye. 36Kuchokera kumwamba, Iye anafuna kuti inu mumve mawu ake ndi kuti mukhale osunga mwambo. Pa dziko lapansi anakuonetsani moto waukulu, ndipo inu munamva mawu ake kuchokera mʼmotomo. 37Popeza anakonda makolo anu ndi kusankha adzukulu awo, a pambuyo pawo, anakutulutsani kuchoka ku Igupto ali pakati panu ndi mphamvu yake, 38kuti akupirikitsireni mayiko akuluakulu ndi amphamvu kuposa inu, ndi kukubweretsani inu ku dziko lawo kuti likhale lanu, monga liliri lero.

39Vomerezani lero ndipo dziwani mu mtima mwanu kuti Yehova ndiye Mulungu kumwamba ndi pa dziko lapansi. Palibenso wina. 40Sungani malangizo ake ndi malamulo ake amene ndikukupatsani lero lino, kuti zikuyendereni bwino inu ndi ana anu kutsogoloko, ndi kuti mukhalitse mʼdziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani kwa nthawi zonse.

Mizinda Yothawirako

41Kenaka Mose anapatula mizinda itatu cha kummawa kwa Yorodani, 42kumene aliyense amene wapha munthu akhoza kuthawirako ngati wopha munthuyo sanaphe mnzakeyo mwadala ndi maganizo oyipa. Iye akhoza kuthawira ku umodzi mwa mizinda imeneyi napulumutsa moyo wake. 43Mizindayo inali iyi: ku fuko la Rubeni, unali mzinda wa Bezeri ku mapiri a ku chipululu; ku fuko la Gadi, unali Ramoti ku Giliyadi; ndipo ku fuko la Manase, unali Golani ku Basani.

Kufotokozera za Malamulo

44Awa ndi malamulo amene Mose anapereka kwa Aisraeli. 45Izi ndi ndondomeko, malangizo ndi malamulo amene Mose anawapatsa iwo pamene anatuluka ku Igupto. 46Anali ku chigwa cha kufupi ndi Beti-Peori mbali ya kummawa kwa Yorodani, mʼdziko la Sihoni mfumu ya Aamori amene ankalamulira ku Hesiboni ndipo anagonjetsedwa ndi Mose ndi Aisraeli pamene ankachokera ku Igupto. 47Iye anamulanda dziko lake ndi dziko la Ogi mfumu ya ku Basani. Awa anali mafumu awiri Aamori a kummawa kwa Yorodani. 48Dziko ili linayambira ku Aroeri cha kumphepete kwa khwawa la Arinoni ku phiri la Siyoni (limeneli ndi phiri la Herimoni), 49ndi kuphatikizapo dziko lonse la Araba cha kummawa kwa Yorodani mpaka kukafika ku Nyanja ya Araba, kumunsi kwa Phiri la Pisiga.

Священное Писание (Восточный перевод), версия с «Аллахом»

Второзаконие 4:1-49

Ценность Закона Аллаха

1Слушайте, исраильтяне, установления и законы, которым я учу вас. Следуйте им, чтобы жить, чтобы пойти и завладеть землёй, которую Вечный, Бог ваших предков, даёт вам. 2Не прибавляйте и не убавляйте ничего к тому, что я повелеваю вам. Исполняйте повеления Вечного, вашего Бога, которые я даю вам.

3Вы своими глазами видели всё, что Вечный сделал в Баал-Пеоре. Вечный, ваш Бог, истребил среди вас всех, кто поклонялся идолу Баал-Пеору, 4но все те, кто остались верны Вечному, вашему Богу, по-прежнему живы и сегодня4:4 См. Чис. 25..

5Смотрите, я научил вас установлениям и законам, как и повелел мне Вечный, мой Бог, чтобы вы следовали им в земле, куда вы вступаете, чтобы завладеть ею. 6Соблюдайте их тщательно, чтобы доказать свою мудрость и рассудительность народам, которые услышат об этих установлениях и скажут: «Конечно, это великий народ, мудрый и разумный». 7Какой ещё народ столь велик, что его боги были близки к нему так, как Вечный, наш Бог, близок к нам, когда бы мы ни молились Ему? 8И какой ещё народ столь велик, что у него были такие же справедливые установления и законы, как те, которые я даю вам сегодня?

9Только будьте осторожны и внимательно следите за собой, чтобы не забыть то, что видели ваши глаза, и не дать ускользнуть воспоминаниям из вашего сердца, пока вы живы. Рассказывайте об этом своим детям и детям их детей. 10Помните тот день, когда вы стояли перед Вечным, вашим Богом, у горы Синай4:10 Букв.: «у Хорива». Хорив – другое название горы Синай. Также в ст. 15 и 5:2. и когда Он сказал мне: «Собери народ предо Мною, Я возвещу им Свои слова, чтобы они научились чтить Меня всю свою жизнь на земле и научили этому своих детей». 11Вы приблизились и встали у подножия горы, которая пылала огнём до самых небес, покрытых чёрными тучами и кромешной тьмой. 12Тогда Вечный заговорил с вами из пламени. Вы слышали слова, но не видели образа – только Его голос был слышен. 13Он объявил вам Своё священное соглашение, десять повелений4:13 Букв.: «десять слов»., которым Он повелел вам следовать, и написал их на двух каменных плитках. 14В то время Вечный повелел мне научить вас установлениям и законам, которые вы должны соблюдать в земле, куда вы вступаете, чтобы завладеть ею.

Запрет идолопоклонства

15Итак, твёрдо помните, что вы не видели никакого образа в тот день, когда Вечный говорил с вами у горы Синай из огня, 16чтобы не развратиться и не сделать себе идола – образ в какой-либо форме, изображающий мужчину или женщину, 17или какое-либо животное на земле, какую-нибудь птицу, летающую под небесами, 18какое-нибудь пресмыкающееся по земле, или рыбу в водах. 19А когда вы посмотрите на небо и увидите солнце, луну и звёзды – всё небесное многообразие, то не соблазняйтесь: не поклоняйтесь и не служите тому, что Вечный, ваш Бог, уделил всем народам под небом. 20Но что до вас – Вечный взял вас и вынес из плавильной печи, из Египта, чтобы вы были народом Его наследия, как сейчас.

21Вечный разгневался на меня из-за вас и поклялся, что я не перейду через Иордан и не войду в благодатную землю, которую Вечный, ваш Бог, даёт вам в наследие. 22Я умру в этой земле; я не перейду через Иордан, но вы перейдёте и завладеете благодатной землёй. 23Берегитесь, чтобы не забыть священное соглашение Вечного, вашего Бога, которое Он заключил с вами. Не делайте себе идола ни в какой форме, как запретил вам Вечный, ваш Бог. 24Ведь Вечный, ваш Бог, – это пожирающий огонь, Он – ревнивый Бог.

25У вас появятся дети и внуки, вы проживёте на земле долгое время, но если потом вы развратитесь и сделаете какого-нибудь идола, совершая зло в глазах Вечного, вашего Бога, и вызывая Его гнев, – 26я призываю сегодня в свидетели против вас небо и землю, – вы будете скоро истреблены из земли, куда вы переходите через Иордан, чтобы завладеть ею. Вы недолго проживёте там и непременно будете уничтожены. 27Вечный рассеет вас между народами, и лишь немногие выживут среди народов, к которым Вечный прогонит вас. 28Там вы будете служить богам, сделанным человеком из дерева и камня, которые не могут ни видеть, ни слышать, ни есть, ни чуять запах. 29Но там-то вы и начнёте искать Вечного, вашего Бога, и найдёте Его, если будете искать всем сердцем и всей душой. 30Когда вас постигнет скорбь и всё это случится с вами, вы вернётесь к Вечному, вашему Богу, и будете слушаться Его. 31Ведь Вечный, ваш Бог, – это милостивый Бог; Он не оставит и не погубит вас и не забудет священное соглашение с вашими предками, которое Он скрепил клятвой.

Вечный – единственный Бог

32Спросите о прежних днях, которые были задолго до вас, с того дня, когда Аллах сотворил на земле человека; спросите от края до края небес. Случалось ли что-нибудь подобное этому великому делу, и разве слышали когда-нибудь о чём-то подобном? 33Разве слышал какой-нибудь другой народ голос Бога, говорящего из огня, как слышали вы, и остался жив? 34Разве когда-нибудь пробовал какой-нибудь бог взять себе народ из другого народа – испытаниями, знамениями и чудесами, войной, могучей и простёртой рукой, великими и ужасными подвигами, как сделал это для вас Вечный, ваш Бог, в Египте у вас на глазах?

35Вам было явлено это, чтобы вы знали, что Вечный – это Бог, и нет другого Бога, кроме Него. 36Он дал вам услышать Свой голос с неба, чтобы наставить вас. На земле Он показал вам Свой великий огонь, и вы слышали Его слова из огня. 37Он полюбил ваших предков и избрал их потомков, Он Сам вывел вас из Египта4:37 Или: «Он вывел вас из Египта Своим присутствием и…» Своей великой силой, 38чтобы прогнать от вас народы, которые многочисленнее и сильнее, и привести вас в их землю, отдав её вам в наследие, как это и есть сегодня.

39Знайте ныне и запомните навсегда, что Вечный – это Бог на небе вверху и на земле внизу, и нет другого. 40Исполняйте Его установления и повеления, которые я даю вам сегодня, чтобы с вами и с вашими детьми всё было благополучно и чтобы вы долго жили на земле, которую Вечный, ваш Бог, даёт вам навсегда.

Города-убежища

(Чис. 35:6-34; Втор. 19:1-14; Иеш. 20:1-9)

41Затем Муса отделил к востоку от Иордана три города, 42куда мог убежать всякий, кто убьёт человека неумышленно, не питая к убитому ненависти. Он мог убежать в один из этих городов и тем спасти свою жизнь. 43Вот эти города: Бецер на пустынном плато для рувимитов; Рамот в Галааде для гадитов; Голан в Башане для манасситов.

Вступление к Закону

44Вот Закон, который Муса изложил исраильтянам. 45Вот заповеди, установления и законы, которые Муса дал им, когда они вышли из Египта 46и находились в долине рядом с Бет-Пеором к востоку от Иордана, в земле Сигона, царя аморреев, который правил в Хешбоне и был побеждён Мусой и исраильтянами, когда они вышли из Египта. 47Они завладели его землёй и землёй Ога, царя Башана, двух аморрейских царей, к востоку от Иордана. 48Эта земля простиралась от города Ароера на берегу реки Арнон до горы Сирион (то есть Хермон), 49и включала всю Иорданскую долину к востоку от Иордана до самого Мёртвого моря4:49 Букв.: «моря Аравы». под склонами Фасги.