Deuteronomo 24 – CCL & BPH

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Deuteronomo 24:1-22

1Ngati mwamuna wakwatira mkazi amene sakukondwera naye chifukwa wapeza vuto pa mkaziyo, namulembera mkaziyo kalata ya chisudzulo, namupatsa ndi kumutulutsa mʼnyumba mwake, 2mkaziyo ndi kukakwatiwa ndi mwamuna wina, 3ndipo mwamuna wachiwiriyo nʼkuyipidwa nayenso ndi kumulemberanso kalata ya chisudzulo nʼkumutulutsa mʼnyumba mwake, kapena ngati mwamunayo amwalira, 4mwamuna wake woyamba uja, amene anamuleka saloledwanso kumukwatira kachiwiri popeza mkaziyo wadetsedwa. Chimenechi ndi chonyansa pamaso pa Yehova. Musalowetse tchimo mʼdziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani ngati cholowa chanu.

5Mwamuna akangokwatira kumene asamatumizidwe ku nkhondo kapena kupatsidwa ntchito ina iliyonse. Kwa chaka chathunthu akhale ndi ufulu wokhala pa khomo pake kumasangalatsa mkazi wakeyo.

6Munthu akakhala nanu ndi ngongole musamutengere mwala wake wa mphero ngati chikole, chifukwa kutero nʼkumutengera moyo kukhala chikole cha ngongole.

7Ngati munthu agwidwa akuba mʼbale wake wa Chiisraeli namamuzunza ngati kapolo kapena kumugulitsa, wogulitsa mnzakeyo ayenera kuphedwa. Muyenera kuchotsa choyipa pakati panu.

8Pakagwa matenda a khate, samalitsani kuchita zonse zimene ansembe, amene ndi Alevi, anakulangizani. Mutsatire mosamalitsa zimene ndinawalamula. 9Kumbukirani zimene Yehova Mulungu wanu anachita kwa Miriamu muli paulendo mutatuluka mu Igupto.

10Ukabwereketsa mnzako kanthu kena kalikonse, usalowe mʼnyumba mwake kukatenga chimene wachipereka ngati chikole. 11Uziyima kunja kwa nyumba kuti munthu amene wamubwereketsa kanthuyo akubweretsere kunja komweko. 12Ngati munthuyo ndi wosauka, usamutengere chikolecho mpaka kukagona nacho kwanu. 13Pomalowa dzuwa ukhale utamubwezera mkanjo wakewo kuti akafunde. Pamenepo adzakuthokoza, ndipo amenewa adzawerengedwa ngati machitidwe olungama kwa iweyo pamaso pa Yehova Mulungu wako.

14Osamapezera mwayi pa anthu aganyu osauka ndi aumphawi, kaya ndi Mwisraeli kapena mlendo wokhala mu umodzi mwa mizinda yanu. 15Mumulipire malipiro ake a tsiku dzuwa lisanalowe chifukwa ndi wosauka ndipo akudalira malipirowo. Kupanda kutero adzakudandaulirani kwa Yehova ndipo mudzapezeka ochimwa.

16Makolo asaphedwe chifukwa cha ana awo, ndipo ana asaphedwe chifukwa cha makolo awo, koma aliyense ayenera kufa chifukwa cha zolakwa zake.

17Musachitire mlendo kapena mwana wamasiye zoyipa, kapena kulanda mkazi wamasiye chovala ngati chikole cha ngongole. 18Kumbukirani kuti munali akapolo mʼdziko la Igupto ndipo Yehova Mulungu wanu anakuwombolani kumeneko. Nʼchifukwa chake ndikukulamulani kuti muzichita zimenezi.

19Mukamakolola mʼmunda mwanu ndipo zokolola zina zikasiyidwa, musamabwerere kukazitola. Muzilekere alendo, ana ndi akazi amasiye, kuti Yehova Mulungu wanu akudalitseni pa zochita zanu zonse. 20Mukathyola zipatso mu mtengo wa olivi, musamabwererenso kachiwiri ku mtengo womwewo. Zotsalazo zilekereni alendo, ana ndi akazi amasiye. 21Mukakolola mphesa mʼmunda mwanu musamabwereremonso kachiwiri. Zotsalazo muzilekere alendo, ana ndi akazi amasiye. 22Kumbukirani kuti munali akapolo mʼdziko la Igupto. Nʼchifukwa chake ndikukulamulani kuti muzichita zimenezi.

Bibelen på hverdagsdansk

5. Mosebog 24:1-22

1Hvis en mand gifter sig, og hvis hans kone senere falder i unåde hos ham, fordi han opdager, at hun har gjort noget usømmeligt, kan han give hende et skilsmissebrev og derefter sende hende bort. 2Hvis hun gifter sig igen, 3og den anden mand også sender hende væk, eller han dør, 4kan den første mand ikke gifte sig med hende igen, for hun er blevet uren, ja, det ville være afskyeligt i Herrens øjne og bringe skyld over det land, han vil give jer i eje.

5En nygift mand må ikke indkaldes til krigstjeneste eller pålægges andre offentlige forpligtelser. Det første år skal han have lov til at blive hjemme og glæde sig sammen med sin kone.

6Det er ulovligt at tage et redskab24,6 Teksten nævner her et specifikt redskab: en håndkværn eller den øverste kværnsten, altså den runde sten, der bruges i husholdningen til at male kornet til mel hver dag. i pant, som ejeren har brug for til den daglige madlavning.

7Hvis nogen kidnapper en landsmand og sælger ham eller på anden måde udnytter ham, skal kidnapperen dø, for at det onde kan udryddes fra jeres midte.

8I tilfælde af smitsomme hudsygdomme skal I nøje følge de instrukser, præsterne giver. Jeg har jo givet dem reglerne, for at de skal følges. 9Glem ikke, hvad Herren gjorde imod Mirjam på vej fra Egypten.

10Hvis I har udlånt noget til en anden, må I ikke gå ind i hans hus for at hente et pant. 11Vent udenfor, til han kommer ud med det, han vil give i pant. 12-13Hvis manden er fattig og kun har sit overtøj at give i pant, må I ikke beholde det natten over, men I skal returnere det senest ved solnedgang, så han kan holde varmen om natten og velsigne jer for jeres godhed. På den måde gør I det, som er rigtigt i Herrens øjne.

14-15I må ikke udnytte en fattig daglejer, hvad enten han er en landsmand eller en fremmed, der bor iblandt jer. Betal ham hans dagløn hver dag ved solnedgang, for han er fattig og har brug for pengene straks. Gør I ikke det, vil Herren høre hans beklagelser og kræve jer til regnskab for jeres synd.

16Forældre må ikke straffes for deres børns synder, og børn må ikke straffes for deres forældres synder. Dødsstraf kan kun idømmes den, der selv er ansvarlig for sin forbrydelse.

17I skal behandle fremmede og forældreløse retfærdigt, og I må ikke tage en enkes tøj i pant for, hvad hun skylder jer. 18Husk på, at I selv var fremmede og hjælpeløse i Egypten, dengang Herren, jeres Gud, befriede jer. Det er baggrunden for denne befaling. 19Hvis I under høstarbejdet overser et neg på marken, skal I lade det ligge, så den fremmede, enken eller den forældreløse kan samle det op. Så vil Herren velsigne jer i jeres arbejde. 20Og når I har høstet jeres oliven ved at slå på træets grene, må I ikke gå grenene efter, men skal efterlade resten til den fremmede, enken og den forældreløse. 21Det samme gælder under vinhøsten: Gå ikke rankerne efter, men efterlad de sidste druer til dem, der ikke selv har marker. 22Husk på, at I selv engang var slaver i Egypten og intet ejede.