Deuteronomo 29 – CCL & NSP

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Deuteronomo 29:1-29

Kukonzanso Pangano

1Awa ndiwo mawu a mʼpangano limene Yehova analamula Mose kuti achite ndi Aisraeli ku Mowabu, powonjezera pa pangano limene anapangana nawo ku Horebu.

2Mose anayitanitsa Aisraeli onse nati kwa iwo:

Inu munaona zonse zimene Yehova anachita kwa Farao, nduna zake ndi dziko lake lonse ku Igupto. 3Ndi maso anu munaona mayesero onse aja, zizindikiro zozizwitsa ndi zodabwitsa zazikulu zija. 4Koma mpaka lero Yehova sanakupatseni mtima wozindikira kapena maso openya kapena makutu akumva. 5Mʼzaka makumi anayi zimene ndinakutsogolerani mʼchipululu, zovala zanu ndiponso nsapato za ku mapazi anu sizinangʼambike. 6Inu simunadye buledi ndi kumwa vinyo kapena chakumwa chilichonse choledzeretsa. Ndinachita izi kuti mudziwe kuti Ine ndine Yehova Mulungu wanu.

7Pamene munafika malo ano, Sihoni mfumu ya ku Hesiboni ndi Ogi mfumu ya ku Basani anabwera kudzamenyana nafe koma tinawagonjetsa iwo. 8Tinatenga dziko lawo ndi kulipereka ngati cholowa cha fuko la Rubeni, fuko la Gadi ndi theka la fuko la Manase.

9Tsatirani mosamalitsa mawu a mʼpangano ili kuti zinthu zizikuyenderani bwino pa zochitika zanu zonse. 10Lero lino nonse mukuyima pamaso pa Yehova Mulungu wanu, atsogoleri a mafuko anu, akuluakulu ndi nduna zanu, ndi amuna ena onse a mu Israeli, 11pamodzi ndi ana ndi akazi anu, kudzanso alendo amene akukhala pakati panu omwe amakuwazirani nkhuni ndi kukutungirani madzi. 12Mukuyimirira pano kuti mulowe mʼpangano ndi Yehova Mulungu wanu, pangano limene Yehova akuchita ndi inu lero ndi kulisindikiza ndi malumbiro, 13kukukhazikitsani lero lino ngati anthu ake, ndi kuti Iye akhale Mulungu wanu monga anakulonjezani inu ndiponso monga analumbira kwa makolo anu Abrahamu, Isake ndi Yakobo. 14Ndikupanga pangano ili ndi malumbiro ake osati kwa inu nokha, 15amene muli pano pamaso pa Yehova Mulungu wathu, koma ndi iwonso amene sali pano lero.

16Inu nomwe mukudziwa mmene tinkakhalira ku Igupto ndi mmene tinadutsira mayiko pa ulendo wobwera kuno. 17Ife tinaona pakati pawo mafanizo ndi mafano awo onyansa, amtengo ndi amiyala, asiliva ndi agolide. 18Onetsetsani kuti pasapezeke mwamuna kapena mkazi, banja kapena fuko pakati panu lero amene mtima wawo udzapandukira Yehova Mulungu wanu ndi kupita kukapembedza milungu ya mitundu iyo. Onetsetsani kuti pasapezeke muzu pakati panu wotulutsa mankhwala akupha otere.

19Munthu wotere akamva mawu a lumbiro ili, asadzidalitse yekha mʼmaganizo mwake namati, “Ine ndidzapulumuka ngakhale nditapitiriza kuyenda njira yanga.” Zoterezi zidzadzetsa masautso pa nthaka ya chinyontho ndi yowuma yomwe. 20Yehova sadzamukhululukira. Mkwiyo ndi nsanje ya Yehova zidzamuyakira munthuyo. Matemberero onse wolembedwa mʼbukuli adzamugwera iye ndipo Yehova adzafafaniza dzina lake pa dziko lapansi. 21Yehova adzasankha pakati pa Aisraeli anthu oyenera masautso monga mwa matemberero onse a mʼpangano olembedwa Mʼbuku la Malamulo.

22Ana anu a mibado yakutsogolo ndi alendo amene adzachokera kutali adzaona matsoka amene adzakugwerani mʼdziko muno ndiponso matenda amene Yehova adzabweretsa pa dzikoli. 23Dziko lonse lidzasanduka nthaka ya mchere ndi ya sulufule. Simudzadzalamo kanthu, simudzakhala chomera chilichonse, ndi mbewu yomera mʼmenemo. Dziko lanu lidzakhala lowonongeka ngati Sodomu ndi Gomora, Adima ndi Zeboimu, mizinda imene Yehova anayiwononga ndi mkwiyo wake waukulu. 24Mitundu yonse ya anthu idzafunsa kuti, “Kodi chifukwa chiyani Yehova anachita zotere mʼdziko lake? Kodi chifukwa chiyani anaonetsa mkwiyo woopsa wotere?”

25Ndipo yankho la mafunso amenewa lidzakhala lakuti, “Chifukwa chakuti anthu awa aphwanya pangano la Yehova Mulungu wa makolo awo, pangano limene Iye anapangana nawo pamene anawatulutsa ku Igupto. 26Iwo anachoka ndi kukatumikira milungu ina ndi kuyipembedza, milungu imene sanayidziwe, milungu imene sanawapatse. 27Choncho Yehova anakwiyira dziko lino, kotero anabweretsa matemberero onse amene analembedwa mʼbuku lino. 28Ndi mkwiyo komanso ukali wake woopsa Yehova anawazula mʼdziko lawo ndi kuwaponyera mʼdziko lina, monga mmene zilili lero lino.”

29Zinsinsi ndi za Yehova Mulungu wathu koma zinthu zimene zaululidwa ndi zathu ndi ana athu kwamuyaya, kuti titsatire mawu onse a mʼmalamulowa.

New Serbian Translation

5. Мојсијева 29:1-29

Обнова савеза

1Ово су речи савеза који је Господ заповедио Мојсију да склопи са Израиљцима у земљи моавској, осим савеза који је склопио са њима на Хориву.

2Мојсије позва све Израиљце и рече им:

Ви сте видели све што је Господ на ваше очи учинио у Египту фараону, свим његовим дворанима и целој његовој земљи. 3Својим очима си видео велика искушења, знакове и она велика чудеса. 4Господ вам све до данас није дао ум да разумете, очи да видите и уши да чујете. 5Четрдесет година сам вас водио по пустињи; одећа вам се није поцепала, нити вам се обућа на вашим ногама подерала. 6Хлеба нисте јели, вина и жестока пића нисте пили, да бисте знали да сам ја Господ, Бог ваш.

7Када сте дошли на ово место у сусрет вам је изашао Сихон, цар есевонски, и Ог, цар васански, да зарате против нас, али смо их ми потукли. 8Узели смо њихову земљу и дали је у наследство Рувимовом и Гадовом племену, и половини Манасијиног племена.

9Зато држите и вршите речи овог савеза, да бисте имали успеха у свему што радите. 10Данас сви стојите у присуству Господа, Бога свога: главари ваших племена, старешине и војни заповедници, сви Израиљци, 11ваша деца и жене, странци који живе у вашем табору – од онога што ти цепа дрва до онога што ти носи воду – 12да ступите у савез са Господом, Богом својим, који Господ, Бог ваш, склапа данас са вама, 13да би те поставио данас себи за народ, и да би био твој Бог, као што ти је обећао, и као што се заклео твојим оцима, Аврахаму, Исаку и Јакову. 14Овај савез и ову заклетву не склапам само са вама, 15који данас стојите овде са нама пред Господом, Богом нашим, него и са онима који данас нису овде.

16Ви, наиме, и сами знате како смо живели у египатској земљи и како смо пролазили посред народа; оних народа кроз које сте прошли. 17Видели сте њихове гадости и идоле од дрвета и камена, сребра и злата, који су код њих. 18Нека се не нађе међу вама мушкарац или жена, породица или племе коме би се данас срце одвратило од Господа, Бога нашег, да иде да служи боговима тих народа. Нека међу вама не буде корена који рађа отров или пелен.

19Ако неко чује речи ове заклетве, и да себи благослов говорећи у себи: „Биће све у реду са мном, па ако и живим по самовољи свога срца“, поплава ће однети суву земљу. 20Господ неће бити вољан да опрости таквоме, него ће Господњи гнев и љубомора планути на њега, па ће свака клетва записана у овој књизи пасти на њега. Тако ће Господ истребити његово име под небом. 21Господ ће одвојити зликовца од свих племена Израиљевих, по свим клетвама савеза које су написане у књизи овог Закона.

22Тада ће каснији нараштај, ваши синови који дођу после вас и дошљак који дође из далеке земље, кад виде ране на земљи и њене болести којима ју је Господ ударио, рећи: 23„Цела је земља спаљена сумпором и сољу! Нико је не сеје, ништа из ње не ниче, никаква трава из ње не расте. Опустошена је као Содома и Гомора, као Адма и Севојим, које Господ уништи у свом гневу и јарости!“ 24Сви ће народи питати: „Зашто Господ учини овако са овом земљом? Шта изазва овај велики пламтећи гнев?“

25Одговориће им: „Зато што су напустили савез Господа, Бога својих отаца, који је склопио са њима кад их је извео из земље египатске. 26Отишли су да служе и клањају се другим боговима, боговима за које нису знали и које им он није наменио. 27Зато је плануо гнев Господњи на ову земљу, пустивши на њу сва проклетства која су записана у овој књизи. 28Господ их је искоренио из њихове земље у љутини, јарости и великом гневу, и бацио их у другу земљу. Тако је и данас.“

29Што је скривено, то припада Господу, Богу нашем, а што је откривено, то припада нама и нашој деци заувек, да вршимо све речи овога Закона.